< Luka 23 >
1 Kenaka gulu lonse la anthuwo linayimirira ndi kumutengera kwa Pilato.
YA todo y linajyanñija mangajulo, ya macone asta as Pilatos.
2 Ndipo iwo anayamba kumuneneza nati, “Ife tinapeza munthu uyu akusokoneza anthu a mtundu wathu ndipo amatsutsa zopereka msonkho kwa Kaisara komanso amati ndi Khristu, Mfumu.”
Ya matutujon mafaaela ilegñija: Inseda este na taotao na janaquequelache y nasionta, yan mañoñoma na umanae tributo si Sesat, ya ilelegña na güiya si Cristo un ray.
3 Pamenepo Pilato anamufunsa Yesu kuti, “Kodi Iwe ndiwe Mfumu ya Ayuda?” Yesu anayankha kuti, “Mwatero ndinu.”
Ayonae si Pilatos finaesen ilegña: Jago y Ray y Judio sija? ya inepe ya ilegña: Jago umalog.
4 Kenaka Pilato anawawuza akulu a ansembe ndi gulu la anthu, “Ine sindikumupeza cholakwa munthuyu.”
Ya si Pilatos ilegña ni y magas y mamale, yan y linajyan taotao sija: Taya isao jusoda güine na taotao.
5 Koma iwo analimbikirabe kuti, “Iyeyu amasokoneza anthu ku Yudeya konse ndi chiphunzitso chake, Iyeyu anayambira ku Galileya ndipo wayenda mtunda wonse mpaka kuno.”
Lao sija japotfia, ilegñija: Jaatbororota y taotao sija, mamananagüe guiya Judea todo, jatutujon desde Galilea asta esteja na lugat.
6 Pakumva zimenezi, Pilato anafunsa ngati munthuyo ndi Mgalileya.
Ya anae jajungog este si Pilatos, mamaesen cao taotao Galilea.
7 Iye atamva kuti Yesu anali pansi pa ulamuliro wa Herode, anamutumiza kwa Herodeyo, amene pa nthawi imeneyo analinso mu Yerusalemu.
Ya anae jatungo na gaegue gui sisiñan Herodes, janamanajanao asta as Herodes, sa estaba güe locue guiya Jerusalem güije sija na jaane.
8 Herode ataona Yesu, anakondwa kwambiri, chifukwa kwa nthawi yayitali, ankafunitsitsa atamuona. Kuchokera pa zimene anamva za Iye, anayembekezera kuti achita zodabwitsa.
Ya si Herodes anae jalie si Jesus, ninasenmagof: sa jagasja jadesea na ulie, sa jajujungog guinin güiya, megae na güinaja: ya jananangga na ufanlie guinin güiya y milagro.
9 Iye anamufunsa mafunso ambiri, koma Yesu sanayankhe.
Ya jafaesen megae na sinangan: lao taya inepe güe.
10 Akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, anayimirira pamenepo ndi kumuneneza kwambiri.
Yan mangaegue y magas y mamale yan y escribas na manmatatachong ya mafaaela güe fijom.
11 Pamenepo Herode ndi asilikali ake anamuseka ndi kumunyoza Iye. Atamuveka mkanjo wonyezimira, anamutumizanso kwa Pilato.
Lao si Herodes yan y sendaluña, madespresia yan mabotlea, yan manaminagago ni lamlam na magago, ya manatalo guato as Pilatos.
12 Tsiku limenelo, Herode ndi Pilato anakhala abwenzi. Zisanachitike izi anali adani.
Ya umamigo si Pilatos yan Herodes güijeja na jaane: sa guinin umachatlie y dos.
13 Pilato anasonkhanitsa akulu a ansembe, oweruza ndi anthu,
Ya si Pilatos janaetnon y magas y mamale, yan y magalaje yan y taotao sija,
14 ndipo anawawuza kuti, “Munabweretsa munthuyu kwa ine ngati ndiye amawuza anthu kuti awukire. Ine ndamufunsa pamaso panu ndipo sindinapeze chomuyimbira mlandu.
