< Luka 18 >
1 Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke.
Jésus leur raconta une parabole, pour montrer qu'il faut prier toujours, sans jamais se lasser.
2 Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu.
Il dit: Il y avait dans une ville un juge qui ne craignait point Dieu, et qui n'avait d'égards pour aucun homme.
3 Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’
Il y avait aussi dans cette ville une veuve, qui venait à lui et lui disait: Fais-moi justice de ma partie adverse.
4 “Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu,
Pendant longtemps, il ne le voulut pas. Mais ensuite, il se dit en lui-même: Quoique je ne craigne pas Dieu et que je n'aie d'égards pour aucun homme,
5 koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’”
néanmoins, comme cette veuve m'importune, je lui ferai justice, afin qu'elle ne vienne pas toujours me rompre la tête.
6 Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena.
Puis le Seigneur ajouta: Vous entendez ce que dit le juge inique?
7 Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira?
Et Dieu ne ferait pas justice à ses élus, qui crient à lui jour et nuit, et il tarderait à les secourir!
8 Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”
Je vous dis qu'il leur fera prompte justice. Mais quand le Fils de l'homme viendra, trouvera-t-il la foi sur la terre?
9 Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse.
Il dit aussi cette parabole, en vue de certaines personnes qui se flattaient d'être justes et qui méprisaient les autres:
10 “Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho.
Deux hommes montèrent au temple pour prier; l'un était pharisien, et l'autre était péager.
11 Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu.
Le pharisien, se tenant debout, priait ainsi en lui-même: Dieu, je te rends grâces de ce que je ne suis pas comme le reste des hommes, qui sont rapaces, injustes, adultères, ni même comme ce péager.
12 Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’
Je jeûne deux fois la semaine; je donne la dîme de tous mes revenus.
13 “Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’
Le péager, se tenant éloigné, n'osait pas même lever les yeux au ciel; mais il se frappait la poitrine, en disant: O Dieu, sois apaisé envers moi, qui suis un pécheur!
14 “Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”
Je vous le déclare, celui-ci s'en retourna justifié dans sa maison plutôt que l'autre; car quiconque s'élève sera abaissé, et quiconque s'abaisse sera élevé.
15 Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula.
On lui présenta aussi des petits enfants, afin qu'il les touchât. Les disciples, voyant cela, reprenaient ceux qui les présentaient.
16 Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere.
Mais Jésus les appela à lui, en disant: Laissez venir à moi les petits enfants, et ne les en empêchez point; car le royaume de Dieu est pour ceux qui leur ressemblent.
17 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”
En vérité, je vous le déclare, quiconque ne recevra pas le royaume de Dieu comme un petit enfant, n'y entrera pas.
18 Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios )
Alors l'un des principaux du pays demanda à Jésus: Mon bon Maître, que dois-je faire pour hériter la vie éternelle? (aiōnios )
19 Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha.
Jésus lui répondit: Pourquoi m'appelles-tu bon? Il n'y a qu'un seul bon, c'est Dieu.
20 Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’”
Tu connais les commandements: «Tu ne commettras point d'adultère; tu ne tueras point; tu ne déroberas point; tu ne diras point de faux témoignage; honore ton père et ta mère.»
21 Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”
Cet homme répondit: J'ai observé toutes ces choses dès ma jeunesse.
22 Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”
Quand Jésus eut entendu cela, il lui dit: Il te manque encore une chose; vends tout ce que tu as et distribue-le aux pauvres, et tu auras un trésor dans les cieux. Viens alors, et suis-moi.
23 Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri.
Mais lui, ayant entendu ces paroles, devint tout triste; car il était fort riche.
24 Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu!
Jésus, le voyant tout triste, dit: Qu'il est difficile à ceux qui ont des richesses d'entrer dans le royaume de Dieu!
25 Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”
Il est plus facile à un chameau de passer par le trou de l'aiguille, qu'il ne l'est à un riche d'entrer dans le royaume de Dieu!
26 Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”
Ceux qui l'entendaient, lui dirent: Et qui peut donc être sauvé?
27 Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”
Il leur répondit: Ce qui est impossible aux hommes est possible à Dieu!
28 Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”
Pierre dit alors: Pour nous, nous avons quitté ce que nous possédions, et nous t'avons suivi!
29 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu
Jésus leur répondit: En vérité, je vous le déclare, tout homme qui aura quitté maison, ou femme, ou frères, ou parents, ou enfants, à cause du royaume de Dieu
30 adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.” (aiōn , aiōnios )
recevra beaucoup plus dans le temps présent, et, dans le siècle à venir, la vie éternelle. (aiōn , aiōnios )
31 Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa.
Ensuite Jésus prit à part les Douze, et il leur dit: Voici que nous montons à Jérusalem, et toutes les choses qui ont été écrites par les prophètes au sujet du Fils de l'homme, s'accompliront.
32 Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira,
Car il sera livré aux Païens; on se moquera de lui, on l'outragera, on crachera sur lui,
33 adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”
et, après l'avoir battu de verges, on le fera mourir. Et le troisième jour, il ressuscitera.
34 Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.
Mais ils ne comprirent rien à cela: le sens de ces paroles leur était caché, et ils ne saisissaient point ce que Jésus leur disait.
35 Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha,
Comme Jésus approchait de Jérico, un aveugle était assis au bord du chemin et demandait l'aumône.
36 anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika.
Entendant la foule qui passait, il s'informa de ce que c'était.
37 Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”
On lui répondit: C'est Jésus de Nazareth qui passe.
38 Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
Alors il cria: Jésus, fils de David, aie pitié de moi!
39 Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”
Et ceux qui allaient devant le reprenaient pour le faire taire; mais il criait encore plus fort: Fils de David, aie pitié de moi!
40 Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti,
Jésus, s'étant arrêté, ordonna qu'on le lui amenât; et quand l'aveugle se fut approché, il lui demanda:
41 “Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?” Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”
Que veux-tu que je te fasse? Il répondit: Seigneur, que je recouvre la vue.
42 Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.”
Jésus lui dit: Recouvre la vue; ta foi t'a guéri!
43 Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.
A l'instant, il recouvra la vue, et il suivait Jésus, glorifiant Dieu. Tout le peuple, voyant cela, donna gloire à Dieu.