< Luka 5 >
1 Tsiku lina Yesu anayima mʼmbali mwa nyanja ya Genesareti, gulu la anthu litamuzungulira likumvetsera mawu a Mulungu.
anantaraṁ yīśurekadā gineṣarathdasya tīra uttiṣṭhati, tadā lokā īśvarīyakathāṁ śrotuṁ tadupari prapatitāḥ|
2 Iye anaona mabwato awiri ali mʼmphepete mwa nyanja, asodzi amene ankachapa makhoka awo atawasiya pamenepo.
tadānīṁ sa hdasya tīrasamīpe naudvayaṁ dadarśa kiñca matsyopajīvino nāvaṁ vihāya jālaṁ prakṣālayanti|
3 Iye analowa mʼbwato limodzi limene linali la Simoni, ndi kumupempha kuti alikankhire mʼkati mwa nyanja pangʼono. Kenaka Iye anakhala pansi nayamba kuphunzitsa anthu ali mʼbwatomo.
tatastayordvayo rmadhye śimono nāvamāruhya tīrāt kiñciddūraṁ yātuṁ tasmin vinayaṁ kṛtvā naukāyāmupaviśya lokān propadiṣṭavān|
4 Atatha kuyankhula anati kwa Simoni, “Kankhirani kwa kuya ndipo muponye makhoka kuti mugwire nsomba.”
paścāt taṁ prastāvaṁ samāpya sa śimonaṁ vyājahāra, gabhīraṁ jalaṁ gatvā matsyān dharttuṁ jālaṁ nikṣipa|
5 Simoni anayankha kuti, “Ambuye, tagwira ntchito molimbika usiku wonse, koma sitinagwire kanthu. Koma pakuti mwatero, ndiponya makhoka.”
tataḥ śimona babhāṣe, he guro yadyapi vayaṁ kṛtsnāṁ yāminīṁ pariśramya matsyaikamapi na prāptāstathāpi bhavato nideśato jālaṁ kṣipāmaḥ|
6 Atachita izi, anagwira nsomba zambiri kotero kuti makhoka awo anayamba kungʼambika.
atha jāle kṣipte bahumatsyapatanād ānāyaḥ pracchinnaḥ|
7 Choncho anakodola anzawo a bwato linalo kuti abwere ndi kuwathandiza, ndipo anabwera nadzaza mabwato onse awiri mpaka kuyamba kumira.
tasmād upakarttum anyanausthān saṅgina āyātum iṅgitena samāhvayan tatasta āgatya matsyai rnaudvayaṁ prapūrayāmāsu ryai rnaudvayaṁ pramagnam|
8 Simoni Petro ataona izi, anagwa pa mawondo a Yesu nati, “Chokani kwa ine Ambuye: Ine ndine munthu wochimwa!”
tadā śimonpitarastad vilokya yīśoścaraṇayoḥ patitvā, he prabhohaṁ pāpī naro mama nikaṭād bhavān yātu, iti kathitavān|
9 Iye ndi anzake onse anadabwa ndi nsomba zimene anagwira,
yato jāle patitānāṁ matsyānāṁ yūthāt śimon tatsaṅginaśca camatkṛtavantaḥ; śimonaḥ sahakāriṇau sivadeḥ putrau yākūb yohan cemau tādṛśau babhūvatuḥ|
10 chimodzimodzinso Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, anzake a Simoniyo. Kenaka Yesu anati kwa Simoni, “Musachite mantha; kuyambira tsopano ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
tadā yīśuḥ śimonaṁ jagāda mā bhaiṣīradyārabhya tvaṁ manuṣyadharo bhaviṣyasi|
11 Kenaka anakokera mabwato awo ku mtunda, nasiya zonse namutsata Iye.
anantaraṁ sarvvāsu nausu tīram ānītāsu te sarvvān parityajya tasya paścādgāmino babhūvuḥ|
12 Yesu ali ku mudzi wina, munthu amene anali ndi khate thupi lonse anabwera kwa Iye. Munthuyo ataona Yesu, anagwa chafufumimba ndipo anamupempha Iye kuti, “Ambuye, ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
tataḥ paraṁ yīśau kasmiṁścit pure tiṣṭhati jana ekaḥ sarvvāṅgakuṣṭhastaṁ vilokya tasya samīpe nyubjaḥ patitvā savinayaṁ vaktumārebhe, he prabho yadi bhavānicchati tarhi māṁ pariṣkarttuṁ śaknoti|
13 Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo. Iye anati, “Ine ndikufuna, yeretsedwa!” Ndipo nthawi yomweyo khate lake linachoka.