Ya ilegña nu sija: Inquene mague guiya guajo este na taotao na janaquequelache y taotao sija; ya, estagüe, na jufaesen gui menanmiyo, ya taya jusoda ni jafa na isao güine na taotao pot y finaaelamimiyo sija.
15 Herodenso sanapeze chifukwa pakuti wamutumizanso kwa ife monga mmene mukuoneramu. Iyeyu sanachite chinthu chakuti aphedwe.
Aje, ni si Herodes: sa junafalag iya güiya, ya, estagüe, ni jafa na ufanmerese na finatae pot y guinin finatinasña.
16 Nʼchifukwa chake, ine ndingomulanga, nʼkumumasula.”
Enao mina bae jucastiga ya jusotta.
17 (Pa nthawi yachikondwerero cha Paska iye ankayenera kumasula munthu mmodzi).
Ya manesesita na umasotta uno gui guipot.
18 Onse pamodzi anafuwula kuti, “Muchotseni munthuyu! Timasulireni Baraba!”
Ya managang cada uno, ilegñija: Nasuja juyong enao na taotao ya umasotta si Barabas:
19 (Baraba anaponyedwa mʼndende chifukwa choyambitsa chipolowe mu mzinda ndi kupha).
Sa mapreso pot un jatsamiento yan mamuno ni y jafatinas gui siuda.
20 Pofuna kumumasula Yesu, Pilato anawadandaulira iwo.
Ya si Pilatos ilegña talo nu sija, Malagomiyo na umasotta si Jesus.
21 Koma iwo anapitirirabe kufuwula kuti, “Mpachikeni! Mpachikeni!”
Lao managang ilegñija: Atane gui quiluus, atane gui quiluus.
22 Kachitatu anawafunsanso iwo kuti, “Chifukwa chiyani? Kodi munthu uyu wachita choyipa chanji? Ine sindinapeze cholakwa mwa Iye chakuti aphedwe choncho ndingomukwapula ndi kumumasula.”
Ya ilegña nu sija gui mina tres biaje: Sa jafa? jafa na taelaye finatinasña este na taotao? Taya ni jafa na causa para umapuno jusoda guiya güiya. Pot este na rason bae jucastigaja ya jusotta.
23 Koma ndi mawu ofuwulitsa, analimbikirabe kuti Iye apachikidwe, ndipo kufuwulako kunapitirira.
Lao sija enseguidas janadangculo inagangñija, ya magagao na umaatane gui quiluus. Ya y inagangñija mangana.
24 Choncho Pilato anatsimikiza kuchita zofuna zawozo.
Ayonae si Pilatos janae sentensia na ufatinas taemano y guinagaoñiñija.
25 Iye anawamasulira munthu amene anaponyedwa mʼndende chifukwa choyambitsa chipolowe ndi kupha, amene ankamufunayo, ndipo anawapatsa Yesu mwakufuna kwawo.
Ya masotta ayo y guinin mapreso pot jatsamiento yan mamuno, ayo y guinin magagagao: ya manmaentrega as Jesus gui minalagoñija.
26 Ndipo pamene ankapita naye, anagwira Simoni wa ku Kurene, amene ankachokera ku munda, namusenzetsa mtanda namuyendetsa pambuyo pa Yesu.
Ya anae macocone güe maguot si Simon, taotao Sirene, ni guinin y fangualuan, ya manae ni quiluus na uapagaye gui taten Jesus.
27 Gulu lalikulu la anthu linamutsata Iye, kuphatikiza amayi amene ankabuma ndi kumulirira.
Ya matatitiye ni y dangculon linajyan taotao yan famalaoan sija ni mangacasao yan manatangis pot güiya.
28 Yesu anatembenuka nati kwa iwo, “Ana aakazi a Yerusalemu, musandilirire Ine; dzililireni nokha ndi ana anu.
Lao si Jesus jabira güe tate guiya sija ilegña; Famalaoan Jerusalem, chamiyo fangacasao pot guajo, lao fangacasao pot jamyoja yan pot y famaguonmiyo.
