< Luka 8 >
1 Zitatha izi, Yesu anayendayenda kuchoka mzinda wina kupita wina ndiponso mudzi wina kupita wina, akulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu. Ophunzira ake khumi ndi awiri aja anali naye,
And it came to pass afterward, that he went throughout every city and village, preaching and showing the glad tidings of the kingdom of God: and the twelve [were] with him,
2 komanso akazi ena amene anachiritsidwa ku mizimu yoyipa ndi matenda: Mariya, wotchedwa Magadalena, amene mwa iye munatuluka ziwanda zisanu ndi ziwiri;
And certain women, who had been healed of evil spirits and infirmities, Mary called Magdalene, out of whom went seven demons.
3 Yohana mkazi wa Kuza, woyangʼanira mʼnyumba ya Herode; Suzana; ndi ena ambiri analinso. Akazi awa ankawathandiza ndi chuma chawo.
And Joanna the wife of Chuza Herod's steward, and Susanna, and many others, who ministered to him of their substance.
4 Anthu ambiri ankasonkhana, ndipo pamene anthu ankabwera kwa Yesu kuchokera ku midzi, Iye anawawuza fanizo ili,
And when many people were collected, and had come to him out of every city, he spoke by a parable:
5 “Mlimi anapita kukafesa mbewu zake. Akufesa mbewuzo, zina zinagwa mʼmbali mwa njira; zinapondedwa, ndipo mbalame zamlengalenga zinadya.
A sower went out to sow his seed: and as he sowed, some fell by the way side; and it was trodden down, and the fowls of the air devoured it.
6 Zina zinagwa pa thanthwe, ndipo pamene zinamera, zinafota chifukwa panalibe chinyezi.
And some fell upon a rock; and as soon as it was sprung up, it withered, because it lacked moisture.
7 Mbewu zina zinagwera pakati pa minga, zinakulira pamodzi ndi mingazo ndipo zinalepheretsa mmerawo kukula.
And some fell among thorns; and the thorns sprang up with it, and choked it.
8 Mbewu zina zinagwera pa nthaka yabwino. Zinamera ndipo zinabala mowirikiza 100 kuposa zimene zinafesedwa zija.” Atanena izi, anafuwula kuti, “Amene ali ndi makutu, amve.”
And other fell on good ground, and sprang up, and bore fruit a hundred-fold. And when he had said these things, he cried, He that hath ears to hear, let him hear.
9 Ophunzira ake anamufunsa tanthauzo lake la fanizolo.
And his disciples asked him, saying, What doth this parable mean?
10 Iye anati, “Kudziwa zinsinsi za ufumu wa Mulungu kwapatsidwa kwa inu, koma kwa ena ndimawayankhula mʼmafanizo kuti, “ngakhale akuona, asapenye; ngakhale akumva, asazindikire.”
And he said, To you it is given to know the mysteries of the kingdom of God: but to others in parables; that seeing they may not see, and hearing they may not understand.
11 “Tanthauzo la fanizoli ndi ili: Mbewu ndi mawu a Mulungu.
Now the parable is this: The seed is the word of God.
12 Mbewu za mʼmbali mwa njira ndi anthu amene amamva mawu, ndipo kenaka mdierekezi amabwera ndi kuchotsa mawuwo mʼmitima mwawo kuti asakhulupirire ndi kupulumutsidwa.
Those by the way side, are they that hear; then cometh the devil, and taketh away the word out of their hearts, lest they should believe and be saved.
13 Mbewu za pa thanthwe ndi anthu amene amalandira mawu mwachimwemwe pamene akumva, koma mawuwo sazika mizu. Iwo amakhulupirira kwa kanthawi, koma pa nthawi ya mayesero, amagwa.
They on the rock [are they], who, when they hear, receive the word with joy; and these have no root, who for a while believe, and in time of temptation fall away.
14 Mbewu zimene zinagwa pakati pa minga zikuyimira anthu amene amamva mawu, koma akamayenda mʼnjira zawo amatsamwitsidwa ndi zodandaulitsa za moyo uno, chuma ndi zosangalatsa, ndipo iwo samakhwima.
And that which fell among thorns are they, who, when they have heard, go forth, and are choked with cares and riches and pleasures of [this] life, and bring no fruit to perfection.
