< Luka 13 >
1 Nthawi yomweyo panali ena amene analipo omwe amamuwuza Yesu za Agalileya amene magazi awo Pilato anawasakaniza ndi nsembe zawo.
Shipindi shilii wantu wamu yawaweriti palii wamgambiriti Yesu kwajili wantu wa Galilaya weni Pilatu kawalagiti pawaweriti wankulaviya tambiku kwa Mlungu.
2 Yesu anayankha kuti, “Kodi mukuganiza kuti Agalileya amenewa anali ochimwa kwambiri kuposa Agalileya ena onse chifukwa anavutika mʼnjira iyi?
Yesu kawakosiya, “Toziya wantu wa Galilaya wawalagiti kwa njira ilii, mlihola kuwera waweriti na vidoda kuliku wantu wa Galilaya wamonga?
3 Ine ndikuti, ayi! Koma ngati inu simutembenuka mtima, inunso mudzawonongeka nonse.
Neni nonga, ndala! Nukugambirani kuwera handa pamlema kuleka vidoda vyamtenda, hamhowi ntambu yawahowiti womberi.
4 Kapena anthu 18 aja amene anafa nsanja ya Siloamu itawagwera, kodi mukuganiza kuti iwo aja anali ochimwa kwambiri kuposa onse amene amakhala mu Yerusalemu?
Ntambu gaa kwajili ya wantu lilongu na wanani wa Silowamu yawahowiti shipindi mnara paguwatulukiriti? Mlihola kuwera womberi waweriti wanavidoda kuliku wantu wamonga wawalikala Yerusalemu?
5 Ine ndikuti, ayi! Koma ngati inu simutembenuka mtima, inunso mudzawonongeka nonse.”
Ndala! Nukugambirani mwenga, handa pamlema kuleka vidoda vyamtenda, hamhowi ntambu yawahowiti womberi.”
6 Kenaka Iye anawawuza fanizo kuti, “Munthu wina anali ndi mtengo wamkuyu, umene anadzala mʼmunda wamphesa, ndipo Iye anapita kukayangʼana zipatso, koma sanazipeze.
Su Yesu kawagambiriti mfanu agu, “Kuweriti na muntu yumu, keniti na mtera gwa tini mulirambu lyakuwi. Kagenditi kwapa tini mumtera kumbiti kapata ndiri.
7 Tsono kwa munthu amene amasamalira munda wamphesawo anati, ‘Kwa zaka zitatu tsopano ndakhala ndikubwera kudzafuna chipatso pa mtengo uwu ndipo sindinachipeze. Udule! Nʼchifukwa chiyani ukuwononga nthaka?’
Su kamgambiriti ntumintumi gwa lirambu, ‘Guloli, kwa mivinja mitatu paniza kwapa mabwajubwaju mumtera gwa tini, kumbiti nugawona ndiri. Gugudumuli! Toziya gumalira hera litapaka.’
8 “Munthuyo anayankha kuti, ‘Bwana, tawusiyani kwa chaka chimodzi chokha ndipo ine ndikumba ngalande mozungulira ndi kuthira manyowa.
Kumbiti ntumintumi kamgambira, ‘Mtuwa, guguleki huti kwa shinja shimu hera, hanugulimili na kugulekera mbotu.
9 Ngati udzabale zipatso chaka chamawa, zili bwino! Koma ngati sudzabala, pamenepo mudzawudule.’”
Pagulera mabwajubwaju shinja shankwiza, hayiherepi nentu, kumbiti pagulera ndiri su guweza kugudumula.’”
10 Pa Sabata Yesu ankaphunzitsa mʼsunagoge ina,
Yesu kaweriti munumba ya Mlungu mulishaka lya kwoyera pakafunda.
11 ndipo momwemo munali mayi amene anali ndi mzimu woyipa umene unamudwalitsa zaka 18. Iye anali wokhota msana ndipo samatha kuweramuka ndi pangʼono pomwe.
Palii peniti na mdala yakeniti na shamshera yakamtenda kalwali mivinja lilongu na nane, kaweriti na shibyongu ata kasinditi kugoloka.
12 Yesu atamuona anamuyitana kutsogolo ndipo anati kwa iye, “Amayi, mwamasulidwa ku mavuto.”
Yesu pakamwoniti kamshema, “Mawu, su guponiziwa ulweli waku!”
13 Kenaka anasanjika manja ake pa iye, ndipo nthawi yomweyo anawongoka nayamika Mulungu.
Kamtulila mawoku gakuwi, na palaa palii shibyongu shihuka na kawera safi, su kamkwisiti Mlungu.
