< Luka 6 >

1 Tsiku lina la Sabata Yesu ankadutsa mʼminda yatirigu, ndipo ophunzira ake anayamba kubudula ngala zatirigu, namazifikisa mʼmanja mwawo ndi kumadya.
Or, le deuxième sabbat après le premier, il parcourait les champs de blé. Ses disciples arrachaient les épis et mangeaient en les frottant dans leurs mains.
2 Ena mwa Afarisi anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mukuchita zosaloledwa pa tsiku la Sabata?”
Mais quelques-uns des pharisiens leur dirent: « Pourquoi faites-vous ce qu'il n'est pas permis de faire le jour du sabbat? »
3 Yesu anawayankha iwo kuti, “Kodi simunawerenge zimene Davide anachita pamene iye ndi anzake anali ndi njala?
Jésus, prenant la parole, leur dit: « N'avez-vous pas lu ce que fit David quand il eut faim, lui et ceux qui étaient avec lui,
4 Iye analowa mʼnyumba ya Mulungu ndipo atatenga buledi wopatulika anadya amene ndi ololedwa kudya ansembe okha. Ndipo anaperekanso wina kwa anzake.”
comment il entra dans la maison de Dieu, prit et mangea le pain de proposition, et en donna aussi à ceux qui étaient avec lui, ce qu'il n'est pas permis de manger, si ce n'est pour les prêtres seuls? »
5 Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Mwana wa Munthu ndi Ambuye wa Sabata.”
Il leur répondit: « Le Fils de l'homme est maître du sabbat. »
6 La Sabata lina Iye analowa mʼsunagoge kukaphunzitsa ndipo mʼmenemo anapeza munthu wadzanja lolumala.
Un autre sabbat, il entra dans la synagogue et enseigna. Il y avait là un homme, dont la main droite était desséchée.
7 Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo ankamuyangʼana kuti apeze chifukwa Yesu, choncho anamuyangʼanitsitsa kuti aone ngati Iye akanamuchiritsa pa Sabata.
Les scribes et les pharisiens l'observaient, pour voir s'il ferait une guérison le jour du sabbat, afin de trouver une accusation contre lui.
8 Koma Yesu anadziwa zimene ankaganiza ndipo anati kwa munthu wadzanja lolumalayo, “Tanyamuka ndipo uyime patsogolo pa onsewa.” Choncho iye ananyamuka nayima pamenepo.
Mais Jésus connaissait leurs pensées, et il dit à l'homme qui avait la main desséchée: « Lève-toi et tiens-toi au milieu. » Il se leva et se tint debout.
9 Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Ndikufunseni, kodi chololedwa pa Sabata ndi chiti: kuchita chabwino kapena kuchita choyipa, kupulumutsa moyo kapena kuwononga?”
Alors Jésus leur dit: « Je vais vous poser une question: est-il permis, le jour du sabbat, de faire du bien ou de faire du mal? De sauver une vie, ou de tuer? »
10 Iye atawayangʼana onsewo, anati kwa munthuyo, “Wongola dzanja lako.” Iye anaterodi, ndipo dzanja lake linachiritsidwa.
Il les regarda tous, et dit à l'homme: « Étends ta main. » Il le fit, et sa main fut rendue aussi saine que l'autre.
11 Koma iwo anapsa mtima nayamba kukambirana wina ndi mnzake chomwe akanamuchitira Yesu.
Mais ils étaient remplis de rage, et ils parlaient entre eux de ce qu'ils pourraient faire à Jésus.
12 Tsiku lina, masiku amenewo, Yesu anapita ku phiri kukapemphera ndipo anakhala usiku wonse akupemphera kwa Mulungu.
En ces jours-là, il se rendit sur la montagne pour prier, et il passa toute la nuit à prier Dieu.
