< Luka 16 >

1 Yesu anawuza ophunzira ake kuti, “Panali munthu wina wachuma amene kapitawo wake anzake anamuneneza kuti amawononga chuma chakecho.
And he went on to say, unto his disciples also, —There was, a certain rich man, who had a steward, and, the same, was accused to him as squandering his goods.
2 Choncho anamuyitana ndi kumufunsa kuti, ‘Kodi nʼchiyani chimene ndikumva za iwe? Pereka tsatanetsatane wa ntchito yako, pakuti supitirizanso kukhala kapitawo wanga.’
And, accosting him, he said unto him—What is this I hear of thee? Render the account of thy stewardship, for thou canst no longer be steward.
3 “Kapitawoyo analingalira kuti, ‘Kodi tsopano ndidzachita chiyani? Bwana wanga andichotsa ntchito. Ine ndilibe mphamvu zokwanira zolimira, komanso ine ndimachita manyazi kupempha.
And the steward said within himself—What shall I do, because my lord taketh away the stewardship from me? Dig, I cannot: to beg, I am ashamed.
4 Ine ndikudziwa chimene ndidzachita kotero kuti, pamene ntchito yanga yatha pano, anthu adzandilandire mʼnyumba zawo.’
I know what I will do, that, when I am removed out of the stewardship, they may welcome me into their own houses.
5 “Choncho iye anayitana aliyense amene anali ndi ngongole kwa bwana wake. Iye anafunsa woyamba, ‘Kodi uli ndi ngongole yotani kwa bwana wanga?’
And, calling unto him each one of the debtors of his own lord, he was saying unto the first, —How much owest thou my lord?
6 “Iye anayankha kuti, ‘Migolo yamafuta a olivi 800.’ “Kapitawo uja anamuwuza iye, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo, khala pansi msanga ndipo lemba kuti ndi migolo 400.’
And, he, said—A hundred baths of oil. And, he, said unto him—Kindly take thine accounts, and, sitting down, make haste and write—Fifty!
7 “Kenaka iye anafunsa wachiwiri kuti, ‘Nanga iwe uli ndi ngongole yotani?’ “Iye ayankha kuti madengu a tirigu 1,000. “Iye anati, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo ndipo ulembepo 800.’
After that, unto another, he said—And how much owest, thou? And, he, said—A hundred homers of wheat. He saith unto him—Kindly take thine accounts, and write—Eighty!
8 “Bwana anayamikira kapitawo wosakhulupirikayo popeza anachita mochenjera. Pakuti anthu a dziko lino lapansi ndi ochenjera kwambiri akamachita zinthu ndi anthu ofanana nawo kuposa anthu a kuwunika. (aiōn g165)
And the lord praised the unrighteous steward, in that with forethought he acted: —Because, the sons of this age, have more forethought than the sons of light, respecting their own generation. (aiōn g165)
9 Ine ndikukuwuzani inu, gwiritsani ntchito chuma cha dziko lapansi kuti mudzipezere nokha abwenzi, kuti pamene chatha mudzalandiridwe mʼmalo okhala amuyaya. (aiōnios g166)
And, I, unto you, say—For yourselves, make ye friends, with the unjust Riches, in order that, as soon as it shall fail, they may welcome you into the age-abiding tents. (aiōnios g166)
10 “Amene akhulupirika pa zinthu zochepa akhoza kukhulupirikanso pa zinthu zambiri, ndipo amene sakhulupirika pa zinthu zochepa adzakhala wosakhulupirika pa zinthu zambiri.
The faithful in least, in much also, is, faithful, and, he that in least is unrighteous, in much also, is, unrighteous.
11 Ndipo ngati simunakhale okhulupirika pogwiritsa ntchito chuma cha dziko lapansi, ndani amene adzakusungitsani chuma chenicheni?
If therefore, in the unjust Riches ye proved unfaithful, the true, who, unto you, will entrust?
12 Ndipo ngati simunakhale okhulupirika ndi chuma cha mwini wake, ndani amene adzakupatsani katundu wanuwanu?
And, if, in what was another’s, ye proved unfaithful, your own, who will give unto you?
13 “Palibe wantchito amene angatumikire mabwana awiri. Mwina iye adzadana ndi wina ndi kukonda winayo, kapena adzakhala wodzipereka kwa wina ndi kumunyoza winayo. Inu simungathe kutumikira Mulungu komanso ndalama nthawi imodzi.”
No domestic, can, unto two masters, be in service; for either, the one, he will hate, and, the other, love, or, unto the one, he will hold, and, the other, despise: Ye cannot, unto God, be in service, and unto Riches.
14 Afarisi amene ankakonda ndalama atamva zimenezi anamuseka Yesu.
Now the Pharisees, who were, lovers of money, were hearing all these things, and were openly sneering at him.
15 Yesu anawawuza kuti, “Inu ndi amene mumadzilungamitsa nokha pamaso pa anthu, koma Mulungu amadziwa mitima yanu. Zinthu zimene anthu amaziyesa zopambana, ndi zonyansa pamaso pa Mulungu.
And he said unto them—Ye, are they who justify themselves before men, but, God, knoweth your hearts; because, that which amongst men is lofty, is an abomination before God.