tadānīṁ sa pāṇiṁ prasāryya tadaṅgaṁ spṛśan babhāṣe tvaṁ pariṣkriyasveti mamecchāsti tatastatkṣaṇaṁ sa kuṣṭhāt muktaḥ|
14 Kenaka Yesu anamulamula kuti, “Usawuze wina aliyense, koma pita, kadzionetse kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose anakulamulirani za kuyeretsedwa kwanu monga umboni kwa iwo.”
paścāt sa tamājñāpayāmāsa kathāmimāṁ kasmaicid akathayitvā yājakasya samīpañca gatvā svaṁ darśaya, lokebhyo nijapariṣkṛtatvasya pramāṇadānāya mūsājñānusāreṇa dravyamutmṛjasva ca|
15 Koma mbiri yake inafalikirabe kwambiri kotero kuti magulu a anthu anabwera kudzamvetsera ndi kuti achiritsidwe ku matenda awo.
tathāpi yīśoḥ sukhyāti rbahu vyāptumārebhe kiñca tasya kathāṁ śrotuṁ svīyarogebhyo moktuñca lokā ājagmuḥ|
16 Koma Yesu nthawi zambiri ankachoka kupita ku malo a yekha kukapemphera.
atha sa prāntaraṁ gatvā prārthayāñcakre|
17 Tsiku lina pamene ankaphunzitsa, Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, amene anachokera ku midzi yonse ya Galileya ndi ku Yudeya ndi Yerusalemu, anakhala pansi pomwepo. Ndipo mphamvu ya Ambuye inalipo yakuti Iye achiritse odwala.
aparañca ekadā yīśurupadiśati, etarhi gālīlyihūdāpradeśayoḥ sarvvanagarebhyo yirūśālamaśca kiyantaḥ phirūśilokā vyavasthāpakāśca samāgatya tadantike samupaviviśuḥ, tasmin kāle lokānāmārogyakāraṇāt prabhoḥ prabhāvaḥ pracakāśe|
18 Amuna ena anabwera atanyamula munthu wofa ziwalo pa mphasa ndipo anayesa kumulowetsa mʼnyumba kuti amugoneke pamaso pa Yesu.
paścāt kiyanto lokā ekaṁ pakṣāghātinaṁ khaṭvāyāṁ nidhāya yīśoḥ samīpamānetuṁ sammukhe sthāpayituñca vyāpriyanta|
19 Atalephera kupeza njira yochitira zimenezi chifukwa cha gulu la anthu, anakwera naye pa denga ali pa mphasa pomwepo ndi kumutsitsira mʼkati pakati pa gulu la anthu, patsogolo penipeni pa Yesu.
kintu bahujananivahasamvādhāt na śaknuvanto gṛhopari gatvā gṛhapṛṣṭhaṁ khanitvā taṁ pakṣāghātinaṁ sakhaṭvaṁ gṛhamadhye yīśoḥ sammukhe 'varohayāmāsuḥ|
20 Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati, “Mnzanga, machimo ako akhululukidwa.”
tadā yīśusteṣām īdṛśaṁ viśvāsaṁ vilokya taṁ pakṣāghātinaṁ vyājahāra, he mānava tava pāpamakṣamyata|
21 Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anayamba kuganiza mwa iwo okha kuti, “Kodi munthu uyu ndi ndani amene ayankhula zamwano? Kodi ndani amene angakhululukire machimo kupatula Mulungu?”
tasmād adhyāpakāḥ phirūśinaśca cittairitthaṁ pracintitavantaḥ, eṣa jana īśvaraṁ nindati koyaṁ? kevalamīśvaraṁ vinā pāpaṁ kṣantuṁ kaḥ śaknoti?
22 Yesu anadziwa zomwe iwo amaganiza ndipo anafunsa kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukuganiza zimenezi mʼmitima mwanu?
tadā yīśusteṣām itthaṁ cintanaṁ viditvā tebhyokathayad yūyaṁ manobhiḥ kuto vitarkayatha?
23 Kodi chapafupi ndi chiti: kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kunena kuti, ‘Nyamuka ndipo yenda?’”
tava pāpakṣamā jātā yadvā tvamutthāya vraja etayo rmadhye kā kathā sukathyā?
24 Koma kuti inu mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo, Iye anati kwa munthu wofa ziwaloyo, “Ine ndikuwuza iwe kuti, ‘Imirira, nyamula mphasa ndipo uzipita kwanu.’”
kintu pṛthivyāṁ pāpaṁ kṣantuṁ mānavasutasya sāmarthyamastīti yathā yūyaṁ jñātuṁ śaknutha tadarthaṁ (sa taṁ pakṣāghātinaṁ jagāda) uttiṣṭha svaśayyāṁ gṛhītvā gṛhaṁ yāhīti tvāmādiśāmi|
25 Nthawi yomweyo anayimirira patsogolo pawo, nanyamula mphasa yake ndipo anapita kwawo akuyamika Mulungu.
tasmāt sa tatkṣaṇam utthāya sarvveṣāṁ sākṣāt nijaśayanīyaṁ gṛhītvā īśvaraṁ dhanyaṁ vadan nijaniveśanaṁ yayau|
26 Aliyense anadabwa ndi kuchita mantha ndipo anayamika Mulungu. Iwo anadabwa kwambiri ndipo anati, “Lero taona zinthu zosayiwalika.”
