< Luka 24 >

1 Pa tsiku loyamba la Sabata, mmamawa kwambiri, amayi anatenga zonunkhira napita ku manda.
Mais, le premier jour de la semaine, de grand matin, elles se rendirent au sépulcre, avec les aromates qu’elles avaient préparés.
2 Anaona mwala wa pa manda utagubuduzika
Elles virent que la pierre avait été roulée loin du sépulcre;
3 ndipo atalowamo sanapeze mtembo wa Ambuye Yesu.
et, étant entrées, elles ne trouvèrent pas le corps du Seigneur Jésus.
4 Pamene iwo ankadabwa za zimenezi, mwadzidzidzi, amuna awiri ovala zovala zonyezimira kwambiri anayimirira pambali pawo.
Tandis qu’elles étaient remplies d’anxiété à ce sujet, voici que deux hommes, vêtus de robes resplendissantes, parurent debout auprès d’elles.
5 Ndi mantha, amayiwo anaweramitsa nkhope zawo pansi, koma amunawo anawawuza kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufuna wamoyo pakati pa akufa?
Comme, dans leur épouvante, elles inclinaient le visage vers la terre, ils leur dirent: « Pourquoi cherchez-vous parmi les morts celui qui est vivant?
6 Iye sali muno ayi. Wauka! Kumbukirani zimene anakuwuzani pamene anali nanu ku Galileya:
Il n’est point ici, mais il est ressuscité. Souvenez-vous de ce qu’il vous a dit, lorsqu’il était encore en Galilée:
7 ‘Mwana wa Munthu ayenera kuperekedwa mʼmanja mwa anthu ochimwa, napachikidwa ndipo tsiku lachitatu adzaukitsidwanso.’”
Il faut que le Fils de l’homme soit livré entre les mains des pécheurs, qu’il soit crucifié, et qu’il ressuscite le troisième jour. »
8 Ndipo anakumbukira mawu ake.
Elles se ressouvinrent alors des paroles de Jésus,
9 Atabwerera kuchokera ku mandako, anafotokoza zinthu zonse kwa khumi ndi mmodziwo ndi kwa ena onse.
et, à leur retour du sépulcre, elles rapportèrent toutes ces choses aux Onze et à tous les autres.
10 Amayi anali Mariya Magadalena, Yohana, Mariya amayi a Yakobo, ndi ena anali nawo amene anawuza atumwi.
Celles qui dirent ces choses aux Apôtres étaient Marie-Madeleine, Jeanne, Marie, mère de Jacques, et leurs autres compagnes.
11 Koma iwo sanawakhulupirire amayiwa, chifukwa mawu awo amaoneka kwa iwo ngati opanda nzeru.
Mais ils regardèrent leurs discours comme vain racontage, et ils ne crurent pas ces femmes.
12 Komabe Petro anayimirira ndi kuthamangira ku manda. Atasuzumira, anaona nsalu zimene anamukulungira zija zili pa zokha, ndipo iye anachoka, akudabwa ndi zimene zinachitikazo.
Toutefois Pierre se leva et courut au sépulcre; et, s’étant penché, il ne vit que les linges par terre, et il s’en alla chez lui, dans l’admiration de ce qui était arrivé.
13 Ndipo tsiku lomwelo, awiri a iwo ankapita ku mudzi wotchedwa Emau, pafupifupi makilomita khumi ndi imodzi kuchokera ku Yerusalemu.
Or, ce même jour, deux disciples étaient en route vers un village nommé Emmaüs, distant de Jérusalem de soixante stades,
14 Iwo ankayankhulana za zonse zimene zinachitikazo.
et ils s’entretenaient de tous ces événements.
15 Pamenepo Yesu mwini wake anabwera ndi kuyenda nawo pamodzi;
Pendant qu’ils discouraient, échangeant leurs pensées, Jésus lui-même les joignit et fit route avec eux;
16 koma iwo sanamuzindikire.
mais leurs yeux étaient retenus de sorte qu’ils ne le reconnaissaient pas.
17 Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukukambirana zotani mʼnjira muno?” Iwo anayima ndi nkhope zakugwa.
Il leur dit: « De quoi vous entretenez-vous ainsi en marchant, que vous soyez tout tristes? »
18 Mmodzi wa iwo wotchedwa Kaliyopa anamufunsa kuti, “Kodi ndiwe wekha wokhala mu Yerusalemu amene sukudziwa zinthu zimene zachitika mʼmasiku awa?”
L’un d’eux, nommé Cléophas, lui répondit: « Tu es bien le seul étranger venu à Jérusalem, qui ne sache pas les choses qui y sont arrivées ces jours-ci? —
19 Iye anafunsa kuti, “Zinthu zotani?” Iwo anayankha nati, “Za Yesu wa ku Nazareti, Iye anali mneneri, wamphamvu mʼmawu ndi mu zochita pamaso pa Mulungu ndi anthu onse.