13 Kutacha, anayitana ophunzira ake ndipo anasankha khumi ndi awiri a iwo amene anawayika kukhala atumwi:
Le jour venu, il appela ses disciples, et il en choisit douze, qu'il appela aussi apôtres:
14 Simoni (amene anamutcha Petro), mʼbale wake wa Andreya, Yakobo, Yohane, Filipo, Bartumeyu,
Simon, qu'il appela aussi Pierre; André, son frère; Jacques; Jean; Philippe; Barthélemy;
15 Mateyu, Tomasi, Yakobo mwana wa Alufeyo, Simoni amene amatchedwa Zaleti,
Matthieu; Thomas; Jacques, fils d'Alphée; Simon, appelé le Zélote;
16 Yudasi mwana wa Yakobo ndi Yudasi Isikarioti amene anamupereka.
Judas, fils de Jacques; et Judas Iscariote, qui devint aussi un traître.
17 Iye anatsika pamodzi ndi atumwiwo ndipo anayima pamalo athyathyathya. Gulu lalikulu la ophunzira ake, gulu lalikulu la anthu ochokera ku Yudeya konse, ku Yerusalemu ndi ochokera mʼmphepete mwa nyanja ya Turo ndi Sidoni anali pomwepo.
Il descendit avec eux et se tint sur un terrain plat, en compagnie d'une foule de ses disciples et d'un grand nombre de gens de toute la Judée, de Jérusalem et de la côte maritime de Tyr et de Sidon, qui venaient l'entendre et se faire guérir de leurs maladies,
18 Iwo anabwera kudzamvetsera ndi kuchiritsidwa ku matenda awo. Osautsidwa ndi mizimu yoyipa anachiritsidwa,
ainsi que de ceux qui étaient tourmentés par des esprits impurs; et ils étaient guéris.
19 ndipo anthu ankayesetsa kuti amukhudze chifukwa mphamvu imatuluka mwa Iye ndi kuchiritsa onse.
Toute la foule cherchait à le toucher, car une force sortait de lui et les guérissait tous.
20 Akuyangʼana ophunzira ake, Iye anati, “Odala ndinu amene ndi osauka, chifukwa ufumu wa Mulungu ndi wanu.
Il leva les yeux vers ses disciples, et dit: « Heureux vous qui êtes pauvres, car le Royaume de Dieu est à vous.
21 Inu amene mukumva njala tsopano, ndinu odala chifukwa mudzakhutitsidwa. Inu amene mukulira tsopano, ndinu odala chifukwa mudzasekerera.
Heureux ceux qui ont faim maintenant, car vous serez comblé. Heureux êtes-vous ceux qui pleurent maintenant, car vous allez rire.
22 Ndinu odala, anthu akamakudani, kukusalani ndi kukunyozani ndi kumayipitsa dzina lanu chifukwa cha Mwana wa Munthu.
Heureux es-tu quand les hommes te haïssent, quand ils t'excluent et se moquent de toi, et qu'ils jettent ton nom en pâture, à cause du Fils de l'homme.
23 “Nthawi imeneyo sangalalani ndipo lumphani ndi chimwemwe chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba. Pakuti ndi zomwezonso zimene makolo awo anachitira aneneri.
Réjouissez-vous en ce jour-là et tressaillez de joie, car voici que votre récompense est grande dans les cieux, car leurs pères ont agi de même envers les prophètes.
24 “Ndinu atsoka, anthu olemera, popeza mwalandiriratu zokusangalatsani.
« Mais malheur à vous qui êtes riches! Car vous avez reçu votre consolation.
25 Tsoka inu amene mukudya bwino tsopano, chifukwa mudzakhala ndi njala. Ndinu atsoka, amene mukusekerera tsopano, chifukwa mudzabuma ndi kulira.
Malheur à vous, vous qui êtes rassasiés maintenant, car vous aurez faim. Malheur à vous qui riez maintenant, car vous serez en deuil et pleurerez.
26 Ndinu atsoka, anthu akamakuyamikirani, popeza makolo anu anawachitira aneneri onama zomwezi.”
Malheur, quand les hommes disent du bien de toi, car leurs pères ont fait la même chose aux faux prophètes.
27 “Koma Ine ndikuwuza inu amene mukundimva: Kondani adani anu, chitirani zabwino amene amakudani.