15 Koma mbewu za pa nthaka yabwino zikuyimira anthu amene ali ndi mtima woona ndi wabwino, amene amamva mawu nawasunga, ndipo amalimbikira mpaka amabala zipatso.
But that on the good ground are they, who in an honest and good heart, having heard the word, keep [it], and bring forth fruit with patience.
16 “Palibe amayatsa nyale ndi kuyibisa mu mtsuko kapena kuyika pansi pa bedi. Koma mʼmalo mwake, amayika pa choyikapo chake, kuti anthu olowamo aone kuwala.
No man, when he hath lighted a candle, covereth it with a vessel, or putteth [it] under a bed; but setteth [it] on a candlestick, that they who enter in may see the light.
17 Pakuti palibe kanthu kobisika kamene sikadzawululika, ndipo palibe kanthu kophimbika kamene sikadzadziwika kapena kuonetsedwa poyera.
For nothing is secret, that shall not be made manifest; neither [any thing] hid, that shall not be known, and come abroad.
18 Choncho ganizirani mozama. Iye amene ali nazo adzapatsidwa zambiri, iye amene alibe, ngakhale chimene akuganiza kuti ali nacho adzalandidwa.”
Take heed therefore how ye hear: for whoever hath, to him shall be given; and whoever hath not, from him shall be taken even that which he seemeth to have.
19 Tsopano amayi ndi abale a Yesu anabwera kudzamuona Iye, koma analephera kuti afike pafupi ndi Iye chifukwa cha gulu la anthu.
Then came to him [his] mother and his brethren, and could not come near to him for the crowd.
20 Wina anamuwuza Iye kuti, “Amayi ndi abale anu ayima kunja, akufuna kukuonani.”
And it was told to him [by certain], who said, Thy mother and thy brethren stand without, desiring to see thee.
21 Yesu anayankha kuti, “Amayi ndi abale anga ndi amene amamva mawu a Mulungu ndi kumachita zimene mawuwo akunena.”
And he answered and said to them, My mother and my brethren are these who hear the word of God, and do it.
22 Tsiku lina Yesu anati kwa ophunzira ake, “Tiyeni tiwolokere tsidya lina la nyanja.” Ndipo analowa mʼbwato nanyamuka.
Now it came to pass on a certain day, that he went into a boat with his disciples: and he said to them, Let us go over to the other side of the lake. And they lanched forth.
23 Akuwoloka, Iye anagona tulo. Namondwe wamkulu anayamba pa nyanja, ndipo bwatolo linayamba kudzaza ndi madzi ndipo anali pa chiopsezo chachikulu.
But as they sailed, he fell asleep: and there came down a storm of wind on the lake; and they were filled [with water], and were in jeopardy.
24 Ophunzira anapita ndi kukamudzutsa Iye, nati, “Ambuye, Ambuye, ife tikumira!” Anadzuka ndipo anadzudzula mphepo ndi madzi owindukawo. Namondwe anasiya, ndipo panali bata.
And they came to him, and awoke him, saying, Master, master, we perish. Then he arose, and rebuked the wind, and the raging of the water: and they ceased, and there was a calm.
25 Iye anafunsa ophunzira ake kuti, “Chikhulupiriro chanu chili kuti?” Koma pogwidwa ndi mantha ndi kudabwa anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Uyu ndi ndani? Iye alamulira ngakhale mphepo ndi madzi, ndipo zimumvera Iye.”
And he said to them, Where is your faith? And they being afraid, wondered, saying one to another, What manner of man is this! for he commandeth even the winds and water, and they obey him.
26 Iwo anawolokera ku chigawo cha Gerasa chimene chili tsidya lina la nyanja kuchokera ku Galileya.
And they arrived at the country of the Gadarenes, which is over against Galilee.
27 Yesu ataponda pa mtunda, anakumana ndi munthu wogwidwa ndi ziwanda wochokera mu mzindawo. Kwa nthawi yayitali munthuyu sanavale zovala kapena kukhala mʼnyumba, koma amakhala ku manda.
And when he went forth to land, there met him out of the city a certain man, who had demons a long time, and wore no clothes, neither abode in [any] house, but in the tombs.
