< Luka 2 >

1 Mʼmasiku amenewo Kaisara Augusto anapereka lamulo kuti kalembera achitike mʼdziko lonse la Aroma.
Men det skete i de dage, at en Befaling udgik fra Kejser Augustus, at al Verden skulde skrives i Mandtal.
2 (Uyu ndi kalembera woyamba amene anachitika pamene Kureniyo anali bwanamkubwa wa Siriya).
(Denne første Indskrivning skete, da Kvirinius var Landshøvding i Syrien, )
3 Ndipo aliyense anapita ku mzinda wa kwawo kukalembetsa.
Og alle gik for at lade sig indskrive, hver til sin By.
4 Choncho Yosefe anachoka ku Nazareti ku Galileya kupita ku Yudeya, ku Betelehemu ku mudzi wa Davide, chifukwa anali wa banja ndi fuko la Davide.
Og også Josef gik op fra Galilæa, fra Byen Nazareth til Judæa til Davids By, som kaldes Bethlehem, fordi han var af Davids Hus og Slægt,
5 Iye anapita kumeneko kukalembetsa pamodzi ndi Mariya, amene anapalana naye ubwenzi kuti akwatirane ndipo anali woyembekezera.
for at lade sig indskrive tillige med Maria, sin trolovede, som var frugtsommelig.
6 Ali kumeneko, nthawi inakwana yakuti mwana abadwe,
Men det skete, medens de vare der, blev Tiden fuldkommet til, at hun skulde føde.
7 ndipo anabereka mwana wake woyamba, wamwamuna. Iye anamukulunga mʼnsalu ndi kumuyika modyera ngʼombe, chifukwa kunalibe malo mʼnyumba ya alendo.
Og hun fødte sin Søn, den førstefødte, og svøbte ham og lagde ham i en Krybbe; thi der var ikke Rum for dem i Herberget.
8 Ndipo kunali abusa amene amakhala ku dera lomwelo, kuyangʼanira ziweto zawo usiku.
Og der var Hyrder i den samme Egn, som lå ude på Marken og holdt Nattevagt over deres Hjord.
9 Mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iwo ndipo ulemerero wa Ambuye unawala mowazungulira. Iwo anachita mantha.
Og se, en Herrens Engel stod for dem, og Herrens Herlighed skinnede om dem, og de frygtede såre
10 Koma mngeloyo anawawuza kuti, “Musachite mantha. Ine ndakubweretserani Uthenga Wabwino wachimwemwe chachikulu umene udzakhala wa anthu onse.
Og Engelen sagde til dem: "Frygter ikke; thi se, jeg forkynder eder en stor Glæde, som skal være for hele Folket.
11 Lero mʼmudzi wa Davide wakubwadwirani Mpulumutsi; Iye ndi Khristu Ambuye.
Thi eder er i dag en Frelser født, som er den Herre Kristus i Davids By.
12 Ichi chidzakhala chizindikiro kwa inu: mukapeza mwana wakhanda wokutidwa ndi nsalu atagona modyera ngʼombe.”
Og dette skulle I have til Tegn: I skulle finde et Barn svøbt, liggende i en Krybbe."
13 Mwadzidzidzi gulu lalikulu la angelo linaonekera pamodzi ndi mngeloyo, kuyamika Mulungu ndi kumati,
Og straks var der med Engelen en himmelsk Hærskares Mangfoldighed, som lovede Gud og sagde:
14 “Ulemerero kwa Mulungu mmwambamwamba, ndi mtendere kwa anthu pa dziko lapansi amene Iye akondwera nawo.”
"Ære være Gud i det højeste! og Fred på Jorden! i Mennesker Velbehag!
15 Angelowo atabwerera kumwamba, abusawo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni ku Betelehemu tikaone zinthu zomwe zachitika, zimene Ambuye atiwuza ife.”
Og det skete, da Englene vare farne fra dem til Himmelen, sagde Hyrderne til hverandre: "Lader os dog gå til Bethlehem og se dette, som er sket, hvilket Herren har kundgjort os."
16 Ndipo iwo anafulumira nyamuka nakapeza Mariya ndi Yosefe ndi mwana wakhanda, amene anagona modyera ngʼombe.
Og de skyndte sig og kom og fandt både Maria og Josef, og Barnet liggende i Krybben.
17 Pamene anamuona Iye, iwo anafotokoza zomwe anawuzidwa za mwanayo,
Men da de så det, kundgjorde de, hvad der var talt til dem om dette Barn.
18 ndipo onse amene anamva zimene abusawa ananena anadabwa.
