< Luka 5 >
1 Tsiku lina Yesu anayima mʼmbali mwa nyanja ya Genesareti, gulu la anthu litamuzungulira likumvetsera mawu a Mulungu.
Men det skete, da Folkeskaren trængte sig sammen om ham og hørte Guds Ord, og han stod ved Genezareths Sø,
2 Iye anaona mabwato awiri ali mʼmphepete mwa nyanja, asodzi amene ankachapa makhoka awo atawasiya pamenepo.
da så han to Skibe stå ved Søen; men Fiskerne vare gåede fra dem og toede Garnene.
3 Iye analowa mʼbwato limodzi limene linali la Simoni, ndi kumupempha kuti alikankhire mʼkati mwa nyanja pangʼono. Kenaka Iye anakhala pansi nayamba kuphunzitsa anthu ali mʼbwatomo.
Og han gik om Bord i et af Skibene, som var Simons, og bad ham at lægge lidt fra Land; og han satte sig og lærte Skarerne fra Skibet.
4 Atatha kuyankhula anati kwa Simoni, “Kankhirani kwa kuya ndipo muponye makhoka kuti mugwire nsomba.”
Men da han holdt op med at tale, sagde han til Simon: "Far ud på Dybet, og kaster eders Garn ud til en Dræt!"
5 Simoni anayankha kuti, “Ambuye, tagwira ntchito molimbika usiku wonse, koma sitinagwire kanthu. Koma pakuti mwatero, ndiponya makhoka.”
Og Simon svarede og sagde til ham: "Mester! vi have arbejdet hele Natten og fik intet; men på dit Ord vil jeg kaste Garnene ud."
6 Atachita izi, anagwira nsomba zambiri kotero kuti makhoka awo anayamba kungʼambika.
Og da de gjorde det, fangede de en stor Mængde Fisk, og deres Garn sønderreves.
7 Choncho anakodola anzawo a bwato linalo kuti abwere ndi kuwathandiza, ndipo anabwera nadzaza mabwato onse awiri mpaka kuyamba kumira.
Og de vinkede ad deres Staldbrødre i det andet Skib, at de skulde komme og hjælpe dem; og de kom og de fyldte begge Skibene, så at de var nær ved at synke.
8 Simoni Petro ataona izi, anagwa pa mawondo a Yesu nati, “Chokani kwa ine Ambuye: Ine ndine munthu wochimwa!”
Men da Simon Peter så det, faldt han ned for Jesu Knæ og sagde: "Gå bort fra mig, thi jeg er en syndig Mand, Herre!"
9 Iye ndi anzake onse anadabwa ndi nsomba zimene anagwira,
Thi en Rædsel var påkommen ham og alle dem, som vare med ham, over den Fiskedræt, som de havde fået;
10 chimodzimodzinso Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, anzake a Simoniyo. Kenaka Yesu anati kwa Simoni, “Musachite mantha; kuyambira tsopano ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
ligeledes også Jakob og Johannes, Zebedæus's Sønner, som vare Simons Staldbrødre. Og Jesus sagde til Simon: "Frygt ikke, fra nu af skal du fange Mennesker."
11 Kenaka anakokera mabwato awo ku mtunda, nasiya zonse namutsata Iye.
Og de lagde Skibene til Land og forlode alle Ting og fulgte ham.
12 Yesu ali ku mudzi wina, munthu amene anali ndi khate thupi lonse anabwera kwa Iye. Munthuyo ataona Yesu, anagwa chafufumimba ndipo anamupempha Iye kuti, “Ambuye, ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
Og det skete, medens han var i en af Byerne, se, da var der en Mand fuld af Spedalskhed; og da han så Jesus, faldt han på sit Ansigt, bad ham og sagde: "Herre! om du vil, kan du rense mig."
13 Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo. Iye anati, “Ine ndikufuna, yeretsedwa!” Ndipo nthawi yomweyo khate lake linachoka.
