< Luka 15 >
1 Tsopano amisonkho ndi “ochimwa” ankasonkhana kudzamvera mawu ake.
တဒါ ကရသဉ္စာယိနး ပါပိနၑ္စ လောကာ ဥပဒေၑ္ကထာံ ၑြောတုံ ယီၑေား သမီပမ် အာဂစ္ဆန်၊
2 Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amangʼungʼudza nati, “Munthu uyu amalandira ochimwa ndi kudya nawo.”
တတး ဖိရူၑိန ဥပါဓျာယာၑ္စ ဝိဝဒမာနား ကထယာမာသုး ဧၐ မာနုၐး ပါပိဘိး သဟ ပြဏယံ ကၖတွာ တဲး သာရ္ဒ္ဓံ ဘုံက္တေ၊
3 Ndipo Yesu anawawuza fanizo ili:
တဒါ သ တေဘျ ဣမာံ ဒၖၐ္ဋာန္တကထာံ ကထိတဝါန်,
4 “Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu ali ndi nkhosa 100 ndipo imodzi yatayika, kodi iye sangasiye 99 zija kutchire ndi kupita kukafuna yotayikayo mpaka atayipeza?
ကသျစိတ် ၑတမေၐေၐု တိၐ္ဌတ္မု တေၐာမေကံ သ ယဒိ ဟာရယတိ တရှိ မဓျေပြာန္တရမ် ဧကောနၑတမေၐာန် ဝိဟာယ ဟာရိတမေၐသျ ဥဒ္ဒေၑပြာပ္တိပရျျနတံ န ဂဝေၐယတိ, ဧတာဒၖၑော လောကော ယုၐ္မာကံ မဓျေ က အာသ္တေ?
5 Ndipo iye akayipeza, amayinyamula pa phewa lake mwachimwemwe
တသျောဒ္ဒေၑံ ပြာပျ ဟၖၐ္ဋမနာသ္တံ သ္ကန္ဓေ နိဓာယ သွသ္ထာနမ် အာနီယ ဗန္ဓုဗာန္ဓဝသမီပဝါသိန အာဟူယ ဝက္တိ,
6 ndi kupita kwawo. Kenaka amayitana anzake ndi anansi pamodzi, ndi kuti, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza nkhosa yanga yotayika ija.’
ဟာရိတံ မေၐံ ပြာပ္တောဟမ် အတော ဟေတော ရ္မယာ သာရ္ဒ္ဓမ် အာနန္ဒတ၊
7 Ine ndikukuwuzani kuti momwemonso kudzakhala chikondwerero chachikulu kumwamba chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima kusiyana ndi anthu olungama 99 amene ali otembenuka mtima kale.”
တဒွဒဟံ ယုၐ္မာန် ဝဒါမိ, ယေၐာံ မနးပရာဝရ္တ္တနသျ ပြယောဇနံ နာသ္တိ, တာဒၖၑဲကောနၑတဓာရ္မ္မိကကာရဏာဒ် ယ အာနန္ဒသ္တသ္မာဒ် ဧကသျ မနးပရိဝရ္တ္တိနး ပါပိနး ကာရဏာတ် သွရ္ဂေ 'ဓိကာနန္ဒော ဇာယတေ၊
8 “Kapena tiyeni tifanizire mayi amene anali ndi ndalama zasiliva khumi ndipo imodzi nʼkutayika, kodi sayatsa nyale ndi kusesa mʼnyumba ndi kufuna mosamalitsa mpaka atayipeza?
အပရဉ္စ ဒၑာနာံ ရူပျခဏ္ဍာနာမ် ဧကခဏ္ဍေ ဟာရိတေ ပြဒီပံ ပြဇွာလျ ဂၖဟံ သမ္မာရ္ဇျ တသျ ပြာပ္တိံ ယာဝဒ် ယတ္နေန န ဂဝေၐယတိ, ဧတာဒၖၑီ ယောၐိတ် ကာသ္တေ?
9 Ndipo pamene wayipeza, amayitana anzake, ndi anansi pamodzi nati, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza ndalama yanga yotayika ija.’
ပြာပ္တေ သတိ ဗန္ဓုဗာန္ဓဝသမီပဝါသိနီရာဟူယ ကထယတိ, ဟာရိတံ ရူပျခဏ္ဍံ ပြာပ္တာဟံ တသ္မာဒေဝ မယာ သာရ္ဒ္ဓမ် အာနန္ဒတ၊
10 Momwemonso, Ine ndikukuwuzani kuti angelo a Mulungu amakondwera kwambiri chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima.”
တဒွဒဟံ ယုၐ္မာန် ဝျာဟရာမိ, ဧကေန ပါပိနာ မနသိ ပရိဝရ္တ္တိတေ, ဤၑွရသျ ဒူတာနာံ မဓျေပျာနန္ဒော ဇာယတေ၊
11 Yesu anapitiriza kunena kuti, “Panali munthu amene anali ndi ana aamuna awiri.
အပရဉ္စ သ ကထယာမာသ, ကသျစိဒ် ဒွေါ် ပုတြာဝါသ္တာံ,
12 Wamngʼonoyo anati kwa abambo ake, ‘Abambo, patseni gawo langa la chuma chanu.’ Ndipo iye anawagawira awiriwo chuma chawo.