Quelles choses? « leur dit-il. Ils répondirent: « Les faits concernant Jésus de Nazareth, qui était un prophète puissant en œuvres et en parole devant Dieu et devant tout le peuple:
20 Akulu a ansembe ndi oweruza anamupereka Iye kuti aphedwe, ndipo anamupachika Iye;
comment les Princes des prêtres et nos magistrats l’ont livré pour être condamné à mort, et l’ont crucifié.
21 koma ife tinkayembekezera kuti Iye ndiye amene akanawombola Israeli. Ndipo kuwonjeza apo, lero ndi tsiku lachitatu chichitikireni izi.
Quant à nous, nous espérions que ce serait lui qui délivrerait Israël; mais, avec tout cela, c’est aujourd’hui le troisième jour que ces choses sont arrivées.
22 Kuwonjezanso apo, ena mwa amayi athu atidabwitsa ife. Iwo anapita ku manda mmamawa
À la vérité, quelques-unes des femmes qui sont avec nous, nous ont fort étonnés: étant allées avant le jour au sépulcre,
23 koma sanakapeze mtembo wake. Iwo anabwera ndi kudzatiwuza ife kuti anaona masomphenya a angelo amene anati Yesu ali moyo.
et n’ayant pas trouvé son corps, elles sont venues dire que des anges leur ont apparu et ont annoncé qu’il est vivant.
24 Kenaka ena mwa anzathu anapita ku manda ndipo anakapeza monga momwe amayiwo ananenera, koma Iye sanamuone.”
Quelques-uns des nôtres sont allés au sépulcre, et ont trouvé toutes choses comme les femmes l’avaient dit; mais lui, ils ne l’ont point vu. »
25 Iye anawawuza kuti, “Inu ndinu anthu opusa, osafuna kukhulupirira msanga zonse zimene aneneri ananena!
Alors Jésus leur dit: « Ô hommes sans intelligence, et dont le cœur est lent à croire tout ce qu’ont dit les Prophètes!
26 Kodi Khristu sanayenera kumva zowawa izi ndipo kenaka ndi kulowa mu ulemerero wake?”
Ne fallait-il pas que le Christ souffrit toutes ces choses pour entrer dans sa gloire? »
27 Ndipo kuyambira ndi Mose ndi aneneri onse Iye anawafotokozera zimene zinalembedwa mʼmalemba wonse zokhudzana ndi Iye mwini.
Puis, commençant par Moïse, et parcourant tous les prophètes, il leur expliqua, dans toutes les Écritures, ce qui le concernait.
28 Atayandikira mudzi omwe amapitako, Yesu anachita ngati akupitirira.
Lorsqu’ils se trouvèrent près du village où ils allaient, lui fit semblant d’aller plus loin.
29 Koma iwo anamupempha Iye kwambiri kuti, “Mukhale ndi ife, popeza kwatsala pangʼono kuda, ndipo dzuwa lili pafupi kulowa.” Ndipo Iye anapita kukakhala nawo.
Mais ils le pressèrent, en disant: « Reste avec nous, car il se fait tard, et déjà le jour baisse. « Et il entra pour rester avec eux.
30 Iye ali pa tebulo pamodzi nawo, anatenga buledi ndipo anayamika, nanyema nayamba kuwagawira.
Or, pendant qu’il était à table avec eux, il prit le pain, prononça une bénédiction, puis le rompit, et le leur donna.
31 Kenaka maso awo anatsekuka ndipo anamuzindikira Iye, ndipo anachoka pakati pawo.
Alors leurs yeux s’ouvrirent, et ils le reconnurent; mais lui devint invisible à leurs yeux.
32 Iwo anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi mitima yathu sinali kutentha mʼkati mwathu pamene Iye ankayankhulana nafe pa njira ndi mmene anatitsekulira malemba?”
Et ils se dirent l’un à l’autre: « N’est-il pas vrai que notre cœur était tout brûlant au dedans de nous, lorsqu’il nous parlait en chemin, et qu’il nous expliquait les Ecritures? »
33 Nthawi yomweyo iwo anayimirira ndi kubwerera ku Yerusalemu. Iwo anapeza khumi ndi mmodziwo ndi ena anali nawo nasonkhana pamodzi
Se levant à l’heure même, ils retournèrent à Jérusalem; où ils trouvèrent réunis les Onze et leurs compagnons,
34 ndipo anati, “Ndi zoonadi! Ambuye auka ndipo anaonekera kwa Simoni.”
qui disaient: « Le Seigneur est vraiment ressuscité, et il est apparu à Simon. »
35 Kenaka awiriwo anawawuza zimene zinachitika pa njira, ndi mmene iwo anamudziwira Yesu, Iye atanyema buledi.
Eux-mêmes, à leur tour, racontèrent ce qui leur était arrivé en chemin, et comment ils l’avaient reconnu à la fraction du pain.
