< Luka 14 >
1 Pa tsiku lina la Sabata, Yesu atapita kukadya ku nyumba ya Mfarisi wodziwika, Afarisi anamulonda mosamalitsa.
And it came to pass, that he went, on the sabbath-day, into the house of one of the chief men of the Pharisees, to eat bread; and they watched him.
2 Poteropo, patsogolo pake panali munthu amene anadwala matenda otupa mimba ndi miyendo.
And behold, there was a man before him, who had the dropsy.
3 Yesu anafunsa Afarisi ndi akatswiri amalamulo kuti, “Kodi ndi zololedwa kuchiritsa pa tsiku la Sabata kapena ayi?”
And Jesus answered and spoke to the lawyers and Pharisees, saying: Is it lawful to cure on the sabbath-day?
4 Koma iwo sanayankhe. Tsono atamutenga munthuyo, Iye anamuchiritsa ndipo anamuwuza kuti azipita.
But they were silent. And he took him, and healed him, and let him go.
5 Kenaka Iye anawafunsa kuti, “Kodi ngati mmodzi mwa inu ali ndi mwana wamwamuna kapena ngʼombe imene yagwera mʼchitsime tsiku la Sabata, kodi simungamuvuwulemo tsiku lomwelo?”
And he answered and said to them: Which of you, if his son or his ox should fall into a pit, would not immediately pull him out on the sabbath-day?
6 Ndipo iwo analibe choyankha.
And they were not able to give him an answer to these things.
7 Iye ataona momwe alendo amasankhira malo aulemu pa tebulo, Iye anawawuza fanizo ili:
And he spoke a parable to those who had been invited, when he observed how they were choosing the first places at table; and he said to them:
8 “Pamene wina wakuyitanani ku phwando la ukwati, musakhale pa malo aulemu ayi, chifukwa mwina anayitananso munthu wina wolemekezeka kuposa inu.
When you are invited by any one to a wedding, do not recline in the first place, lest a more honorable man than you may have been invited by him;
9 Ngati zitatero, ndiye kuti munthu uja amene anakuyitani inu nonse awiri adzakuwuzani kuti, ‘Mupatseni munthu uyu malo anu.’ Pamenepo inu mudzachita manyazi, pokakhala malo wotsika.
and he that invited you and him, come and say to you, Give place to this man; and then you shall begin with shame to take the last place.
10 Koma akakuyitanani, khalani pa malo otsika, kuti amene anakuyitanani uja adzakuwuzeni kuti, ‘Bwenzi, bwera udzakhale pa malo aulemu pano.’ Pamenepo inu mudzalandira ulemu pamaso pa alendo anzanu onse.
But when you are invited, go and recline in the last place, that when he that invited you shall come, he may say to you, Friend, go up higher. Then you shall have honor in the presence of those who recline with you.
11 Pakuti aliyense wodzikuza adzamuchepetsa, ndipo aliyense wodzichepetsa adzamukweza.”
For every one that exalts himself shall be humbled; and he that humbles himself shall be exalted.
12 Kenaka Yesu anati kwa mwini malo uja, “Ukakonza chakudya chamasana kapena chamadzulo, usamayitane abwenzi ako, abale ako, anthu afuko lako kapena anzako achuma; ngati iwe utero, iwo adzakuyitananso, choncho udzalandiriratu mphotho yako.
Then he said also to him that had invited him: When you make a dinner or a supper, call not your friends, nor your brothers, nor your relatives, nor your rich neighbors, lest they also invite you in return, and a recompense be made you.
13 Koma ukakonza phwando, itana anthu osauka, ofa ziwalo, olumala ndi osaona.
But when you make a feast, invite the poor, the maimed, the lame, the blind;
14 Pamenepo udzakhala wodala, chifukwa iwo sangakubwezere kanthu, koma Mulungu ndiye adzakubwezera pa chiukitso cha olungama.”
and you shall be blessed; for they have no power to repay you; but you shall be repaid at the resurrection of the just.
15 Mmodzi mwa amene amadya naye atamva izi, anati kwa Yesu, “Ndi wodala munthu amene adzadye nawo mu ufumu wa Mulungu.”
And a certain one of those who reclined at table with him, after hearing these things, said to him: Blessed is he who shall cat bread in the kingdom of God.
16 Yesu anayankha kuti, “Munthu wina ankakonza phwando lalikulu ndipo anayitana alendo ambiri.
And he said to him: A certain man made a great supper, and invited many.
17 Nthawi yaphwando itakwana anatuma wantchito wake kuti akawuze onse amene anayitanidwa kuti, ‘Bwerani, pakuti zonse zakonzeka.’
And he sent his servant at the hour of supper, to say to those who had been invited, Come, for all things are now ready.
