< Luka 15 >

1 Tsopano amisonkho ndi “ochimwa” ankasonkhana kudzamvera mawu ake.
Pašo Isus ćidije pe pherdo carincura thaj but grešnikura te šunen so sikavol.
2 Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amangʼungʼudza nati, “Munthu uyu amalandira ochimwa ndi kudya nawo.”
Al e fariseja thaj e učitelja tare Mojsijaso zakon vaćarena maškar peste: “Kava primil e grešnikuren thaj xal lencar.”
3 Ndipo Yesu anawawuza fanizo ili:
Golese o Isus lenđe vaćarda kaja paramič:
4 “Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu ali ndi nkhosa 100 ndipo imodzi yatayika, kodi iye sangasiye 99 zija kutchire ndi kupita kukafuna yotayikayo mpaka atayipeza?
“Te khanika tumendar isi šel bakre thaj jekh lendar hasardol, so ka ćerol? Ka ačhavol e enjavardeš thaj enja ki pustinja thaj ka džal te rodol gola jekha so hasajli sa dok ni aračhol la.
5 Ndipo iye akayipeza, amayinyamula pa phewa lake mwachimwemwe
Thaj kana aračhol la, čhuvol la radosno ke piro piko.
6 ndi kupita kwawo. Kenaka amayitana anzake ndi anansi pamodzi, ndi kuti, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza nkhosa yanga yotayika ija.’
Kana avol čhere, dol vika pe amalen thaj e pašutnen vaćarindoj: ‘Radujin tumen mancar! Arakhljem mingra hasarde bakra!’
7 Ine ndikukuwuzani kuti momwemonso kudzakhala chikondwerero chachikulu kumwamba chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima kusiyana ndi anthu olungama 99 amene ali otembenuka mtima kale.”
Vaćarav tumenđe kaj ano nebo ka avol pobaro radost baše jekh grešniko savo iril pe tare pe grehura nego baše enjavardeš thaj enja pravedna savenđe ni trubul pokajipe.”
8 “Kapena tiyeni tifanizire mayi amene anali ndi ndalama zasiliva khumi ndipo imodzi nʼkutayika, kodi sayatsa nyale ndi kusesa mʼnyumba ndi kufuna mosamalitsa mpaka atayipeza?
O Isus vaćarda thaj kava: “Il, te nesavi džuvli isi la deš srebrenjakura thaj hasarol jekh, so ka ćerol? Ka phabarol i svetiljka thaj ka šulavol o čher thaj ka rodol šukar sa dok ni aračhol la?
9 Ndipo pamene wayipeza, amayitana anzake, ndi anansi pamodzi nati, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza ndalama yanga yotayika ija.’
Thaj kana aračhol la, akharol pe amalinjen thaj e pašutnen thaj phenol lenđe: ‘Radujin tumen mancar! Me arakhljem o srebrenjako so hasardem!’
10 Momwemonso, Ine ndikukuwuzani kuti angelo a Mulungu amakondwera kwambiri chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima.”
Gija, vaćarav tumenđe kaj maškare anđelura e Devlese ka avol pobaro radost baše jekh grešniko savo iril pe tare pe grehura.”
11 Yesu anapitiriza kunena kuti, “Panali munthu amene anali ndi ana aamuna awiri.
Thaj o Isus vaćarda: “Jekhe manuše sesa duj čhave.
12 Wamngʼonoyo anati kwa abambo ake, ‘Abambo, patseni gawo langa la chuma chanu.’ Ndipo iye anawagawira awiriwo chuma chawo.
O ciknjeder vaćarda e dadese: ‘Dade! De man kotor taro barvalipe so preperol manđe.’ Thaj o dad ulada lenđe o barvalipe.
13 “Pasanapite nthawi, wamngʼonoyo anasonkhanitsa chuma chake chonse, napita ku dziko lakutali ndipo kumeneko anayamba kumwaza chuma chake mʼnjira zachitayiko.
Pale nekobor đivesa, ćidija o ciknjeder čhavo sa piro, đelo ani durutni phuv, odori xalja sa o barvalipe thaj živisada dilikane.
14 Iye atawononga zonse, kunagwa njala yoopsa mʼdziko lonselo ndipo anayamba kusauka.
Kana xalja sa e pare, sasa but baro bokhalipe ane goja phuv thaj ni sasa le so te xal.
15 Iye anapita kwa nzika ina ya dzikolo nakakhala naye ndi kumagwira ntchito, amene anamutumiza ku munda kukadyetsa nkhumba.
Golese đelo ki jekh manuš te ćerol bući. Gova manuš bičhalda le ane piro polje te aračhol e balen.
16 Iye analakalaka atakhutitsa mimba yake ndi makoko amene nkhumbazo zinkadya, koma panalibe wina amene anamupatsa kanthu.
O čhavo sasa gija bokhalo kaj bi xala i gova so xan e bale, al khoni ni dija le ni gova.
17 “Maganizo ake atabweramo, iye anati, ‘Ndi antchito angati a abambo anga amene ali ndi chakudya chimene amadya nʼkutsalako ndipo ine ndili pano kufa ndi njala!
