< Luka 5 >

1 Tsiku lina Yesu anayima mʼmbali mwa nyanja ya Genesareti, gulu la anthu litamuzungulira likumvetsera mawu a Mulungu.
Busuba nabumbi Yesu walikuba wemana mumbali mwa lwenje lwa Genesaleti. Bantu bangi bali kabanyakana kwambeti banyumfwe Maswi a Lesa.
2 Iye anaona mabwato awiri ali mʼmphepete mwa nyanja, asodzi amene ankachapa makhoka awo atawasiya pamenepo.
Lino Yesu walabona mato abili asungwa mumbali, beshikushina inswi balikuba balafumumo kabasuka tombe twabo.
3 Iye analowa mʼbwato limodzi limene linali la Simoni, ndi kumupempha kuti alikankhire mʼkati mwa nyanja pangʼono. Kenaka Iye anakhala pansi nayamba kuphunzitsa anthu ali mʼbwatomo.
Yesu walengila mubwato bumo ubo bwalikuba bwa Shimoni, neye walasengeti abunyakileko pa lwenje. Walekala mubwato nekutatika kwiyisha bantu.
4 Atatha kuyankhula anati kwa Simoni, “Kankhirani kwa kuya ndipo muponye makhoka kuti mugwire nsomba.”
Mpwalapwisha kwiyisha, walambila Shimoni eti, “Bunyakileni bwato pakati, kwambeti muwale tombe twenu mumenshi mwikate inswi.”
5 Simoni anayankha kuti, “Ambuye, tagwira ntchito molimbika usiku wonse, koma sitinagwire kanthu. Koma pakuti mwatero, ndiponya makhoka.”
Shimoni walakumbuleti, “Shikwiyisha, kufuma mashiku bulatucele tuliya kwikatapo inswi, pakwinga mulamba njamwe ningwale tombe.”
6 Atachita izi, anagwira nsomba zambiri kotero kuti makhoka awo anayamba kungʼambika.
Lino balawala tombe twabo, nekwikata inswi shingi, tombe twabo twalatatika kupasuka.
7 Choncho anakodola anzawo a bwato linalo kuti abwere ndi kuwathandiza, ndipo anabwera nadzaza mabwato onse awiri mpaka kuyamba kumira.
Lino balakuwa banabo balikuba mubwato bumbi kwambeti bese babanyafweko kusabula, naboyo balesa, nomba balesusha mato abili nkayanda kwibila.
8 Simoni Petro ataona izi, anagwa pa mawondo a Yesu nati, “Chokani kwa ine Ambuye: Ine ndine munthu wochimwa!”
Shimoni Petulo mpwalaboneco walasuntama pantangu pa Yesu nekwambeti, “Kamundekelela Mwami Pakwinga ndeshikwinsa byaipa.”
9 Iye ndi anzake onse anadabwa ndi nsomba zimene anagwira,
Shimoni ne banendi balenseco pakwinga balakankamana pa kufula kwa inswi isho nshobalekata.
10 chimodzimodzinso Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, anzake a Simoniyo. Kenaka Yesu anati kwa Simoni, “Musachite mantha; kuyambira tsopano ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
Neco Jemusi ne Yohane bana bendi Zebediya kayi nebanendi Shimoni, naboyo balakankamana. Lino Yesu walambila Shimoni eti, “Kotatina pakwinga kufuma lelo nube weshikwikata bantu.”
11 Kenaka anakokera mabwato awo ku mtunda, nasiya zonse namutsata Iye.
Popelapo balatanta mato ayo kuya kutala kwa mulonga, balashiya byonse nekunkokela Yesu.
12 Yesu ali ku mudzi wina, munthu amene anali ndi khate thupi lonse anabwera kwa Iye. Munthuyo ataona Yesu, anagwa chafufumimba ndipo anamupempha Iye kuti, “Ambuye, ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
Yesu mpwalikuba mumunshi naumbi walakumana ne muntu wali kukolwa bulwashi bwa mankuntu mubili wonse. Mpwalabona Yesu mulwashi uyu walasuntama kuntangu nekumusengeti, “Mwami ndicishi kwambeti mukute ngofu shakusengula nsenguleni.”
13 Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo. Iye anati, “Ine ndikufuna, yeretsedwa!” Ndipo nthawi yomweyo khate lake linachoka.
Yesu walatandabula likasa lyakendi, walamwikata ne kwambeti, “Ee ndayandanga, koba cena!” Popelapo mankuntu alapwa.
14 Kenaka Yesu anamulamula kuti, “Usawuze wina aliyense, koma pita, kadzionetse kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose anakulamulirani za kuyeretsedwa kwanu monga umboni kwa iwo.”