Og alle de, som hørte det, undrede sig over det, der blev talt til dem af Hyrderne.
19 Koma Mariya anasunga zonsezi mu mtima mwake ndi kumazilingalira.
Men Maria gemte alle disse Ord og overvejede dem i sit Hjerte.
20 Abusa anabwerera, akulemekeza ndi kuyamika Mulungu chifukwa cha zonse anazimva ndi kuziona, zomwe zinali monga anawuzidwira ndi angelo aja.
Og Hyrderne vendte tilbage, idet de priste og lovede Gud for alt, hvad de havde hørt og set, således som der var talt til dem.
21 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, tsiku loti amuchite mdulidwe anamutcha Yesu, dzina limene mngelo anamupatsa asanabadwe.
Og da otte Dage vare fuldkommede, så han skulde omskæres, da blev hans Navn kaldt Jesus, som det var kaldt af Engelen, før han blev undfangen i Moders Liv.
22 Nthawi yoyeretsedwa kwawo itatha, monga mwa lamulo la Mose, Yosefe ndi Mariya anapita naye ku Yerusalemu kukamupereka kwa Ambuye.
Og da deres Renselsesdage efter Mose Lov vare fuldkommede, bragte de ham op til Jerusalem for at fremstille ham for Herren,
23 (Monga mmene zinalembedwera mu lamulo la Ambuye kuti, “Muzikapereka kwa Ambuye mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa”),
som der er skrevet i Herrens Lov, at alt Mandkøn, som åbner Moders Liv, skal kaldes helligt for Herren,
24 ndi kupereka nsembe posunga zimene zinanenedwa mulamulo la Ambuye: “Njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri.”
og for at bringe Offer efter det, som er sagt i Herrens Lov, et Par Turtelduer eller to unge Duer.
25 Ndipo taonani, mu Yerusalemu munali munthu wotchedwa Simeoni, amene anali wolungama ndi wodzipereka. Iye ankadikira chitonthozo cha Israeli, ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.
Og se, der var en Mand i Jerusalem ved Navn Simeon, og denne Mand var retfærdig og gudfrygtig og forventede Israels Trøst, og den Helligånd var over ham.
26 Mzimu Woyera anamuwululira kuti sadzafa asanaone Khristu wa Ambuye.
Og det var varslet ham af den Helligånd, at han ikke skulde se Døden, førend han havde set Herrens Salvede.
27 Motsogozedwa ndi Mzimu Woyera, iye anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Makolo ake a Yesu atabwera naye kuti achite naye mwambo malingana ndi malamulo,
Og han kom af Åndens Drift til Helligdommen; og idet Forældrene bragte Barnet Jesus ind for at gøre med ham efter Lovens Skik,
28 Simeoni anamunyamula mʼmanja mwake nayamika Mulungu, nati:
da tog han det på sine Arme og priste Gud og sagde:
29 “Ambuye waulamuliro, monga munalonjeza, tsopano lolani kuti mtumiki wanu apite mu mtendere.
"Herre! nu lader du din Tjener fare i Fred, efter dit Ord.
30 Pakuti maso anga aona chipulumutso chanu,
Thi mine Øjne have set din Frelse,
31 chimene Inu munakonza pamaso pa anthu onse,
som du beredte for alle Folkeslagenes Åsyn,
32 kuwala kowunikira anthu a mitundu ina ndi kwa ulemerero kwa anthu anu Aisraeli.”
et Lys til at oplyse Hedningerne og en Herlighed for dit Folk Israel."
33 Abambo ndi amayi a Mwanayo anadabwa chifukwa cha zimene zinanenedwa za Iye.
Og hans Fader og hans Moder undrede sig over de Ting, som bleve sagte om ham.
34 Kenaka Simeoni anawadalitsa ndipo anati kwa Mariya amayi ake: “Mwana uyu wakonzedwa kukhala kugwa ndi kudzuka kwa ambiri mu Israeli, ndi kukhala chizindikiro chimene adzayankhula motsutsana nacho,
Og Simeon velsignede dem og sagde til hans Moder Maria: "Se, denne er sat mange i Israel til Fald og Oprejsning og til et Tegn, som imodsiges,
35 kotero kuti malingaliro a mitima ya ambiri adzawululidwa. Ndipo lupanga lidzabaya moyo wakonso.”
ja, også din egen Sjæl skal et Sværd gennemtrænge! for at mange Hjerters Tanker skulle åbenbares."