တယေား ကနိၐ္ဌး ပုတြး ပိတြေ ကထယာမာသ, ဟေ ပိတသ္တဝ သမ္ပတ္တျာ ယမံၑံ ပြာပ္သျာမျဟံ ဝိဘဇျ တံ ဒေဟိ, တတး ပိတာ နိဇာံ သမ္ပတ္တိံ ဝိဘဇျ တာဘျာံ ဒဒေါ်၊
13 “Pasanapite nthawi, wamngʼonoyo anasonkhanitsa chuma chake chonse, napita ku dziko lakutali ndipo kumeneko anayamba kumwaza chuma chake mʼnjira zachitayiko.
ကတိပယာတ် ကာလာတ် ပရံ သ ကနိၐ္ဌပုတြး သမသ္တံ ဓနံ သံဂၖဟျ ဒူရဒေၑံ ဂတွာ ဒုၐ္ဋာစရဏေန သရွွာံ သမ္ပတ္တိံ နာၑယာမာသ၊
14 Iye atawononga zonse, kunagwa njala yoopsa mʼdziko lonselo ndipo anayamba kusauka.
တသျ သရွွဓနေ ဝျယံ ဂတေ တဒ္ဒေၑေ မဟာဒုရ္ဘိက္ၐံ ဗဘူဝ, တတသ္တသျ ဒဲနျဒၑာ ဘဝိတုမ် အာရေဘေ၊
15 Iye anapita kwa nzika ina ya dzikolo nakakhala naye ndi kumagwira ntchito, amene anamutumiza ku munda kukadyetsa nkhumba.
တတး ပရံ သ ဂတွာ တဒ္ဒေၑီယံ ဂၖဟသ္ထမေကမ် အာၑြယတ; တတး သတံ ၑူကရဝြဇံ စာရယိတုံ ပြာန္တရံ ပြေၐယာမာသ၊
16 Iye analakalaka atakhutitsa mimba yake ndi makoko amene nkhumbazo zinkadya, koma panalibe wina amene anamupatsa kanthu.
ကေနာပိ တသ္မဲ ဘက္ၐျာဒါနာတ် သ ၑူကရဖလဝလ္ကလေန ပိစိဏ္ဍပူရဏာံ ဝဝါဉ္ဆ၊
17 “Maganizo ake atabweramo, iye anati, ‘Ndi antchito angati a abambo anga amene ali ndi chakudya chimene amadya nʼkutsalako ndipo ine ndili pano kufa ndi njala!
ၑေၐေ သ မနသိ စေတနာံ ပြာပျ ကထယာမာသ, ဟာ မမ ပိတုး သမီပေ ကတိ ကတိ ဝေတနဘုဇော ဒါသာ ယထေၐ္ဋံ တတောဓိကဉ္စ ဘက္ၐျံ ပြာပ္နုဝန္တိ ကိန္တွဟံ က္ၐုဓာ မုမူရ္ၐုး၊
18 Ine ndinyamuka ndi kubwerera kwa abambo anga ndipo ndikati kwa iwo: abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi kwa inu.
အဟမုတ္ထာယ ပိတုး သမီပံ ဂတွာ ကထာမေတာံ ဝဒိၐျာမိ, ဟေ ပိတရ် ဤၑွရသျ တဝ စ ဝိရုဒ္ဓံ ပါပမကရဝမ္
19 Ndine wosayeneranso kutchedwa mwana wanu; munditenge ngati mmodzi wa antchito anu.’
တဝ ပုတြဣတိ ဝိချာတော ဘဝိတုံ န ယောဂျောသ္မိ စ, မာံ တဝ ဝဲတနိကံ ဒါသံ ကၖတွာ သ္ထာပယ၊
20 Ndipo iye ananyamuka ndi kupita kwa abambo ake. “Koma iye akanali patali, abambo ake anamuona ndipo anamvera chisoni; anathamangira mwanayo, namukumbatira ndi kupsompsona.
ပၑ္စာတ် သ ဥတ္ထာယ ပိတုး သမီပံ ဇဂါမ; တတသ္တသျ ပိတာတိဒူရေ တံ နိရီက္ၐျ ဒယာဉ္စကြေ, ဓာဝိတွာ တသျ ကဏ္ဌံ ဂၖဟီတွာ တံ စုစုမ္ဗ စ၊
21 “Mwanayo anati, ‘Abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi inunso. Ine sindiyenera konse kutchedwa mwana wanu.’
တဒါ ပုတြ ဥဝါစ, ဟေ ပိတရ် ဤၑွရသျ တဝ စ ဝိရုဒ္ဓံ ပါပမကရဝံ, တဝ ပုတြဣတိ ဝိချာတော ဘဝိတုံ န ယောဂျောသ္မိ စ၊
22 “Koma abambowo anati kwa antchito ake, ‘Fulumirani! Bweretsani mkanjo wabwino kwambiri ndipo mumuveke. Muvekeni mphete ndi nsapato.
