< Luka 23 >
1 Kenaka gulu lonse la anthuwo linayimirira ndi kumutengera kwa Pilato.
And the whole multitude of them rising up, led him to Pilate.
2 Ndipo iwo anayamba kumuneneza nati, “Ife tinapeza munthu uyu akusokoneza anthu a mtundu wathu ndipo amatsutsa zopereka msonkho kwa Kaisara komanso amati ndi Khristu, Mfumu.”
And they began to accuse him, saying: We have found this man perverting our nation, and forbidding to give tribute to Caesar, and saying that he is Christ the king.
3 Pamenepo Pilato anamufunsa Yesu kuti, “Kodi Iwe ndiwe Mfumu ya Ayuda?” Yesu anayankha kuti, “Mwatero ndinu.”
And Pilate asked him, saying: Art thou the king of the Jews? But he answering, said: Thou sayest it.
4 Kenaka Pilato anawawuza akulu a ansembe ndi gulu la anthu, “Ine sindikumupeza cholakwa munthuyu.”
And Pilate said to the chief priests and to the multitudes: I find no cause in this man.
5 Koma iwo analimbikirabe kuti, “Iyeyu amasokoneza anthu ku Yudeya konse ndi chiphunzitso chake, Iyeyu anayambira ku Galileya ndipo wayenda mtunda wonse mpaka kuno.”
But they were more earnest, saying: He stirreth up the people, teaching throughout all Judea, beginning from Galilee to this place.
6 Pakumva zimenezi, Pilato anafunsa ngati munthuyo ndi Mgalileya.
But Pilate hearing Galilee, asked if the man were of Galilee?
7 Iye atamva kuti Yesu anali pansi pa ulamuliro wa Herode, anamutumiza kwa Herodeyo, amene pa nthawi imeneyo analinso mu Yerusalemu.
And when he understood that he was of Herod’s jurisdiction, he sent him away to Herod, who was also himself at Jerusalem, in those days.
8 Herode ataona Yesu, anakondwa kwambiri, chifukwa kwa nthawi yayitali, ankafunitsitsa atamuona. Kuchokera pa zimene anamva za Iye, anayembekezera kuti achita zodabwitsa.
And Herod, seeing Jesus, was very glad; for he was desirous of a long time to see him, because he had heard many things of him; and he hoped to see some sign wrought by him.
9 Iye anamufunsa mafunso ambiri, koma Yesu sanayankhe.
And he questioned him in many words. But he answered him nothing.
10 Akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, anayimirira pamenepo ndi kumuneneza kwambiri.
And the chief priests and the scribes stood by, earnestly accusing him.
11 Pamenepo Herode ndi asilikali ake anamuseka ndi kumunyoza Iye. Atamuveka mkanjo wonyezimira, anamutumizanso kwa Pilato.
And Herod with his army set him at nought, and mocked him, putting on him a white garment, and sent him back to Pilate.
12 Tsiku limenelo, Herode ndi Pilato anakhala abwenzi. Zisanachitike izi anali adani.
And Herod and Pilate were made friends, that same day; for before they were enemies one to another.
13 Pilato anasonkhanitsa akulu a ansembe, oweruza ndi anthu,
And Pilate, calling together the chief priests, and the magistrates, and the people,
14 ndipo anawawuza kuti, “Munabweretsa munthuyu kwa ine ngati ndiye amawuza anthu kuti awukire. Ine ndamufunsa pamaso panu ndipo sindinapeze chomuyimbira mlandu.
Said to them: You have presented unto me this man, as one that perverteth the people; and behold I, having examined him before you, find no cause in this man, in those things wherein you accuse him.
15 Herodenso sanapeze chifukwa pakuti wamutumizanso kwa ife monga mmene mukuoneramu. Iyeyu sanachite chinthu chakuti aphedwe.
No, nor Herod neither. For I sent you to him, and behold, nothing worthy of death is done to him.
16 Nʼchifukwa chake, ine ndingomulanga, nʼkumumasula.”
I will chastise him therefore, and release him.
17 (Pa nthawi yachikondwerero cha Paska iye ankayenera kumasula munthu mmodzi).
Now of necessity he was to release unto them one upon the feast day.
18 Onse pamodzi anafuwula kuti, “Muchotseni munthuyu! Timasulireni Baraba!”
But the whole multitude together cried out, saying: Away with this man, and release unto us Barabbas:
19 (Baraba anaponyedwa mʼndende chifukwa choyambitsa chipolowe mu mzinda ndi kupha).