Kufumapo Yesu walamwambileti, “Konyumfwa, kotambila muntu nambi umo makani awa. Nomba obe ululame wenga kuli beshikwiyisha, uyenga ulileshe kuli beshimilumbo kwambeti ulaba cena. Uye ubenge bupe kwelana ne ncalamba Mose kwambeti bantu bashometi ulaba cena.”
15 Koma mbiri yake inafalikirabe kwambiri kotero kuti magulu a anthu anabwera kudzamvetsera ndi kuti achiritsidwe ku matenda awo.
Necikabeco impuwo ya Yesu yalanyumfwika kubantu bangi. Neco bantu balikwisa kuli endiye kwambeti banyumfwe Maswi akendi kayi nekubasengula malwashi abo.
16 Koma Yesu nthawi zambiri ankachoka kupita ku malo a yekha kukapemphera.
Lino nendi Yesu walaya kwa enka akupaila.
17 Tsiku lina pamene ankaphunzitsa, Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, amene anachokera ku midzi yonse ya Galileya ndi ku Yudeya ndi Yerusalemu, anakhala pansi pomwepo. Ndipo mphamvu ya Ambuye inalipo yakuti Iye achiritse odwala.
Nabumbi busuba Yesu walikeyisha, popelapo palikuba Bafalisi ne beshikwiyisha milawo nabambi. Bantu aba balafuma muminshi yonse ya ku Galileya, ku Yudeya kayi neku Yelusalemu. Ngofu sha Lesa shalikuba muli Yesu kwambeti abasengule.
18 Amuna ena anabwera atanyamula munthu wofa ziwalo pa mphasa ndipo anayesa kumulowetsa mʼnyumba kuti amugoneke pamaso pa Yesu.
Kufumapo bantu nabambi balaleta mutuloba walikuba watontola mubili nkabali bamunyamuna pa mpasa. Balelesha kwambeti bamwingishe mu ng'andeti bamoneke pantangu pa Yesu.
19 Atalephera kupeza njira yochitira zimenezi chifukwa cha gulu la anthu, anakwera naye pa denga ali pa mphasa pomwepo ndi kumutsitsira mʼkati pakati pa gulu la anthu, patsogolo penipeni pa Yesu.
Naboyo balikuyanda kumwingishila pacishinga, lino pakwinga bantu balafula balalilwa kwambeti bamutwale mukati. Neco balatanta nendi pa ciluli ca ng'anda ne kupasula mulyango, balamwingisha ne kumulelesha pampasa yakendi pakati pabantu ne kumushikisha pantangu pa Yesu.
20 Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati, “Mnzanga, machimo ako akhululukidwa.”
Yesu mpwalabona kushoma kwakendi, “Walambeti, bwipishi bwakobe bulalekelelwa.”
21 Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anayamba kuganiza mwa iwo okha kuti, “Kodi munthu uyu ndi ndani amene ayankhula zamwano? Kodi ndani amene angakhululukire machimo kupatula Mulungu?”
Lino beshikwiyisha Milawo kayi ne Bafalisi balatatika kwipushaneti, “Nomba uyu niyani lanyashanga Lesa? Niyani welela kulekelela bwipishi sena nte Lesa enka?”
22 Yesu anadziwa zomwe iwo amaganiza ndipo anafunsa kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukuganiza zimenezi mʼmitima mwanu?
Lino Yesu walenshiba ncobalikuyeya mumyoyo yabo neku bepusheti, “Nomba mulayeyelenga cani bintu bya mushoboyo mu myoyo yenu?
23 Kodi chapafupi ndi chiti: kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kunena kuti, ‘Nyamuka ndipo yenda?’”
Nicipeyo capuba kwambila muntu eti, ‘Bwipishi bwakobe bulalekelelwa,’ Nambi kwambeti, ‘Nyamuka, wende’
24 Koma kuti inu mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo, Iye anati kwa munthu wofa ziwaloyo, “Ine ndikuwuza iwe kuti, ‘Imirira, nyamula mphasa ndipo uzipita kwanu.’”
Lino ndayandanga kumwambileti mwinshibe kwambeti mwana muntu ukute ngofu shakulekelela bwipishi pacishi ca panshi.” Kufumapo walambila usa watontola mubileti, “Ndakwambilinga, nyamuka, manta mpasa yakobe wenga kucomwenu.”
25 Nthawi yomweyo anayimirira patsogolo pawo, nanyamula mphasa yake ndipo anapita kwawo akuyamika Mulungu.
Popelapo walapunduka bonse kabalanga nemenso abo, walamanta mpasa mpwalikuba wona nekutatika kuya nkalumbaisha Lesa.