16 “Malamulo ndi Aneneri zinagwira ntchito mpaka nthawi ya Yohane. Kuyambira nthawi imeneyo, Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ukulalikidwa, ndipo aliyense akuyesetsa mwamphamvu kuti alowemo.
The law and the prophets, were until John, —from that time, the good news of the kingdom of God, is being proclaimed, and, everyone, thereinto, is forcing his way.
17 Nʼkwapafupi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zichoke kulekana ndi kuti kalemba kakangʼono kachoke mʼMalamulo.
But it is, easier, for heaven and earth to pass away, than that, of the law, one little point, should fail.
18 “Aliyense amene asiya mkazi wake ndi kukakwatira mkazi wina akuchita chigololo, ndipo mwamuna amene akwatira mkazi wosiyidwayo akuchitanso chigololo.”
Every one divorcing his wife and marrying another, committeth adultery; and, he that marrieth a woman divorced from a husband, committeth adultery.
19 “Panali munthu wachuma amene ankavala zovala zofiirira za mtengowapatali ndipo ankakhala moyo wachisangalalo tsiku lililonse.
Now, a certain man, was rich, and he used to clothe himself with purple and fine linen, making merry day by day, brilliantly.
20 Pa khomo la mpanda wake ankagonekapo munthu wopempha wotchedwa Lazaro, wazilonda thupi lonse
And, a certain beggar, by name Lazarus, used to be cast near his gate, full of sores,
21 ndipo ankafunitsitsa atadya zomwe zinkagwa pansi kuchokera pamene munthu wolemerayo amadyerapo. Agalu ankabweranso ndi kumanyambita zilonda zake.
and to long to be fed from the crumbs that fell from the table of the rich man: nay! even, the dogs, used to come and lick his sores.
22 “Nthawi inafika imene wopemphayo anamwalira ndipo angelo anamunyamula nakamuyika mʼmanja mwa Abrahamu. Munthu wolemerayo anamwaliranso ndipo anayikidwa mʼmanda.
And it came to pass that the beggar died, and was carried away by the messengers, into the bosom of Abraham. And, the rich man also, died, and was buried.
23 Ali mʼgehena kuzunzika, anakweza maso ake ndipo anaona Abrahamu ali ndi Lazaro pambali pake. (Hadēs g86)
And, in hades, lifting up his eyes, being in torments, he seeth Abraham afar off, and Lazarus in his bosom. (Hadēs g86)
24 Ndipo anafuwula kwa iye kuti, ‘Abambo Abrahamu, mundimvere chisoni ine ndipo mutumeni Lazaroyo kuti aviyike msonga ya chala chake mʼmadzi kuti aziziritse lilime langa, chifukwa ndikumva ululu mʼmoto muno.’
And, he, calling out, said—Father Abraham! have mercy upon me, and send Lazarus, that he may dip the tip of his finger in water, and cool my tongue, —because I am in anguish in this flame.
25 “Koma Abrahamu anayankha kuti, ‘Mwanawe kumbukira kuti nthawi yamoyo wako unalandira zinthu zako zabwino, pamene Lazaro analandira zinthu zoyipa, koma tsopano akusangalatsidwa kuno ndipo iwe uli mʼmazunzo.
But Abraham said—Child! remember—That thou didst duly received thy good things in thy life, and, Lazarus, in like manner, the evil things; but, now, here, he is comforted, and, thou, art in anguish.
26 Ndipo kuwonjezera pa zonsezi, pakati pa inu ndi ife pali chiphompho chachikulu chimene chinayikidwa, kotero kuti amene akufuna kubwera kumeneko sangathe, kapena palibe amene angawoloke kuchokera kumeneko kudzafika kuno.’
And, besides all these things, betwixt us and you, a great chasm, hath been fixed, —so that, they who might wish to cross over from hence unto you, should not be able, nor any, from thence unto us, be crossing over.
27 “Iye anayankha kuti, ‘Ndipo ndikupemphani inu, abambo, mutumeni Lazaro ku nyumba ya abambo anga,
But he said—I request thee then, father, that thou wouldst send him unto my father’s house, —
28 pakuti ine ndili ndi abale asanu. Lolani iye akawachenjeze kotero kuti asadzabwere kumalo ano amazunzo.’
for I have five brethren; —that he may solemnly testify unto them, lest, they also, come into this place of torment.
29 “Abrahamu anayankha kuti, ‘Ali ndi Mose ndi Aneneri; aleke amvere iwo.’
But Abraham saith—They have Moses and the Prophets: Let them hearken unto them.
30 “Iye anati, ‘Ayi, bambo Abrahamu, koma ngati wina ochokera kwa akufa adzapita kwa iwo, adzatembenuka mtima.’
But, he, said—Nay! father Abraham, but, if one, from the dead, should go unto them, they would repent.
31 “Anati kwa iye, ‘Ngati iwo samvera Mose ndi Aneneri, sadzakhulupirira ngakhale wina atauka kwa akufa.’”
But he said unto him—If, unto Moses and the Prophets, they do not hearken, neither, if one, from among the dead, should arise, would they be persuaded.

< Luka 16 >