Who, for a certain sedition made in the city, and for a murder, was cast into prison.
20 Pofuna kumumasula Yesu, Pilato anawadandaulira iwo.
And Pilate again spoke to them, desiring to release Jesus.
21 Koma iwo anapitirirabe kufuwula kuti, “Mpachikeni! Mpachikeni!”
But they cried again, saying: Crucify him, crucify him.
22 Kachitatu anawafunsanso iwo kuti, “Chifukwa chiyani? Kodi munthu uyu wachita choyipa chanji? Ine sindinapeze cholakwa mwa Iye chakuti aphedwe choncho ndingomukwapula ndi kumumasula.”
And he said to them the third time: Why, what evil hath this man done? I find no cause of death in him. I will chastise him therefore, and let him go.
23 Koma ndi mawu ofuwulitsa, analimbikirabe kuti Iye apachikidwe, ndipo kufuwulako kunapitirira.
But they were instant with loud voices, requiring that he might be crucified; and their voices prevailed.
24 Choncho Pilato anatsimikiza kuchita zofuna zawozo.
And Pilate gave sentence that it should be as they required.
25 Iye anawamasulira munthu amene anaponyedwa mʼndende chifukwa choyambitsa chipolowe ndi kupha, amene ankamufunayo, ndipo anawapatsa Yesu mwakufuna kwawo.
And he released unto them him who for murder and sedition, had been cast into prison, whom they had desired; but Jesus he delivered up to their will.
26 Ndipo pamene ankapita naye, anagwira Simoni wa ku Kurene, amene ankachokera ku munda, namusenzetsa mtanda namuyendetsa pambuyo pa Yesu.
And as they led him away, they laid hold of one Simon of Cyrene, coming from the country; and they laid the cross on him to carry after Jesus.
27 Gulu lalikulu la anthu linamutsata Iye, kuphatikiza amayi amene ankabuma ndi kumulirira.
And there followed him a great multitude of people, and of women, who bewailed and lamented him.
28 Yesu anatembenuka nati kwa iwo, “Ana aakazi a Yerusalemu, musandilirire Ine; dzililireni nokha ndi ana anu.
But Jesus turning to them, said: Daughters of Jerusalem, weep not over me; but weep for yourselves, and for your children.
29 Pakuti nthawi idzabwera imene inu mudzati, ‘Ndi odala amayi osabereka, mimba zimene sizinabereke ndi mawere amene sanayamwitse!’
For behold, the days shall come, wherein they will say: Blessed are the barren, and the wombs that have not borne, and the paps that have not given suck.
30 Kenaka, “adzawuza mapiri kuti tigwereni ife; zitunda kuti tiphimbeni ife.
Then shall they begin to say to the mountains: Fall upon us; and to the hills: Cover us.
31 Chifukwa ngati anthu akuchita izi pa mtengo wauwisi, chidzachitike nʼchiyani ndi wowuma?”
For if in the green wood they do these things, what shall be done in the dry?
32 Amuna ena awiri, onsewo achifwamba, anatengedwanso pamodzi ndi Yesu kukaphedwa.
And there were also two other malefactors led with him to be put to death.
33 Pamene anafika pamalo otchedwa Bade, anamupachika Iye pamodzi ndi achifwambawo, mmodzi kudzanja lake lamanja ndi winayo la ku lamazere.
And when they were come to the place which is called Calvary, they crucified him there; and the robbers, one on the right hand, and the other on the left.
34 Yesu anati, “Atate, akhululukireni, pakuti sakudziwa chimene akuchita.” Ndipo anagawana malaya ake mochita maere.
And Jesus said: Father, forgive them, for they know not what they do. But they, dividing his garments, cast lots.
35 Anthu anayimirira nʼkumaonerera, ngakhalenso akuluakulu ankamulalatira Iye. Iwo anati, “Iye anapulumutsa ena; adzipulumutse yekha ngati ndi Khristu wa Mulungu, Wosankhidwayo.”
And the people stood beholding, and the rulers with them derided him, saying: He saved others; let him save himself, if he be Christ, the elect of God.
36 Asilikalinso anabwera ndi kumunyoza Iye. Iwo anamupatsa vinyo wosasa,
And the soldiers also mocked him, coming to him, and offering him vinegar,
37 ndipo anati, “Ngati ndiwe Mfumu ya Ayuda, dzipulumutse wekha.”
And saying: If thou be the king of the Jews, save thyself.