36 Panalinso mneneri wamkazi, dzina lake Ana, mwana wa Fanuelo, wa fuko la Aseri. Anali wokalamba kwambiri; anakhala ndi mwamuna wake zaka zisanu ndi ziwiri atakwatiwa,
Og der var en Profetinde Anna, Fanuels Datter, af Asers Stamme; hun var meget fremrykket i Alder, havde levet syv År med sin Mand efter sin Jomfrustand
37 ndipo kenaka anakhala wamasiye mpaka pamene anali ndi zaka 84. Iye sanachoke mʼNyumba ya Mulungu koma ankapembedza usiku ndi usana, kusala kudya ndi kupemphera.
og var nu en Enke ved fire og firsindstyve År, og hun veg ikke fra Helligdommen, tjenende Gud med Faste og Bønner Nat og Dag.
38 Pa nthawiyo pamene ankapita kwa iwo, iye anayamika Mulungu ndi kuyankhula za Mwanayo kwa onse amene ankayembekezera chipulumutso cha Yerusalemu.
Og hun trådte til i den samme Stund og priste Gud og talte om ham til alle, som forventede Jerusalems Forløsning.
39 Yosefe ndi Mariya atachita zonse zimene zinkafunikira ndi lamulo la Ambuye, anabwerera ku Galileya ku mudzi wa Nazareti.
Og da de havde fuldbyrdet alle Ting efter Herrens Lov, vendte de tilbage til Galilæa til deres egen By Nazareth.
40 Ndipo Mwanayo anakula nakhala wamphamvu; Iye anadzazidwa ndi nzeru, ndipo chisomo cha Mulungu chinali pa Iye.
Men Barnet voksede og blev stærkt og blev fuldt af Visdom: og Guds Nåde var over det.
41 Chaka chilichonse makolo ake ankapita ku Yerusalemu ku phwando la Paska.
Og hans Forældre droge hvert År op til Jerusalem på Påskehøjtiden.
42 Iye ali ndi zaka khumi ndi ziwiri, anapita ku phwando, monga mwa mwambo.
Og da han var bleven tolv År gammel, og de gik op efter Højtidens Sædvane
43 Phwando litatha, pamene makolo ake ankabwerera kwawo, mnyamata Yesu anatsalira ku Yerusalemu, koma iwo sanadziwe zimenezi.
og havde tilendebragt de Dage, blev Barnet Jesus i Jerusalem, medens de droge hjem, og hans Forældre mærkede det ikke.
44 Poganiza kuti anali nawo mʼgulu lawo, anayenda tsiku limodzi. Kenaka anayamba kumufunafuna pakati pa abale awo ndi anzawo.
Men da de mente, at han var i Rejsefølget, kom de en Dags Rejse frem, og de ledte efter ham iblandt deres Slægtninge og Kyndinge.
45 Atalephera kumupeza, anabwerera ku Yerusalemu kukamufuna.
Og da de ikke fandt ham, vendte de tilbage til Jerusalem og ledte efter ham.
46 Patatha masiku atatu anamupeza ali mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, atakhala pakati pa aphunzitsi, akumvetsera ndi kuwafunsa mafunso.
Og det skete efter tre Dage, da fandt de ham i Helligdommen, hvor han sad midt iblandt Lærerne og både hørte på dem og adspurgte dem.
47 Aliyense amene anamumva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake ndi mayankho ake.
Men alle, som hørte ham, undrede sig såre over hans Forstand og Svar.
48 Makolo ake atamuona, anadabwa. Amayi ake anati kwa Iye, “Mwanawe, watichitira zimenezi chifukwa chiyani? Abambo ako ndi ine takhala tili ndi nkhawa kukufunafuna Iwe.”
Og da de så ham, bleve de forfærdede; og hans Moder sagde til ham:"Barn! hvorfor gjorde du således imod os? Se, din Fader og jeg have ledt efter dig med Smerte."
49 Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumandifunafuna? Kodi simukudziwa kuti ndikuyenera kukhala mʼnyumba ya Atate anga?”
Og han sagde til dem: "Hvorfor ledte I efter mig? Vidste I ikke, at jeg bør være i min Faders Gerning?"
50 Koma iwo sanazindikire chomwe Iye amatanthauza.
Og de forstode ikke det Ord, som han talte til dem.
51 Kenaka anapita nawo ku Nazareti ndipo anawamvera iwo. Koma amayi ake anasunga zinthu zonsezi mu mtima mwawo.
Og han drog ned med dem og kom til Nazareth og var dem lydig og hans Moder gemte alle de Ord i sit Hjerte.
52 Ndipo Yesu anakula mu nzeru, msinkhu ndi chisomo cha Mulungu ndi anthu.
Og Jesus forfremmedes i Visdom og Alder og yndest hos Gud og Mennesker.

< Luka 2 >