ကိန္တု တသျ ပိတာ နိဇဒါသာန် အာဒိဒေၑ, သရွွောတ္တမဝသ္တြာဏျာနီယ ပရိဓာပယတဲနံ ဟသ္တေ စာင်္ဂုရီယကမ် အရ္ပယတ ပါဒယောၑ္စောပါနဟော် သမရ္ပယတ;
23 Bweretsani mwana wangʼombe wonenepa ndipo iphani. Tiyeni tikhale ndi phwando ndi kukondwerera.
ပုၐ္ဋံ ဂေါဝတ္သမ် အာနီယ မာရယတ စ တံ ဘုက္တွာ ဝယမ် အာနန္ဒာမ၊
24 Pakuti mwana wangayu anali wakufa, ndipo ali ndi moyonso; iye anatayika ndipo wapezeka.’ Chomwecho anayamba kukondwerera.
ယတော မမ ပုတြောယမ် အမြိယတ ပုနရဇီဝီဒ် ဟာရိတၑ္စ လဗ္ဓောဘူတ် တတသ္တ အာနန္ဒိတုမ် အာရေဘိရေ၊
25 “Nthawi imeneyi, mwana wake wamkulu uja anali ku munda. Iye atafika pafupi ndi nyumba, anamva anthu akuyimba ndi kuvina.
တတ္ကာလေ တသျ ဇျေၐ္ဌး ပုတြး က္ၐေတြ အာသီတ်၊ အထ သ နိဝေၑနသျ နိကဋံ အာဂစ္ဆန် နၖတျာနာံ ဝါဒျာနာဉ္စ ၑဗ္ဒံ ၑြုတွာ
26 Ndipo iye anayitana mmodzi wa antchito, namufunsa chimene chimachitika.
ဒါသာနာမ် ဧကမ် အာဟူယ ပပြစ္ဆ, ကိံ ကာရဏမသျ?
27 Iye anayankha kuti, ‘Mʼbale wako wabwera ndipo abambo ako apha mwana wangʼombe wonenepa chifukwa wabwera wamoyo ndipo ali bwino.’
တတး သောဝါဒီတ်, တဝ ဘြာတာဂမတ်, တဝ တာတၑ္စ တံ သုၑရီရံ ပြာပျ ပုၐ္ဋံ ဂေါဝတ္သံ မာရိတဝါန်၊
28 “Mwana wamkulu anakwiya ndipo anakana kulowa. Chomwecho abambo ake anatuluka ndi kumudandaulira.
တတး သ ပြကုပျ နိဝေၑနာန္တး ပြဝေၐ္ဋုံ န သမ္မေနေ; တတသ္တသျ ပိတာ ဗဟိရာဂတျ တံ သာဓယာမာသ၊
29 Koma iye anayankha abambo ake kuti, ‘Taonani! Zaka zonsezi ndakhala ndikukutumikirani kugwira ntchito yowawa ndipo palibe pamene sindinamvere malamulo anu. Koma inu simunandipatse ngakhale mwana wambuzi kuti ine ndichite phwando ndi anzanga.
တတး သ ပိတရံ ပြတျုဝါစ, ပၑျ တဝ ကာဉ္စိဒပျာဇ္ဉာံ န ဝိလံဃျ ဗဟူန် ဝတ္သရာန် အဟံ တွာံ သေဝေ တထာပိ မိတြဲး သာရ္ဒ္ဓမ် ဥတ္သဝံ ကရ္တ္တုံ ကဒါပိ ဆာဂမေကမပိ မဟျံ နာဒဒါး;
30 Koma pamene mwana wanu uyu amene wawononga chuma chanu ndi achiwerewere wabwera ku nyumba, inu mwamuphera mwana wangʼombe wonenepa.’”
ကိန္တု တဝ ယး ပုတြော ဝေၑျာဂမနာဒိဘိသ္တဝ သမ္ပတ္တိမ် အပဝျယိတဝါန် တသ္မိန္နာဂတမာတြေ တသျဲဝ နိမိတ္တံ ပုၐ္ဋံ ဂေါဝတ္သံ မာရိတဝါန်၊
31 Abambowo anati, “Mwana wanga, iwe umakhala ndi ine nthawi zonse ndipo zonse ndili nazo ndi zako.
တဒါ တသျ ပိတာဝေါစတ်, ဟေ ပုတြ တွံ သရွွဒါ မယာ သဟာသိ တသ္မာန် မမ ယဒျဒါသ္တေ တတ္သရွွံ တဝ၊
32 Koma tinayenera kukondwera ndi kusangalala, chifukwa mʼbale wako uyu anali wakufa ndipo ali ndi moyonso; iye anali wotayika ndipo wapezeka.”
ကိန္တု တဝါယံ ဘြာတာ မၖတး ပုနရဇီဝီဒ် ဟာရိတၑ္စ ဘူတွာ ပြာပ္တောဘူတ်, ဧတသ္မာတ် ကာရဏာဒ် ဥတ္သဝါနန္ဒော် ကရ္တ္တုမ် ဥစိတမသ္မာကမ်၊