< Luka 5 >

1 Tsiku lina Yesu anayima mʼmbali mwa nyanja ya Genesareti, gulu la anthu litamuzungulira likumvetsera mawu a Mulungu.
Y anacó que abillando a sueti en plastañías somia junelar a varda de Debél, sinaba ó á la cunara de la pani de Genesareth.
2 Iye anaona mabwato awiri ali mʼmphepete mwa nyanja, asodzi amene ankachapa makhoka awo atawasiya pamenepo.
Y dicó dui berdés, sos sinaban á la cunara de la pani: y os machadores habian ardiñado en chiquen, y muchobelaban desqueres redes.
3 Iye analowa mʼbwato limodzi limene linali la Simoni, ndi kumupempha kuti alikankhire mʼkati mwa nyanja pangʼono. Kenaka Iye anakhala pansi nayamba kuphunzitsa anthu ali mʼbwatomo.
Y chalando andré yeque de oconas berdés, sos sinaba de Simon, le mangó, que le guillase yeque fremi de la chiquen. Y sinando bestelado, bedaba á la sueti desde o berdo.
4 Atatha kuyankhula anati kwa Simoni, “Kankhirani kwa kuya ndipo muponye makhoka kuti mugwire nsomba.”
Y yescotria que acabó de chamuliar, penó á Simon: Chala butér andré, y chibela jires redes somia machorar.
5 Simoni anayankha kuti, “Ambuye, tagwira ntchito molimbika usiku wonse, koma sitinagwire kanthu. Koma pakuti mwatero, ndiponya makhoka.”
Y rudelando Simon, le penó: Duquendio, sari a rachi hemos sinado machorando, bi ustilar chichi: tami en tiri varda chibaré a red.
6 Atachita izi, anagwira nsomba zambiri kotero kuti makhoka awo anayamba kungʼambika.
Y pur tereláron querdi ocolo, ustiláron tan baró numero de maches, que se asparababa a red de junos.
7 Choncho anakodola anzawo a bwato linalo kuti abwere ndi kuwathandiza, ndipo anabwera nadzaza mabwato onse awiri mpaka kuyamba kumira.
Y quereláron simaches á os averes manuces sos sinaban andré o aver berdo, somia que abillasen á ayudarlos. Ocolas abilláron, y de tal beda pereláron os dui berdes, que casi chalaban abajines.
8 Simoni Petro ataona izi, anagwa pa mawondo a Yesu nati, “Chokani kwa ine Ambuye: Ine ndine munthu wochimwa!”
Y pur dicó Simon Pedro ocolo, se chibó á os pindrés de Jesus, penando: Erañó, chatucue de mangue, que sinelo manu choro.
9 Iye ndi anzake onse anadabwa ndi nsomba zimene anagwira,
Presas ó, y os sares sos sat ó sinaban, sináron atonitos de os butres maches, que terelaban ustilado:
10 chimodzimodzinso Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, anzake a Simoniyo. Kenaka Yesu anati kwa Simoni, “Musachite mantha; kuyambira tsopano ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
Yandiar matejo Santiago, y Juan, chabores del Zebedéo, sos sinaban candones de Simon: Y penó Jesus á Simon: Na darañeles: desde ocona chiros sinarás machador de manuces.
11 Kenaka anakokera mabwato awo ku mtunda, nasiya zonse namutsata Iye.
Y lliguerando os berdes á chiquen, mequeláron o saro, y le plastañáron.
12 Yesu ali ku mudzi wina, munthu amene anali ndi khate thupi lonse anabwera kwa Iye. Munthuyo ataona Yesu, anagwa chafufumimba ndipo anamupempha Iye kuti, “Ambuye, ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
Y anacó, que sinando andré yeque de ocolas fores, abilló manu perelalo de zarapia, y pur dicó á Jesus, se chibó mui por chiquen, y le mangó, penando: Erañó, si camelas, astisarelas chibarme lacho.
13 Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo. Iye anati, “Ine ndikufuna, yeretsedwa!” Ndipo nthawi yomweyo khate lake linachoka.
Y ó bucharando la baste le pajabó, penando: Camelo: sinele limpio. Y yescotria chaló de ó a zarapia.
