< Luka 2 >

1 Mʼmasiku amenewo Kaisara Augusto anapereka lamulo kuti kalembera achitike mʼdziko lonse la Aroma.
Ara anyimo atiye me, kaisar Augustas ma buki guna abassa vat anu unce.
2 (Uyu ndi kalembera woyamba amene anachitika pamene Kureniyo anali bwanamkubwa wa Siriya).
Ubassa utuba uganiya sa kiriniyus mā zi ugumna usuriya.
3 Ndipo aliyense anapita ku mzinda wa kwawo kukalembetsa.
Anime kondevi ma dusa ani pin nuwe me bati aka bassa we.
4 Choncho Yosefe anachoka ku Nazareti ku Galileya kupita ku Yudeya, ku Betelehemu ku mudzi wa Davide, chifukwa anali wa banja ndi fuko la Davide.
Isubu ma hiri u Nazarat ani pin nu Baita Lami uhana Yahudiya, aba sa agusan nipin ni Dauda. Barki me bisana bi Dauda bini.
5 Iye anapita kumeneko kukalembetsa pamodzi ndi Mariya, amene anapalana naye ubwenzi kuti akwatirane ndipo anali woyembekezera.
Ma ha nan Maryamu de sa mazin inti nyari tume inna puru bati aka bassa we.
6 Ali kumeneko, nthawi inakwana yakuti mwana abadwe,
Uganiya sa wa rani abirko me uganiya me uni madi yoo vana.
7 ndipo anabereka mwana wake woyamba, wamwamuna. Iye anamukulunga mʼnsalu ndi kumuyika modyera ngʼombe, chifukwa kunalibe malo mʼnyumba ya alendo.
Ma yoo Uvana, utuba uyoo uvana, ma impi me in mapori ma natti me uhugu, barki sa wa zowe unu denge ba abini me.
8 Ndipo kunali abusa amene amakhala ku dera lomwelo, kuyangʼanira ziweto zawo usiku.
Uwata me aye wa rani ama saa unu bee itam iwee in niye.
9 Mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iwo ndipo ulemerero wa Ambuye unawala mowazungulira. Iwo anachita mantha.
Bibe bika dura ka Asere bi ē ahira awe, Ma saa ma Asere maketi we, wa kunna biyan bidandang.
10 Koma mngeloyo anawawuza kuti, “Musachite mantha. Ine ndakubweretserani Uthenga Wabwino wachimwemwe chachikulu umene udzakhala wa anthu onse.
Abinime bibe bika dura ka Asere be gun we “Kati ikunna biyan ba, ma aye shi inna banga aririn age sa Vat anu wadi kunna urunta udandang.
11 Lero mʼmudzi wa Davide wakubwadwirani Mpulumutsi; Iye ndi Khristu Ambuye.
Ayoo unu bura kānime ani pin ni Dauda, memani Asere Ugomo Asere.
12 Ichi chidzakhala chizindikiro kwa inu: mukapeza mwana wakhanda wokutidwa ndi nsalu atagona modyera ngʼombe.”
Ma saa me mazigenme sa adi nya shi, idi iri vana a impo me imma pori anata me hungu”.
13 Mwadzidzidzi gulu lalikulu la angelo linaonekera pamodzi ndi mngeloyo, kuyamika Mulungu ndi kumati,
Sārki ucara uganiyan wa iri nigura nanuu nan Bibe bikadura ka Asere unu nonzo Asere innugusa.
14 “Ulemerero kwa Mulungu mmwambamwamba, ndi mtendere kwa anthu pa dziko lapansi amene Iye akondwera nawo.”
“Ninonzo na Asere unaza, nan ticukum tihuma acee anu nee nan de sa ma kunna urunta ume”.
15 Angelowo atabwerera kumwamba, abusawo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni ku Betelehemu tikaone zinthu zomwe zachitika, zimene Ambuye atiwuza ife.”
Abiki uganiya me sa Bibe bika dura ka Asere ba dusa anyimo a seseri, ani tam me wa gun nacece “Ca tihaa ubaitalami, tika iri imum igeme sa takunna sa Asere abukan duru”.
16 Ndipo iwo anafulumira nyamuka nakapeza Mariya ndi Yosefe ndi mwana wakhanda, amene anagona modyera ngʼombe.
Wa haa dibe-dibe waka kem Maryamu nan Isubu wan vana me anata uhungu.
17 Pamene anamuona Iye, iwo anafotokoza zomwe anawuzidwa za mwanayo,
Sa wa ira me, wa buki anu imum me sa abuka we anicee ne vana me.
18 ndipo onse amene anamva zimene abusawa ananena anadabwa.
Vat ande sa wa kunna icukuno Imum ugamara imum me sa anu hira itam me wa buka.