Tegani avilo ane peste thaj vaćarda: ‘Kobor e bućarne ke mingro dad isi len so te xan, a me kate merav bokhalo!
18 Ine ndinyamuka ndi kubwerera kwa abambo anga ndipo ndikati kwa iwo: abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi kwa inu.
Ka džav ke mingro dad thaj ka vaćarav lese: “Dade, grešisadem anglo Dol thaj angle tute.
19 Ndine wosayeneranso kutchedwa mwana wanu; munditenge ngati mmodzi wa antchito anu.’
Naj sem vadži dostojno te akhardivav ćiro čhavo. Le man sar jekhe tare ćire bućarne.”’
20 Ndipo iye ananyamuka ndi kupita kwa abambo ake. “Koma iye akanali patali, abambo ake anamuona ndipo anamvera chisoni; anathamangira mwanayo, namukumbatira ndi kupsompsona.
Tegani uštilo thaj đelo ke piro dad. A kana sasa vadži dur, dikhlja le leso dad thaj pelo lese žal. Prastija ke leste, zagrlisada le thaj čumidija le.
21 “Mwanayo anati, ‘Abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi inunso. Ine sindiyenera konse kutchedwa mwana wanu.’
Tegani o čhavo vaćarda lese: ‘Dade, grešisadem anglo Dol thaj angle tute! Naj sem vadži dostojno te akhardivav ćiro čhavo.’
22 “Koma abambowo anati kwa antchito ake, ‘Fulumirani! Bweretsani mkanjo wabwino kwambiri ndipo mumuveke. Muvekeni mphete ndi nsapato.
Al o dad phenda pe slugenđe: ‘Sigate! Ikalen emlačho fostano thaj uraven le! Čhuven lese angrustik ko va thaj sandale ke pingre!
23 Bweretsani mwana wangʼombe wonenepa ndipo iphani. Tiyeni tikhale ndi phwando ndi kukondwerera.
Anen e terne thule guruve thaj čhinen le, te xa thaj te raduji amen,
24 Pakuti mwana wangayu anali wakufa, ndipo ali ndi moyonso; iye anatayika ndipo wapezeka.’ Chomwecho anayamba kukondwerera.
golese kaj mingro čhavo sasa mulo thaj džuvdilo; sasa hasardo thaj arakhadilo!’ Thaj lije te radujin pe.
25 “Nthawi imeneyi, mwana wake wamkulu uja anali ku munda. Iye atafika pafupi ndi nyumba, anamva anthu akuyimba ndi kuvina.
O phureder čhavo sasa ano polje. Kana avilo pašo čher, šunda čhelipe thaj bašalipe.
26 Ndipo iye anayitana mmodzi wa antchito, namufunsa chimene chimachitika.
Tegani dija vika jekhe sluga thaj pučlja le: ‘So si gova?’
27 Iye anayankha kuti, ‘Mʼbale wako wabwera ndipo abambo ako apha mwana wangʼombe wonenepa chifukwa wabwera wamoyo ndipo ali bwino.’
Vov phenda lese: ‘Ćiro phral avilo. Ćiro dad čhinda e terne thule guruve, golese so dikhlja le džuvde thaj saste.’
28 “Mwana wamkulu anakwiya ndipo anakana kulowa. Chomwecho abambo ake anatuluka ndi kumudandaulira.
Tegani o phureder phral holajlo thaj ni manglja te avol andre. Al iklilo leso dad thaj molisada le te dol ano čher.
29 Koma iye anayankha abambo ake kuti, ‘Taonani! Zaka zonsezi ndakhala ndikukutumikirani kugwira ntchito yowawa ndipo palibe pamene sindinamvere malamulo anu. Koma inu simunandipatse ngakhale mwana wambuzi kuti ine ndichite phwando ndi anzanga.
Al vov vaćarda pe dadese: ‘Akh, služiv tut sar robo gaći berša thaj nikad ni phagljem ćiro lafi. Thaj manđe ni jekh drom ni dijan ni buzore te radujiv man mingre amalencar.
30 Koma pamene mwana wanu uyu amene wawononga chuma chanu ndi achiwerewere wabwera ku nyumba, inu mwamuphera mwana wangʼombe wonenepa.’”
Al kana avilo ćiro čhavo savo ćiro barvalipe čhorda e bludnicencar, čhindan lese terne thule guruve.’
31 Abambowo anati, “Mwana wanga, iwe umakhala ndi ine nthawi zonse ndipo zonse ndili nazo ndi zako.
A o dad phenda lese: ‘Mo čhavo! Tu san uvek mancar thaj sa so si mingro, si ćiro.
32 Koma tinayenera kukondwera ndi kusangalala, chifukwa mʼbale wako uyu anali wakufa ndipo ali ndi moyonso; iye anali wotayika ndipo wapezeka.”
Al trubul te raduji amen thaj te ava baxtale, golese kaj ćiro phral sasa mulo thaj džuvdilo; sasa hasardo thaj arakhadilo.’”

< Luka 15 >