< Luka 7 >

1 Yesu atamaliza kunena zonsezi pamaso pa anthu amene ankamvetsera, analowa mu Kaperenawo.
(since *N(k)O*) to fulfill all the/this/who declaration it/s/he toward the/this/who hearing the/this/who a people to enter toward Capernaum
2 Kumeneko wantchito wa Kenturiyo, amene amamukhulupirira kwambiri, anadwala ndipo anali pafupi kufa.
centurion then one slave badly to have/be to ensue to decease which to be it/s/he valued/honored
3 Kenturiyo anamva za Yesu ndipo anatumiza ena a akulu Ayuda kwa Iye kuti abwere adzachiritse wantchito wakeyo.
to hear then about the/this/who Jesus to send to/with it/s/he elder: Elder the/this/who Jew to ask it/s/he that to come/go to save the/this/who slave it/s/he
4 Iwo atafika kwa Yesu, anamudandaulira kwambiri, nati, “Munthuyu ayenera kuthandizidwa
the/this/who then to come to/with the/this/who Jesus to plead/comfort it/s/he diligently to say that/since: that worthy to be which (to furnish occasion *N(K)O*) this/he/she/it
5 chifukwa amakonda mtundu wathu ndipo anatimangira sunagoge wathu.”
to love for the/this/who Gentiles me and the/this/who synagogue it/s/he to build me
6 Pamenepo Yesu anapita nawo. Iye sanali patali ndi nyumba pamene Kenturiyo anatumiza anzake kuti akamuwuze kuti, “Ambuye, musadzivutitse, pakuti ndine wosayenera kuti mulowe mʼnyumba mwanga.
the/this/who then Jesus to travel with it/s/he already then it/s/he no far to have in full away from the/this/who home to send (to/with it/s/he *ko*) friendly/friend the/this/who centurion to say it/s/he lord: God not to trouble no for sufficient to be in order that/to by/under: under the/this/who roof me to enter
7 Nʼchifukwa chake sindinadziyenereze ndi pangʼono pomwe kuti ndibwere kwa inu. Koma nenani mawu, ndipo wantchito wanga adzachira.
therefore nor I/we to deem worthy to/with you to come/go but to say word and (to heal *N(k)O*) the/this/who child me
8 Pakuti ndili pansi paulamuliro, ndiponso ndili ndi asilikali pansi panga. Ndikamuwuza uyu kuti, ‘Pita,’ iye amapita; ndi uyo kuti, ‘Bwera,’ amabwera. Ndikamuwuza wantchito wanga kuti, ‘Chita ichi,’ amachita.”
and for I/we a human to be by/under: under authority to appoint to have/be by/under: under I/we soldier and to say this/he/she/it to travel and to travel and another to come/go and to come/go and the/this/who slave me to do/make: do this/he/she/it and to do/make: do
9 Yesu atamva izi, anadabwa naye, ndipo anatembenukira gulu la anthu limene limamutsatira nati, “Ndikukuwuzani kuti, sindinapeze chikhulupiriro chachikulu ngati ichi mu Israeli.”
to hear then this/he/she/it the/this/who Jesus to marvel it/s/he and to turn the/this/who to follow it/s/he crowd to say to say you (nor *NK(o)*) in/on/among the/this/who Israel so great faith to find/meet
10 Kenaka anthu amene anatumidwawo anabwerera ku nyumba ndipo anakamupeza wantchitoyo atachira.
and to return toward the/this/who house: home the/this/who to send to find/meet the/this/who (be weak: ill *K*) slave be healthy
11 Zitangotha izi, Yesu anapita ku mudzi wa Naini ndipo ophunzira ake ndi gulu lalikulu la anthu linapita naye pamodzi.
and to be in/on/among (the/this/who *N(k)O*) next/afterward (to travel *N(k)O*) toward city to call: call Nain and to go with it/s/he the/this/who disciple it/s/he (sufficient *K*) and crowd much
12 Akufika pa chipata cha mudziwo, anakumana ndi anthu amene ankatuluka ndi munthu wakufa amene anali mwana yekhayo wa mkazi wamasiye. Gulu lalikulu la anthu a mʼmudziwo linali naye.