19 Koma Mariya anasunga zonsezi mu mtima mwake ndi kumazilingalira.
Maryamu ma meki ubassa utimum me sa ma kunna, unu gamara me Iruba.
20 Abusa anabwerera, akulemekeza ndi kuyamika Mulungu chifukwa cha zonse anazimva ndi kuziona, zomwe zinali monga anawuzidwira ndi angelo aja.
Anu hira itam me wa kuri. Ininonzo nan ununonzo Asere, barki imum me sa wa kunna, wa ira, ka si ubuka me sa wa kunna.
21 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, tsiku loti amuchite mdulidwe anamutcha Yesu, dzina limene mngelo anamupatsa asanabadwe.
Sa tiyee uwito-utari ta wuna sa adi gbari me, anya me niza Yeso, niza me sa Bibe bika dura ka Asere ba nyame ada Sārki uzika apuru amè.
22 Nthawi yoyeretsedwa kwawo itatha, monga mwa lamulo la Mose, Yosefe ndi Mariya anapita naye ku Yerusalemu kukamupereka kwa Ambuye.
Sa tiyee tusuro tawuna kasi u' inko utize ta Asere “Vat utuba uyoo uruma adi witi Asere me”.
23 (Monga mmene zinalembedwera mu lamulo la Ambuye kuti, “Muzikapereka kwa Ambuye mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa”),
Kasi unyertike U' inko utize ta Asere “Vat utuba uyoo uruma adi witi Asere me”.
24 ndi kupereka nsembe posunga zimene zinanenedwa mulamulo la Ambuye: “Njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri.”
Wa nya me unyanki kasi u' inko utize ta Asere “Mu hurbe muni muree nan matatabara marce”.
25 Ndipo taonani, mu Yerusalemu munali munthu wotchedwa Simeoni, amene anali wolungama ndi wodzipereka. Iye ankadikira chitonthozo cha Israeli, ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.
Ure unyu marani ujerusalem niza nume Siman, una biyan ba Asere mani ini ruba ilau. Mazin nunyara ubarka u Isaraila, Bibe ba Asere baazi nan me.
26 Mzimu Woyera anamuwululira kuti sadzafa asanaone Khristu wa Ambuye.
Bibe bilau ba Asere ba bezi me unu guna mada wono ba senke ma ira Asere Yeso.
27 Motsogozedwa ndi Mzimu Woyera, iye anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Makolo ake a Yesu atabwera naye kuti achite naye mwambo malingana ndi malamulo,
Uru wui Bibe bilau ba Asere bihan Siman udenge Asere. An ka coo me wa ēn Yeso vana uneze, kasi utanda nan u'inko utize ta Asere.
28 Simeoni anamunyamula mʼmanja mwake nayamika Mulungu, nati:
Ma gbindirko me abigiri ma nonziko Asere ma gu.
29 “Ambuye waulamuliro, monga munalonjeza, tsopano lolani kuti mtumiki wanu apite mu mtendere.
“Aname ca urere uweme madusa inna puru arum Asere, kasi ubuka uweme.
30 Pakuti maso anga aona chipulumutso chanu,
Barki sa aje am a'era nibussi nuweme,
31 chimene Inu munakonza pamaso pa anthu onse,
Sa wa wuza amu hennu manun vat.
32 kuwala kowunikira anthu a mitundu ina ndi kwa ulemerero kwa anthu anu Aisraeli.”
Ma saa mani mati roo uhana anuu uzati utarsa Asere nan ninonzo uhana anuu aweme Isarailawa”.
33 Abambo ndi amayi a Mwanayo anadabwa chifukwa cha zimene zinanenedwa za Iye.
Acoo avana me nan ka inoo we wa kunna urunta imum me sa mubuka.
34 Kenaka Simeoni anawadalitsa ndipo anati kwa Mariya amayi ake: “Mwana uyu wakonzedwa kukhala kugwa ndi kudzuka kwa ambiri mu Israeli, ndi kukhala chizindikiro chimene adzayankhula motsutsana nacho,
Siman ma nonziko we ma gun Maryamu a inoo me “Kunna memmerum Vana ugeme madi cukuno unaa urizo nan uhira wa nun gbardang anyimo Isaraila nan ubezi sa adi nyarime.
35 kotero kuti malingaliro a mitima ya ambiri adzawululidwa. Ndipo lupanga lidzabaya moyo wakonso.”
Uvira udi watti iruba iweme bati arusi muruba manu”.
36 Panalinso mneneri wamkazi, dzina lake Ana, mwana wa Fanuelo, wa fuko la Aseri. Anali wokalamba kwambiri; anakhala ndi mwamuna wake zaka zisanu ndi ziwiri atakwatiwa,
Unun kurzuzo utize ta Asere ahiran me unani zaa Hanatu. Ucaa ufanuyila nilem ni Ashiru mamu wuna uwari kang. Wa wuu tiwee usunare inna nyaa nan uruma umeme.