14 Chifukwa cha kuyipidwa kuti Yesu anachiritsa pa Sabata, wolamulira sunagoge anati kwa anthu, “Pali masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito. Choncho bwerani kuti mudzachiritsidwe masiku amenewo osati pa Sabata.”
Mkulu gwa numba ya Mlungu kaweriti kakalala Yesu pakamponiziyiti mulishaka lya kwoyera, su kawagambiriti wantu, “Kwana mashaka sita gamuweza kutenda lihengu, mwizi mumashaka aga muponiziwi malweli genu, namwiza Mulishaka lya kwoyera!”
15 Ambuye anamuyankha kuti, “Iwe wachiphamaso! Kodi nonsenu simumasula pa Sabata ngʼombe zanu kapena bulu kumuchotsa mʼkhola ndi kupita naye kukamupatsa madzi?
Mtuwa kamwankula, “Gwamfyangu gwenga! Ndo gaa pakati penu mekamvuguli ng'ombi ama punda gwakuwi kulawa mulizizi na kumtenda kalandi mashi ata payiwera lishaka lya kwoyera?
16 Nanga mayiyu, amene ndi mwana wa Abrahamu, ndipo anamangidwa ndi Satana zaka 18, kodi siwoyenera kuti amasulidwe msinga imeneyi pa tsiku la Sabata?”
Vinu su peni panu kwana muhinga gwa Aburahamu ndomweni Shetani kamtenda shibyongu kwa mivinja lilongu na nane, su iherepa ndiri kumponiziya mulishaka lya kwoyera?”
17 Atanena izi, onse omutsutsa anachititsidwa manyazi, koma anthu anakondwera ndi zodabwitsa zonse zimene Iye anazichita.
Kuwankula kwakuwi kuwatenditi wadoda wawoni soni weni, kumbiti wantu wamonga wanemeleriti toziya ya vitwatira vyakatenditi.
18 Kenaka Yesu anafunsa kuti, “Kodi ufumu wa Mulungu uli ngati chiyani? Kodi Ine ndingawufanizire ndi chiyani?
Yesu kakosiyiti, “Ufalumi wa Mlungu ulifana na shishi? Nuufaniziyi na shintu gaa?
19 Uli ngati mbewu ya mpiru, imene munthu anatenga ndi kudzala mʼmunda mwake. Inakula, nʼkukhala mtengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinakhala mʼnthambi zake.”
Ulifana hangu. Muntu katola mbeyu ndidini nentu ya haradali na kuyala mulirambu. Mbeyu imera na kuwera mtera, na wampongu wiza na kunyawa vitukulu vyawu mumitambi.”
20 Iye anafunsanso kuti, “Kodi ufumu wa Mulungu ndingawufanizire ndi chiyani?
Kayi Yesu kakosiya, “Hanuufaniziyi Ufalumi wa Mlungu na shintu gaa?
21 Uli ngati yisiti amene mayi anatenga ndi kusakaniza ndi ufa wambiri mpaka anafufumitsa ufawo.”
Ulifana na simika yakatoliti mawu yumu na kuyihanganyiya pamuhera na ubumu vipimu vitatu, su ubumu woseri ututumuka.”
22 Ndipo Yesu anayendayenda mʼmizinda ndi mʼmidzi, kumaphunzitsa pamene Iye ankapita ku Yerusalemu.
Yesu kendereyiti na mwanja gwakuwi kugenda muisi na muvijiji, pakafunda wantu na pakanyawa njira yakuwi kugenda Yerusalemu.
23 Wina anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi ndi anthu ochepa okha amene adzapulumutsidwe?” Iye anawawuza kuti,
Muntu yumu su kamkosiya, “Mtuwa, wantu hawawalopoziyi ndo wadidini hera?” Yesu kawagambiriti,
24 “Yesetsani kulowa pa khomo lopapatiza, chifukwa ndikukuwuzani kuti ambiri adzafuna kulowa koma sadzatha kutero.
“Mkamaliri nentu kwingira mumlyangu mdidini, toziya wantu wavuwa hawajeli nakaka kwingira kumbiti hapeni wingiri.
25 Nthawi yomwe mwini nyumba adzayimirira ndi kutseka chitseko, inu mudzayima kunja kugogoda ndi kudandaula kuti, ‘Bwana, tatitsekulirani khomo.’ “Koma Iye adzayankha kuti, ‘Ine sindikukudziwani ndipo sindikudziwanso kumene mwachokera.’