29 Pakuti nthawi idzabwera imene inu mudzati, ‘Ndi odala amayi osabereka, mimba zimene sizinabereke ndi mawere amene sanayamwitse!’
Sa, estagüe, na ufato sija jaane nae umaalog: Mandichoso sa y manmachora, yan y tiyan sija ni ti manmamañago, yan y pecho sija ni ti manmamómogsae.
30 Kenaka, “adzawuza mapiri kuti tigwereni ife; zitunda kuti tiphimbeni ife.
Ayonae matutujon maalog ni egso sija: Famodong gui jilonmame; ya y sabana sija: Tampe jam.
31 Chifukwa ngati anthu akuchita izi pa mtengo wauwisi, chidzachitike nʼchiyani ndi wowuma?”
Sa yaguin y betde na jayo jafatinas estesija, y anglo, jafa uchogüe?
32 Amuna ena awiri, onsewo achifwamba, anatengedwanso pamodzi ndi Yesu kukaphedwa.
Ya macone locue dos palo na taelaye finatinasñija para ufanmapuno yan güiya.
33 Pamene anafika pamalo otchedwa Bade, anamupachika Iye pamodzi ndi achifwambawo, mmodzi kudzanja lake lamanja ndi winayo la ku lamazere.
Ya anae manmato güije na lugat ni mafanaan Calabera, maatane gui quiluus güije yan ayo y dos ni y taelaye finatinasñija, uno gui agapa ya y otro gui acagüe.
34 Yesu anati, “Atate, akhululukireni, pakuti sakudziwa chimene akuchita.” Ndipo anagawana malaya ake mochita maere.
Ya si Jesus ilegña: Tata, asie estesija; sa ti jatungo jafa jachochogüe. Ya manafacae entre sija y magaguña, ya marifa.
35 Anthu anayimirira nʼkumaonerera, ngakhalenso akuluakulu ankamulalatira Iye. Iwo anati, “Iye anapulumutsa ena; adzipulumutse yekha ngati ndi Khristu wa Mulungu, Wosankhidwayo.”
Ya y taotao sija manotojgue ya maaatanja. Ya mabotlelea ni y magas sija locue, ya ilelegñija: Ufañatba otrosija: palo ya usatban maesagüe, yaguin este si Cristo, ni guine as Yuus.
36 Asilikalinso anabwera ndi kumunyoza Iye. Iwo anamupatsa vinyo wosasa,
Ya mamofefea ni y sendalo sija, manmato guiya güiya, ya mafanunue ni y binagle.
37 ndipo anati, “Ngati ndiwe Mfumu ya Ayuda, dzipulumutse wekha.”
Ya ilegñija: Yaguin jago Ray y Judio sija, satban maesa jao.
38 Ndipo panalembedwa chikwangwani pamwamba pake chimene chinati: uyu ndi mfumu ya ayuda.
Ya guaja locue un tinigue gui jiloña: ESTE GUIYA Y RAY Y JUDIO SIJA.
39 Mmodzi wa achifwambawo, amene anapachikidwa, anamunenera Iye zamwano nati, “Kodi sindiwe Khristu? Dzipulumutse wekha ndi ifenso!”
Ya uno gui ayo y taelaye finatinasñija ilegna: Yaguin jago si Cristojao? Satban maesajao yan jame.
40 Koma wachifwamba winayo anamudzudzula iye nati, “Suopa Mulungu, iwenso ukulandira chilango chomwechi?
Lao inepe ni otro, ya linalatde ilegña: Ti maañao jao as Yuus, sa gaegue jao gui mismo sinentensia?
41 Ife tikulangidwa mwachilungamo, pakuti ife tikulandira monga mwa ntchito zathu. Koma munthu uyu sanachimwe kanthu.”
Lao jita magajet na tunas; sa utafanresibe pot y finatinasta: lao este na taotao, taya taelaye finatinasña.
42 Kenaka anati, “Yesu, mundikumbukire ine pamene mulowa mu ufumu wanu.”
Ya ilegña: Jesus, jajaso yo yaguin matojao gui raenomo.