37 ndipo kenaka anakhala wamasiye mpaka pamene anali ndi zaka 84. Iye sanachoke mʼNyumba ya Mulungu koma ankapembedza usiku ndi usana, kusala kudya ndi kupemphera.
Ma zi'inti wee a'ino-uwitotari intini tinazi (84 years). Daki maceki udenge Asere ba inka tuma unu canti anyoo nan biringara niyee nan nuwui.
38 Pa nthawiyo pamene ankapita kwa iwo, iye anayamika Mulungu ndi kuyankhula za Mwanayo kwa onse amene ankayembekezera chipulumutso cha Yerusalemu.
Uganiya me ma nyene uhana ahira awe unu nonzo Asere, ma buki vat ande sa waazin nubee uburu Urshalima abanga a vana me.
39 Yosefe ndi Mariya atachita zonse zimene zinkafunikira ndi lamulo la Ambuye, anabwerera ku Galileya ku mudzi wa Nazareti.
Sa wa mara kondi nyani wa wuzi kasi u inko utize ta Asere, wa kuri Ugalili ani pin nuweme Unazarat.
40 Ndipo Mwanayo anakula nakhala wamphamvu; Iye anadzazidwa ndi nzeru, ndipo chisomo cha Mulungu chinali pa Iye.
Vaname ma uu mawu nikara, nan ukingizi urusa, nan ubenki Asere anicee nume.
41 Chaka chilichonse makolo ake ankapita ku Yerusalemu ku phwando la Paska.
Anka coo me waka haa Ujerusalem ingi niwee na kette barki u'idin Faska.
42 Iye ali ndi zaka khumi ndi ziwiri, anapita ku phwando, monga mwa mwambo.
Sa mawuna tiwe ukirau-tire, Wa kuri kurri uganiya u'idi utanda.
43 Phwando litatha, pamene makolo ake ankabwerera kwawo, mnyamata Yesu anatsalira ku Yerusalemu, koma iwo sanadziwe zimenezi.
Sa tiyee tu idi ta mara, wa tubi kurso ati kura. Yeso ma dii adumo Ujerusalem Sārki urusan anka coo me.
44 Poganiza kuti anali nawo mʼgulu lawo, anayenda tsiku limodzi. Kenaka anayamba kumufunafuna pakati pa abale awo ndi anzawo.
Wa bassa nan mazi nanni goo nanume sa wa haka nan we, wa hiri tanu. Wa tubi u nyara ume anyimo anu turra uweme nan aronni.
45 Atalephera kumupeza, anabwerera ku Yerusalemu kukamufuna.
Sa daki wa ira me ba, wa kuri Ujerusalem waka tunguno unyara ume abini me.
46 Patatha masiku atatu anamupeza ali mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, atakhala pakati pa aphunzitsi, akumvetsera ndi kuwafunsa mafunso.
Wawu tiyee titaru unu nyara ume wa tinka me udenge Asere, ma ciki atii anu bezizi, unu kunna nan nu'igizo uwe.
47 Aliyense amene anamumva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake ndi mayankho ake.
Vat andee sa wa kunna me wa meki ugamara urusa nan ukabara umeme.
48 Makolo ake atamuona, anadabwa. Amayi ake anati kwa Iye, “Mwanawe, watichitira zimenezi chifukwa chiyani? Abambo ako ndi ine takhala tili ndi nkhawa kukufunafuna Iwe.”
Sa wa ira me wa meki ugamara me kang. A'inome ma gun me “Vana, nyanini wa wuzan duru aname? Kunna, acoo uweme nan mi tizin nunyara uwe unu curnome Iruba”.
49 Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumandifunafuna? Kodi simukudziwa kuti ndikuyenera kukhala mʼnyumba ya Atate anga?”
Ma gun we, “Barki nyani izin nunyan um? Ita shi izi gbass incukuno akura acou um ba?”
50 Koma iwo sanazindikire chomwe Iye amatanthauza.
Daki wa rusa imum sa ma boo ba.
51 Kenaka anapita nawo ku Nazareti ndipo anawamvera iwo. Koma amayi ake anasunga zinthu zonsezi mu mtima mwawo.
Ma dusa akura nan we Unazarat ma tarsi tize tuweme. A'ino me ma inki Vat timum tigeme Iruba.
52 Ndipo Yesu anakula mu nzeru, msinkhu ndi chisomo cha Mulungu ndi anthu.
Yeso ma re'aje unu uzza nan nurusa, ma kuri ma kinki ukem ukaba ahira Asere nan nanuu.

< Luka 2 >