< Luka 2 >
1 Mʼmasiku amenewo Kaisara Augusto anapereka lamulo kuti kalembera achitike mʼdziko lonse la Aroma.
Ăm aje vremi dă pă šje su avut Ivan, zapovjed u fost mănată dă la car August să fakă skritura dă stanovništvo ăm ăntragă cara.
2 (Uyu ndi kalembera woyamba amene anachitika pamene Kureniyo anali bwanamkubwa wa Siriya).
Aje are elši skritura dă stanovništvo kari u fost kănd Kvirinije are vladar dă Sirija.
3 Ndipo aliyense anapita ku mzinda wa kwawo kukalembetsa.
Aša toc ur mers să să prijavalaskă ăm varušu hunđi preci alor u kustat.
4 Choncho Yosefe anachoka ku Nazareti ku Galileya kupita ku Yudeya, ku Betelehemu ku mudzi wa Davide, chifukwa anali wa banja ndi fuko la Davide.
Aša Josip dăm mik varuš Nazaret ăm Galileja, u mers ăm varuš Betlehem ăm Judeja hunđi su avut David daje kă jej as re njamu alu kralj David.
5 Iye anapita kumeneko kukalembetsa pamodzi ndi Mariya, amene anapalana naye ubwenzi kuti akwatirane ndipo anali woyembekezera.
Josip u mers akulo să să jivaskă dă skritura una ku Marija zaručnica aluj, kari are gărjonă.
6 Ali kumeneko, nthawi inakwana yakuti mwana abadwe,
Šă kum asre dăm Betlehem akulo vreme u vinjit să să ajvi kupilu.
7 ndipo anabereka mwana wake woyamba, wamwamuna. Iye anamukulunga mʼnsalu ndi kumuyika modyera ngʼombe, chifukwa kunalibe malo mʼnyumba ya alendo.
Je u avut elši fišjor, lu ănvălitălu šă lu pus ăm hištalov daje kă nu are soba păntru jej ăm fugadov.
8 Ndipo kunali abusa amene amakhala ku dera lomwelo, kuyangʼanira ziweto zawo usiku.
Ăm ala lok dă apropi dă Betlehem asre pastirur kari rămănje afară pă otvoreno šă păze stadurlje alor totă nopće.
9 Mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iwo ndipo ulemerero wa Ambuye unawala mowazungulira. Iwo anachita mantha.
Šă dăm turdată su pojavalit anđalu alu Domnuluj! Anđalu u stat ăm nenće alor, šă slava alu Domnuluj lju svitlăzăt pă jej. Šă pastiri u gălbănjit ăm ubraz dă frikă.
10 Koma mngeloyo anawawuza kuti, “Musachite mantha. Ine ndakubweretserani Uthenga Wabwino wachimwemwe chachikulu umene udzakhala wa anthu onse.
Ali anđalu lju zăs: “Nu vă fijă frikă! Ju vjuv să vă aduk Hir fălos, dă mari fălušăjă păntru totă lume.
11 Lero mʼmudzi wa Davide wakubwadwirani Mpulumutsi; Iye ndi Khristu Ambuye.
Ăm varušu hunđi su avut Kralj David, astăs su avut Spasitelj. Jăl are Krist, Domnu!
12 Ichi chidzakhala chizindikiro kwa inu: mukapeza mwana wakhanda wokutidwa ndi nsalu atagona modyera ngʼombe.”
Asta ăj znak dă pă kari să ăl šćijec: voj vic afla pă kupilu ănvălit ăm hištalov.”
13 Mwadzidzidzi gulu lalikulu la angelo linaonekera pamodzi ndi mngeloyo, kuyamika Mulungu ndi kumati,
Atunšje dăm turdată lăngă parće dă anđal u vinjit mulc anđej dăm nor kari hvalale pă Dimizov. Šă jej slavale:
14 “Ulemerero kwa Mulungu mmwambamwamba, ndi mtendere kwa anthu pa dziko lapansi amene Iye akondwera nawo.”