18 “Koma onse anayamba kupereka zifukwa mofanana. Woyamba anati, ‘Ine ndangogula kumene munda, ndipo ndikuyenera kupita kuti ndikawuone. Pepani mundikhululukire.’
And they all, with one consent, began to make excuse. The first said to him, I have bought a farm, and I must go and see it; I pray you, have me excused.
19 “Wina anati, ‘Ndangogula kumene ngʼombe khumi zokoka ngolo ndipo kupita kukaziyesa. Pepani mundikhululukire.’
And another said, I have bought five yoke of oxen, and I am going to try them; I pray you, have me excused.
20 “Wina anatinso, ‘Ine ndangokwatira kumene, choncho sinditha kubwera.’
And another said, I have married a wife, and, for this reason, I can not come.
21 “Wantchitoyo anabwera ndikudzamuwuza bwana wakeyo zimenezi. Pamenepo mphwandoyo anapsa mtima ndipo analamula wantchito wakeyo kuti, ‘Pita msangamsanga kunja mʼmisewu ndi mʼmakwalala a mu mzinda ndipo ukabweretse osauka, ofa ziwalo, osaona ndi olumala.’
And that servant came and told his lord these things. Then the master of the house was angry, and said to his servant, Go out quickly into the streets and lanes of the city, and bring in hither the poor and the maimed, the lame and the blind.
22 “Wantchitoyo anati, ‘Bwana, zimene munanena zachitika koma malo akanalipobe.’
And the servant said, Lord, it is done as you commanded, and yet there is room.
23 “Ndipo mbuye uja anawuza wantchito wake kuti, ‘Pita kunja ku misewu ikuluikulu ndi kunja kwa mpanda ndipo ukawawuze kuti alowe, kuti nyumba yanga idzaze.
And the lord said to his servant, Go out into the roads, and among the hedges, and compel them to come in, that my house may be full.
24 Ine ndikukuwuzani inu kuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anayitanidwa adzalawa phwandolo.’”
For I say to you, that not one of those men who have been invited, shall taste of my supper.
25 Gulu lalikulu la anthu linkayenda naye Yesu ndipo atatembenukira kwa iwo anati,
And many multitudes were journeying with him; and he turned and said to them:
26 “Ngati wina aliyense abwera kwa Ine ndipo sadana ndi abambo ndi amayi ake, mkazi wake ndi ana, abale ake ndi alongo ake, inde ngakhale moyo wake omwe, iye sangakhale ophunzira wanga.
If any one comes to me, and hates not his father and mother and wife and children and brothers and sisters, and his own life also, he can not be my disciple.
27 Ndipo aliyense amene sasenza mtanda wake ndi kunditsata Ine sangakhale ophunzira wanga.
And whoever does not bear his cross, and come after me, can not be my disciple.
28 “Taganizani, ngati wina mwa inu akufuna kumanga nsanja, kodi iye sayamba wakhala pansi ndi kuganizira za mtengo wake kuti aone ngati ali ndi ndalama zokwanira kuti atsirizire?
For which of you, intending to build a tower, does not first sit down, and count the cost, whether he has the means to finish it?
29 Pakuti ngati ayika maziko ndi kulephera kutsiriza, aliyense amene adzayiona adzamuseka,
Lest, when he has laid the foundation, and is not able to finish, all that see it begin to deride him,
30 nanena kuti, ‘Munthu uyu anayamba kumanga koma sanathe kutsiriza.’
saying, This man began to build, and was not able to finish.
31 “Kapena mfumu imene ikupita ku nkhondo kukamenyana ndi mfumu ina, kodi siyamba yakhala pansi ndi kulingalira ngati ingathe ndi anthu 10,000 kulimbana ndi amene akubwera ndi 20,000?
Or, what king, going to make war against another king, does not first sit down, and deliberate whether he is able, with ten thousand, to meet him that is coming; against him with twenty thousand?
32 Ngati singathe, idzatuma nthumwi pomwe winayo ali kutali ndi kukapempha mgwirizano wamtendere.
And if not, while he is yet at a distance, he sends an embassy, and asks for conditions of peace.
33 Mʼnjira yomweyo, wina aliyense wa inu amene sasiya zonse ali nazo sangakhale ophunzira wanga.
So, then, whoever of you does not forsake all that he has, can not be my disciple.
34 “Mchere ndi wabwino, koma ngati usukuluka adzawukoleretsanso ndi chiyani?
Salt is good; but if the salt become tasteless, by what means shall it become salt again?
35 Suyeneranso ngakhale mʼnthaka kapena kudzala la manyowa; umatayidwa kunja. “Amene ali ndi makutu akumva, amve.”
It is fit neither for earth, nor for manure; but they cast it out. He that has ears to hear, let him hear.