« Mais moi, je vous dis, à vous qui m'écoutez: aimez vos ennemis, faites du bien à ceux qui vous haïssent,
28 Dalitsani amene amakutembererani, apempherereni amene amakusautsani.
bénissez ceux qui vous maudissent, et priez pour ceux qui vous maltraitent.
29 Ngati wina akumenyani patsaya limodzi mupatseninso tsaya linalo. Ngati wina akulanda mwinjiro wako, umulole atenge ndi mkanjo omwe.
A celui qui te frappe sur la joue, présente aussi l'autre; et à celui qui te prend ton manteau, ne refuse pas aussi ta tunique.
30 Mupatseni aliyense amene akupemphani kanthu ndipo ngati wina atenga chinthu chanu, musamulamule kuti akubwezereni.
Donne à quiconque te demande, et ne demande pas à celui qui te prive de tes biens de te les rendre.
31 Inu muwachitire anthu ena, zomwe mukanafuna kuti iwo akuchitireni.
« Comme vous voulez que les gens vous fassent, faites-leur exactement la même chose.
32 “Ngati mukonda okhawo amene amakukondani, mwapindula chiyani? Ngakhale ‘ochimwa’ amakonda amene amawakondanso.
« Si vous aimez ceux qui vous aiment, en quoi cela vous honore-t-il? Car même les pécheurs aiment ceux qui les aiment.
33 Ndipo ngati muchita zabwino kwa amene ndi abwino kwa inu, mwapindula chiyani? Ngakhale ‘ochimwa’ amachita izi.
Si vous faites du bien à ceux qui vous font du bien, quel honneur cela vous fait-il? Car même les pécheurs font de même.
34 Ndipo ngati mukongoza amene mukuyembekeza kuti abweza, mwapindula chiyani? Ngakhale ‘ochimwa’ amabwereketsa kwa ochimwa anzawo, ndipo amayembekezera kubwezeredwa zonse.
Si vous prêtez à ceux dont vous espérez recevoir, quel mérite avez-vous? Les pécheurs eux-mêmes prêtent aux pécheurs, pour en recevoir autant en retour.
35 Koma kondani adani anu, achitireni zabwino, akongozeni koma osayembekezera kulandira kanthu. Pamenepo mphotho yanu idzakhala yayikulu ndipo inu mudzakhala ana a Wammwambamwamba, chifukwa ndi wokoma mtima kwa anthu osayamika ndi oyipa.
Mais aimez vos ennemis, faites le bien, prêtez sans rien attendre en retour, et votre récompense sera grande, et vous serez les enfants du Très-Haut, car il est bon envers les ingrats et les méchants.
36 Khalani achifundo, monga momwe Atate anu ali achifundo.”
« Soyez donc miséricordieux, comme votre Père est aussi miséricordieux.
37 “Musaweruze, ndipo inu simudzaweruzidwa. Musatsutse ndipo inu simudzatsutsidwa. Khululukirani ena ndipo mudzakhululukidwa.
Ne jugez pas, et vous ne serez pas jugés. Ne condamnez pas, et tu ne seras pas condamné. Libérez-vous, et tu seras libéré.
38 Perekani ndipo mudzapatsidwa. Adzakupatsani mʼthumba mwanu muyeso wabwino, wotsenderezeka, wokhutchumuka ndi wosefukira. Pakuti muyeso umene mumagwiritsa ntchito, ndi omwewo adzakuyeserani.”
« Donnez, et l'on vous donnera: on vous donnera une bonne mesure, tassée, secouée et débordante. Car c'est avec la même mesure que vous mesurez qu'on vous mesurera. »
39 Iye anawawuzanso fanizo ili, “Kodi munthu wakhungu angatsogolere munthu wakhungu mnzake? Kodi onse sadzagwera mʼdzenje?
Il leur adressa une parabole. « Un aveugle peut-il guider un aveugle? Ne tomberont-ils pas tous deux dans une fosse?