as/when then to come near the/this/who gate the/this/who city and look! to carry out to die/be dead unique son the/this/who mother it/s/he and it/s/he to be widow and crowd the/this/who city sufficient to be with it/s/he
13 Ambuye atamuona mayiyo, mtima wawo unagwidwa naye chifundo ndipo anati, “Usalire.”
and to perceive: see it/s/he the/this/who lord: God to pity upon/to/against it/s/he and to say it/s/he not to weep
14 Kenaka anapita nakakhudza chithatha cha maliro ndipo amene anachinyamulawo anayima. Iye anati, “Mnyamata, ndikukuwuza kuti, dzuka!”
and to come near/agree to touch the/this/who bier the/this/who then to carry to stand and to say young man you to say to arise
15 Wakufayo anakhala tsonga ndi kuyamba kuyankhula, ndipo Yesu anamupereka mnyamatayo kwa amayi ake.
and to sit up the/this/who dead and be first to speak and to give it/s/he the/this/who mother it/s/he
16 Onse anachita mantha kwambiri nalemekeza Mulungu. Iwo anati, “Mneneri wamkulu waonekera pakati pathu. Mulungu wabwera kudzathandiza anthu ake.”
to take then fear (all *N(k)O*) and to glorify the/this/who God to say that/since: that prophet great (to arise *N(k)O*) in/on/among me and that/since: that to visit/care for the/this/who God the/this/who a people it/s/he
17 Mbiriyi inafalikira ku Yudeya konse ndi ku madera ozungulira.
and to go out the/this/who word this/he/she/it in/on/among all the/this/who Judea about it/s/he and (in/on/among *ko*) all the/this/who region
18 Ndipo ophunzira a Yohane anamuwuza Yohaneyo zinthu zonsezi. Atayitana awiri a ophunzirawo,
and to announce John the/this/who disciple it/s/he about all this/he/she/it
19 anawatumiza kwa Ambuye kukafunsa kuti, “Kodi ndinu anayenera kubwerayo, kapena tiyembekezere wina?”
and to call to/summon two one the/this/who disciple it/s/he the/this/who John to send to/with the/this/who (lord: God *N(K)O*) to say you to be the/this/who to come/go or (another *NK(o)*) to look for
20 Anthuwo atafika kwa Yesu anati, “Yohane Mʼbatizi watituma kwa Inu kuti tidzafunse kuti, ‘Kodi ndinu anayenera kubwerayo, kapena tiyembekezere wina?’”
to come then to/with it/s/he the/this/who man to say John the/this/who one who baptizes (to send *N(k)O*) me to/with you to say you to be the/this/who to come/go or another to look for
21 Pa nthawi yomweyo, Yesu anachiritsa ambiri amene ankavutika, odwala ndi amene anali mizimu yoyipa, ndiponso anapenyetsa anthu osaona.
in/on/among (that *N(k)O*) (then *k*) the/this/who hour to serve/heal much away from illness and whip and spirit/breath: spirit evil/bad and blind much to give grace (the/this/who *k*) to see
22 Ndipo Iye anawayankha otumidwawo kuti, “Bwererani ndi kukamuwuza Yohane zimene mwaona ndi kumva: Osaona akuona, olumala akuyenda, akhate akuchiritsidwa, osamva akumva, akufa akuukitsidwa, ndipo Uthenga Wabwino ukulalikidwa kwa osauka.
and to answer (the/this/who Jesus *k*) to say it/s/he to travel to announce John which to perceive: see and to hear (that/since: that *ko*) blind to look up/again lame to walk leprous to clean (and *no*) deaf/mute to hear dead to arise poor to speak good news
23 Odala munthu amene sakhumudwa chifukwa cha Ine.”
and blessed to be which if not to cause to stumble in/on/among I/we
24 Anthu otumidwa ndi Yohane aja atachoka, Yesu anayamba kuyankhula ndi gulu la anthu za Yohaneyo kuti, “Kodi munkapita ku chipululu kukaona chiyani? Bango logwedezeka ndi mphepo?
to go away then the/this/who angel: messenger John be first to say to/with (the/this/who crowd *NK(o)*) about John which? (to go out *N(k)O*) toward the/this/who deserted to look at reed/stick/pen by/under: by wind to shake
25 Ngati si choncho, munkapita kukaona chiyani? Munthu wovala zovala zabwino? Ayi, ovala zovala zodula ndi okhala moyo wapamwamba ali mʼnyumba zaufumu.
