< Luka 15 >

1 Tsopano amisonkho ndi “ochimwa” ankasonkhana kudzamvera mawu ake.
Or, tous les publicains et les pécheurs s'approchaient de lui pour l'entendre.
2 Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amangʼungʼudza nati, “Munthu uyu amalandira ochimwa ndi kudya nawo.”
Les pharisiens et les scribes murmuraient, disant: « Cet homme accueille les pécheurs et mange avec eux. »
3 Ndipo Yesu anawawuza fanizo ili:
Il leur dit cette parabole:
4 “Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu ali ndi nkhosa 100 ndipo imodzi yatayika, kodi iye sangasiye 99 zija kutchire ndi kupita kukafuna yotayikayo mpaka atayipeza?
« Lequel d'entre vous, s'il avait cent brebis et en perdait une, ne laisserait pas les quatre-vingt-dix-neuf autres dans le désert pour courir après celle qui est perdue, jusqu'à ce qu'il la retrouve?
5 Ndipo iye akayipeza, amayinyamula pa phewa lake mwachimwemwe
Lorsqu'il l'a trouvée, il la porte sur ses épaules en se réjouissant.
6 ndi kupita kwawo. Kenaka amayitana anzake ndi anansi pamodzi, ndi kuti, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza nkhosa yanga yotayika ija.’
De retour à la maison, il appelle ses amis et ses voisins, en leur disant: « Réjouissez-vous avec moi, car j'ai retrouvé ma brebis qui était perdue! ».
7 Ine ndikukuwuzani kuti momwemonso kudzakhala chikondwerero chachikulu kumwamba chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima kusiyana ndi anthu olungama 99 amene ali otembenuka mtima kale.”
Je vous le dis, de même, il y aura plus de joie dans le ciel pour un seul pécheur qui se repent, que pour quatre-vingt-dix-neuf justes qui n'ont pas besoin de se repentir.
8 “Kapena tiyeni tifanizire mayi amene anali ndi ndalama zasiliva khumi ndipo imodzi nʼkutayika, kodi sayatsa nyale ndi kusesa mʼnyumba ndi kufuna mosamalitsa mpaka atayipeza?
« Ou quelle femme, si elle avait dix drachmes, si elle en perdait une, n'allumerait pas une lampe, ne balaierait pas la maison et ne chercherait pas diligemment jusqu'à ce qu'elle la trouve?
9 Ndipo pamene wayipeza, amayitana anzake, ndi anansi pamodzi nati, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza ndalama yanga yotayika ija.’
Lorsqu'elle l'a trouvée, elle convoque ses amies et ses voisines en disant: « Réjouissez-vous avec moi, car j'ai trouvé la drachme que j'avais perdue! ».
10 Momwemonso, Ine ndikukuwuzani kuti angelo a Mulungu amakondwera kwambiri chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima.”
De même, je vous le dis, il y a de la joie en présence des anges de Dieu pour un seul pécheur qui se repent. »
11 Yesu anapitiriza kunena kuti, “Panali munthu amene anali ndi ana aamuna awiri.
Il dit: « Un homme avait deux fils.
12 Wamngʼonoyo anati kwa abambo ake, ‘Abambo, patseni gawo langa la chuma chanu.’ Ndipo iye anawagawira awiriwo chuma chawo.
Le plus jeune dit à son père: « Père, donne-moi ma part de tes biens ». Il partagea donc entre eux son gagne-pain.
13 “Pasanapite nthawi, wamngʼonoyo anasonkhanitsa chuma chake chonse, napita ku dziko lakutali ndipo kumeneko anayamba kumwaza chuma chake mʼnjira zachitayiko.
Peu de jours après, le fils cadet rassembla tout cela et s'en alla dans un pays lointain. Là, il gaspilla ses biens en vivant dans la débauche.
14 Iye atawononga zonse, kunagwa njala yoopsa mʼdziko lonselo ndipo anayamba kusauka.
Lorsqu'il eut tout dépensé, une grande famine survint dans ce pays, et il commença à être dans le besoin.
15 Iye anapita kwa nzika ina ya dzikolo nakakhala naye ndi kumagwira ntchito, amene anamutumiza ku munda kukadyetsa nkhumba.
Il alla s'attacher à l'un des citoyens de ce pays, qui l'envoya dans ses champs pour nourrir les porcs.
16 Iye analakalaka atakhutitsa mimba yake ndi makoko amene nkhumbazo zinkadya, koma panalibe wina amene anamupatsa kanthu.
Il voulait se remplir le ventre avec les cosses que mangeaient les porcs, mais personne ne lui en donnait.
17 “Maganizo ake atabweramo, iye anati, ‘Ndi antchito angati a abambo anga amene ali ndi chakudya chimene amadya nʼkutsalako ndipo ine ndili pano kufa ndi njala!