28 Iye ataona Yesu, anakuwa nagwa pa mapazi ake akufuwula kwambiri kuti, “Mukufuna chiyani ndi ine, Yesu Mwana wa Mulungu Wammwambamwamba? Ndikupemphani Inu, musandizunze ine!”
When he saw Jesus, he cried out, and fell down before him, and with a loud voice said, What have I to do with thee, Jesus, [thou] Son of God most high? I beseech thee torment me not.
29 Pakuti Yesu analamula mzimu woyipawo kuti utuluke mwa munthuyo. Kawirikawiri umamugwira iye, ndipo ngakhale anali womangidwa ndi unyolo dzanja ndi mwendo ndi kuti ankamuyangʼanira, koma amadula maunyolo akewo ndipo ziwanda zimamutengera kumalo a yekha.
(For he had commanded the unclean spirit to come out of the man. For often it had caught him, and he was kept bound with chains, and in fetters: and he broke the bands, and was driven by the demon into the wilderness.)
30 Yesu anamufunsa kuti, “Dzina lako ndani?” Iye anayankha kuti, “Legiyo,” chifukwa ziwanda zambiri zinalowa mwa iye.
And Jesus asked him, saying, What is thy name? And he said, Legion: because many demons had entered into him.
31 Ndipo ziwandazo zimamupempha mobwerezabwereza kuti asazitumize ku dzenje la mdima. (Abyssos )
And they besought him, that he would not command them to go out into the deep. (Abyssos )
32 Gulu lalikulu la nkhumba limadya pamenepo mʼmbali mwa phiri. Ziwandazo zinamupempha Yesu kuti azilole kuti zikalowe mu nkhumbazo ndipo Iye anazilola.
And there was there a herd of many swine feeding on the mountain: and they besought him that he would suffer them to enter into them. And he suffered them.
33 Ziwanda zija zitatuluka mwa munthuyo, zinakalowa mwa nkhumbazo, ndipo gulu lonselo linathamangira ku mtsetse ndi kukalowa mʼnyanja ndi kumira.
Then the demons went out of the man, and entered into the swine: and the herd ran violently down a steep place into the lake, and were choked.
34 Oweta nkhumbazo ataona zimene zinachitikazo, anathamanga ndi kukanena izi mu mzinda ndi ku madera a ku midzi.
When they that fed [them] saw what was done, they fled, and went and told [it] in the city and in the country.
35 Ndipo anthu anapita kukaona zimene zinachitika. Atafika kwa Yesu, anapeza munthu amene anatulutsidwa ziwanda uja atakhala pa mapazi a Yesu, atavala ndipo ali ndi nzeru zake; ndipo iwo anachita mantha.
Then they went out to see what was done; and came to Jesus, and found the man out of whom the demons had departed, sitting at the feet of Jesus, clothed, and in his right mind: and they were afraid.
36 Amene anaona izi anawuza anthu mmene munthu wogwidwa ndi ziwandayo anachiritsidwira.
They also who saw [it], told them by what means he that was possessed by the demons was healed.
37 Kenaka anthu onse a ku chigawo cha Gerasa anamupempha Yesu kuti achoke kwa iwo, chifukwa anadzazidwa ndi mantha. Choncho Iye analowa mʼbwato nachoka.
Then the whole multitude of the surrounding country of the Gadarenes, besought him to depart from them: for they were taken with great fear. And he went into the boat, and returned.
38 Munthu amene anatulutsidwa ziwanda uja, anapempha Yesu kuti apite nawo, koma Yesu anamubweza nati,
Now the man out of whom the demons had departed, besought him that he might be with him. But Jesus sent him away, saying,
39 “Bwerera kwanu kafotokoze zimene Mulungu wakuchitira.” Ndipo munthuyo anachoka ndi kukanena ku mzinda wonsewo zimene Yesu anamuchitira iye.
Return to thy own house, and show how great things God hath done to thee. And he went away and published throughout the whole city, how great things Jesus had done to him.
40 Yesu atabwerera, gulu lalikulu la anthu linamulandira, chifukwa onse ankamuyembekezera.
And it came to pass, that, when Jesus had returned, the people [gladly] received him: for they were all waiting for him.
