< Luka 7 >

1 Yesu atamaliza kunena zonsezi pamaso pa anthu amene ankamvetsera, analowa mu Kaperenawo.
Jesuh naw ngthu pyen law päng lü Kapenawma citki.
2 Kumeneko wantchito wa Kenturiyo, amene amamukhulupirira kwambiri, anadwala ndipo anali pafupi kufa.
Acunüng Romah ngvai naw a jawngnaka m'ya mat thi law hlü khaia a mhnat awmki.
3 Kenturiyo anamva za Yesu ndipo anatumiza ena a akulu Ayuda kwa Iye kuti abwere adzachiritse wantchito wakeyo.
Jesuha mawng a ngjak üng, a m'ya mdaw law be khaia, Jesuh va nghui na u lü, khü khai hea, Judah ngvai he a jah tüih.
4 Iwo atafika kwa Yesu, anamudandaulira kwambiri, nati, “Munthuyu ayenera kuthandizidwa
Jesuha veia law u lü aktäa nghui naki he naw, “Hina khyang ta na kpüi vaia ngkawi ve,
5 chifukwa amakonda mtundu wathu ndipo anatimangira sunagoge wathu.”
ani cun mi khyang he jah jawng na lü, Sinakok pi jah sak peki ni,” ami ti.
6 Pamenepo Yesu anapita nawo. Iye sanali patali ndi nyumba pamene Kenturiyo anatumiza anzake kuti akamuwuze kuti, “Ambuye, musadzivutitse, pakuti ndine wosayenera kuti mulowe mʼnyumba mwanga.
Acuna Jesuh ami veia citki. Acunüng a pha law tawm tawm la Romah ngvai naw a püi he jah tüi lü, “Bawipa aw, ka im na luhnak ngkawi vaia am kya ve, ä kha heia,
7 Nʼchifukwa chake sindinadziyenereze ndi pangʼono pomwe kuti ndibwere kwa inu. Koma nenani mawu, ndipo wantchito wanga adzachira.
acunakyase, na veia ka law vaia pi ka ngkawikia am ngai kyu veng, ngthu däng pyen lü, ka m'ya daw be khai ni.
8 Pakuti ndili pansi paulamuliro, ndiponso ndili ndi asilikali pansi panga. Ndikamuwuza uyu kuti, ‘Pita,’ iye amapita; ndi uyo kuti, ‘Bwera,’ amabwera. Ndikamuwuza wantchito wanga kuti, ‘Chita ichi,’ amachita.”
“Isetiakyaküng, kei haw anaa takia keha ka awmki. Ka keha yekap he awmki he, mat am ‘cita’ ka ti üng citki, akce mat am ‘lawa’ ka ti üng lawki, ka m'ya am hin pawha ka ti üng pawhki,” a ti.
9 Yesu atamva izi, anadabwa naye, ndipo anatembenukira gulu la anthu limene limamutsatira nati, “Ndikukuwuzani kuti, sindinapeze chikhulupiriro chachikulu ngati ichi mu Israeli.”
Jesuh naw acun a ngjak üng, cäieiki naw, mang hü lü, amät läkia khyang he üng, “Isarel he üng pi ahikba sena jumeiki am hmu khawi nawng,” a ti.
10 Kenaka anthu amene anatumidwawo anabwerera ku nyumba ndipo anakamupeza wantchitoyo atachira.
A khyang tüihe ima ami ceh be üng, m'ya cun daw be se ami hmuh.
11 Zitangotha izi, Yesu anapita ku mudzi wa Naini ndipo ophunzira ake ndi gulu lalikulu la anthu linapita naye pamodzi.
Acun käna Jesuh Nai ami tia mlüha cit se, axüisaw he la khyang khawjah a veia cit hngaki he.
12 Akufika pa chipata cha mudziwo, anakumana ndi anthu amene ankatuluka ndi munthu wakufa amene anali mwana yekhayo wa mkazi wamasiye. Gulu lalikulu la anthu a mʼmudziwo linali naye.
Mlüh mkawt pei a pha law üng, hmeinu naw mat däng a canak, khyang kthi ami yawknak kawt law u se, mlüh üngka he khawjah law hngaki he.
13 Ambuye atamuona mayiyo, mtima wawo unagwidwa naye chifundo ndipo anati, “Usalire.”
Acunüng, Bawipa naw acuna hmeinu a hmuh üng, m'yenei leng leng lü, “Ä kyapa” a ti.