40 Wophunzira sangapose mphunzitsi wake, koma yense amene waphunzitsidwa bwinobwino adzakhala ngati mphunzitsi wake.
Un disciple n'est pas au-dessus de son maître, mais chacun, lorsqu'il sera bien formé, sera comme son maître.
41 “Kodi ndi chifukwa chiyani mumaona kachitsotso mʼdiso la mʼbale wanu ndi kusasamala mtengo uli mʼdiso mwanu?
Pourquoi vois-tu la paille qui est dans l'œil de ton frère, mais ne considères-tu pas la poutre qui est dans ton propre œil?
42 Kodi munganene bwanji kwa mʼbale wanu kuti, ‘Mʼbale nʼtakuchotsa kachitsotso mʼdiso mwako,’ pamene inu eni ake mukulephera kuona mtengo uli mʼdiso mwanu? Inu achiphamaso, yambani mwachotsa mtengo uli mʼdiso mwanu, ndipo kenaka mudzaona bwinobwino ndi kuchotsa kachitsotso mʼdiso la mʼbale wanu.”
Ou comment peux-tu dire à ton frère: « Mon frère, laisse-moi enlever la paille qui est dans ton œil », alors que tu ne vois pas toi-même la poutre qui est dans ton œil? Hypocrite! Enlève d'abord la poutre de ton œil, et alors tu pourras voir clairement pour enlever la paille qui est dans l'œil de ton frère.
43 Palibe mtengo wabwino umene umabala chipatso choyipa, kapena mtengo oyipa umene umabala chipatso chabwino.
« Car il n'y a pas de bon arbre qui produise des fruits pourris, ni d'arbre pourri qui produise de bons fruits.
44 Mtengo uliwonse umadziwika ndi chipatso chake. Anthu sathyola nkhuyu pa mtengo waminga, kapena mphesa pa nthungwi.
Car on reconnaît chaque arbre à son fruit. Car on ne cueille pas des figues sur des épines, ni des raisins sur un buisson de ronces.
45 Munthu wabwino amatulutsa zinthu zabwino zosungidwa mu mtima mwake, koma munthu oyipa amatulutsa zinthu zoyipa zosungidwa mu mtima mwake. Pakamwa pake pamayankhula zimene zadzaza mu mtima mwake.
L'homme bon tire du bon trésor de son cœur ce qui est bon, et l'homme mauvais tire du mauvais trésor de son cœur ce qui est mauvais, car c'est de l'abondance du cœur que parle la bouche.
46 “Kodi nʼchifukwa chiyani munditchula kuti, ‘Ambuye, Ambuye’ koma simuchita zimene Ine ndinena?
Pourquoi m'appelez-vous: « Seigneur, Seigneur », et ne faites-vous pas ce que je dis?
47 Ine ndidzakuonetsani mmene alili munthu amene amabwera kwa Ine ndi kumva mawu anga ndi kuwachita.
Quiconque vient à moi, entend mes paroles et les met en pratique, je vous montrerai à qui il est semblable.
48 Iye ali ngati munthu womanga nyumba, amene anakumba mozama nayika maziko ake pa mwala. Madzi osefukira atabwera ndi mphamvu, nawomba nyumbayo koma sinagwedezeka, chifukwa anayimanga bwino.
Il est semblable à un homme qui construit une maison, qui a creusé et approfondi, et qui a posé le fondement sur le roc. Quand il y a eu une inondation, le torrent s'est jeté contre cette maison et n'a pu l'ébranler, parce qu'elle était fondée sur le roc.
49 Koma amene amamva mawu anga koma osawachita, akufanana ndi munthu amene anamanga nyumba yake koma yopanda maziko. Nthawi yomwe madziwo anawomba nyumbayo, inagwa ndipo inawonongekeratu.”
Mais celui qui entend et ne fait pas, est semblable à un homme qui a bâti sur la terre une maison sans fondement, contre laquelle le torrent s'est brisé, et aussitôt elle est tombée; et la ruine de cette maison a été grande. »

< Luka 6 >