< Luka 19 >

1 Yesu analowa mu Yeriko napitirira.
Jésus étant entré à Jéricho, traversa la ville.
2 Kunali munthu kumeneko dzina lake Zakeyu; iye anali mkulu wa wolandira msonkho ndipo anali wolemera.
Et un homme riche, nommé Zachée, chef des publicains,
3 Iye ankafuna kuona Yesu kuti ndani, koma pokhala wamfupi sanathe chifukwa cha gulu la anthu.
cherchait à voir qui était Jésus, et il ne le pouvait à cause de la foule, car il était de petite taille.
4 Choncho iye anathamangira patsogolo ndipo anakwera mu mtengo wamkuyu kuti amuone Iye, pakuti Yesu ankadutsa njira imeneyo.
Il courut donc en avant, et monta sur un sycomore pour le voir, parce qu'il devait passer par là.
5 Yesu atafika pa malopo, anayangʼana mmwamba ndipo anati kwa iye, “Zakeyu, tsika msangamsanga. Ine ndiyenera kukhala mʼnyumba mwako lero.”
Lorsque Jésus fut arrivé à cet endroit, il leva les yeux, et l'ayant aperçu, lui dit: «Zachée, hâte-toi de descendre, car il faut que je loge aujourd'hui chez toi.»
6 Ndipo nthawi yomweyo anatsika ndipo anamulandira mosangalala.
Zachée se hâta de descendre, et le reçut avec joie.
7 Anthu onse ataona zimenezi anayamba kungʼungʼudza, nati, “Iye akupita kuti akakhale mlendo wa wochimwa.”
Voyant cela, tous murmuraient, et disaient: «Il est allé loger chez un homme pécheur.»
8 Koma Zakeyu anayimirira ndipo anati kwa Ambuye, “Taonani Ambuye! Theka la chuma changa ndipereka kwa osauka ndipo ngati ndinamubera wina aliyense pa chilichonse, ndidzamubwezera mochulukitsa kanayi.”
Cependant Zachée se présentant devant le Seigneur, lui dit: «Voici, Seigneur, je donne la moitié de mes biens aux pauvres, et si j'ai fait tort à quelqu'un en quoi que ce soit, je lui rends le quadruple.»
9 Yesu anati kwa iye, “Lero chipulumutso chafika mʼnyumba ino, chifukwa munthu uyu nayenso ndi mwana wa Abrahamu.
Jésus lui dit: «Le salut est venu aujourd'hui sur cette maison, parce que celui-ci est aussi un fils d'Abraham;
10 Pajatu Mwana wa Munthu anabwera kudzafunafuna ndi kupulumutsa chotayikacho.”
car le Fils de l'homme est venu chercher et sauver ce qui était perdu.»
11 Pamene iwo ankamvera izi, Iye anapitiriza kuwawuza fanizo, chifukwa Iye anali kufupi ndi Yerusalemu ndipo anthu ankaganiza kuti ufumu wa Mulungu ukanaoneka nthawi yomweyo.
Comme on écoutait sa parole, il ajouta une parabole, parce qu'il était près de Jérusalem, et qu'on s'imaginait que le royaume de Dieu allait paraître immédiatement.
12 Iye anati, “Munthu wa banja laufumu anapita ku dziko lakutali kukadzozedwa ufumu ndipo kenaka abwerenso kwawo.
Il dit donc: «Un homme de haute naissance s'en alla dans un pays lointain, pour être investi de la royauté, et revenir ensuite.
13 Tsono iye anayitana antchito ake khumi ndi kuwapatsa ndalama khumi. Iye anati, ‘Gwiritsani ntchito ndalama izi mpaka nditabwerera.’
Il appela dix de ses serviteurs, leur donna dix mines, et leur dit: «Faites- les valoir, jusqu’à ce que je revienne.»
14 “Koma anthu ake anamuda ndipo anatuma nthumwi pambuyo pake kukanena kuti, ‘Sitikufuna munthuyu kuti akhale mfumu yathu.’
Mais ses concitoyens, qui le haïssaient, envoyèrent une ambassade après lui, pour dire: «Nous ne voulons pas qu'il règne sur nous.»
15 “Iye analandira ufumuwo ngakhale zinali zotero, ndipo anabwerera kwawo. Kenaka iye anatumiza uthenga kwa antchito ake amene anawapatsa ndalama aja, ndi cholinga chakuti adziwe chimene anapindula nazo.
Quand il fut de retour, après avoir été investi de la royauté, il lit appeler ses serviteurs à qui il avait remis son argent, afin de connaître ceux qui l'avaient fait valoir, et ce qu'ils avaient gagné.
