< Luka 7 >

1 Yesu atamaliza kunena zonsezi pamaso pa anthu amene ankamvetsera, analowa mu Kaperenawo.
A kad o Isus završinđa plo vaćeriba anglo narodo, đerdinđa ki diz Kafarnaum.
2 Kumeneko wantchito wa Kenturiyo, amene amamukhulupirira kwambiri, anadwala ndipo anali pafupi kufa.
A jekhe rimljanengere kapetane, kova inele upreder šel vojnici, ine sluga kova inele namborme, anglo meriba, a ceninđa le.
3 Kenturiyo anamva za Yesu ndipo anatumiza ena a akulu Ayuda kwa Iye kuti abwere adzachiritse wantchito wakeyo.
I kad o kapetani šunđa e Isusese, bičhalđa koro leste nesave jevrejengere starešinen te pučen le te šaj avel te sasljari lesere sluga.
4 Iwo atafika kwa Yesu, anamudandaulira kwambiri, nati, “Munthuyu ayenera kuthandizidwa
A kad ale koro Isus, šukar zamolinde le vaćerindoj: “Ov zaslužini te ćere lese adava,
5 chifukwa amakonda mtundu wathu ndipo anatimangira sunagoge wathu.”
adalese so mangela amare narodo, a ćerđa amenđe hem sinagoga.”
6 Pamenepo Yesu anapita nawo. Iye sanali patali ndi nyumba pamene Kenturiyo anatumiza anzake kuti akamuwuze kuti, “Ambuye, musadzivutitse, pakuti ndine wosayenera kuti mulowe mʼnyumba mwanga.
I o Isus dželo olencar. A kad inele paše uzalo čher, o kapetani bičhalđa lese ple amalen vaćerindoj: “Gospode, ma mučin tut, adalese so na injum dostojno te đerdine maje ko čher.
7 Nʼchifukwa chake sindinadziyenereze ndi pangʼono pomwe kuti ndibwere kwa inu. Koma nenani mawu, ndipo wantchito wanga adzachira.
Adalese na dikhljum man dostojno te avav đi tute. Nego samo naredin hem mlo sluga ka ovel sasto.
8 Pakuti ndili pansi paulamuliro, ndiponso ndili ndi asilikali pansi panga. Ndikamuwuza uyu kuti, ‘Pita,’ iye amapita; ndi uyo kuti, ‘Bwera,’ amabwera. Ndikamuwuza wantchito wanga kuti, ‘Chita ichi,’ amachita.”
Adalese so hem me injum manuš talo autoritet, hem isi man vojnici teleder mande. I jekhese vaćerava: ‘Dža!’, i ov džala. A averese vaćerava: ‘Ava!’, i ov avela. A mle slugase vaćerava: ‘Ćer adava!’, i ov ćerela.”
9 Yesu atamva izi, anadabwa naye, ndipo anatembenukira gulu la anthu limene limamutsatira nati, “Ndikukuwuzani kuti, sindinapeze chikhulupiriro chachikulu ngati ichi mu Israeli.”
A kad o Isus šunđa adava olestar, iznenadinđa pe, irinđa pe nakoro narodo kova džala ine palo leste hem phenđa: “Vaćerava tumenđe, na arakhljum nijekhe ano Izrael te ovel le esavki vera.”
10 Kenaka anthu amene anatumidwawo anabwerera ku nyumba ndipo anakamupeza wantchitoyo atachira.
I kad okola kola inele bičhalde irinde pe čhere, arakhle e sluga saste.
11 Zitangotha izi, Yesu anapita ku mudzi wa Naini ndipo ophunzira ake ndi gulu lalikulu la anthu linapita naye pamodzi.
Na but palo adava, o Isus dželo ki diz savi vičini pe Nain. Oleja džele lesere učenici hem but narodo.
12 Akufika pa chipata cha mudziwo, anakumana ndi anthu amene ankatuluka ndi munthu wakufa amene anali mwana yekhayo wa mkazi wamasiye. Gulu lalikulu la anthu a mʼmudziwo linali naye.
A kad alo paše uzalo udar e dizjakoro, reslja e dizutnen sar legarena e mule čhave, kova inele jekhoro pe dajaće koja inele udovica. But dizutne džana ine e dajaja te parunen e čhave.
