< Luka 4 >
1 Yesu, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anachoka ku mtsinje wa Yorodani ndipo anatsogozedwa ndi Mzimu Woyerayo kupita ku chipululu,
Then Jesus, full of the Holy Spirit, returned from the Jordan, and was led about by the Spirit in the Desert for forty days,
2 kumene anayesedwa ndi mdierekezi masiku makumi anayi. Sanadye kena kalikonse pa masiku amenewo, ndipo pa mapeto pake anamva njala.
tempted all the while by the Devil. During those days He ate nothing, and at the close of them He suffered from hunger.
3 Mdierekezi anati kwa Iye, “Ngati ndiwe Mwana wa Mulungu, uza mwala uwu kuti usanduke buledi.”
Then the Devil said to Him, "If you are God's Son, tell this stone to become bread."
4 Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha.’”
"It is written," replied Jesus, "'It is not on bread alone that a man shall live.'"
5 Mdierekezi anamutengera Iye pamalo aatali ndipo mʼkamphindi namuonetsa maufumu onse a dziko lapansi.
The Devil next led Him up and caused Him to see at a glance all the kingdoms of the world.
6 Ndipo anati kwa Iye, “Ndidzakupatsani ulamuliro ndi ulemerero wawo; pakuti anandipatsa ine, ndipo ndingathe kupereka kwa aliyense amene ndikufuna.
And the Devil said to Him, "To you will I give all this authority and this splendour; for it has been handed over to me, and on whomsoever I will I bestow it.
7 Ngati mutandilambira, zonsezi zidzakhala zanu.”
If therefore you do homage to me, it shall all be yours.'
8 Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Pembedza Yehova Mulungu wako ndi kumutumikira Iye yekha.’”
Jesus answered him, "It is written, 'To the Lord thy God thou shalt do homage, and to Him alone shalt thou render worship.'"
9 Mdierekezi anapita naye ku Yerusalemu namuyimiritsa pamwamba penipeni pa Nyumba ya Mulungu. Ndipo anati, “Ngati ndinu Mwana wa Mulungu dziponyeni nokha pansi kuchokera pano.
Then he brought Him to Jerusalem and caused Him to stand on the roof of the Temple, and said to Him, "If you are God's Son, throw yourself down from here; for it is written,
10 Pakuti kwalembedwa, “Adzalamulira angelo ake za iwe kuti akutchinjirize mosamala;
'He will give orders to His angels concerning thee, to guard thee safely;'
11 ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.”
and 'On their hands they shall bear thee up, Lest at any moment thou shouldst strike thy foot against a stone.'"
12 Yesu anayankha kuti, “Mawu akuti, ‘Musamuyese Yehova Mulungu wanu.’”
The reply of Jesus was, "It is said, 'Thou shalt not put the Lord they God to the proof.'"
13 Mdierekezi atamaliza mayesero awa onse, anamusiya Iye kufikira atapeza mpata wina.
So the Devil, having fully tried every kind of temptation on Him, left Him for a time.
14 Yesu anabwerera ku Galileya mu mphamvu ya Mzimu Woyera, ndipo mbiri yake inafalikira ku madera onse a ku midzi.
Then Jesus returned in the Spirit's power to Galilee; and His fame spread through all the adjacent districts.
15 Iye ankaphunzitsa mʼmasunagoge awo, ndipo aliyense ankamulemekeza.
And He proceeded to teach in their synagogues, winning praise from all.
16 Iye anapita ku Nazareti, kumene anakulira, ndipo pa tsiku la Sabata anakalowa mʼsunagoge, monga mwa chikhalidwe chake. Ndipo anayimirira kuti awerenge malemba.
He came to Nazareth also, where He had been brought up; and, as was His custom, He went to the synagogue on the Sabbath, and stood up to read.
17 Anamupatsa buku la mneneri Yesaya. Atalitsekula, anapeza pamalo pamene panalembedwa kuti,
And there was handed to Him the book of the Prophet Isaiah, and, opening the book, He found the place where it was written,
18 “Mzimu wa Ambuye ali pa Ine; chifukwa wandidzoza kuti ndilalikire Uthenga Wabwino kwa osauka. Wandituma kuti ndilalikire kwa a mʼndende kuti amasulidwe ndi kwa osaona kuti apenyenso, kumasulidwa kwa osautsidwa,
"The Spirit of the Lord is upon me, because He has anointed me to proclaim Good News to the poor; He has sent me to announce release to the prisoners of war and recovery of sight to the blind: to send away free those whom tyranny has crushed,
19 ndi kulalikira za nthawi imene Ambuye adzakomere mtima anthu awo.”
to proclaim the year of acceptance with the Lord."
20 Kenaka Iye anatseka bukulo, nalibwezera kwa wotumikira ndipo anakakhala pansi. Maso a aliyense mʼsunagogemo anali pa Iye,
And rolling up the book, He returned it to the attendant, and sat down--to speak. And the eyes of all in the synagogue were fixed on Him.
21 ndipo anawawuza kuti, “Lero malemba awa akwaniritsidwa mmene mwamveramu.”
Then He proceeded to say to them, "To-day is this Scripture fulfilled in your hearing."
22 Onse anayankhula zabwino za Iye ndipo anadabwa ndi mawu ogwira moyo amene anatuluka mʼkamwa mwake. Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu si mwana wa Yosefe?”
And they all spoke well of Him, wondering at the sweet words of kindness which fell from His lips, while they asked one another, "Is not this Joseph's son?"
23 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, mudzandiwuza mwambi uwu: Singʼanga, dzichiritse wekha! Chitanso mʼmudzi wa kwanu kuno zimene ife tamva kuti Iwe unazichita ku Kaperenawo.”