16 “Woyamba anabwera ndipo anati, ‘Bwana ndalama zanu zapindula khumi zina.’
Le premier serviteur vint, et dit: «Seigneur, ta mine en a rapporté dix autres.»
17 “Bwana wakeyo anayankha kuti, Wachita bwino wantchito wabwino. ‘Chifukwa wakhulupirika pa zinthu zazingʼono, lamulira mizinda khumi.’
Et le roi lui dit: «C'est bien, bon serviteur, puisque tu as été fidèle dans une chose de minime valeur, reçois le gouvernement de dix villes.»
18 “Wachiwiri anabwera ndipo anati, ‘Bwana, ndalama zanu zapindula zisanu zina.’
Le second vint, et dit: «Seigneur, ta mine en a produit cinq autres.»
19 “Bwana anayankha kuti, ‘Iwe lamulira mizinda isanu.’
Le roi lui dit de même: «Toi aussi, gouverne cinq villes.»
20 “Kenaka wantchito wina anabwera ndipo anati, ‘Bwana, ndalama yanu nayi; ine ndinayibisa ndi kuyisunga mʼkansalu.
Le troisième vint et dit: «Seigneur, voici ta mine que j'ai gardée soigneusement dans un linge,
21 Ine ndimakuopani, chifukwa ndinu munthu wowuma mtima. Inu mumatenga chimene simunachiyike ndi kukolola chimene simunadzale.’
car je te craignais, parce que tu es un homme rigide: tu retires l'argent que tu n'as pas placé, et tu moissonnes ce que tu n'as pas semé.»
22 “Bwana wake anayankha kuti, ‘Ine ndikukuweruza iwe ndi mawu ako omwewo. Ndiwe wantchito woyipa. Kani umadziwa kuti ndine munthu wowuma mtima ndi wotenga chimene sindinasungitse, ndi kukolola chimene sindinadzale?
Le roi lui dit: «Mauvais serviteur, je te jugerai, sur tes propres paroles. Tu savais que je suis un homme rigide, qui retire l’argent qu'il n'a pas placé, et qui moissonne ce qu'il n'a pas semé!
23 Nanga nʼchifukwa chiyani sunasungitse ndalama yanga, kuti ine pobwera, ndidzayitenge ndi chiwongoladzanja?’
pourquoi donc n'as-tu pas mis mon argent dans une banque? et à mon retour, je l'aurais retiré avec intérêt.
24 “Ndipo iye anawuza amene anayimirira pafupi kuti, ‘Tengani ndalama yake ndi kumupatsa amene ali ndi ndalama khumiyo!’”
Puis, il dit à ses gardes: «Otez-lui cette mine, et la donnez à celui qui en a dix.»
25 Iwo anati, “Bwana iyeyu ali nazo kale khumi!”
— Ils lui dirent: «Seigneur, il en a déjà dix.»
26 Iye anayankha kuti, “Ndikukuwuzani kuti, aliyense amene ali nazo, adzapatsidwa zambiri, koma amene alibe, adzalandidwa ngakhale chimene ali nacho.
— «Je vous dis que l'on donnera à tout homme qui a; quant à celui qui n'a pas, on lui ôtera même ce qu'il a...
27 Tsono adani anga aja amene sankafuna kuti ndikhale mfumu yawo, abweretseni pano ndi kuwapha ine ndikuona.”
Seulement, amenez ici mes ennemis, ces gens qui n'ont pas voulu que je règne sur eux, et les égorgez en ma présence.»
28 Yesu atatha kunena izi, anayendabe kupita ku Yerusalemu.
Ayant ainsi parlé, Jésus se mit en marche, en tête de la foule, pour monter à Jérusalem.
29 Iye atayandikira ku Betifage ndi Betaniya pa phiri lotchedwa Olivi, Iye anatuma awiri a ophunzira nati kwa iwo,
Lorsqu'il approcha de Bethphagé et de Béthanie, vers la montagne appelée Bois d'oliviers, il envoya deux de ses disciples,
30 “Pitani mʼmudzi uli patsogolo panu, mukakalowa mʼmudzimo, mukapeza mwana wabulu womangiriridwa amene wina aliyense sanakwerepo. Mukamumasule ndi kubwera naye kuno.
en disant: «Allez à ce village qui est en face; en y entrant vous trouverez un ânon attaché, sur lequel jamais homme ne s'est assis: détachez-le, et amenez-le moi.
31 Ngati wina aliyense akakufunsani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mukumumasula mwana buluyo?’ Mukamuwuze kuti, ‘Ambuye akumufuna.’”