13 Ambuye atamuona mayiyo, mtima wawo unagwidwa naye chifundo ndipo anati, “Usalire.”
I kad dikhlja la o Gospod, pelo lese žal olaće hem phenđa laće: “Ma rov!”
14 Kenaka anapita nakakhudza chithatha cha maliro ndipo amene anachinyamulawo anayima. Iye anati, “Mnyamata, ndikukuwuza kuti, dzuka!”
I alo paše hem dolinđa pe upro nosilja, i tegani okola so akharde terdine. A o Isus phenđa: “Terneja, tuće vaćerava, ušti!”
15 Wakufayo anakhala tsonga ndi kuyamba kuyankhula, ndipo Yesu anamupereka mnyamatayo kwa amayi ake.
I o mulo beštino hem lelja te vaćeri, i o Isus dinđa le lesere dajaće.
16 Onse anachita mantha kwambiri nalemekeza Mulungu. Iwo anati, “Mneneri wamkulu waonekera pakati pathu. Mulungu wabwera kudzathandiza anthu ake.”
Tegani sare darandile hem slavinde e Devle vaćerindoj: “Baro proroko iklilo maškar amende!” hem: “O Devel alo te pomožini ple narodose!”
17 Mbiriyi inafalikira ku Yudeya konse ndi ku madera ozungulira.
I adava šundilo ki sa i phuv e jevrejengiri hem ko sa o pašutne thana.
18 Ndipo ophunzira a Yohane anamuwuza Yohaneyo zinthu zonsezi. Atayitana awiri a ophunzirawo,
I sa adava e Jovanese e Krstiteljese vaćerde lesere učenici. Tegani o Jovan vičinđa kora peste nesave dujen ple učenikonendar
19 anawatumiza kwa Ambuye kukafunsa kuti, “Kodi ndinu anayenera kubwerayo, kapena tiyembekezere wina?”
hem bičhalđa len koro Gospod Isus vaćerindoj: “Tu li injan adava kova valjani te avel ili te adžićera avere?”
20 Anthuwo atafika kwa Yesu anati, “Yohane Mʼbatizi watituma kwa Inu kuti tidzafunse kuti, ‘Kodi ndinu anayenera kubwerayo, kapena tiyembekezere wina?’”
I adala manuša ale koro Isus hem phende: “O Jovan o Krstitelj bičhalđa amen kora tute vaćerindoj: ‘Tu li injan adava kova valjani te avel ili te adžićera avere?’”
21 Pa nthawi yomweyo, Yesu anachiritsa ambiri amene ankavutika, odwala ndi amene anali mizimu yoyipa, ndiponso anapenyetsa anthu osaona.
Baš tegani o Isus sasljarđa buten oto nambormipa, oto pharipa hem oto bišukar duhija, hem bute kororenđe dinđa dikhiba.
22 Ndipo Iye anawayankha otumidwawo kuti, “Bwererani ndi kukamuwuza Yohane zimene mwaona ndi kumva: Osaona akuona, olumala akuyenda, akhate akuchiritsidwa, osamva akumva, akufa akuukitsidwa, ndipo Uthenga Wabwino ukulalikidwa kwa osauka.
Tegani o Isus phenđa e Jovanesere učenikonenđe: “Džan hem vaćeren e Jovanese so dikhljen hem so šunđen: o korore dikhena, o bange phirena, o gubavci čistinena pe, o kašuke šunena, o mule uštena, e čororenđe vaćeri pe o Šukar lafi.
23 Odala munthu amene sakhumudwa chifukwa cha Ine.”
I bahtaloi okova kova na našali pli vera ana mande.”
24 Anthu otumidwa ndi Yohane aja atachoka, Yesu anayamba kuyankhula ndi gulu la anthu za Yohaneyo kuti, “Kodi munkapita ku chipululu kukaona chiyani? Bango logwedezeka ndi mphepo?
Kad e Jovanesere manuša džele, o Isus lelja te vaćeri e narodose e Jovanestar: “So ikliljen ki pustinja te dikhen? I trska sava phudela i barval?
25 Ngati si choncho, munkapita kukaona chiyani? Munthu wovala zovala zabwino? Ayi, ovala zovala zodula ndi okhala moyo wapamwamba ali mʼnyumba zaufumu.
