< Luka 2 >

1 Mʼmasiku amenewo Kaisara Augusto anapereka lamulo kuti kalembera achitike mʼdziko lonse la Aroma.
Just at this time an edict was issued by Caesar Augustus for the registration of the whole Empire.
2 (Uyu ndi kalembera woyamba amene anachitika pamene Kureniyo anali bwanamkubwa wa Siriya).
It was the first registration made during the governorship of Quirinius in Syria;
3 Ndipo aliyense anapita ku mzinda wa kwawo kukalembetsa.
and all went to be registered--every one to the town to which he belonged.
4 Choncho Yosefe anachoka ku Nazareti ku Galileya kupita ku Yudeya, ku Betelehemu ku mudzi wa Davide, chifukwa anali wa banja ndi fuko la Davide.
So Joseph went up from Galilee, from the town of Nazareth, to Judaea, to David's town of Bethlehem, because he was of the house and lineage of David,
5 Iye anapita kumeneko kukalembetsa pamodzi ndi Mariya, amene anapalana naye ubwenzi kuti akwatirane ndipo anali woyembekezera.
to have himself registered together with Mary, who was betrothed to him and was with child.
6 Ali kumeneko, nthawi inakwana yakuti mwana abadwe,
But while they were there, her full time came,
7 ndipo anabereka mwana wake woyamba, wamwamuna. Iye anamukulunga mʼnsalu ndi kumuyika modyera ngʼombe, chifukwa kunalibe malo mʼnyumba ya alendo.
and she gave birth to her first-born son, and wrapped Him round, and laid Him in a manger, because there was no room for them in the inn.
8 Ndipo kunali abusa amene amakhala ku dera lomwelo, kuyangʼanira ziweto zawo usiku.
Now there were shepherds in the same part of the country, keeping watch over their sheep by night in the open fields,
9 Mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iwo ndipo ulemerero wa Ambuye unawala mowazungulira. Iwo anachita mantha.
when suddenly an angel of the Lord stood by them, and the glory of the Lord shone round them; and they were filled with terror.
10 Koma mngeloyo anawawuza kuti, “Musachite mantha. Ine ndakubweretserani Uthenga Wabwino wachimwemwe chachikulu umene udzakhala wa anthu onse.
But the angel said to them, "Put away all fear; for I am bringing you good news of great joy--joy for all the People.
11 Lero mʼmudzi wa Davide wakubwadwirani Mpulumutsi; Iye ndi Khristu Ambuye.
For a Saviour who is the Anointed Lord is born to you to-day, in the town of David.
12 Ichi chidzakhala chizindikiro kwa inu: mukapeza mwana wakhanda wokutidwa ndi nsalu atagona modyera ngʼombe.”
And this is the token for you: you will find a babe wrapped in swaddling clothes and lying in a manger."
13 Mwadzidzidzi gulu lalikulu la angelo linaonekera pamodzi ndi mngeloyo, kuyamika Mulungu ndi kumati,
And immediately there was with the angel a multitude of the army of Heaven praising God and saying,
14 “Ulemerero kwa Mulungu mmwambamwamba, ndi mtendere kwa anthu pa dziko lapansi amene Iye akondwera nawo.”
"Glory be to God in the highest Heavens, And on earth peace among men who please Him!"
15 Angelowo atabwerera kumwamba, abusawo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni ku Betelehemu tikaone zinthu zomwe zachitika, zimene Ambuye atiwuza ife.”
Then, as soon as the angels had left them and returned to Heaven, the shepherds said to one another, "Let us now go over as far as Bethlehem and see this that has happened, which the Lord has made known to us."
16 Ndipo iwo anafulumira nyamuka nakapeza Mariya ndi Yosefe ndi mwana wakhanda, amene anagona modyera ngʼombe.
So they made haste and came and found Mary and Joseph, with the babe lying in the manger.
17 Pamene anamuona Iye, iwo anafotokoza zomwe anawuzidwa za mwanayo,
And when they saw the child, they told what had been said to them about Him;
18 ndipo onse amene anamva zimene abusawa ananena anadabwa.
and all who listened were astonished at what the shepherds told them.