“Slava alu Dimizov ăm nor šă pă pămănt putuljală alu eje ominj kari lju izabralit.”
15 Angelowo atabwerera kumwamba, abusawo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni ku Betelehemu tikaone zinthu zomwe zachitika, zimene Ambuye atiwuza ife.”
Dă pă šje ur fužit anđelji dă la pastir ăm nor, pastiri ur zăs una la alt: “Haj aku am Betlehem, šă să viđenj aje dă šje Domnu nju spus!”
16 Ndipo iwo anafulumira nyamuka nakapeza Mariya ndi Yosefe ndi mwana wakhanda, amene anagona modyera ngʼombe.
Aša sur ăngribit ăm Betlehem šă ur aflat pă Marija, šă pă Josip, a kupilu are ăm hištalov.
17 Pamene anamuona Iye, iwo anafotokoza zomwe anawuzidwa za mwanayo,
Šă kănd pastiri ur văzut pă kupil, jej sur apukatăsă să spujă šje lju fost spus dă la anđej dă kupil.
18 ndipo onse amene anamva zimene abusawa ananena anadabwa.
Toc eje kari ur auzăt šje pastiri ur spus, jej toc asre ămirac.
19 Koma Mariya anasunga zonsezi mu mtima mwake ndi kumazilingalira.
Ali Marija cănje toći vorbilje alor ăm sufljičilje alor šă mult su gănđit dă jelji.
20 Abusa anabwerera, akulemekeza ndi kuyamika Mulungu chifukwa cha zonse anazimva ndi kuziona, zomwe zinali monga anawuzidwira ndi angelo aja.
Atunšje pastiri ur fužjit la stadurlje alor šă jej dăđe hvală šă slavă lu Dimizov dă kutotu stvarurlje šje ur auzăt šă šje ur văzut, točno kum lju fost najavalit alor.
21 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, tsiku loti amuchite mdulidwe anamutcha Yesu, dzina limene mngelo anamupatsa asanabadwe.
Osma zuva kănd kupilu su avut u fost obrezalit, šă u fost čimat Isus, numilje u dată aluj dă la anđal majnti dă šje Marija u rămas gărjonă.
22 Nthawi yoyeretsedwa kwawo itatha, monga mwa lamulo la Mose, Yosefe ndi Mariya anapita naye ku Yerusalemu kukamupereka kwa Ambuye.
Šă kănd u vinjit vreme alu Marija obred dă čistilală kum are zapovjedălală dă la zakonu alu Mojsije, Marije šă Josip ur dus pă Isus am Jeruzalem să ăl posvetilaskă la Domnu,
23 (Monga mmene zinalembedwera mu lamulo la Ambuye kuti, “Muzikapereka kwa Ambuye mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa”),
kă ăj skris ăm zakonu alu Domnu: “Tot elši fišjor u fi posvetilită la Domnu.”
24 ndi kupereka nsembe posunga zimene zinanenedwa mulamulo la Ambuye: “Njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri.”
Jej trăbă isto să adukă žrtvă: “Dovă grlicur ili doj tănjiră puromb,” kum ăj zapovjedalit dă la zakonu alu Domnu anostru.
25 Ndipo taonani, mu Yerusalemu munali munthu wotchedwa Simeoni, amene anali wolungama ndi wodzipereka. Iye ankadikira chitonthozo cha Israeli, ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.
Atunšje are om ăm Jeruzalem šje să čima Šimun. Jăl are pravedan šă svet šă aščipta pă Mesija să izbavalaskă pă Izrael šă Duhu Svănt are ku jăl.
26 Mzimu Woyera anamuwululira kuti sadzafa asanaone Khristu wa Ambuye.
Šă Duhu Svănt majnti ju spus aluj kă no mori majnti dă šje no viđe pă Mesija alu Domnu anostru.