but which? (to go out *N(k)O*) to perceive: see a human in/on/among soft/effeminate clothing to clothe look! the/this/who in/on/among clothing honored and self-indulgence be already in/on/among the/this/who palace to be
26 Koma inu munkapita kukaona chiyani? Mneneri? Inde, Ine ndikukuwuzani, woposa mneneri.
but which? (to go out *N(k)O*) to perceive: see prophet yes to say you and more excessive prophet
27 Uyu ndi amene malemba akunena za Iye kuti, “‘Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu, amene adzakonza njira yanu.’
this/he/she/it to be about which to write look! (I/we *k*) to send the/this/who angel: messenger me before face you which to prepare the/this/who road you before you
28 Ine ndikukuwuzani kuti pakati pa obadwa kuchokera mwa mkazi palibe wina wamkulu kuposa Yohane; komabe amene ali wamngʼono mu ufumu wa Mulungu ndi wamkulu kuposa iye.”
to say (for *k*) you great in/on/among born woman (prophet *KO*) (the/this/who *k*) (John *N(K)O*) none to be the/this/who then small in/on/among the/this/who kingdom the/this/who God great it/s/he to be
29 Anthu onse, ngakhale amisonkho, atamva mawu a Yesu, anavomereza kuti njira ya Mulungu ndi yolondola, chifukwa anabatizidwa ndi Yohane.
and all the/this/who a people to hear and the/this/who tax collector to justify the/this/who God to baptize the/this/who baptism John
30 Koma Afarisi ndi akatswiri amalamulo anakana cholinga cha Mulungu kwa iwo okha, chifukwa sanabatizidwe ndi Yohane.
the/this/who then Pharisee and the/this/who lawyer the/this/who plan the/this/who God to reject toward themself not to baptize by/under: by it/s/he
31 “Kodi ndingawafanizire chiyani anthu a mʼbado uno? Ali ngati chiyani?
(to say then the/this/who lord: God *K*) which? therefore/then to liken the/this/who a human the/this/who generation this/he/she/it and which? to be like
32 Ali ngati ana amene akukangana pa msika, ena akufunsa anzawo kuti, “‘Ife tinakuyimbirani chitoliro, koma inu simunavine. Tinakuyimbirani nyimbo zamaliro, koma inu simunalire.’
like to be child the/this/who in/on/among marketplace to sit and to call to/summon one another (which *no*) (and *k*) (to say *N(k)(o)*) to play the flute you and no to dance to lament (you *k*) and no to weep
33 Pakuti Yohane Mʼbatizi sanabwere kudzadya buledi kapena kumwa vinyo, koma inu mumati, ‘Ali ndi chiwanda.’
to come/go for John the/this/who one who baptizes (not *N(k)O*) to eat bread neither to drink wine and to say demon to have/be
34 Mwana wa Munthu anabwera nadya ndi kumwa, ndipo inu mukuti, ‘Ali ndi dyera komanso ndi woledzera, bwenzi la amisonkho ndi ochimwa.’
to come/go the/this/who son the/this/who a human to eat and to drink and to say look! a human glutton and drunkard friendly/friend tax collector and sinful
35 Ndipo nzeru zimaoneka zolondola mwa ana ake onse.”
and to justify the/this/who wisdom away from all the/this/who child it/s/he
36 Tsopano mmodzi mwa Afarisi anayitana Yesu kuti akadye naye ku nyumba kwake ndipo anapita nakakhala pa tebulo.
to ask then one it/s/he the/this/who Pharisee in order that/to to eat with/after it/s/he and to enter toward (the/this/who house: home *N(k)O*) the/this/who Pharisee (to sit *N(K)O*)
37 Mayi amene amakhala moyo wauchimo mu mzindawo atadziwa kuti Yesu akudya ku nyumba ya Mfarisiyo, anabweretsa botolo la mafuta onunkhira a alabasta.
and look! woman who/which to be in/on/among the/this/who city sinful (and *no*) to come to know that/since: that (to recline *N(k)O*) in/on/among the/this/who home the/this/who Pharisee to bring/be repaid jar ointment
38 Iye anayimirira kumbuyo kwa Yesu pa mapazi ake akulira, nayamba kumadontheza misozi pa mapazi ake. Ndipo iye anapukuta mapaziwo ndi tsitsi lake, nawapsompsona ndi kuwathira mafuta onunkhirawo.