Si quelqu'un vous demande pourquoi vous le détachez, vous lui direz: «Parce que le Seigneur en a besoin.»
32 Otumidwawo anapita nakamupeza mwana wabulu monga momwe Yesu anawawuzira.
Ceux qui étaient envoyés partirent, et trouvèrent les choses comme Jésus le leur avait dit.
33 Pamene ankamasula mwana wabuluyo, eni ake anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukumasula mwana wabuluyo?”
Comme ils détachaient l'ânon, les maîtres de l'animal leur dirent: «Pourquoi détachez-vous cet ânon?»
34 Iwo anayankha kuti, “Ambuye akumufuna.”
Ils dirent: «Le Seigneur en a besoin, »
35 Iwo anabweretsa buluyo kwa Yesu, naponya zovala zawo pa bulupo ndi kumukwezapo Yesu.
et ils l'amenèrent à Jésus. Puis ayant jeté leurs manteaux sur l'ânon, ils y firent monter Jésus.
36 Pamene ankapita, anthu anayala zovala zawo mu msewu.
Pendant que Jésus cheminait, les gens étendaient leurs manteaux sur la route;
37 Iye atafika pafupi ndi pamene msewu umatsikira ku phiri la Olivi, gulu lonse la ophunzira linayamba kuyamika Mulungu mwachimwemwe ndi mawu ofuwula chifukwa cha zodabwitsa zonse anaziona.
mais lorsqu'il approcha de Jérusalem, déjà à la descente de la montagne des Oliviers, toute la foule des disciples, transportée d'allégresse, se mit à louer Dieu à haute voix de tous les miracles qu'elle avait vus.
38 “Yodala mfumu imene ikubwera mʼdzina la Ambuye!” “Mtendere kumwamba ndi ulemerero mmwambamwamba!”
Elle disait: «Béni soit le roi qui vient au nom du Seigneur!» «Paix dans le ciel, et gloire dans les lieux très-hauts!»
39 Ena mwa Afarisi mʼgulumo anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, adzudzuleni ophunzira anu!”
Quelques pharisiens mêlés à la foule, dirent à Jésus: «Maître, reprends tes disciples.»
40 Iye anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani kuti, ngati atakhala chete, miyala idzafuwula.”
Il répondit: «Je vous dis que s'ils se taisent, les pierres crieront.»
41 Iye atayandikira ku Yerusalemu ndi kuona mzindawo, anawulirira
Quand il fut proche de Jérusalem, à la vue de cette ville, il pleura sur elle, et dit:
42 nati, “Iwe ukanadziwa lero lino zinthu zokubweretsera mtendere, koma tsopano zabisikira maso ako.
«Ah! si tu connaissais, toi aussi, du moins en ce jour qui t'est donné, les choses qui appartiennent à ta paix! Hélas! elles sont cachées à tes yeux.
43 Pakuti masiku adzabwera pamene adani ako adzamanga mitumbira yankhondo nakuzungulira, nadzakutsekereza mbali zonse.
Des jours de malheur fondront sur toi: tes ennemis t'environneront de tranchées, ils t'investiront, ils te serreront de toutes parts,
44 Iwo adzakugwetsera pansi, iwe, ana ako onse a mʼkati mwako. Iwo sadzasiya mwa iwe mwala wina pa unzake, chifukwa sunazindikire nthawi ya kubwera kwa Mulungu.”
ils te détruiront, toi et tes enfants qui sont dans ton sein, et ils ne te laisseront pierre sur pierre, parce que tu n'as pas connu le temps où tu as été visitée.»
45 Kenaka Iye analowa mʼdera la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kutulutsa kunja amene amachita malonda.
Ensuite, étant entré dans le temple, il se mit à chasser les vendeurs, en leur disant:
46 Iye anawawuza kuti, “Zinalembedwa kuti Nyumba yanga idzakhala nyumba ya mapemphero, koma inu mwayisadutsa phanga la achifwamba.”
«Il est écrit: «Ma maison sera une maison de prière, » mais vous, vous en avez fait «une caverne de voleurs.»
47 Tsiku lililonse amaphunzitsa mʼNyumba ya Mulungu. Koma akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo ndi atsogoleri pakati pa anthu amayesetsa kuti amuphe.
Jésus passait toutes ses journées à enseigner dans le temple. Les principaux sacrificateurs, les scribes, ainsi que les grands cherchaient à le faire périr;
48 Komabe iwo sanathe kupeza njira ina iliyonse kuti achite izi, chifukwa anthu onse anakhulupirira mawu ake.
mais ils ne savaient comment s'y prendre, car tout le peuple s'attachait à lui pour l'entendre.

< Luka 19 >