19 Koma Mariya anasunga zonsezi mu mtima mwake ndi kumazilingalira.
But Mary treasured up all these things, often dwelling on them in her mind.
20 Abusa anabwerera, akulemekeza ndi kuyamika Mulungu chifukwa cha zonse anazimva ndi kuziona, zomwe zinali monga anawuzidwira ndi angelo aja.
And the shepherds returned, glorifying and praising God for all that they had heard and seen in accordance with the announcement made to them.
21 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, tsiku loti amuchite mdulidwe anamutcha Yesu, dzina limene mngelo anamupatsa asanabadwe.
When eight days had passed and the time for circumcising Him had come, He was called JESUS, the name given Him by the angel before His conception in the womb.
22 Nthawi yoyeretsedwa kwawo itatha, monga mwa lamulo la Mose, Yosefe ndi Mariya anapita naye ku Yerusalemu kukamupereka kwa Ambuye.
And when the days for their purification appointed by the Law of Moses had passed, they took Him up to Jerusalem to present Him to the Lord--
23 (Monga mmene zinalembedwera mu lamulo la Ambuye kuti, “Muzikapereka kwa Ambuye mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa”),
as it is written in the Law of the Lord: "Every first-born male shall be called holy to the Lord."
24 ndi kupereka nsembe posunga zimene zinanenedwa mulamulo la Ambuye: “Njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri.”
And they also offered a sacrifice as commanded in the Law of the Lord, "a pair of turtle doves or two young pigeons."
25 Ndipo taonani, mu Yerusalemu munali munthu wotchedwa Simeoni, amene anali wolungama ndi wodzipereka. Iye ankadikira chitonthozo cha Israeli, ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.
Now there was a man in Jerusalem of the name of Symeon, an upright and God-fearing man, who was waiting for the consolation of Israel, and the Holy Spirit was upon him.
26 Mzimu Woyera anamuwululira kuti sadzafa asanaone Khristu wa Ambuye.
To him it had been revealed by the Holy Spirit that he should not see death until he had seen the Lord's Anointed One.
27 Motsogozedwa ndi Mzimu Woyera, iye anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Makolo ake a Yesu atabwera naye kuti achite naye mwambo malingana ndi malamulo,
Led by the Spirit he came to the Temple; and when the parents brought in the child Jesus to do with regard to Him according to the custom of the Law,
28 Simeoni anamunyamula mʼmanja mwake nayamika Mulungu, nati:
he took Him up in his arms and blessed God and said,
29 “Ambuye waulamuliro, monga munalonjeza, tsopano lolani kuti mtumiki wanu apite mu mtendere.
"Now, O Sovereign Lord, Thou dost send Thy servant away in peace, in fulfilment of Thy word,
30 Pakuti maso anga aona chipulumutso chanu,
Because mine eyes have seen Thy salvation,
31 chimene Inu munakonza pamaso pa anthu onse,
Which Thou hast made ready in the sight of all nations--
32 kuwala kowunikira anthu a mitundu ina ndi kwa ulemerero kwa anthu anu Aisraeli.”
A light to shine upon the Gentiles, And the glory of Thy people Israel."
33 Abambo ndi amayi a Mwanayo anadabwa chifukwa cha zimene zinanenedwa za Iye.
And while the child's father and mother were wondering at the words of Symeon concerning Him,
34 Kenaka Simeoni anawadalitsa ndipo anati kwa Mariya amayi ake: “Mwana uyu wakonzedwa kukhala kugwa ndi kudzuka kwa ambiri mu Israeli, ndi kukhala chizindikiro chimene adzayankhula motsutsana nacho,
Symeon blessed them and said to Mary the mother, "This child is appointed for the falling and the uprising of many in Israel and for a token to be spoken against;
35 kotero kuti malingaliro a mitima ya ambiri adzawululidwa. Ndipo lupanga lidzabaya moyo wakonso.”
and a sword will pierce through your own soul also; that the reasonings in many hearts may be revealed."