Mkulu gwa numba hakimuki na kutata mlyangu, mwenga hamgoloki kunja na kwanja kukota mlyangu na kulonga, ‘Mtuwa, mtuwa! Gutuvuguliri mlyangu!’ Nayomberi hakawankuli, ‘Nuwamana ndiri mwenga na pamlawa!’
26 “Ndipo inu mudzati, tinkadya ndi kumwa ndi inu ndipo munkaphunzitsa mʼmisewu yathu.
Su mwenga hamwankuli, ‘Tuliya na kulanda pamuwera na gwenga, na gwenga gutufunditi muisi yetu!’
27 “Koma Iye adzayankha kuti, ‘Ine sindikukudziwani ndipo sindikudziwanso kumene mwachokera. Chokereni inu nonse ochita zoyipa!’
Kumbiti yomberi kayi hakalongi, ‘Nupamana ndiri pamlawa. Muwuki kulawa kwaneni mwoseri mtenda vidoda!’
28 “Mudzalira ndi kukuta mano mukadzaona Abrahamu, Isake ndi Yakobo ndi aneneri onse ali mu ufumu wa Mulungu koma inuyo mutaponyedwa kunja.
Su panu hamulili na kugayagaya menu genu pawakwasirani kunja na hamuwaloli Aburahamu na Isaka na Yakobu na wambuyi wa Mlungu Muufalumi wa Mlungu!
29 Anthu adzachokera kummawa ndi kumadzulo, kumpoto ndi kummwera, kudzakhala pa phwando mu ufumu wa Mulungu.
Wantu hawizi kulawa kwagulawa mushenji na kwaguzyeta mushenji, kulawa kushana na kusika, su hawaweri mumsambu Muufalumi wa Mlungu.
30 Ndithudi otsirizira ndiye adzakhale oyambirira, ndipo oyambirira ndiye adzakhale otsirizira.”
Su woseri yawawera wa upeleru hawaweri wa kwanja, na woseri yawawera vinu wa kwanja hawaweri wa upeleru.”
31 Pa nthawi imeneyo Afarisi anabwera kwa Yesu ndipo anati kwa Iye, “Chokani malo ano ndipo pitani kumalo ena aliwonse. Herode akufuna kukuphani.”
Shipindi shilaa shiliya Wamafalisayu wamu wamwiziriti Yesu na kumgambira, “Gufiruwa guwuki panu na gugendi pahala pingi, toziya Herodi kafira kakulagi gwenga!”
32 Iye anayankha kuti, “Pitani kawuzeni nkhandweyo, Ine ndikutulutsa ziwanda ndi kuchiritsa anthu lero ndi mawa ndipo tsiku lachitatu ndidzakwaniritsa cholinga changa.”
Yesu kawankula, “Mgendi mwakamgambiri shibweta ulii hangu, ‘Nankuwalaviya washamshera na kuwaponiziya walweli leru na shilawu, na lishaka lya tatu hamalili lihengu lyangu.’
33 Mʼnjira ina iliyonse, Ine ndiyenera kupitirira ulendo wanga lero, mawa ndi mkuja. Zoona nʼzakuti mneneri sangafere kunja kwa Yerusalemu.
Vila vilii mpaka nweri mumwanja leru, na shilawu, na lishaka limonga, toziya iherepa ndiri kwa mbuyi gwa Mlungu wamlagi kunja kwa Yerusalemu.
34 Iwe Yerusalemu, Yerusalemu! Umapha aneneri ndi kuwagenda miyala anthu amene atumizidwa kwa iwe. Nthawi zambiri ndakhala ndikufuna kusonkhanitsa ana ako pamodzi, monga nkhuku imasonkhanitsira anapiye pansi pa mapiko ake, koma iwe sunafune!
“Yerusalemu! Shondi shondi Yerusalemu bamu! Guwalaga wambuyi wa Mlungu, guwagumanga kwa mabuwi walii yawatumitwi kwaku! Vipindi vivuwa nfira kuwatula wana waku mumawoku mwangu gambira nkuku pakavigupika vyana vyakuwi kwa mbapatiru zyakuwi, kumbiti gwenga gunema!
35 Taona, nyumba yako yasanduka bwinja. Ine ndikukuwuza kuti, sudzandionanso mpaka pamene udzati, “Wodala amene akubwera mʼdzina la Ambuye!”
Su hawakulekeli gumweni numba yaku. Nukugambira nakaka gwenga hapeni muwoni mpaka shipindi shiza pamtakula, ‘Mlungu gumtekeleri ulii yakiza mulitawu lya Mtuwa.’”