27 Motsogozedwa ndi Mzimu Woyera, iye anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Makolo ake a Yesu atabwera naye kuti achite naye mwambo malingana ndi malamulo,
Aša Duhu Svănt lu dus pă Šimun ăm Hram kănd ur adus roditelji pă kupilu Isus ăm nontru šă să fakă obred kum are običaju dă zakonu alu Mojsije.
28 Simeoni anamunyamula mʼmanja mwake nayamika Mulungu, nati:
Šimun lu apukat ăm mănjilješ pă Isus, slavale pă Dimizov, šă u zăs:
29 “Ambuye waulamuliro, monga munalonjeza, tsopano lolani kuti mtumiki wanu apite mu mtendere.
“Aku lasă pă sluga atov să moră ăm putuljală, Domnu, kum tu aj zăs,
30 Pakuti maso anga aona chipulumutso chanu,
kă oči amej ur văzut spasenje ata.
31 chimene Inu munakonza pamaso pa anthu onse,
Asta tu aj făkut dă totă lume.
32 kuwala kowunikira anthu a mitundu ina ndi kwa ulemerero kwa anthu anu Aisraeli.”
Asta ăj lumina dă ominj šă lji svitlizaskă alu ominj kari nus Židov, slava alu lume dă Izrael!”
33 Abambo ndi amayi a Mwanayo anadabwa chifukwa cha zimene zinanenedwa za Iye.
Tata šă mama alu Isus asre umpljec ku ămirală dă kutotu šje Šimun u zăs dă jăl.
34 Kenaka Simeoni anawadalitsa ndipo anati kwa Mariya amayi ake: “Mwana uyu wakonzedwa kukhala kugwa ndi kudzuka kwa ambiri mu Israeli, ndi kukhala chizindikiro chimene adzayankhula motsutsana nacho,
Atunšje Šimun u blagoslovulit pă jej šă u zăs lu Marija: “Dimizov u odredilit pă ala kupil kă păntru jăl mulc Izraelc ur kăđe šă su riđikasă. Jăl ăj odredilit să fijă znaku alu Dimizov, ali mulc lur odbacalilă
35 kotero kuti malingaliro a mitima ya ambiri adzawululidwa. Ndipo lupanga lidzabaya moyo wakonso.”
aša u vinji pă lumină găndurlje askunšă alu mulc, a maču či ămpunžji ăm duša ata.”
36 Panalinso mneneri wamkazi, dzina lake Ana, mwana wa Fanuelo, wa fuko la Aseri. Anali wokalamba kwambiri; anakhala ndi mwamuna wake zaka zisanu ndi ziwiri atakwatiwa,
Are isto aša proročica Ana fată alu Fanuel kari ăj dăm pleme alu Ašer. Ana are tari bătărnă mujeri, je are šapči aj ăm brak
37 ndipo kenaka anakhala wamasiye mpaka pamene anali ndi zaka 84. Iye sanachoke mʼNyumba ya Mulungu koma ankapembedza usiku ndi usana, kusala kudya ndi kupemphera.
šă aku ăj vădojă, mar hunđiva osamdeset patru aj. Ana nu fužje dăm Hram, nego služule akulo zuva šă nopće ăm post šă ăm aruguminći.
38 Pa nthawiyo pamene ankapita kwa iwo, iye anayamika Mulungu ndi kuyankhula za Mwanayo kwa onse amene ankayembekezera chipulumutso cha Yerusalemu.
Baš pă aje vremi Ana u vinjit, hvalale pă Dimizov, šă je spunje dă kupilu Isus alu toc kari ašćipta pă Dimizov să otkupilaskă pă Jeruzalem.
39 Yosefe ndi Mariya atachita zonse zimene zinkafunikira ndi lamulo la Ambuye, anabwerera ku Galileya ku mudzi wa Nazareti.
Dă pă šje ur făkut Josip šă Marije kutotu šje zakonu alu Domnu u šjirut dă la jej, jej ur mers ăm napoj ăm varušu alor Nazaret ăm Galileja.
