< Luka 3 >

1 Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene.
В пятое же надесяте лето владычества Тивериа кесаря, обладающу Понтийскому Пилату Иудеею, и четвертовластвующу Галилеею Ироду, Филиппу же брату его четвертовластвующу Итуреею и Трахонитскою страною, и Лисанию Авилиниею четвертовластвующу,
2 Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu.
при архиереи Анне и Каиафе, бысть глаголгол Божий ко Иоанну Захариину сыну в пустыни.
3 Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo.
И прииде во всю страну Иорданскую, проповедая крещение покаяния во оставление грехов:
4 Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti: “Mawu a wofuwula mʼchipululu, konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.
якоже есть писано в книзе словес Исаии пророка, глаголюща: глас вопиющаго в пустыни: уготовайте путь Господень: правы творите стези Его:
5 Chigwa chilichonse chidzadzazidwa ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa, misewu yokhotakhota idzawongoledwa, ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.
всяка дебрь исполнится, и всяка гора и холм смирится: и будут стропотная в правая, и острии в пути гладки:
6 Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”
и узрит всяка плоть спасение Божие.
7 Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera?
Глаголаше же исходящым народом креститися от него: порождения ехиднова, кто сказа вам бежати от грядущаго гнева?
8 Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana.
Сотворите убо плоды достойны покаяния: и не начинайте глаголати в себе: отца имамы Авраама: глаголю бо вам, яко может Бог от камения сего воздвигнути чада Аврааму.
9 Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”
Уже бо и секира при корени древа лежит: всяко убо древо не творящее плода добра посекается и во огнь вметается.
10 Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”
И вопрошаху его народи, глаголюще: что убо сотворим?
11 Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”
Отвещав же глагола им: имеяй две ризе, да подаст неимущему: и имеяй брашна, такожде да творит.
12 Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”
Приидоша же и мытари креститися от него и реша к нему: учителю, что сотворим?
13 Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.”
Он же рече к ним: ничтоже более от повеленнаго вам творите.
14 Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?” Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”
Вопрошаху же его и воини, глаголюще: и мы что сотворим? И рече к ним: ни когоже обидите, ни оклеветавайте: и доволни будите оброки вашими.
15 Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu.
Чающым же людем, и помышляющым всем в сердцах своих о Иоанне, еда той есть Христос,
16 Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto.
отвещаваше Иоанн всем, глаголя: аз убо водою крещаю вы: грядет же Креплий мене, Емуже несмь достоин отрешити ремень сапогу Его: Той вы крестит Духом Святым и огнем:
17 Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.”
Емуже лопата в руку Его, и отребит гумно Свое, и соберет пшеницу в житницу Свою, плевы же сожжет огнем негасающим.
18 Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.
Многа же убо и ина утешая благовествоваша людем.
19 Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita,
Ирод же четвертовластник, обличаемь от него о Иродиаде жене брата своего, и о всех, яже сотвори злая Ирод,
20 Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.
приложи и сие над всеми, и затвори Иоанна в темнице.
21 Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka.
Бысть же егда крестишася вси людие, и Иисусу крещашуся и молящуся, отверзеся небо,
22 Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”
и сниде Дух Святый телесным образом, яко голубь, Нань: и глас с небесе бысть, глаголя: Ты еси Сын Мой Возлюбленный, о Тебе благоволих.
23 Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe, mwana wa Heli,
И той бе Иисус яко лет тридесять начиная, сый, яко мнимь, Сын Иосифов, Илиев,
24 mwana wa Matate, mwana wa Levi, mwana wa Meliki, mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe
Матфатов, Левиин, Мелхиин, Ианнаев, Иосифов,
25 mwana wa Matati, mwana wa Amosi, mwana wa Naomi, mwana wa Esli, mwana wa Nagai,
Маттафиев, Амосов, Наумов, Еслимов, Наггеов,
26 mwana wa Maati, mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni, mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda
Маафов, Маттафиев, Семеиев, Иосифов, Иудин,
27 mwana wa Yohanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli, mwana wa Neri,
Иоаннанов, Рисаев, Зоровавелев, Салафиилев, Нириев,
28 mwana wa Meliki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,
Мелхиев, Аддиев, Косамов, Елмодамов, Иров,
29 mwana wa Jose, mwana wa Eliezara, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,
Иосиев, Елиезеров, Иоримов, Матфатов, Левиин,
30 mwana wa Simeoni, mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,
Симеонов, Иудин, Иосифов, Ионанов, Елиакимов,
31 mwana wa Meleya, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natani, mwana wa Davide,
Мелеаев, Маинанов, Маттафаев, Нафанов, Давидов,
32 mwana wa Yese, mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi, mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,
Иессеов, Овидов, Воозов, Салмонов, Наассонов,
33 mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni, mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi, mwana wa Yuda,
Аминадавов, Арамов, Есромов, Фаресов, Иудин,
34 mwana wa Yakobo, mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,
Иаковль, Исааков, Авраамов, Фарин, Нахоров,
35 mwana wa Serugi, mwana wa Reu, mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi, mwana wa Sela,
Серухов, Рагавов, Фалеков, Еверов, Саланов,
36 mwana wa Kainane, mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,
Каинанов, Арфаксадов, Симов, Ноев, Ламехов,
37 mwana wa Metusela, mwana wa Enoki, mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli, mwana wa Kainane,
Мафусалев, Енохов, Иаредов, Малелеилов, Каинанов,
38 mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.
Еносов, Сифов, Адамов, Божий.

< Luka 3 >