and to stand after from/with/beside the/this/who foot it/s/he to weep the/this/who teardrop be first to rain down the/this/who foot it/s/he and the/this/who hair the/this/who head it/s/he to wipe off and to kiss the/this/who foot it/s/he and to anoint the/this/who ointment
39 Mfarisiyo anamuyitanayo ataona izi, anati mu mtima mwake, “Ngati munthuyu akanakhala mneneri, akanadziwa kuti akumukhudzayo ndi mayi otani, kuti ndi wochimwa.”
to perceive: see then the/this/who Pharisee the/this/who to call: call it/s/he to say in/on/among themself to say this/he/she/it if to be (the/this/who *o*) prophet to know if which? and of what kind? the/this/who woman who/which to touch it/s/he that/since: since sinful to be
40 Yesu anamuyankha iye kuti, “Simoni, ndili ndi kanthu koti ndikuwuze.” Iye anati, “Ndiwuzeni Aphunzitsi.”
and to answer the/this/who Jesus to say to/with it/s/he Simon to have/be you one to say the/this/who then teacher to say to assert
41 “Anthu awiri anakongola ndalama kwa munthu wina wokongoletsa ndalama: mmodzi ndalama zokwana 500 ndi winayo ndalama makumi asanu.
two debtor to be moneylender one the/this/who one to owe denarius five hundred the/this/who then other fifty
42 Panalibe mmodzi mwa iwo anali ndi ndalama zobwezera, ndipo iye anawakhululukira ngongole zawo. Tsopano ndi ndani mwa awiriwa adzamukonde koposa?”
not to have/be (then *k*) it/s/he to pay both to give grace which? therefore/then it/s/he (to say *k*) greater to love it/s/he
43 Simoni anayankha kuti, “Ndikuganiza kuti ndi amene anamukhululukira ngongole yayikulu.” Yesu anati, “Wayankha molondola.”
to answer (then the/this/who *ko*) Simon to say to take up/suppose that/since: that which the/this/who greater to give grace the/this/who then to say it/s/he correctly to judge
44 Kenaka anatembenukira kwa mayiyo nati kwa Simoni, “Ukumuona mayiyu? Ine ndabwera mʼnyumba yako. Iwe sunandipatse madzi otsukira mapazi anga, koma iyeyu wanyowetsa mapazi anga ndi misozi yake ndi kuwapukuta ndi tsitsi lake.
and to turn to/with the/this/who woman the/this/who Simon to assert to see this/he/she/it the/this/who woman to enter you toward the/this/who home water me upon/to/against (the/this/who *ko*) foot (me *k*) no to give this/he/she/it then the/this/who teardrop to rain down me the/this/who foot and the/this/who hair (the/this/who head *K*) it/s/he to wipe off
45 Iwe sunandipsompsone, koma mayiyu, kuyambira pamene Ine ndalowa, sanaleke kupsompsona mapazi anga.
kiss me no to give this/he/she/it then away from which to enter no to stop to kiss me the/this/who foot
46 Iwe sunadzoze mutu wanga mafuta, koma iye wadzoza mapazi anga mafuta onunkhira.
olive oil the/this/who head me no to anoint this/he/she/it then ointment to anoint the/this/who foot me
47 Tsono, ndikukuwuza iwe, machimo ake amene ndi ambiri akhululukidwa, monga chaonetsera chikondi chake chachikulu. Koma iye amene wakhululukidwa zochepa amakonda pangʼono.”
which because of to say you to release: forgive the/this/who sin it/s/he the/this/who much that/since: since to love much which then little/few to release: forgive little/few to love
48 Kenaka anati kwa mayiyo, “Machimo ako akhululukidwa.”
to say then it/s/he to release: forgive you the/this/who sin
49 Alendo enawo anayamba kumanena mʼmitima mwawo kuti, “Uyu ndi ndani amene akhululukiranso machimo?”
and be first the/this/who to dine with to say in/on/among themself which? this/he/she/it to be which and sin to release: forgive
50 Yesu anati kwa mayiyo, “Chikhulupiriro chako chakupulumutsa. Pita mu mtendere.”
to say then to/with the/this/who woman the/this/who faith you to save you to travel toward peace

< Luka 7 >