< Luka 2 >
1 Mʼmasiku amenewo Kaisara Augusto anapereka lamulo kuti kalembera achitike mʼdziko lonse la Aroma.
Kwasekusithi ngalezonsuku, isimiso saphuma kuKesari uAgastasi, sokuthi kubhalwe umhlaba wonke.
2 (Uyu ndi kalembera woyamba amene anachitika pamene Kureniyo anali bwanamkubwa wa Siriya).
Lokhukubhalwa kwakungokokuqala ukwenziwa lapho uKwiriniya engumbusi weSiriya.
3 Ndipo aliyense anapita ku mzinda wa kwawo kukalembetsa.
Bonke basebesiya ukuze bayebhalwa, ngulowo lalowo emzini wakibo.
4 Choncho Yosefe anachoka ku Nazareti ku Galileya kupita ku Yudeya, ku Betelehemu ku mudzi wa Davide, chifukwa anali wa banja ndi fuko la Davide.
LoJosefa laye wenyuka esuka eGalili, emzini iNazaretha, waya eJudiya, emzini kaDavida, othiwa yiBhethelehema, ngoba wayengowendlu lowosendo lukaDavida,
5 Iye anapita kumeneko kukalembetsa pamodzi ndi Mariya, amene anapalana naye ubwenzi kuti akwatirane ndipo anali woyembekezera.
ukuyabhalwa kanye loMariya umkakhe ayemganile, owayezithwele.
6 Ali kumeneko, nthawi inakwana yakuti mwana abadwe,
Kwasekusithi belapho, zaseziphelela insuku zokubeletha kwakhe.
7 ndipo anabereka mwana wake woyamba, wamwamuna. Iye anamukulunga mʼnsalu ndi kumuyika modyera ngʼombe, chifukwa kunalibe malo mʼnyumba ya alendo.
Wasebeletha indodana yakhe eyingqabutho, wayigoqela ngamalembu, wayilalisa emkolweni, ngoba kwakungelandawo yabo endlini yezihambi.
8 Ndipo kunali abusa amene amakhala ku dera lomwelo, kuyangʼanira ziweto zawo usiku.
Njalo kwakukhona kulelolizwe abelusi ababehlala egangeni futhi belinde umhlambi wabo ebusuku.
9 Mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iwo ndipo ulemerero wa Ambuye unawala mowazungulira. Iwo anachita mantha.
Njalo khangela, ingilosi yeNkosi yema eduze kwabo, lenkazimulo yeNkosi yakhanya ibazingelezele; njalo besaba ngokwesaba okukhulu.
10 Koma mngeloyo anawawuza kuti, “Musachite mantha. Ine ndakubweretserani Uthenga Wabwino wachimwemwe chachikulu umene udzakhala wa anthu onse.
Ingilosi yasisithi kubo: Lingesabi; ngoba khangelani, ngitshumayela indaba ezinhle kini ezentokozo enkulu, ezakuba kubantu bonke;
11 Lero mʼmudzi wa Davide wakubwadwirani Mpulumutsi; Iye ndi Khristu Ambuye.
ngoba lizalelwe lamuhla uMsindisi, onguKristu iNkosi, emzini kaDavida.
12 Ichi chidzakhala chizindikiro kwa inu: mukapeza mwana wakhanda wokutidwa ndi nsalu atagona modyera ngʼombe.”
Njalo lokhu kuzakuba yisibonakaliso kini: Lizathola usane lugoqelwe ngamalembu, lulele emkolweni.
13 Mwadzidzidzi gulu lalikulu la angelo linaonekera pamodzi ndi mngeloyo, kuyamika Mulungu ndi kumati,
Njalo kwahle kwaba khona kanye lengilosi ixuku lebutho lasezulwini, lidumisa uNkulunkulu, lisithi:
14 “Ulemerero kwa Mulungu mmwambamwamba, ndi mtendere kwa anthu pa dziko lapansi amene Iye akondwera nawo.”
Udumo kalube kuNkulunkulu kweliphezulu, lokuthula emhlabeni; isifiso esihle ebantwini.
15 Angelowo atabwerera kumwamba, abusawo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni ku Betelehemu tikaone zinthu zomwe zachitika, zimene Ambuye atiwuza ife.”
Kwasekusithi, ingilosi sezisukile kubo zisiya ezulwini, abantu, abangabelusi, bakhulumisana besithi: Ake siye eBhethelehema, sibone leyonto eyenzakeleyo, iNkosi esazise yona.
16 Ndipo iwo anafulumira nyamuka nakapeza Mariya ndi Yosefe ndi mwana wakhanda, amene anagona modyera ngʼombe.
Basebesiza ngokuphangisa, bathola oMariya loJosefa, losane lulele emkolweni.
17 Pamene anamuona Iye, iwo anafotokoza zomwe anawuzidwa za mwanayo,
Sebebonile basebesazisa indawo ezizingelezeleyo ngelizwi ababelitshelwe mayelana lalo umntwana omncane.
18 ndipo onse amene anamva zimene abusawa ananena anadabwa.