36 Akufotokoza zimenezi, Yesu mwini wake anayimirira pakati pawo ndipo anati, “Mukhale ndi mtendere.”
Pendant qu’ils s’entretenaient ainsi, Jésus se présenta au milieu d’eux, et leur dit: « La paix soit avec vous! c’est moi, ne craignez point. »
37 Koma chifukwa choti anathedwa nzeru ndi kuchita mantha, ankaganiza kuti akuona mzukwa.
Saisis de stupeur et d’effroi, ils pensaient voir un esprit.
38 Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuvutika? Nʼchifukwa chiyani mukukayika mu mtima mwanu?
Mais il leur dit: « Pourquoi vous troublez-vous, et pourquoi des doutes s’élèvent-ils dans vos cœurs?
39 Taonani manja anga ndi mapazi anga. Ine ndine amene! Khudzeni kuti muone. Mzukwa ulibe mnofu ndi mafupa monga mukuonera ndili nazo.”
Voyez mes mains et mes pieds; c’est bien moi. Touchez-moi, et considérez qu’un esprit n’a ni chair ni os, comme vous voyez que j’en ai. »
40 Iye atanena izi anawaonetsa manja ake ndi mapazi ake.
Ayant ainsi parlé, il leur montra ses mains et ses pieds.
41 Ndipo pamene iwo samakhulupirirabe, chifukwa cha chimwemwe ndi kudabwa, Iye anawafunsa kuti, “Kodi muli ndi chakudya chilichonse pano?”
Comme dans leur joie, ils hésitaient encore à croire, et ne revenaient pas de leur étonnement, il leur dit: « Avez-vous ici quelque chose à manger? »
42 Iwo anamupatsa Iye kachidutswa ka nsomba yophika.
Ils lui présentèrent un morceau de poisson rôti et un rayon de miel.
43 Iye anakatenga ndi kukadya iwo akuona.
Il les prit, et en mangea devant eux.
44 Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene ndinakuwuzani pamene ndinali nanu: chilichonse chiyenera kukwaniritsidwa chimene chinalembedwa cha Ine mʼbuku la Malamulo a Mose, Aneneri ndi Masalimo.”
Puis il leur dit: « C’est là ce que je vous disais, étant encore avec vous, qu’il fallait que tout ce qui est écrit de moi dans la loi de Moïse, dans les Prophètes et dans les Psaumes s’accomplît. »
45 Kenaka anawatsekula maganizo kuti azindikire Malemba.
Alors il leur ouvrit l’esprit, pour comprendre les Ecritures;
46 Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene zinalembedwa: Khristu adzazunzika ndipo adzauka kwa akufa tsiku lachitatu.
et il leur dit: « Ainsi il est écrit: et ainsi il fallait que le Christ souffrît, qu’il ressuscitât des morts le troisième jour,
47 Ndipo kutembenuka mtima ndi kukhululukidwa kwa machimo zidzalalikidwa mu dzina lake kwa anthu amitundu yonse kuyambira mu Yerusalemu.
et que le repentir et la rémission des péchés soient prêchés en son nom à toutes les nations, à commencer par Jérusalem.
48 Inu ndinu mboni za zimenezi.
Vous êtes témoins de ces choses.
49 Ine ndidzakutumizirani chimene Atate anga analonjeza. Koma khalani mu mzinda muno mpaka mutavekedwa mphamvu yochokera kumwamba.”
Moi, je vais envoyer sur vous le don promis par mon Père; et vous, restez dans la ville, jusqu’à ce que vous soyez revêtus d’une force d’en haut. »
50 Iye atawatengera kunja kwa mzindawo mpaka ku Betaniya, anakweza manja ake ndi kuwadalitsa.
Puis il les conduisit hors de la ville, jusque vers Béthanie, et, ayant levé les mains, il les bénit.
51 Iye akuwadalitsa, anawasiya ndipo anatengedwa kupita kumwamba.
Pendant qu’il les bénissait, il se sépara d’eux et il fut enlevé au ciel.
52 Pamenepo anamulambira Iye ndipo anabwerera ku Yerusalemu ndi chimwemwe chachikulu.
Pour eux, après l’avoir adoré, ils retournèrent à Jérusalem avec une grande joie.
53 Ndipo iwo anakhalabe ku Nyumba ya Mulungu, akulemekeza Mulungu.
Et ils étaient continuellement dans le temple, louant et bénissant Dieu. [Amen!]

< Luka 24 >