Og han udrakte Hånden og rørte ved ham og sagde: "Jeg vil; bliv ren!" Og straks forlod Spedalskheden ham.
14 Kenaka Yesu anamulamula kuti, “Usawuze wina aliyense, koma pita, kadzionetse kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose anakulamulirani za kuyeretsedwa kwanu monga umboni kwa iwo.”
Og han bød ham, at han skulde ikke sige det til nogen, men "gå bort, og fremstil dig for Præsten, og offer for din Renselse, således som Moses har befalet, til Vidnesbyrd for dem!"
15 Koma mbiri yake inafalikirabe kwambiri kotero kuti magulu a anthu anabwera kudzamvetsera ndi kuti achiritsidwe ku matenda awo.
Men Rygtet om ham udbredte sig end mere, og store Skarer kom sammen for at høre og for at helbredes for deres Sygdomme.
16 Koma Yesu nthawi zambiri ankachoka kupita ku malo a yekha kukapemphera.
Men han gik bort til Ørkenerne og bad.
17 Tsiku lina pamene ankaphunzitsa, Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, amene anachokera ku midzi yonse ya Galileya ndi ku Yudeya ndi Yerusalemu, anakhala pansi pomwepo. Ndipo mphamvu ya Ambuye inalipo yakuti Iye achiritse odwala.
Og det skete en af de Dage, at han lærte, og der sad Farisæere og Lovlærere, som vare komne fra enhver Landsby i Galilæa og Judæa og fra Jerusalem; og Herrens Kraft var hos ham til at helbrede.
18 Amuna ena anabwera atanyamula munthu wofa ziwalo pa mphasa ndipo anayesa kumulowetsa mʼnyumba kuti amugoneke pamaso pa Yesu.
Og se, nogle Mænd bare på en Seng en Mand, som var værkbruden, og de søgte at bære ham ind og lægge ham foran ham.
19 Atalephera kupeza njira yochitira zimenezi chifukwa cha gulu la anthu, anakwera naye pa denga ali pa mphasa pomwepo ndi kumutsitsira mʼkati pakati pa gulu la anthu, patsogolo penipeni pa Yesu.
Og da de ikke fandt nogen Vej til at bære ham ind for Skarens Skyld, stege de op oven på Taget og firede ham tillige med Sengen ned imellem Tagstenene midt iblandt dem foran Jesus.
20 Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati, “Mnzanga, machimo ako akhululukidwa.”
Og da han så deres Tro, sagde han: "Menneske! dine Synder ere dig forladte."
21 Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anayamba kuganiza mwa iwo okha kuti, “Kodi munthu uyu ndi ndani amene ayankhula zamwano? Kodi ndani amene angakhululukire machimo kupatula Mulungu?”
Og de skriftkloge og Farisæerne begyndte at tænke således ved sig selv: "Hvem er denne, som taler Gudsbespottelser? Hvem kan forlade Synder, uden Gud alene?"
22 Yesu anadziwa zomwe iwo amaganiza ndipo anafunsa kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukuganiza zimenezi mʼmitima mwanu?
Men da Jesus kendte deres Tanker, svarede han og sagde til dem: "Hvad tænke I på i eders Hjerter?
23 Kodi chapafupi ndi chiti: kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kunena kuti, ‘Nyamuka ndipo yenda?’”
Hvilket er lettest at sige: Dine Synder ere dig forladte? eller at sige: Stå op og gå?
24 Koma kuti inu mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo, Iye anati kwa munthu wofa ziwaloyo, “Ine ndikuwuza iwe kuti, ‘Imirira, nyamula mphasa ndipo uzipita kwanu.’”
Men for at I skulle vide, at Menneskesønnen har Magt på Jorden til at forlade Synder," så sagde han til den værkbrudne: "Jeg siger dig, stå op, og tag din Seng, og gå til dit Hus!"
25 Nthawi yomweyo anayimirira patsogolo pawo, nanyamula mphasa yake ndipo anapita kwawo akuyamika Mulungu.
Og han stod straks op for deres Øjne og tog det, som han lå på, og gik hen til sit Hus og priste Gud.