41 Nthawi yomweyo munthu wotchedwa Yairo, woweruza wa mu sunagoge, anabwera ndi kugwa pa mapazi a Yesu, namupempha Iye kuti apite ku nyumba kwake,
And behold, there came a man named Jairus, and he was a ruler of the synagogue: and he fell down at the feet of Jesus, and besought him that he would come into his house:
42 chifukwa mwana wake yekhayo wamkazi, kamtsikana ka zaka khumi ndi ziwiri, kanali pafupi kufa. Pamene Yesu ankapita gulu la anthu linkamupanikiza.
For he had one daughter only, about twelve years of age, and she lay dying. (But as he was going, the people thronged him.
43 Ndipo pomwepo panali mayi wina amene ankataya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri, koma panalibe wina akanamuchiritsa.
And a woman having an issue of blood twelve years, who had spent all her living upon physicians, neither could be healed by any,
44 Iye anafika kumbuyo kwake ndi kukhudza mothera mwa chovala chake, ndipo nthawi yomweyo magazi ake analeka kutuluka.
Came behind [him], and touched the border of his garment: and immediately her issue of blood stanched.
45 Yesu anafunsa kuti, “Wandikhudza ndani?” Onse atakana, Petro anati, “Anthu akukupanikizani ndi kukukankhani.”
And Jesus said, Who touched me? When all denied, Peter, and they that were with him, said, Master, the multitude throng thee, and press [thee], and sayest thou, Who touched me?
46 Koma Yesu anati, “Wina wandikhudza; ndikudziwa chifukwa mphamvu yachoka mwa Ine.”
And Jesus said, Somebody hath touched me: for I perceive that virtue hath gone out of me.
47 Ndipo mayiyo podziwa kuti sanathe kuchoka wosadziwika, anabwera akunjenjemera ndipo anagwa pa mapazi a Yesu. Pamaso pa anthu onse, anafotokoza chifukwa chimene anamukhudzira Iye ndi mmene iye anachiritsidwira nthawi yomweyo.
And when the woman saw that she was not hid, she came trembling, and falling down before him, she declared to him before all the people for what cause she had touched him, and how she was healed immediately.
48 Kenaka anati kwa iye, “Mwana wamkazi, chikhulupiriro chako chakuchiritsa. Pita mu mtendere.”
And he said to her, Daughter, be of good comfort: thy faith hath made thee whole; go in peace.
49 Pamene Yesu ankayankhulabe, munthu wina anabwera kuchokera ku nyumba ya Yairo, woweruza wa ku sunagoge uja. Iye anati, “Mwana wanu wa mkazi wamwalira, musawavutitsenso Aphunzitsiwa.”
While he was yet speaking, there cometh one from the house of the ruler of the synagogue, saying to him, Thy daughter is dead: trouble not the Master.
50 Atamva zimenezi, Yesu anati kwa Yairo, “Usachite mantha, ingokhulupirira basi ndipo adzachiritsidwa.”
But when Jesus heard [it], he answered him, saying, Fear not: believe only, and she shall be healed.
51 Iye atafika ku nyumba ya Yairo, sanalole wina aliyense kulowa kupatula Petro, Yohane, ndi Yakobo ndi abambo ndi amayi a mwanayo.
And when he came into the house, he suffered no man to go in, save Peter, and James, and John, and the father and the mother of the maiden.
52 Pa nthawiyi nʼkuti anthu onse akubuma ndi kumulirira iye. Yesu anati, “Lekani kulira, sanafe koma wagona tulo.”
And all wept and bewailed her: but he said, Weep not: she is not dead, but sleepeth.
53 Iwo anamuseka podziwa kuti anali atamwalira.
And they derided him, knowing that she was dead.
54 Koma Iye anamugwira dzanja lake ndipo anati, “Mwana wanga, dzuka!”
And he put them all out, and took her by the hand, and called, saying, Maid, arise.
55 Mzimu wake unabwerera, ndipo nthawi yomweyo anayimirira. Kenaka Yesu anawawuza kuti amupatse chakudya.
And her spirit came again, and she arose immediately: and he commanded to give her food.
56 Makolo ake anadabwa, koma Iye anawalamulira kuti asawuze wina aliyense zimene zinachitikazo.
And her parents were astonished: but he charged them that they should tell no man what was done.