43 Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, ndikukuwuza kuti lero lino udzakhala ndi Ine mʼparadaiso.”
Ayonae ilegña nu güiya: Magajet jusangane jao: Pago mismo na jaane utajita na dos guiya Paraiso.
44 Linali tsopano pafupi ora lachisanu ndi chimodzi, ndipo mdima unagwa pa dziko lonse mpaka ora lachisanu ndi chinayi,
Ya anae buente y oran a las sais, jumuyong jomjom todo y jilo y tano asta y oran a las nuebe,
45 pakuti dzuwa linaleka kuwala. Ndipo chinsalu cha mʼNyumba ya Mulungu chinangʼambika pakati.
Ya y atdao jomjom, ya y cottinan templo maipe gui talo.
46 Yesu anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Atate, ndikupereka mzimu wanga mʼmanja mwanu.” Atanena zimenezi, anamwalira.
Ya anae umagang si Jesus, ni dangculo na inagang, ilegña: Tata, y canaemo nae jupolo y espiritujo; ya anae munjayan jasangan este, jaentrega y espiritu.
47 Kenturiyo, ataona zimene zinachitikazi, analemekeza Mulungu ndipo anati, “Zoonadi, uyu anali munthu wolungama.”
Ya anae jalie y senturion estesija y manmalofan, janamalag si Yuus, ilegña: Sen magajet este na taotao na tunas.
48 Anthu onse amene anasonkhana kudzaonerera izi, ataona zinachitikazo, anadziguguda pachifuwa ndipo anachoka.
Ya todo y linajyan taotao ni mandaña anae manmalofan este sija, anae malie y jagas sinesede, natumalo guato ya jaseco pechonñija.
49 Koma onse amene anamudziwa Iye, kuphatikiza amayi amene anamutsatira kuchokera ku Galileya, anayimirira akuona zinthu izi.
Lao todo y atungoña yan y famalaoan ni tumatitiye güe desde Galilea, manestaba manlachago maatanja este sija.
50 Ndipo taonani panali munthu wina wotchedwa Yosefe, mmodzi wa gulu loweruza, munthu wabwino ndi wolungama.
Ya estagüe, un taotao na y naanña si José, un taotao na pápagat, mauleg na taotao yan tunas:
51 Iye sanavomereze zimene anzake abwalo anagwirizana ndi kuchita. Iye ankachokera ku mudzi wa Arimateyu wa ku Yudeya ndipo ankayembekezera ufumu wa Mulungu.
(Ti jaconsiente y pinagatñija ni y finatinasñija: ) Taotao Arimatea, gui Siuda y Judiosija, ya güiya locue jananangga y raenon Yuus.
52 Atapita kwa Pilato, iye anakapempha mtembo wa Yesu.
Este mato gui as Pilatos, ya jagagao y tataotao Jesus.
53 Ndipo anawutsitsa, nawukulunga nsalu yabafuta nawuyika mʼmanda wosemedwa mʼmwala, amene panalibe wina amene anayikidwamo.
Ya janatunog gui quiluus, ya jabalutan gui un sabanas, ya japolo gui un naftan ni maguadog gui acho, ya taya ni uno mapolo güije antes.
54 Linali tsiku lokonzekera ndipo Sabata linatsala pangʼono kuyamba.
Ya ayo na jaane y inaregla y pascua, ya pago manana gui sabado.
55 Amayi amene anabwera ndi Yesu kuchokera ku Galileya, anatsata Yosefe ndipo anaona manda ndi momwe mtembo wake anawuyikira.
Ya manmato locue y famalaoan ni y tumatitiye desde Galilea, ya malie y naftan yan jaftaemano mapoloña y tataotaoña.
56 Kenaka anapita ku mudzi ndi kukakonza mafuta onunkhira. Koma anapuma pa tsiku la Sabata pomvera malamulo.
Ya tumalo guato sija, ya manmamamauleg paopao yan inggüente sija: ya mandescansa gui sabado na jaane jaftaemanoja y tinago.