tasmāt sarvve vismaya prāptā manaḥsu bhītāśca vayamadyāsambhavakāryyāṇyadarśāma ityuktvā parameśvaraṁ dhanyaṁ proditāḥ|
27 Zitatha izi, Yesu anachoka ndipo anaona wolandira msonkho dzina lake Levi atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anati kwa iye, “Nditsate Ine.”
tataḥ paraṁ bahirgacchan karasañcayasthāne levināmānaṁ karasañcāyakaṁ dṛṣṭvā yīśustamabhidadhe mama paścādehi|
28 Ndipo Levi anayimirira, nasiya zonse ndi kumutsata Iye.
tasmāt sa tatkṣaṇāt sarvvaṁ parityajya tasya paścādiyāya|
29 Kenaka Levi anakonzera Yesu phwando lalikulu ku nyumba yake ndipo gulu lalikulu la amisonkho ndi ena ankadya naye pamodzi.
anantaraṁ levi rnijagṛhe tadarthaṁ mahābhojyaṁ cakāra, tadā taiḥ sahāneke karasañcāyinastadanyalokāśca bhoktumupaviviśuḥ|
30 Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amene anali a gulu lawo anadandaula kwa ophunzira ake, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukudya ndi kumwa pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”
tasmāt kāraṇāt caṇḍālānāṁ pāpilokānāñca saṅge yūyaṁ kuto bhaṁgdhve pivatha ceti kathāṁ kathayitvā phirūśino'dhyāpakāśca tasya śiṣyaiḥ saha vāgyuddhaṁ karttumārebhire|
31 Yesu anawayankha kuti, “Amene sakudwala safuna singʼanga, koma odwala.
tasmād yīśustān pratyavocad arogalokānāṁ cikitsakena prayojanaṁ nāsti kintu sarogāṇāmeva|
32 Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa kuti atembenuke mtima.”
ahaṁ dhārmmikān āhvātuṁ nāgatosmi kintu manaḥ parāvarttayituṁ pāpina eva|
33 Iwo anati kwa Iye, “Ophunzira a Yohane amasala kudya ndi kupemphera kawirikawiri, monganso ophunzira a Afarisi, koma anu amangodya ndi kumwa.”
tataste procuḥ, yohanaḥ phirūśināñca śiṣyā vāraṁvāram upavasanti prārthayante ca kintu tava śiṣyāḥ kuto bhuñjate pivanti ca?
34 Yesu anawayankha kuti, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya pamene mkwati ali pakati pawo?
tadā sa tānācakhyau vare saṅge tiṣṭhati varasya sakhigaṇaṁ kimupavāsayituṁ śaknutha?
35 Koma nthawi ikubwera pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo. Masiku amenewo adzasala kudya.”
kintu yadā teṣāṁ nikaṭād varo neṣyate tadā te samupavatsyanti|
36 Iye anawawuza fanizo ili: “Palibe amene amangʼamba chigamba kuchokera pa chovala chatsopano ndi kuchisokerera pa chakale. Ngati atatero, ndiye kuti adzangʼamba chovala chatsopanocho, ndipo chigamba chochokera pa chovala chatsopano chija sichidzagwirizana ndi chakale.
soparamapi dṛṣṭāntaṁ kathayāmbabhūva purātanavastre kopi nutanavastraṁ na sīvyati yatastena sevanena jīrṇavastraṁ chidyate, nūtanapurātanavastrayo rmelañca na bhavati|
37 Ndipo palibe amene amakhuthulira vinyo watsopano mʼmatumba a vinyo akale. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa zikopazo, vinyo adzatayika ndipo zikopa za vinyozo zidzawonongeka.
purātanyāṁ kutvāṁ kopi nutanaṁ drākṣārasaṁ na nidadhāti, yato navīnadrākṣārasasya tejasā purātanī kutū rvidīryyate tato drākṣārasaḥ patati kutūśca naśyati|
38 Ayi, vinyo watsopano ayenera kuthiridwa mʼmatumba a vinyo azikopa zatsopano.
tato heto rnūtanyāṁ kutvāṁ navīnadrākṣārasaḥ nidhātavyastenobhayasya rakṣā bhavati|
39 Ndipo palibe amene atamwa vinyo wakale amafuna watsopano, pakuti amati, ‘Wakale ndi okoma.’”
aparañca purātanaṁ drākṣārasaṁ pītvā kopi nūtanaṁ na vāñchati, yataḥ sa vakti nūtanāt purātanam praśastam|