14 Kenaka anapita nakakhudza chithatha cha maliro ndipo amene anachinyamulawo anayima. Iye anati, “Mnyamata, ndikukuwuza kuti, dzuka!”
Jesuh naw law lü, yawkkawng hnet se, kawtki he ngdüiki he. Acunüng Jesuh naw, “Cawngpyang, tho law, ti veng,” ti se,
15 Wakufayo anakhala tsonga ndi kuyamba kuyankhula, ndipo Yesu anamupereka mnyamatayo kwa amayi ake.
akthi cun tho law lü ngthuhei law se, Jesuh naw a nu üng a pet.
16 Onse anachita mantha kwambiri nalemekeza Mulungu. Iwo anati, “Mneneri wamkulu waonekera pakati pathu. Mulungu wabwera kudzathandiza anthu ake.”
Acunüng, ami van kyü lawki he naw, Pamhnam mküimto u lü, “Mi ksunga sahma akyäp awm law ve; Pamhnam a khyang he jah küikyan khaia law ve,” ami ti.
17 Mbiriyi inafalikira ku Yudeya konse ndi ku madera ozungulira.
Acuna Jesuha mawng cun khaw avan la a pipeia hne avan üng ngthang hüki.
18 Ndipo ophunzira a Yohane anamuwuza Yohaneyo zinthu zonsezi. Atayitana awiri a ophunzirawo,
Johana axüisaw he naw acuna mawng avan cun Johan üng ami mtheh.
19 anawatumiza kwa Ambuye kukafunsa kuti, “Kodi ndinu anayenera kubwerayo, kapena tiyembekezere wina?”
Acunüng, Johan naw axüisaw nghngih jah khüki naw, Bawipa veia jah tüi lü, “Johan naw law khai a tia khyanga na kyaki aw? Akce kami na äpei khai aw?” tia a jah va kthähsak.
20 Anthuwo atafika kwa Yesu anati, “Yohane Mʼbatizi watituma kwa Inu kuti tidzafunse kuti, ‘Kodi ndinu anayenera kubwerayo, kapena tiyembekezere wina?’”
Acunüng, Jesuh veia law u lü, “Law khai mata na kyaki aw? Akce kami na äpei khai aw? tia ni kthäh vaia baptican Johan naw na veia a jah tüih law ni,” ami ti.
21 Pa nthawi yomweyo, Yesu anachiritsa ambiri amene ankavutika, odwala ndi amene anali mizimu yoyipa, ndiponso anapenyetsa anthu osaona.
Acunapät üng Jesuh naw, a jah huieie, natnak khihlau akce kcea jah awmnak he, ngmüimkhya ksea awmnak he khawjah jah mdaw be lü, amikmü khawjah a jah mdeisak be.
22 Ndipo Iye anawayankha otumidwawo kuti, “Bwererani ndi kukamuwuza Yohane zimene mwaona ndi kumva: Osaona akuona, olumala akuyenda, akhate akuchiritsidwa, osamva akumva, akufa akuukitsidwa, ndipo Uthenga Wabwino ukulalikidwa kwa osauka.
Jesuh naw, “Citbe u lü, nami hmuh la nami sim he Johan üng jah va mtheh ua; amikmüe mdei law be ve u, akhawkxo he ami khaw am cit ve u, mnehkse mnehkie ngcim be ve u, ami nghnga kpangki he pi ami nghnga ngjang be ve u, akthi he xüng law be ve u, khuikha m’yetsekiea veia thangkdaw sanga kya ve.
23 Odala munthu amene sakhumudwa chifukwa cha Ine.”
“Upi, keia phäha, a mlung am hlawtlatki ta a jo sen ve,” a ti.
24 Anthu otumidwa ndi Yohane aja atachoka, Yesu anayamba kuyankhula ndi gulu la anthu za Yohaneyo kuti, “Kodi munkapita ku chipululu kukaona chiyani? Bango logwedezeka ndi mphepo?
Johana xüisaw he ami ktawih be käna, Jesuh naw Johana mawng khyang he üng jah mtheh lü, “Johana veia, khawkhyawng khawa nami ceh üng, i teng khaia ni nami ceh? Khawkhia aksün khuhlip teng khaia aw nami ceh?
25 Ngati si choncho, munkapita kukaona chiyani? Munthu wovala zovala zabwino? Ayi, ovala zovala zodula ndi okhala moyo wapamwamba ali mʼnyumba zaufumu.