Lorsqu'il revint à lui, il dit: « Combien de mercenaires de mon père ont du pain en abondance, et moi, je meurs de faim!
18 Ine ndinyamuka ndi kubwerera kwa abambo anga ndipo ndikati kwa iwo: abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi kwa inu.
Je me lèverai et j'irai vers mon père, et je lui dirai: « Père, j'ai péché contre le ciel et à tes yeux.
19 Ndine wosayeneranso kutchedwa mwana wanu; munditenge ngati mmodzi wa antchito anu.’
Je ne suis plus digne d'être appelé ton fils. Fais de moi un de tes mercenaires. »''
20 Ndipo iye ananyamuka ndi kupita kwa abambo ake. “Koma iye akanali patali, abambo ake anamuona ndipo anamvera chisoni; anathamangira mwanayo, namukumbatira ndi kupsompsona.
« Il se leva et alla vers son père. Mais, comme il était encore loin, son père le vit et fut ému de compassion; il courut, se jeta à son cou et le baisa.
21 “Mwanayo anati, ‘Abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi inunso. Ine sindiyenera konse kutchedwa mwana wanu.’
Le fils lui dit: « Père, j'ai péché contre le ciel et à tes yeux. Je ne suis plus digne d'être appelé ton fils ».
22 “Koma abambowo anati kwa antchito ake, ‘Fulumirani! Bweretsani mkanjo wabwino kwambiri ndipo mumuveke. Muvekeni mphete ndi nsapato.
« Mais le père dit à ses serviteurs: « Apportez la plus belle robe et mettez-la sur lui. Mettez un anneau à sa main et des sandales à ses pieds.
23 Bweretsani mwana wangʼombe wonenepa ndipo iphani. Tiyeni tikhale ndi phwando ndi kukondwerera.
Amenez le veau gras, tuez-le, mangeons et faisons la fête;
24 Pakuti mwana wangayu anali wakufa, ndipo ali ndi moyonso; iye anatayika ndipo wapezeka.’ Chomwecho anayamba kukondwerera.
car celui-ci, mon fils, était mort et il revit. Il était perdu et il est retrouvé. Et ils se mirent à célébrer.
25 “Nthawi imeneyi, mwana wake wamkulu uja anali ku munda. Iye atafika pafupi ndi nyumba, anamva anthu akuyimba ndi kuvina.
« Or, son fils aîné était aux champs. Comme il s'approchait de la maison, il entendit de la musique et des danses.
26 Ndipo iye anayitana mmodzi wa antchito, namufunsa chimene chimachitika.
Il appela un des serviteurs et lui demanda ce qui se passait.
27 Iye anayankha kuti, ‘Mʼbale wako wabwera ndipo abambo ako apha mwana wangʼombe wonenepa chifukwa wabwera wamoyo ndipo ali bwino.’
Il lui dit: « Ton frère est arrivé et ton père a tué le veau gras, car il l'a reçu sain et sauf.
28 “Mwana wamkulu anakwiya ndipo anakana kulowa. Chomwecho abambo ake anatuluka ndi kumudandaulira.
Mais il se mit en colère et ne voulut pas entrer. Alors son père sortit et le supplia.
29 Koma iye anayankha abambo ake kuti, ‘Taonani! Zaka zonsezi ndakhala ndikukutumikirani kugwira ntchito yowawa ndipo palibe pamene sindinamvere malamulo anu. Koma inu simunandipatse ngakhale mwana wambuzi kuti ine ndichite phwando ndi anzanga.
Mais il répondit à son père: « Voici tant d'années que je te sers et je n'ai jamais désobéi à un de tes commandements, mais tu ne m'as jamais donné de chèvre pour que je puisse faire la fête avec mes amis.
30 Koma pamene mwana wanu uyu amene wawononga chuma chanu ndi achiwerewere wabwera ku nyumba, inu mwamuphera mwana wangʼombe wonenepa.’”
Mais lorsque ton fils est arrivé, lui qui a dévoré ta vie avec des prostituées, tu as tué pour lui le veau gras.
31 Abambowo anati, “Mwana wanga, iwe umakhala ndi ine nthawi zonse ndipo zonse ndili nazo ndi zako.
Il lui dit: « Mon fils, tu es toujours avec moi, et tout ce qui est à moi est à toi.
32 Koma tinayenera kukondwera ndi kusangalala, chifukwa mʼbale wako uyu anali wakufa ndipo ali ndi moyonso; iye anali wotayika ndipo wapezeka.”
Mais il convenait de célébrer et de se réjouir, car celui-ci, ton frère, était mort, et il est ressuscité. Il était perdu, et il est retrouvé. »

< Luka 15 >