40 Ndipo Mwanayo anakula nakhala wamphamvu; Iye anadzazidwa ndi nzeru, ndipo chisomo cha Mulungu chinali pa Iye.
Kupilu u kriskut šă su ămbălurităsă, are pljin dă mudrost, šă blagoslovurlje alu Dimizov asre ku Isus.
41 Chaka chilichonse makolo ake ankapita ku Yerusalemu ku phwando la Paska.
Roditelji alu Isus măržje ăm tot anu ăm Jeruzalem să fijă akulo pă blagdan dă Pasha.
42 Iye ali ndi zaka khumi ndi ziwiri, anapita ku phwando, monga mwa mwambo.
Aša kănd are Isus dvanaest aj dă bătărn jăl una ku jej u mers pă blagdan ka kum stalno măržje.
43 Phwando litatha, pamene makolo ake ankabwerera kwawo, mnyamata Yesu anatsalira ku Yerusalemu, koma iwo sanadziwe zimenezi.
Šă kănd u trikut blagdanu jej sur gătatăsă akasă, ali făr dă šćučilje alu roditelji, kupilu Isus u rămas ăm Jeruzalem.
44 Poganiza kuti anali nawo mʼgulu lawo, anayenda tsiku limodzi. Kenaka anayamba kumufunafuna pakati pa abale awo ndi anzawo.
Jej gănđe kă ăj hunđiva ăm grupă. Jej ur trikut mari kalji totă zuva, kapu sur apukatăsă să ăl koći ăntri njamu šă ăntri hej kari ăl kunošći.
45 Atalephera kumupeza, anabwerera ku Yerusalemu kukamufuna.
Kum nu lor aflat, jej ur mers ăm napoj ăm Jeruzalem šă ăl koći.
46 Patatha masiku atatu anamupeza ali mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, atakhala pakati pa aphunzitsi, akumvetsera ndi kuwafunsa mafunso.
Tri zălji dă pă aje jej lor aflat. Isus are ăm Hram, šăđe ăntri učitelji dă zakonu alu Mojsije, punje ureče šă lji ăntriba.
47 Aliyense amene anamumva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake ndi mayankho ake.
Toc kari ăl punje ureče asre ămirac la fire aluj, šă la odgovurlje aluj.
48 Makolo ake atamuona, anadabwa. Amayi ake anati kwa Iye, “Mwanawe, watichitira zimenezi chifukwa chiyani? Abambo ako ndi ine takhala tili ndi nkhawa kukufunafuna Iwe.”
Roditelji aluj isto aša asre tari ămirac kănd lor văzutălă akulo šă mumăsa ju zăs: “Fišjoru amnjov adăšje njaj făkut asta anovă? Tata atov šă ju as renj ăm mari brigur dă činji, păšći tot či kutanj!”
49 Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumandifunafuna? Kodi simukudziwa kuti ndikuyenera kukhala mʼnyumba ya Atate anga?”
Isus u ăntors vorba: “Ali adăšje mă kutac? Nu šćijec kă ju aš trăbuji să fjuv ăm kasa alu Tata amnjov?”
50 Koma iwo sanazindikire chomwe Iye amatanthauza.
Jej nur prišjiput šje gănđe să lji spujă.
51 Kenaka anapita nawo ku Nazareti ndipo anawamvera iwo. Koma amayi ake anasunga zinthu zonsezi mu mtima mwawo.
Ali Isus u mers ăm napoj ku roditelji ăm Nazaret, šă jăl lju u pus ureći. Šă mumăsa aluj u cănut kutotu vorbilje ăm sufljituš.
52 Ndipo Yesu anakula mu nzeru, msinkhu ndi chisomo cha Mulungu ndi anthu.
Šă ăm aje vremi Isus u kriskut ăm gănd šă ăm telă šă ku milă dă la Dimizov šă dă la lumi.