“Am acunüng i teng khaia ni nami ceh? Suisak akdaw suisaki teng khaia aw nami ceh? Suisak akdaw suisaki he cun sangpuxang hea ima ni ami awm khawi.
26 Koma inu munkapita kukaona chiyani? Mneneri? Inde, Ine ndikukuwuzani, woposa mneneri.
“Am acunüng sahma teng khaia aw nami ceh? Ä, ka ning jah mtheki, sahmaa kthaka pi kyäp bawki hia awm ve,
27 Uyu ndi amene malemba akunena za Iye kuti, “‘Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu, amene adzakonza njira yanu.’
cangcim naw ‘Ngaia ka khyang na ma ka tüih, ani naw na maa lam pyang khai’ tia a mawng ami yuk cen ahina Johan ni.
28 Ine ndikukuwuzani kuti pakati pa obadwa kuchokera mwa mkazi palibe wina wamkulu kuposa Yohane; komabe amene ali wamngʼono mu ufumu wa Mulungu ndi wamkulu kuposa iye.”
“Ka ning jah mthehki, nghnumi hea ca avan üng Johana kyäp bawki sahma am awm naw; cunsepi, Pamhnama khawa akjaw säih pi Johana kthaka kyäp bawki ni,” a ti.
29 Anthu onse, ngakhale amisonkho, atamva mawu a Yesu, anavomereza kuti njira ya Mulungu ndi yolondola, chifukwa anabatizidwa ndi Yohane.
Acunüng, khyang avan naw ami ngjak; aktunga ngcawnklawk he cun Pamhnama ngsungpyunak vaia Johana baptican khanki he.
30 Koma Afarisi ndi akatswiri amalamulo anakana cholinga cha Mulungu kwa iwo okha, chifukwa sanabatizidwe ndi Yohane.
Cunsepi, Pharise he la, thum mksingki he naw, ami hama Pamhnama pyan ma u lü, Johana baptican ä khanki he.
31 “Kodi ndingawafanizire chiyani anthu a mʼbado uno? Ali ngati chiyani?
Jesuh naw pyen be tü lü, “Tuhkbäiha ngsawn he hin i am ni ka jah msuimcäp kawm? Ia mäih ni ami law?
32 Ali ngati ana amene akukangana pa msika, ena akufunsa anzawo kuti, “‘Ife tinakuyimbirani chitoliro, koma inu simunavine. Tinakuyimbirani nyimbo zamaliro, koma inu simunalire.’
“Ahin he cun Anghmawe jawihtuknaka ngawki he, ngkhü kyu u lü, ‘Cambumak pülün ning jah tum pe ung se am nami nglamki, yawk la sa ung se pi am nami kyapki’ ti am tängki he.
33 Pakuti Yohane Mʼbatizi sanabwere kudzadya buledi kapena kumwa vinyo, koma inu mumati, ‘Ali ndi chiwanda.’
“Baptican Johan a law üng ei nghmü lü capyitui am aw se, ‘khawyaia awmnak’ nami tiki.
34 Mwana wa Munthu anabwera nadya ndi kumwa, ndipo inu mukuti, ‘Ali ndi dyera komanso ndi woledzera, bwenzi la amisonkho ndi ochimwa.’
“Khyanga Capa law lü ei aw se, ‘Teng u, eiaw aih ve, ngcawnklawk he la khyang kse hea püi cen’ nami tiki.
35 Ndipo nzeru zimaoneka zolondola mwa ana ake onse.”
“Mhnama ksingkhyapnak cun dokhameiki he naw a cangnak mdangki he ni,” a ti.
36 Tsopano mmodzi mwa Afarisi anayitana Yesu kuti akadye naye ku nyumba kwake ndipo anapita nakakhala pa tebulo.
Pharise mat naw a veia buh ei khaia khü se, Jesuh Pharisea ima lut lü buh ei khaia ngawki.
37 Mayi amene amakhala moyo wauchimo mu mzindawo atadziwa kuti Yesu akudya ku nyumba ya Mfarisiyo, anabweretsa botolo la mafuta onunkhira a alabasta.
Acuna mlüh üng nghnumi kse mat awmki naw Pharisea ima Jesuh buh ei lü awmki ti, a ksing üng, alabasta um üng situi ngui lawpüiki naw,
38 Iye anayimirira kumbuyo kwa Yesu pa mapazi ake akulira, nayamba kumadontheza misozi pa mapazi ake. Ndipo iye anapukuta mapaziwo ndi tsitsi lake, nawapsompsona ndi kuwathira mafuta onunkhirawo.