Ili so ikliljen te dikhen? E manuše ano barvale šeja urjavde? Na! Okola ano skupa šeja hem so živinena ano luksuz, eče tane ano palate.
26 Koma inu munkapita kukaona chiyani? Mneneri? Inde, Ine ndikukuwuzani, woposa mneneri.
Ili so ikliljen te dikhen? E proroko? Oja, vaćerava tumenđe, ovi po više oto proroko!
27 Uyu ndi amene malemba akunena za Iye kuti, “‘Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu, amene adzakonza njira yanu.’
Ovi okova kastar pisime ano Sveto lil: ‘Ače, bičhalava mle glasniko angla tute, kova ka pripremini će o drom.’
28 Ine ndikukuwuzani kuti pakati pa obadwa kuchokera mwa mkazi palibe wina wamkulu kuposa Yohane; komabe amene ali wamngʼono mu ufumu wa Mulungu ndi wamkulu kuposa iye.”
Vaćerava tumenđe: maškar okolende kolai bijande e đuvljendar nijekh nane po baro e Jovanestar, a o najtikoro e Devlese ano carstvo po baroi olestar.”
29 Anthu onse, ngakhale amisonkho, atamva mawu a Yesu, anavomereza kuti njira ya Mulungu ndi yolondola, chifukwa anabatizidwa ndi Yohane.
I sa o manuša hem o carinici kola šunde adava, pendžarde dai e Devlesoro sikaviba čačikano, adaleja so krstinde pe e Jovanesere krstibnaja.
30 Koma Afarisi ndi akatswiri amalamulo anakana cholinga cha Mulungu kwa iwo okha, chifukwa sanabatizidwe ndi Yohane.
A o fariseja hem o učitelja e Zakonestar odbacinde o plan e Devlesoro pumenđe. Oni adala so na mangle o Jovan te krstini len.
31 “Kodi ndingawafanizire chiyani anthu a mʼbado uno? Ali ngati chiyani?
O Isus phenđa: “Kasar akana te uporedinav e manušen oti akaja generacija? Kasei slična?
32 Ali ngati ana amene akukangana pa msika, ena akufunsa anzawo kuti, “‘Ife tinakuyimbirani chitoliro, koma inu simunavine. Tinakuyimbirani nyimbo zamaliro, koma inu simunalire.’
Sličnai e čhavorenđe kola bešena ko trg hem vaćerena jekh averese: ‘Bašalđam tumenđe veselo, a na čhelđen! Đilabđam tužno, a na runđen!’
33 Pakuti Yohane Mʼbatizi sanabwere kudzadya buledi kapena kumwa vinyo, koma inu mumati, ‘Ali ndi chiwanda.’
Ađahar, kad alo o Jovan o Krstitelj, ni halja maro ni pilja mol, a phenena: ‘O demoni ano leste!’
34 Mwana wa Munthu anabwera nadya ndi kumwa, ndipo inu mukuti, ‘Ali ndi dyera komanso ndi woledzera, bwenzi la amisonkho ndi ochimwa.’
A kad aljum me, o Čhavo e manušesoro, hava hem pijava, a phenena: ‘Eče manuš halano hem mato, amal e carinikonengoro hem e avere grešnikonegoro!’
35 Ndipo nzeru zimaoneka zolondola mwa ana ake onse.”
Ali i mudrost e Devlesiri dokažini pe sa lakere čhavendar.”
36 Tsopano mmodzi mwa Afarisi anayitana Yesu kuti akadye naye ku nyumba kwake ndipo anapita nakakhala pa tebulo.
Nesavo farisej palo anav Simon vičinđa e Isuse te avel te hal koro leste. Ov đerdinđa e farisejese ko čher hem čhivđa pe uzalo astali.
37 Mayi amene amakhala moyo wauchimo mu mzindawo atadziwa kuti Yesu akudya ku nyumba ya Mfarisiyo, anabweretsa botolo la mafuta onunkhira a alabasta.
I eče, adari ali i đuvli kolaće džanđa pe dai grešnica ani diz, adalese so šunđa da o Isus inele uzalo astali e farisejese ko čher, i anđa miris ko čaro savo inele ćerdo oto šužo bar.
38 Iye anayimirira kumbuyo kwa Yesu pa mapazi ake akulira, nayamba kumadontheza misozi pa mapazi ake. Ndipo iye anapukuta mapaziwo ndi tsitsi lake, nawapsompsona ndi kuwathira mafuta onunkhirawo.