26 Aliyense anadabwa ndi kuchita mantha ndipo anayamika Mulungu. Iwo anadabwa kwambiri ndipo anati, “Lero taona zinthu zosayiwalika.”
Bantu bonse balakankamana kayi balatina. Lino balatatika kulumbaisha Lesa ne kwambeti, “Ici ncotulabono lelo, nkatutana tucibonapo sobwe.”
27 Zitatha izi, Yesu anachoka ndipo anaona wolandira msonkho dzina lake Levi atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anati kwa iye, “Nditsate Ine.”
Popelapo Yesu walafuma pansa nekubona weshikusonkesha musonko walikukwiweti Levi, nkali ekala mu ng'anda yamusonko. Yesu walamwambileti, “Nkonkele.”
28 Ndipo Levi anayimirira, nasiya zonse ndi kumutsata Iye.
Popelapo neye walanyamuka, nekushiya byonse nekumukonkela.
29 Kenaka Levi anakonzera Yesu phwando lalikulu ku nyumba yake ndipo gulu lalikulu la amisonkho ndi ena ankadya naye pamodzi.
Lino Levi walabamba byakulya bingi kwambeti basekelele ne Yesu mu ng'anda yakendi. Kwalikuba beshikusonkesha misonko bangi ne bantu nabambi kabalya pamo.
30 Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amene anali a gulu lawo anadandaula kwa ophunzira ake, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukudya ndi kumwa pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”
Bafalisi nabambi ne beshikwiyisha milawo balatatika kudandaulila beshikwiya ba Yesu eti, “Nomba nicani mulalyelenga nekunwa pamo ne beshikusonkesha kayi ne bantu babwipishi?”
31 Yesu anawayankha kuti, “Amene sakudwala safuna singʼanga, koma odwala.
Lino Yesu walabakumbuleti, “Bayumi nkabakute kulangaula mu ng'anga sobwe, nsombi balwashi.
32 Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa kuti atembenuke mtima.”
Ndiya kwishila balulama nsombi babwipishi kwambeti basanduke mu myoyo yabo.”
33 Iwo anati kwa Iye, “Ophunzira a Yohane amasala kudya ndi kupemphera kawirikawiri, monganso ophunzira a Afarisi, koma anu amangodya ndi kumwa.”
Bantu nabambi balepusha Yesu eti, “Beshikwiya ba Yohane mubatishi bali kuba necindi cakulikanisha kulya nekupaila, naboyo beshikwiya ba Bafalisi bangi balikwinsa copeleco, bakobe baliya cindi camushoboyo, balo bakute kulya ne kunwowa.”
34 Yesu anawayankha kuti, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya pamene mkwati ali pakati pawo?
Lino Yesu walabakumuleti, “Sena balikubwinga ingamubakakatisha kutalya nebanabo, shibwinga kacilipo? Sobwe!
35 Koma nthawi ikubwera pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo. Masiku amenewo adzasala kudya.”
Nsombi cindi nicikashike shibwinga mpoti bakamufunyepo pali endibo, Lino ico cindi nibakalikanishe kulya.”
36 Iye anawawuza fanizo ili: “Palibe amene amangʼamba chigamba kuchokera pa chovala chatsopano ndi kuchisokerera pa chakale. Ngati atatero, ndiye kuti adzangʼamba chovala chatsopanocho, ndipo chigamba chochokera pa chovala chatsopano chija sichidzagwirizana ndi chakale.
Kufumapo Yesu walabambila cikoshanisho eti, “Kuliya muntu welela kukwamuna cimami cacikwisa caina nekutunga pa cakufwala cakeendi. Nkela kwinseco pakwinga naco ngacononga cikwisa kayi cimami nkacela kwendelana pacakufwala ico sobwe.
37 Ndipo palibe amene amakhuthulira vinyo watsopano mʼmatumba a vinyo akale. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa zikopazo, vinyo adzatayika ndipo zikopa za vinyozo zidzawonongeka.
Kuliya muntu welela kubika waini walino lino munkomwa yacipaya cakendi. Nalabikimo waini walino lino ukute kupasula nkomwa. Waini wonse ngawitika ne konongeka.
38 Ayi, vinyo watsopano ayenera kuthiridwa mʼmatumba a vinyo azikopa zatsopano.
Nomba waini walino lino welela kubikiwa mucinkuli calino lino.
39 Ndipo palibe amene atamwa vinyo wakale amafuna watsopano, pakuti amati, ‘Wakale ndi okoma.’”
Kuliya muntu welela kuyanda kunwa waini walino lino na lanu waini wakaindi pakwinga mukute kwambeti, ‘Usa wakaindi ewaina.’”

< Luka 5 >