14 Kenaka Yesu anamulamula kuti, “Usawuze wina aliyense, koma pita, kadzionetse kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose anakulamulirani za kuyeretsedwa kwanu monga umboni kwa iwo.”
Y le penó, que na lo penase á cayque: Tami chatucue, le penó, y muestrate al erajai, y díñela por tiri limpieza ma mandó Moyses, en machiria á junos.
15 Koma mbiri yake inafalikirabe kwambiri kotero kuti magulu a anthu anabwera kudzamvetsera ndi kuti achiritsidwe ku matenda awo.
Y trincho butér se voltisaraba desquero chimusolano: y abillaba en plastañias a sueti somia junelarle, y somia que nicobelase de junos desqueres merdipénes.
16 Koma Yesu nthawi zambiri ankachoka kupita ku malo a yekha kukapemphera.
Tami ó se chaló al desierto á manguelar á Un-debél.
17 Tsiku lina pamene ankaphunzitsa, Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, amene anachokera ku midzi yonse ya Galileya ndi ku Yudeya ndi Yerusalemu, anakhala pansi pomwepo. Ndipo mphamvu ya Ambuye inalipo yakuti Iye achiritse odwala.
Y anacó, que yeque chibes ó sinaba bestelado bedando. Y sinaban tambien bestelados oté yeques Phariseyes, y Chandés de la Eschastra, sos abilláron de sares os gaues e Galiléa, y de Judéa, y de Jerusalém: y a sila e Erañoro sinaba randiñando somia chibarlos lacho.
18 Amuna ena anabwera atanyamula munthu wofa ziwalo pa mphasa ndipo anayesa kumulowetsa mʼnyumba kuti amugoneke pamaso pa Yesu.
Y abilláron yeques manuces sos ligueraban opré cheripen yeque manu, sos sinaba paralitico, y le camelaban sinchitar andré, y chibarle anglal de ó.
19 Atalephera kupeza njira yochitira zimenezi chifukwa cha gulu la anthu, anakwera naye pa denga ali pa mphasa pomwepo ndi kumutsitsira mʼkati pakati pa gulu la anthu, patsogolo penipeni pa Yesu.
Tami na rachelando por anduque astisar sinchitarlo por la plastañi e sueti, costunáron opré o techo y pre ó tejado le deschindaron sat a cheripen, sinchitandolo en medio anglal de Jesus.
20 Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati, “Mnzanga, machimo ako akhululukidwa.”
Y pur dicó a fé de junos, penó: Manu, ertinados á tucue sinelan os grecos.
21 Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anayamba kuganiza mwa iwo okha kuti, “Kodi munthu uyu ndi ndani amene ayankhula zamwano? Kodi ndani amene angakhululukire machimo kupatula Mulungu?”
Y os Libanes, y Phariseyes se chibaron á penchabar, y penar: ¿Coin sinela ocona sos chamulia solajais: Coin astisarela ertinar grecos, sino Un-debél colcoro?
22 Yesu anadziwa zomwe iwo amaganiza ndipo anafunsa kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukuganiza zimenezi mʼmitima mwanu?
Y Jesus, sasta jabilló as suncais de junos, les rudeló, y penó: ¿Qué penchabais andré jirés carlochines?
23 Kodi chapafupi ndi chiti: kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kunena kuti, ‘Nyamuka ndipo yenda?’”
¿Qué sinela mas astis, penar: Ertinados á tucue sinelan os grecos; o penar: Costunate y pirela?
24 Koma kuti inu mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo, Iye anati kwa munthu wofa ziwaloyo, “Ine ndikuwuza iwe kuti, ‘Imirira, nyamula mphasa ndipo uzipita kwanu.’”
Pues somia que chaneleis, que o Chaboro e manu terela sila opré la pu de ertinar grecos, penó al Paralitico: A tucue penelo, costunatucue, ustila tun cheripen, y chatucue á tun quer.
25 Nthawi yomweyo anayimirira patsogolo pawo, nanyamula mphasa yake ndipo anapita kwawo akuyamika Mulungu.
Y se costunó yescotria anglal de as aquias de junos, y ustiló a cheripen, andré que sinaba: y se chaló a desquero quer, diñando chimusolano á Debél.