"Doubtless," said He, "you will quote to me the proverb, 'Physician, cure yourself: all that we hear that you have done at Capernaum, do here also in your native place.'"
24 Iye anapitiriza kuti, “Zoonadi, ndikukuwuzani kuti palibe mneneri amene amavomerezedwa ku mudzi kwawo.
"I tell you in solemn truth," He added, "that no Prophet is welcomed among his own people.
25 Ine ndikukutsimikizirani kunali amayi ambiri amasiye mu Israeli mʼnthawi ya Eliya, kumwamba kutatsekedwa kwa zaka zitatu ndi theka ndipo kunali njala yayikulu mʼdziko lonselo.
But I tell you in truth that there was many a widow in Israel in the time of Elijah, when there was no rain for three years and six months and there came a severe famine over all the land;
26 Komabe Eliya sanatumidwe kwa mmodzi mwa iwo, koma kwa mkazi wamasiye wa ku Zerefati ku chigawo cha Sidoni.
and yet to not one of them was Elijah sent: he was only sent to a widow at Zarephath in the Sidonian country.
27 Ndipo kunali akhate ambiri ku Israeli mʼnthawi ya mneneri Elisa, koma panalibe mmodzi mwa iwo anachiritsidwa kupatula Naamani wa ku Siriya.”
And there was also many a leper in Israel in the time of the Prophet Elisha, and yet not one of them was cleansed, but Naaman the Syrian was."
28 Anthu onse mʼsunagogemo anapsa mtima atamva izi.
Then all in the synagogue, while listening to these words, were filled with fury.
29 Anayimirira namutulutsira kunja kwa mzindawo, ndipo anamutengera pamwamba pa phiri pamene mzindawo unamangidwapo, ndi cholinga chakuti amuponyere ku phompho.
They rose, hurried Him outside the town, and brought Him to the brow of the hill on which their town was built, to throw Him down the cliff;
30 Koma Iye anangoyenda pakati pa gulu la anthulo nachokapo.
but He passed through the midst of them and went His way.
31 Kenaka Iye anapita ku Kaperenawo, mudzi wa ku Galileya, ndipo pa Sabata anayamba kuphunzitsa anthu.
So He came down to Capernaum, a town in Galilee, where He frequently taught the people on the Sabbath days.
32 Iwo anadabwa ndi chiphunzitso chake chifukwa uthenga wake unali ndi ulamuliro.
And they were greatly impressed by His teaching, because He spoke with the language of authority.
33 Mʼsunagogemo munali munthu wogwidwa ndi mzimu woyipa. Iye analira ndi mawu akulu, akuti
But in the synagogue there was a man possessed by the spirit of a foul demon. In a loud voice he cried out,
34 “Aa! Kodi mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
"Ha! Jesus the Nazarene, what have you to do with us? I know who you are--God's Holy One!"
35 Yesu anachidzudzula kwambiri nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye.” Chiwandacho chinamugwetsa munthuyo pansi pamaso pa onse ndipo chinatuluka wosamupweteka.
But Jesus rebuked the demon. "Silence!" He exclaimed; "come out of him." Upon this, the demon hurled the man into the midst of them, and came out of him without doing him any harm.
36 Anthu onse anadabwa ndipo anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi chiphunzitso ichi ndi chotani? Ndi ulamuliro ndi mphamvu Iye akulamulira mizimu yoyipa ndipo ikutuluka!”
All were astonished and awe-struck; and they asked one another, "What sort of language is this? For with authority and real power He gives orders to the foul spirits and they come out."
37 Ndipo mbiri yake inafalikira madera onse ozungulira.
And the talk about Him spread into every part of the neighbouring country.
38 Yesu anatuluka mʼsunagoge ndipo anapita kwa Simoni. Tsopano mpongozi wake wa Simoni amadwala malungo akulu, ndipo anamupempha Yesu kuti amuthandize.
Now when He rose and left the synagogue He went to Simon's house. Simon's mother-in-law was suffering from an acute attack of fever; and they consulted Him about her.
39 Ndipo anawerama nadzudzula malungowo ndipo anamusiya. Anadzuka nthawi yomweyo nayamba kuwatumikira.
Then standing over her He rebuked the fever, and it left her; and she at once rose and waited on them.
40 Pamene dzuwa linkalowa, anthu anabweretsa kwa Yesu onse amene anali ndi matenda osiyanasiyana, ndipo atasanjika manja ake pa aliyense, anachiritsidwa.
At sunset all who had friends suffering from any illness brought them to Him, and He laid His hands on them all, one by one, and cured them.
41 Komanso ziwanda zinkatuluka mwa anthu ambiri, zikufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!” Koma Iye anazidzudzula ndipo sanazilole kuyankhula chifukwa zimadziwa kuti Iye ndi Khristu.
Demons also came out of many, loudly calling out, "You are the Son of God." But He rebuked them and forbad them to speak, because they knew Him to be the Christ.
42 Kutacha, Yesu anapita ku malo a yekha. Anthu ankamufunafuna Iye ndipo pamene anafika kumene anali, anthuwo anayesetsa kumuletsa kuti asawachokere.
Next morning, at daybreak, He left the town and went away to a solitary place; but the people flocked out to find Him, and, coming to the place where He was, they endeavoured to detain Him that He might not leave them.
43 Koma Iye anati, “Ine ndikuyenera kulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ku mizinda inanso chifukwa ichi ndi chimene ananditumira.”
But He said to them, "I have to tell the Good News of the Kingdom of God to the other towns also, because for this purpose I was sent."
44 Ndipo Iye anapitirirabe kulalikira mʼmasunagoge a ku Yudeya.
And for some time He preached in the synagogues in Galilee.