36 Panalinso mneneri wamkazi, dzina lake Ana, mwana wa Fanuelo, wa fuko la Aseri. Anali wokalamba kwambiri; anakhala ndi mwamuna wake zaka zisanu ndi ziwiri atakwatiwa,
There was also Anna, a prophetess, the daughter of Phanuel, belonging to the tribe of Asher. She was of a very great age, having had after her maidenhood seven years of married life,
37 ndipo kenaka anakhala wamasiye mpaka pamene anali ndi zaka 84. Iye sanachoke mʼNyumba ya Mulungu koma ankapembedza usiku ndi usana, kusala kudya ndi kupemphera.
and then being a widow of eighty-four years. She was never absent from the Temple, but worshipped, by day and by night, with fasting and prayer.
38 Pa nthawiyo pamene ankapita kwa iwo, iye anayamika Mulungu ndi kuyankhula za Mwanayo kwa onse amene ankayembekezera chipulumutso cha Yerusalemu.
And coming up just at that moment, she gave thanks to God, and spoke about the child to all who were expecting the deliverance of Jerusalem.
39 Yosefe ndi Mariya atachita zonse zimene zinkafunikira ndi lamulo la Ambuye, anabwerera ku Galileya ku mudzi wa Nazareti.
Then, as soon as they had accomplished all that the Law required, they returned to Galilee to their own town of Nazareth.
40 Ndipo Mwanayo anakula nakhala wamphamvu; Iye anadzazidwa ndi nzeru, ndipo chisomo cha Mulungu chinali pa Iye.
And the child grew and became strong and full of wisdom, and the favour of God rested upon Him.
41 Chaka chilichonse makolo ake ankapita ku Yerusalemu ku phwando la Paska.
Now His parents used to go up year by year to Jerusalem at the Feast of the Passover.
42 Iye ali ndi zaka khumi ndi ziwiri, anapita ku phwando, monga mwa mwambo.
And when He was twelve years old they went up as was customary at the time of the Feast, and,
43 Phwando litatha, pamene makolo ake ankabwerera kwawo, mnyamata Yesu anatsalira ku Yerusalemu, koma iwo sanadziwe zimenezi.
after staying the full number of days, when they started back home the boy Jesus remained behind in Jerusalem. His parents did not discover this,
44 Poganiza kuti anali nawo mʼgulu lawo, anayenda tsiku limodzi. Kenaka anayamba kumufunafuna pakati pa abale awo ndi anzawo.
but supposing Him to be in the travelling company, they proceeded a day's journey. Then they searched up and down for Him among their relatives and acquaintances;
45 Atalephera kumupeza, anabwerera ku Yerusalemu kukamufuna.
but being unable to find Him they returned to Jerusalem, making anxious inquiry for Him.
46 Patatha masiku atatu anamupeza ali mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, atakhala pakati pa aphunzitsi, akumvetsera ndi kuwafunsa mafunso.
On the third day they found Him in the Temple sitting among the Rabbis, both listening to them and asking them questions,
47 Aliyense amene anamumva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake ndi mayankho ake.
while all who heard Him were astonished at His intelligence and at the answers He gave.
48 Makolo ake atamuona, anadabwa. Amayi ake anati kwa Iye, “Mwanawe, watichitira zimenezi chifukwa chiyani? Abambo ako ndi ine takhala tili ndi nkhawa kukufunafuna Iwe.”
When they saw Him, they were smitten with amazement, and His mother said to Him, "My child, why have you behaved thus to us? Your father and I have been searching for you in anguish."
49 Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumandifunafuna? Kodi simukudziwa kuti ndikuyenera kukhala mʼnyumba ya Atate anga?”
"Why is it that you have been searching for me?" He replied; "did you not know that it is my duty to be engaged upon my Father's business?"
50 Koma iwo sanazindikire chomwe Iye amatanthauza.
But they did not understand the significance of these words.
51 Kenaka anapita nawo ku Nazareti ndipo anawamvera iwo. Koma amayi ake anasunga zinthu zonsezi mu mtima mwawo.
Then He went down with them and came to Nazareth, and was always obedient to them; but His mother carefully treasured up all these incidents in her memory.
52 Ndipo Yesu anakula mu nzeru, msinkhu ndi chisomo cha Mulungu ndi anthu.
And as Jesus grew older He gained in both wisdom and stature, and in favour with God and man.

< Luka 2 >