Jesuha hnu, a khaw kunga kyap lü ngdüiki. A miktui naw a khawpha msüi se, a lusam am xüt lü, a khawpha mhnamki naw, situi ng'ui am a hluk.
39 Mfarisiyo anamuyitanayo ataona izi, anati mu mtima mwake, “Ngati munthuyu akanakhala mneneri, akanadziwa kuti akumukhudzayo ndi mayi otani, kuti ndi wochimwa.”
Pharise naw hmu lü, a mlung k'uma, “Hin hin sahma kcanga a kya vai sü, hnetkia nghnuminu hin u ni, ia mäih ni ti ksing khai sü. Khyangka kyalang se,” a ti.
40 Yesu anamuyankha iye kuti, “Simoni, ndili ndi kanthu koti ndikuwuze.” Iye anati, “Ndiwuzeni Aphunzitsi.”
Jesuh naw, “Sihmon, na veia ngthu mat ka pyen vai awm ve,” ti lü a msang. Acunüng Sihmon naw, “Saja aw pyena,” a ti.
41 “Anthu awiri anakongola ndalama kwa munthu wina wokongoletsa ndalama: mmodzi ndalama zokwana 500 ndi winayo ndalama makumi asanu.
Jesuh naw, “Ngui jah kpuki, mat naw, khyang nghngih üng ngui a jah kpu; mat üng phya mhma a kpu, mat am mhmakip a kpu.
42 Panalibe mmodzi mwa iwo anali ndi ndalama zobwezera, ndipo iye anawakhululukira ngongole zawo. Tsopano ndi ndani mwa awiriwa adzamukonde koposa?”
“Ani thungnak be vai am ta ni se, ani nghngih a jah mhlät. Acunüng, acun xawi üng u naw jawng na bawk khai ni?” a ti.
43 Simoni anayankha kuti, “Ndikuganiza kuti ndi amene anamukhululukira ngongole yayikulu.” Yesu anati, “Wayankha molondola.”
Sihmon naw, “A mhlät däm naw jawng na bawk khaia ngai veng,” ti lü, msang se, Jesuh naw, “Cang veki,” a ti.
44 Kenaka anatembenukira kwa mayiyo nati kwa Simoni, “Ukumuona mayiyu? Ine ndabwera mʼnyumba yako. Iwe sunandipatse madzi otsukira mapazi anga, koma iyeyu wanyowetsa mapazi anga ndi misozi yake ndi kuwapukuta ndi tsitsi lake.
Acunüng, nghnumi nghlat si lü, Sihmona veia, “Hina nghnuminu na hmuki aw? Na ima lut law ni se, ka khaw ka mthinak vaia tui am na na peki, hina nghnuminu naw a miktui am ka khaw mthi lü, a lusam am xütki.
45 Iwe sunandipsompsone, koma mayiyu, kuyambira pamene Ine ndalowa, sanaleke kupsompsona mapazi anga.
“Nang naw am na na mhnamki, hina nghnumi naw ka luh law üng tün lü ka khawpha am pyai lü mhnamki.
46 Iwe sunadzoze mutu wanga mafuta, koma iye wadzoza mapazi anga mafuta onunkhira.
“Nang naw ka lü situi am na hluki, hina nghnumi naw ka khawpha situi am hluki.
47 Tsono, ndikukuwuza iwe, machimo ake amene ndi ambiri akhululukidwa, monga chaonetsera chikondi chake chachikulu. Koma iye amene wakhululukidwa zochepa amakonda pangʼono.”
“Acunakyase, ning mtheh veng, aktäa jawng nakia kyase, a katnak he khawjah cun mhlät pänga kya ve. A katnak ajaw däng mhlät naw ajawha jawng naki,” a ti.
48 Kenaka anati kwa mayiyo, “Machimo ako akhululukidwa.”
Acunüng, Jesuh naw nghnumi üng, “Na katnak he jah mhlät pänga kya ve,” a ti.
49 Alendo enawo anayamba kumanena mʼmitima mwawo kuti, “Uyu ndi ndani amene akhululukiranso machimo?”
Buh a eipüi he naw, “Katnak pi jah mhlätki hin u ni,” ami ti.
50 Yesu anati kwa mayiyo, “Chikhulupiriro chako chakupulumutsa. Pita mu mtendere.”
Acunüng, Jesuh naw nghnumi üng, “Na jumnak naw ning küikyan ve, dim’yenak am cita,” a ti.

< Luka 7 >