I terdindoj palo lesere pre, runđa hem lelja te sampaćeri lesere pre ple asvencar hem koslja len ple balencar. I tegani čumudinđa lesere pre hem makhlja len miriseja.
39 Mfarisiyo anamuyitanayo ataona izi, anati mu mtima mwake, “Ngati munthuyu akanakhala mneneri, akanadziwa kuti akumukhudzayo ndi mayi otani, kuti ndi wochimwa.”
Kad adava dikhlja o farisej kova vičinđa le, phenđa ana peste: “Tei akava manuš proroko, ka džanel ine koi hem savi akaja đuvli koja pipini le – dai grešnica.”
40 Yesu anamuyankha iye kuti, “Simoni, ndili ndi kanthu koti ndikuwuze.” Iye anati, “Ndiwuzeni Aphunzitsi.”
A o Isus phenđa lese: “Simone, isi man nešto te vaćerav će.” A ov phenđa: “Učitelju, vaćer!”
41 “Anthu awiri anakongola ndalama kwa munthu wina wokongoletsa ndalama: mmodzi ndalama zokwana 500 ndi winayo ndalama makumi asanu.
I o Isus phenđa: “Duj džene inele dužnici nesave manušese kova dela pare ko zajam. Jekh dugujini lese panšel e rimljanengere denarija, a o dujto pinda.
42 Panalibe mmodzi mwa iwo anali ndi ndalama zobwezera, ndipo iye anawakhululukira ngongole zawo. Tsopano ndi ndani mwa awiriwa adzamukonde koposa?”
Adalese so na ine len te irinen, ov oprostinđa o dugo sodujenđe. Kova, onda, olendar više ka mangel le?”
43 Simoni anayankha kuti, “Ndikuganiza kuti ndi amene anamukhululukira ngongole yayikulu.” Yesu anati, “Wayankha molondola.”
O Simon phenđa: “Mislinava da okova kase oprostinđa više.” Tegani ov phenđa lese: “Oja, šukar phenđan.”
44 Kenaka anatembenukira kwa mayiyo nati kwa Simoni, “Ukumuona mayiyu? Ine ndabwera mʼnyumba yako. Iwe sunandipatse madzi otsukira mapazi anga, koma iyeyu wanyowetsa mapazi anga ndi misozi yake ndi kuwapukuta ndi tsitsi lake.
Irinđa pe nakori đuvli, i phenđa e Simonese: “Dikheja li akala đuvlja? Đerdinđum tuće ko čher, pani mle prenđe na anđan, a oj sampaćerđa mle pre ple asvencar hem koslja len ple balencar.
45 Iwe sunandipsompsone, koma mayiyu, kuyambira pamene Ine ndalowa, sanaleke kupsompsona mapazi anga.
Na pozdravinđan man čumudipnaja, a oj, sar đerdinđum na ačhavđa te čumudini mle pre.
46 Iwe sunadzoze mutu wanga mafuta, koma iye wadzoza mapazi anga mafuta onunkhira.
Na makhljan mlo šero uljeja, a oj makhlja mle pre miriseja.
47 Tsono, ndikukuwuza iwe, machimo ake amene ndi ambiri akhululukidwa, monga chaonetsera chikondi chake chachikulu. Koma iye amene wakhululukidwa zochepa amakonda pangʼono.”
Adalese phenava će: But mangipe mothovđa, adalese soi laće oprostime but grehija. A hari mangipe mothoj okova kolesei oprostime hari grehija.”
48 Kenaka anati kwa mayiyo, “Machimo ako akhululukidwa.”
A olaće phenđa: “Oprostimei će te grehija.”
49 Alendo enawo anayamba kumanena mʼmitima mwawo kuti, “Uyu ndi ndani amene akhululukiranso machimo?”
A o manuša kola inele uzalo astali lelje ana peste te vaćeren: “Kovai akava so šaj hem o grehija te oprostini?”
50 Yesu anati kwa mayiyo, “Chikhulupiriro chako chakupulumutsa. Pita mu mtendere.”
Tegani o Isus phenđa e đuvljaće: “Ti vera spasinđa tut! Dža ano mir!”

< Luka 7 >