38 Ndipo panalembedwa chikwangwani pamwamba pake chimene chinati: uyu ndi mfumu ya ayuda.
And there was also a superscription written over him in letters of Greek, and Latin, and Hebrew: THIS IS THE KING OF THE JEWS.
39 Mmodzi wa achifwambawo, amene anapachikidwa, anamunenera Iye zamwano nati, “Kodi sindiwe Khristu? Dzipulumutse wekha ndi ifenso!”
And one of those robbers who were hanged, blasphemed him, saying: If thou be Christ, save thyself and us.
40 Koma wachifwamba winayo anamudzudzula iye nati, “Suopa Mulungu, iwenso ukulandira chilango chomwechi?
But the other answering, rebuked him, saying: Neither dost thou fear God, seeing thou art condemned under the same condemnation?
41 Ife tikulangidwa mwachilungamo, pakuti ife tikulandira monga mwa ntchito zathu. Koma munthu uyu sanachimwe kanthu.”
And we indeed justly, for we receive the due reward of our deeds; but this man hath done no evil.
42 Kenaka anati, “Yesu, mundikumbukire ine pamene mulowa mu ufumu wanu.”
And he said to Jesus: Lord, remember me when thou shalt come into thy kingdom.
43 Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, ndikukuwuza kuti lero lino udzakhala ndi Ine mʼparadaiso.”
And Jesus said to him: Amen I say to thee, this day thou shalt be with me in paradise.
44 Linali tsopano pafupi ora lachisanu ndi chimodzi, ndipo mdima unagwa pa dziko lonse mpaka ora lachisanu ndi chinayi,
And it was almost the sixth hour; and there was darkness over all the earth until the ninth hour.
45 pakuti dzuwa linaleka kuwala. Ndipo chinsalu cha mʼNyumba ya Mulungu chinangʼambika pakati.
And the sun was darkened, and the veil of the temple was rent in the midst.
46 Yesu anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Atate, ndikupereka mzimu wanga mʼmanja mwanu.” Atanena zimenezi, anamwalira.
And Jesus crying out with a loud voice, said: Father, into thy hands I commend my spirit. And saying this, he gave up the ghost.
47 Kenturiyo, ataona zimene zinachitikazi, analemekeza Mulungu ndipo anati, “Zoonadi, uyu anali munthu wolungama.”
Now the centurion, seeing what was done, glorified God, saying: Indeed this was a just man.
48 Anthu onse amene anasonkhana kudzaonerera izi, ataona zinachitikazo, anadziguguda pachifuwa ndipo anachoka.
And all the multitude of them that were come together to that sight, and saw the things that were done, returned striking their breasts.
49 Koma onse amene anamudziwa Iye, kuphatikiza amayi amene anamutsatira kuchokera ku Galileya, anayimirira akuona zinthu izi.
And all his acquaintance, and the women that had followed him from Galilee, stood afar off, beholding these things.
50 Ndipo taonani panali munthu wina wotchedwa Yosefe, mmodzi wa gulu loweruza, munthu wabwino ndi wolungama.
And behold there was a man named Joseph, who was a counsellor, a good and just man,
51 Iye sanavomereze zimene anzake abwalo anagwirizana ndi kuchita. Iye ankachokera ku mudzi wa Arimateyu wa ku Yudeya ndipo ankayembekezera ufumu wa Mulungu.
(The same had not consented to their counsel and doings; ) of Arimathea, a city of Judea; who also himself looked for the kingdom of God.
52 Atapita kwa Pilato, iye anakapempha mtembo wa Yesu.
This man went to Pilate, and begged the body of Jesus.
53 Ndipo anawutsitsa, nawukulunga nsalu yabafuta nawuyika mʼmanda wosemedwa mʼmwala, amene panalibe wina amene anayikidwamo.
And taking him down, he wrapped him in fine linen, and laid him in a sepulchre that was hewed in stone, wherein never yet any man had been laid.
54 Linali tsiku lokonzekera ndipo Sabata linatsala pangʼono kuyamba.
And it was the day of the Parasceve, and the sabbath drew on.
55 Amayi amene anabwera ndi Yesu kuchokera ku Galileya, anatsata Yosefe ndipo anaona manda ndi momwe mtembo wake anawuyikira.
And the women that were come with him from Galilee, following after, saw the sepulchre, and how his body was laid.
56 Kenaka anapita ku mudzi ndi kukakonza mafuta onunkhira. Koma anapuma pa tsiku la Sabata pomvera malamulo.
And returning, they prepared spices and ointments; and on the sabbath day they rested, according to the commandment.