26 Aliyense anadabwa ndi kuchita mantha ndipo anayamika Mulungu. Iwo anadabwa kwambiri ndipo anati, “Lero taona zinthu zosayiwalika.”
Og Forfærdelse betog alle, og de priste Gud; og de bleve fulde af Frygt og sagde: "Vi have i Dag set utrolige Ting."
27 Zitatha izi, Yesu anachoka ndipo anaona wolandira msonkho dzina lake Levi atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anati kwa iye, “Nditsate Ine.”
Og derefter gik han ud og så en Tolder ved Navn Levi sidde ved Toldboden, og han sagde til ham: "Følg mig!"
28 Ndipo Levi anayimirira, nasiya zonse ndi kumutsata Iye.
Og han forlod alle Ting og stod op og fulgte ham.
29 Kenaka Levi anakonzera Yesu phwando lalikulu ku nyumba yake ndipo gulu lalikulu la amisonkho ndi ena ankadya naye pamodzi.
Og Levi gjorde et stort Gæstebud for ham i sit Hus; og der var en stor Skare af Toldere og andre, som sade til Bords med dem.
30 Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amene anali a gulu lawo anadandaula kwa ophunzira ake, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukudya ndi kumwa pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”
Og Farisæerne og deres Skriftkloge knurrede imod hans Disciple og sagde: "Hvorfor spise og drikke I med Toldere og Syndere?"
31 Yesu anawayankha kuti, “Amene sakudwala safuna singʼanga, koma odwala.
Og Jesus svarede og sagde til dem: "De raske trænge ikke til Læge, men de syge.
32 Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa kuti atembenuke mtima.”
Jeg er ikke kommen for at kalde retfærdige, men Syndere til Omvendelse."
33 Iwo anati kwa Iye, “Ophunzira a Yohane amasala kudya ndi kupemphera kawirikawiri, monganso ophunzira a Afarisi, koma anu amangodya ndi kumwa.”
Men de sagde til ham: "Johannes's Disciple faste ofte og holde Bønner og Farisæernes ligeså; men dine spise og drikke?"
34 Yesu anawayankha kuti, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya pamene mkwati ali pakati pawo?
Men Jesus sagde til dem: "Kunne I vel få Brudesvendene til at faste, så længe Brudgommen er hos dem?
35 Koma nthawi ikubwera pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo. Masiku amenewo adzasala kudya.”
Men der skal komme Dage, da Brudgommen bliver tagen fra dem; da skulle de faste i de Dage."
36 Iye anawawuza fanizo ili: “Palibe amene amangʼamba chigamba kuchokera pa chovala chatsopano ndi kuchisokerera pa chakale. Ngati atatero, ndiye kuti adzangʼamba chovala chatsopanocho, ndipo chigamba chochokera pa chovala chatsopano chija sichidzagwirizana ndi chakale.
Men han sagde også en Lignelse til dem: "Ingen river en Lap af et nyt Klædebon og sætter den på et gammelt Klædebon; ellers river han både det nye sønder, og Lappen fra det nye vil ikke passe til det gamle.
37 Ndipo palibe amene amakhuthulira vinyo watsopano mʼmatumba a vinyo akale. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa zikopazo, vinyo adzatayika ndipo zikopa za vinyozo zidzawonongeka.
Og ingen kommer ung Vin på gammle Læderflasker; ellers sprænger den unge Vin Læderflaskerne, og den spildes, og Læderflaskerne ødelægges.
38 Ayi, vinyo watsopano ayenera kuthiridwa mʼmatumba a vinyo azikopa zatsopano.
Men man skal komme ung Vin på nye Læderflasker, så blive de begge bevarede.
39 Ndipo palibe amene atamwa vinyo wakale amafuna watsopano, pakuti amati, ‘Wakale ndi okoma.’”
Og ingen, som har drukket den gamle, vil have den unge; thi han siger: Den gamle er god."