26 Aliyense anadabwa ndi kuchita mantha ndipo anayamika Mulungu. Iwo anadabwa kwambiri ndipo anati, “Lero taona zinthu zosayiwalika.”
Y sináron os sares pasmados, y majarificaban á Debél: y perelales de dal, penaban: Achibes hemos dicado zibos.
27 Zitatha izi, Yesu anachoka ndipo anaona wolandira msonkho dzina lake Levi atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anati kwa iye, “Nditsate Ine.”
Y despues de ocono chaló abrí, y dicó a yeque Publicano araquerado Levi, sos sinaba bestelado á la quejeña, y le penó: Plastañamangue.
28 Ndipo Levi anayimirira, nasiya zonse ndi kumutsata Iye.
Y ardiñelandose mecó sarias desquerias buchias: y le plastañó.
29 Kenaka Levi anakonzera Yesu phwando lalikulu ku nyumba yake ndipo gulu lalikulu la amisonkho ndi ena ankadya naye pamodzi.
Y le queró Levi yeque jachipen bari andré desquero quer, y abilló oté yeque plastañi bari de Publicanes, y de averes, sos sinaban bestelados sat junos á la mensalle.
30 Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amene anali a gulu lawo anadandaula kwa ophunzira ake, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukudya ndi kumwa pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”
Tami os Phariseyes, y os Libanes sinaban ululés, y penaban á os discipules de Jesus: ¿Presás jamais, y piyais sat os Publicanes y chores?
31 Yesu anawayankha kuti, “Amene sakudwala safuna singʼanga, koma odwala.
Y Jesus les rudeló, y penó: A ocolas sos sinelan mistos, salamito no les sinela necesario, sino á ocolas sos sinelan merdés.
32 Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa kuti atembenuke mtima.”
Na he abillado á araquerar á os laches á penitencia, sino á os chores.
33 Iwo anati kwa Iye, “Ophunzira a Yohane amasala kudya ndi kupemphera kawirikawiri, monganso ophunzira a Afarisi, koma anu amangodya ndi kumwa.”
Y ocolas le penáron: ¿Presas os discipules de Juan ayunan tanto, y manguelan, y tambien os es Phariseyes, y os de tucue jamelan y piyelan?
34 Yesu anawayankha kuti, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya pamene mkwati ali pakati pawo?
O penó á junos: ¿Por baji astisarelas querelar, que os chabores e Rom ayunen, o chiros que o Rom sinela sat junos?
35 Koma nthawi ikubwera pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo. Masiku amenewo adzasala kudya.”
Tami abillarán chibeses, andré que o Rom les sinará nicabado, y ayunarán andré ocolas chibeses.
36 Iye anawawuza fanizo ili: “Palibe amene amangʼamba chigamba kuchokera pa chovala chatsopano ndi kuchisokerera pa chakale. Ngati atatero, ndiye kuti adzangʼamba chovala chatsopanocho, ndipo chigamba chochokera pa chovala chatsopano chija sichidzagwirizana ndi chakale.
Y les penó yeque semejanza: Na chibela cayque remiendo de chan nebó andré plata puri: presas de aver beda o nebó parabela al puro: y ademas na nichobela mistos remiendo nebó sat o puro.
37 Ndipo palibe amene amakhuthulira vinyo watsopano mʼmatumba a vinyo akale. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa zikopazo, vinyo adzatayika ndipo zikopa za vinyozo zidzawonongeka.
Y cayque chibela mol nebó andré pigotes purés, presas de aver beda o mol nebó parabelará á os pigotes, o mol se butanará, y se chibelarán a najabar os pigotes.
38 Ayi, vinyo watsopano ayenera kuthiridwa mʼmatumba a vinyo azikopa zatsopano.
Tami jomte chibar o mol nebó andré pigotes nebés, y o yeque y o aver se conserva.
39 Ndipo palibe amene atamwa vinyo wakale amafuna watsopano, pakuti amati, ‘Wakale ndi okoma.’”
Y cayque sos piyela o puro camela yescotria o nebó, presas penela: fetér sinela o puro.

< Luka 5 >