Labo bonke abakuzwayo bamangala ngezinto ezazikhulunywe ngabelusi kubo.
19 Koma Mariya anasunga zonsezi mu mtima mwake ndi kumazilingalira.
Kodwa uMariya walondoloza wonke la amazwi, enakana ngawo enhliziyweni yakhe.
20 Abusa anabwerera, akulemekeza ndi kuyamika Mulungu chifukwa cha zonse anazimva ndi kuziona, zomwe zinali monga anawuzidwira ndi angelo aja.
Basebebuyela abelusi, bemdumisa bembonga uNkulunkulu ngazo zonke izinto ababezizwile lababezibonile, njengalokho okwakukhulunywe kubo.
21 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, tsiku loti amuchite mdulidwe anamutcha Yesu, dzina limene mngelo anamupatsa asanabadwe.
Kwathi seziphelile insuku eziyisificaminwembili zokuthi umntwana omncane asokwe, ibizo lakhe laselithiwa nguJesu, elalibizwe yingilosi engakomulwa esiswini.
22 Nthawi yoyeretsedwa kwawo itatha, monga mwa lamulo la Mose, Yosefe ndi Mariya anapita naye ku Yerusalemu kukamupereka kwa Ambuye.
Kwathi seziphelele insuku zokuhlanjululwa kwakhe ngokomlayo kaMozisi, bamletha eJerusalema, ukuze bammise phambi kweNkosi
23 (Monga mmene zinalembedwera mu lamulo la Ambuye kuti, “Muzikapereka kwa Ambuye mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa”),
(njengokulotshiweyo emlayweni weNkosi ukuthi konke okwesilisa okuvula isibeletho kuzathiwa kungcwele eNkosini)
24 ndi kupereka nsembe posunga zimene zinanenedwa mulamulo la Ambuye: “Njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri.”
lokuthi banikele umhlatshelo njengokutshiwo emlayweni weNkosi, amajuba amabili kumbe amaphuphu amabili enkwilimba.
25 Ndipo taonani, mu Yerusalemu munali munthu wotchedwa Simeoni, amene anali wolungama ndi wodzipereka. Iye ankadikira chitonthozo cha Israeli, ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.
Njalo khangela, kwakukhona eJerusalema umuntu, obizo lakhe linguSimeyoni, njalo lumuntu wayelungile ekhuthele ekukhonzeni, elindele induduzo kaIsrayeli, loMoya oNgcwele wayephezu kwakhe.
26 Mzimu Woyera anamuwululira kuti sadzafa asanaone Khristu wa Ambuye.
Futhi kwakubonakalisiwe kuye nguMoya oyiNgcwele, ukuthi kayikubona ukufa engakamboni uKristu weNkosi.
27 Motsogozedwa ndi Mzimu Woyera, iye anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Makolo ake a Yesu atabwera naye kuti achite naye mwambo malingana ndi malamulo,
Wasengena ethempelini ngoMoya; kwathi abazali bemletha umntwana omncane uJesu, ukuze benze ngaye ngokomkhuba womlayo,
28 Simeoni anamunyamula mʼmanja mwake nayamika Mulungu, nati:
yena wasemthatha wamphatha engalweni zakhe, wabonga uNkulunkulu, wathi:
29 “Ambuye waulamuliro, monga munalonjeza, tsopano lolani kuti mtumiki wanu apite mu mtendere.
Nkosi, khathesi iyekele inceku yakho ihambe ngokuthula, njengokwelizwi lakho;
30 Pakuti maso anga aona chipulumutso chanu,
ngoba amehlo ami alubonile usindiso lwakho
31 chimene Inu munakonza pamaso pa anthu onse,
olulungisileyo phambi kobuso babantu bonke;
32 kuwala kowunikira anthu a mitundu ina ndi kwa ulemerero kwa anthu anu Aisraeli.”
ukukhanya kokwembulela abezizwe, lenkazimulo yesizwe sakho uIsrayeli.
33 Abambo ndi amayi a Mwanayo anadabwa chifukwa cha zimene zinanenedwa za Iye.
UJosefa lonina basebemangala ngezinto ezatshiwo ngaye.
34 Kenaka Simeoni anawadalitsa ndipo anati kwa Mariya amayi ake: “Mwana uyu wakonzedwa kukhala kugwa ndi kudzuka kwa ambiri mu Israeli, ndi kukhala chizindikiro chimene adzayankhula motsutsana nacho,
USimeyoni wasebabusisa, wathi kuMariya unina: Khangela, lo umiselwe ukuwa lokuvuka kwabanengi kuIsrayeli, lokuba yisibonakaliso esizaphikiswa;
35 kotero kuti malingaliro a mitima ya ambiri adzawululidwa. Ndipo lupanga lidzabaya moyo wakonso.”
futhi lawe, inkemba izadabula owakho umphefumulo; ukuze imicabango yenhliziyo ezinengi yembulwe.
