< Luka 18 >

1 Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke.
Ježíš ještě připojil podobenství o tom, jak je zapotřebí vytrvale se modlit:
2 Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu.
„V jednom městě žil soudce, který na Boha nedal a na lidi se neohlížel.
3 Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’
Byla tam také jedna vdova a ta za ním neustále chodila, aby jí dopomohl v právu proti člověku, který jí ublížil.
4 “Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu,
Soudce ji dlouho odbýval, ale nakonec si řekl: ‚Je mi sice jedno, co si Bůh nebo lidé o té věci myslí,
5 koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’”
ale když je tak neodbytná, vyhovím jí. Jinak bude stále za mnou chodit, až mne umoří.‘
6 Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena.
Vidíte, neodbytné prosebnici nakonec vyhoví i tak špatný soudce.
7 Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira?
Jak by Bůh nepřišel na pomoc těm, kteří k němu volají dnem i nocí.
8 Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”
I když jim okamžitě nevyhoví, přesto jim trpělivě naslouchá a nakonec pomůže v pravý čas. Ale až znovu přijdu, naleznu lidi s tak vytrvalou vírou?“
9 Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse.
Těm, kteří si myslí, že jsou bez chyby, a dívají se na druhé spatra, vyprávěl Ježíš toto podobenství:
10 “Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho.
„Dva muži přišli do chrámu, aby se pomodlili; jeden farizej a druhý publikán.
11 Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu.
Farizej si stoupl dopředu a modlil se: ‚Bože, děkuji ti, že nejsem tak chamtivý, nečestný nebo rozbíječ rodiny jako ostatní lidé, třeba jako tady ten výběrčí daní.
12 Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’
Dvakrát týdně se postím a dávám ti desetinu ze všech svých příjmů.‘
13 “Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’
Ten výběrčí stál úplně vzadu, hlavu měl skloněnou, ani se neodvážil pohlédnout vzhůru. Na znamení lítosti se bil do prsou a modlil se: ‚Bože, slituj se nade mnou, jsem velký hříšník.‘“
14 “Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”
Ježíš uzavřel: „Publikán nebyl v chrámu nadarmo; Bůh ho vzal na milost, ale toho farizeje si ani nevšiml. Každý, kdo vynáší sám sebe, bude pokořen, a kdo se před Bohem koří, bude povýšen.“
15 Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula.
Lidé přinášeli k Ježíšovi i malé děti, aby jim žehnal. Když to učedníci viděli, odháněli je.
16 Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere.
Ježíš však zavolal rodiče s dětmi k sobě a řekl: „Nebraňte dětem v přístupu ke mně, neodhánějte je. Boží království je právě pro takové, jako jsou ony;
17 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”
kdo neuvěří tak prostě jako dítě, nevejde do něho.“
18 Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios g166)
Jeden vznešený muž se Ježíše zeptal: „Svatý učiteli, co musím dělat, abych získal věčný život?“ (aiōnios g166)
19 Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha.
Ježíš mu řekl: „Co tě vede k tomu, že mě nazýváš svatým? Vždyť svatý je pouze Bůh!
20 Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’”
Znáš jeho přikázání: Nezcizoložíš, nezabiješ, nikoho neokradeš, nepomluvíš a nenařkneš nikoho křivě, budeš si vážit svých rodičů.“
21 Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”
Muž odpověděl: „Tato přikázání se snažím dodržovat už od svého mládí.“
22 Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”
Ježíš mu řekl: „A přece ti ještě něco chybí. Prodej všechno, co máš, rozdej to chudým, a budeš mít poklad v nebi. Pak přijď a následuj mne.“
23 Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri.
Jak to muž uslyšel, zesmutněl a odešel, protože byl velice bohatý.
24 Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu!
Když to Ježíš uviděl, řekl: „Jak nesnadno přicházejí lidé k Bohu.
25 Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”
To spíš projde velbloud uchem jehly než boháč do Božího království.“
26 Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”
Lidé, kteří to slyšeli, se ptali: „Kdo tedy vůbec může být spasen?“
27 Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”
On odpověděl: „Na co člověk nestačí, to může učinit Bůh.“
28 Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”
Na to řekl Petr: „Ty víš, že jsme pro tebe opustili všechno a šli za tebou.“
29 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu
Ježíš odpověděl: „Žádný, kdo se musel pro Boží království něčeho vzdát – domova, manželky, sourozenců, rodičů nebo dětí, nezůstane bez odměny.
30 adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.” (aiōn g165, aiōnios g166)
Již v tomto světě získá mnohem více a v budoucím obdrží život věčný.“ (aiōn g165, aiōnios g166)
31 Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa.
Ježíš si vzal stranou svých dvanáct učedníků a řekl jim: „Jdeme teď do Jeruzaléma a tam se vyplní všechno, co napsali starodávní proroci o Synu člověka.
32 Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira,
Budu vydán do rukou pohanů, budou se mi vysmívat, budou mne týrat a plivat na mě.
33 adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”
Pak mne zbičují a zabijí, ale třetího dne vstanu z mrtvých.“
34 Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.
Učedníci to vůbec nechápali a jeho slova jim byla záhadou.
35 Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha,
Když se blížili k Jerichu, seděl u cesty slepec a žebral.
36 anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika.
Slyšel, že kolem proudí davy lidí a ptal se, co to má znamenat.
37 Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”
Řekli mu, že tudy jde Ježíš z Nazaretu.
38 Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
Začal volat: „Ježíši, Davidův potomku, slituj se nade mnou.“
39 Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”
Lidé, kteří Ježíše provázeli, slepce okřikovali, ale on volal tím víc: „Králi z Davidova rodu, slituj se nade mnou.“
40 Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti,
Ježíš se zastavil a zavolal slepce k sobě.
41 “Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?” Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”
Když ho k němu přivedli, zeptal se Ježíš: „Co pro tebe mám udělat?“Slepec odpověděl: „Pane, ať vidím!“
42 Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.”
Ježíš řekl: „Prohlédni! Tvá víra tě zachránila.“
43 Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.
V tom okamžiku slepec nabyl zrak, děkoval Bohu a šel za Ježíšem. A všichni, kteří toho byli svědky, chválili Boha.

< Luka 18 >