< Luka 3 >
1 Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene.
Now in the fifteenth year of the reign of Tiberius Caesar, Pontius Pilate being governor of Judaea, and Herod tetrarch of Galilee, and his brother Philip tetrarch of Ituraea and of the region of Trachonitis, and Lysanias tetrarch of Abilene,
2 Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu.
when Annas and Caiaphas were high-priests, the word of God came to John, the son of Zachariah, in the wilderness.
3 Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo.
And he came into all the country about the Jordan, preaching the baptism of repentance for the remission of sins;
4 Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti: “Mawu a wofuwula mʼchipululu, konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.
as it is written in the book of the words of Isaiah the prophet: “The voice of one crying in the wilderness, Prepare the way of the Lord, make straight his paths!
5 Chigwa chilichonse chidzadzazidwa ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa, misewu yokhotakhota idzawongoledwa, ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.
Every valley shall be filled, and every mountain and hill shall be made low; and the crooked places shall be made straight, and the rough ways smooth;
6 Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”
and all flesh shall see the salvation of God.”
7 Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera?
He said therefore to the multitudes that came forth to be baptized by him, Brood of vipers, who warned you to flee from the coming wrath?
8 Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana.
Bring forth therefore fruits worthy of repentance; and begin not to say within yourselves, We have Abraham for our father; for I say to you, that God is able out of these stones to raise up children to Abraham.
9 Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”
And already also is the axe lying at the root of the trees; every tree therefore that beareth not good fruit is to be cut down, and cast into the fire.
10 Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”
And the multitudes asked him, saying, What then must we do?
11 Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”
He answered and said to them, He that hath two coats, let him impart to him that hath none; and he that hath food, let him do likewise.
12 Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”
And there came also publicans to be baptized, and said to him, Teacher, what must we do?
13 Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.”
And he said to them, Exact no more than hath been ordered you.
14 Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?” Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”
And soldiers also asked him, saying, And what must we do? And he said to them, Do violence to no one, accuse no one falsely, and be content with your wages.
15 Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu.
And while the people were in expectation, and all were considering in their hearts concerning John, whether he were the Christ,
16 Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto.
John answered and said to them all, I indeed baptize you with water; but he who is mightier than I is coming, the latchet of whose sandals I am not worthy to loose; he will baptize you in the Holy Spirit and in fire.
17 Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.”
His winnowing-shovel is in his hand to thoroughly cleanse his threshing-floor, and gather the wheat into his garner; but the chaff he will burn up with unquenchable fire.
18 Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.
And giving many other exhortations he published the glad tidings to the people.
19 Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita,
But Herod the tetrarch, being reproved by him on account of Herodias the wife of his brother, and on account of all the evil deeds which Herod had done,
20 Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.
added this also to them all, that he shut up John in prison.
21 Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka.
And it came to pass, when all the people had been baptized, and Jesus also had been baptized, and was praying, that the heaven was opened,
22 Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”
and the Holy Spirit descended upon him in a bodily shape as a dove; and a voice came from heaven: “Thou art my beloved Son; with thee I am well pleased.”
23 Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe, mwana wa Heli,
And Jesus himself was, when he began, about thirty years of age, being, as was supposed, the son of Joseph, who was the son of Heli,
24 mwana wa Matate, mwana wa Levi, mwana wa Meliki, mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe
who was the son of Matthath, who was the son of Levi, who was the son of Melchi, who was the son of Jannai, who was the son of Joseph,
25 mwana wa Matati, mwana wa Amosi, mwana wa Naomi, mwana wa Esli, mwana wa Nagai,
who was the son of Mattathias, who was the son of Amos, who was the son of Nahum, who was the son of Esli, who was the son of Naggai,
26 mwana wa Maati, mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni, mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda
who was the son of Maath, who was the son of Mattathias, who was the son of Shimei, who was the son of Josech, who was the son of Joda,
27 mwana wa Yohanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli, mwana wa Neri,
who was the son of Joanan, who was the son of Rhesa, who was the son of Zerubbabel, who was the son of Shealtiel, who was the son of Neri,
28 mwana wa Meliki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,
who was the son of Melchi, who was the son of Addi, who was the son of Kosam, who was the son of Elmadam, who was the son of Er,
29 mwana wa Jose, mwana wa Eliezara, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,
who was the son of Jesus, who was the son of Eliezer, who was the son of Jorim, who was the son of Matthath, who was the son of Levi,
30 mwana wa Simeoni, mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,
who was the son of Simeon, who was the son of Judah, who was the son of Joseph, who was the son of Jonam, who was the son of Eliakim,
31 mwana wa Meleya, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natani, mwana wa Davide,
who was the son of Melea, who was the son of Menna, who was the son of Mattatha, who was the son of Nathan, who was the son of David,
32 mwana wa Yese, mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi, mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,
who was the son of Jesse, who was the son of Obed, who was the son of Boaz, who was the son of Salma, who was the son of Nahshon,
33 mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni, mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi, mwana wa Yuda,
who was the son of Amminadab, who was the son of Admin, who was the son of Arni, who was the son of Hezron, who was the son of Pharez, who was the son of Judah,
34 mwana wa Yakobo, mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,
who was the son of Jacob, who was the son of Isaac, who was the son of Abraham, who was the son of Terah, who was the son of Nahor,
35 mwana wa Serugi, mwana wa Reu, mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi, mwana wa Sela,
who was the son of Serug, who was the son of Reu, who was the son of Peleg, who was the son of Eber, who was the son of Shelah,
36 mwana wa Kainane, mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,
who was the son of Cainan, who was the son of Arphaxad, who was the son of Shem, who was the son of Noah, who was the son of Lamech,
37 mwana wa Metusela, mwana wa Enoki, mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli, mwana wa Kainane,
who was the son of Methuselah, who was the son of Enoch, who was the son of Jared, who was the son of Mahalaleel, who was the son of Cainan,
38 mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.
who was the son of Enos, who was the son of Seth, who was the son of Adam, who was the son of God.