36 Panalinso mneneri wamkazi, dzina lake Ana, mwana wa Fanuelo, wa fuko la Aseri. Anali wokalamba kwambiri; anakhala ndi mwamuna wake zaka zisanu ndi ziwiri atakwatiwa,
Njalo kwakukhona uAna umprofethikazi, indodakazi kaFanuweli, owesizwe sikaAsheri; wayesekhulile kakhulu, ebehlale lendoda iminyaka eyisikhombisa kusukela ebuntombini bakhe,
37 ndipo kenaka anakhala wamasiye mpaka pamene anali ndi zaka 84. Iye sanachoke mʼNyumba ya Mulungu koma ankapembedza usiku ndi usana, kusala kudya ndi kupemphera.
njalo wayengumfelokazi owayengaba leminyaka engamatshumi ayisificaminwembili lane, engasuki ethempelini, ekhonza ngokuzila ukudla langemikhuleko ebusuku lemini.
38 Pa nthawiyo pamene ankapita kwa iwo, iye anayamika Mulungu ndi kuyankhula za Mwanayo kwa onse amene ankayembekezera chipulumutso cha Yerusalemu.
Laye efika ngalelohola wadumisa uNkulunkulu, wakhuluma ngaye kubo bonke ababelindele inkululeko eJerusalema.
39 Yosefe ndi Mariya atachita zonse zimene zinkafunikira ndi lamulo la Ambuye, anabwerera ku Galileya ku mudzi wa Nazareti.
Kwathi sebeqedile konke okungokomlayo weNkosi, babuyela eGalili, emzini wakibo iNazaretha.
40 Ndipo Mwanayo anakula nakhala wamphamvu; Iye anadzazidwa ndi nzeru, ndipo chisomo cha Mulungu chinali pa Iye.
Lomntwana omncane wakhula, waqina emoyeni, wagcwala inhlakanipho; lomusa kaNkulunkulu wawuphezu kwakhe.
41 Chaka chilichonse makolo ake ankapita ku Yerusalemu ku phwando la Paska.
Njalo abazali bakhe babesiya eJerusalema iminyaka yonke ngomkhosi wephasika.
42 Iye ali ndi zaka khumi ndi ziwiri, anapita ku phwando, monga mwa mwambo.
Kwathi eseleminyaka elitshumi lambili, sebenyukele eJerusalema njengomkhuba womkhosi,
43 Phwando litatha, pamene makolo ake ankabwerera kwawo, mnyamata Yesu anatsalira ku Yerusalemu, koma iwo sanadziwe zimenezi.
njalo sebeziqedile insuku, ekubuyeleni kwabo, umntwana uJesu wasala eJerusalema; njalo uJosefa lonina bengazi;
44 Poganiza kuti anali nawo mʼgulu lawo, anayenda tsiku limodzi. Kenaka anayamba kumufunafuna pakati pa abale awo ndi anzawo.
kodwa becabanga ukuthi wayesexukwini endleleni, bahamba uhambo losuku, bamdinga phakathi kwezinini labazana labo;
45 Atalephera kumupeza, anabwerera ku Yerusalemu kukamufuna.
kodwa bengamtholi, babuyela eJerusalema, bemdinga.
46 Patatha masiku atatu anamupeza ali mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, atakhala pakati pa aphunzitsi, akumvetsera ndi kuwafunsa mafunso.
Kwasekusithi emva kwensuku ezintathu, bamthola ethempelini, ehlezi phakathi kwabafundisi, njalo ebalalela, futhi ebabuza.
47 Aliyense amene anamumva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake ndi mayankho ake.
Njalo bonke ababemuzwa bamangala kakhulu ngolwazi lempendulo zakhe.
48 Makolo ake atamuona, anadabwa. Amayi ake anati kwa Iye, “Mwanawe, watichitira zimenezi chifukwa chiyani? Abambo ako ndi ine takhala tili ndi nkhawa kukufunafuna Iwe.”
Kwathi bembona bamangala; lonina wathi kuye: Mntanami, wenzeleni okunje kithi? Khangela, uyihlo lami besikudinga sidubekile.
49 Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumandifunafuna? Kodi simukudziwa kuti ndikuyenera kukhala mʼnyumba ya Atate anga?”
Wasesithi kubo: Kungani lingidinga? Belingakwazi yini ukuthi kumele ukuthi ngibe sezintweni zikaBaba?
50 Koma iwo sanazindikire chomwe Iye amatanthauza.
Kodwa bona kabaliqedisisanga ilizwi alikhuluma kubo.
51 Kenaka anapita nawo ku Nazareti ndipo anawamvera iwo. Koma amayi ake anasunga zinthu zonsezi mu mtima mwawo.
Wasesehla labo, weza eNazaretha; wazehlisela ngaphansi kwabo. Unina wasegcina zonke lezizinto enhliziyweni yakhe.
52 Ndipo Yesu anakula mu nzeru, msinkhu ndi chisomo cha Mulungu ndi anthu.
UJesu waseqhubeka enhlakanipheni lekukhuleni, lekuthandekeni kuNkulunkulu lebantwini.