< Luka 12 >

1 Nthawi yomweyo, anthu miyandamiyanda atasonkhana, ndi kumapondanapondana, Yesu anayamba kuyankhula poyamba kwa ophunzira ake, nati, “Chenjereni ndi yisiti wa Afarisi, amene ndi chinyengo.
Meanwhile, when a crowd of thousands had converged, so that they were stepping on each other, He began to speak first to His disciples: “Guard yourselves from the ‘yeast’ of the Pharisees, which is hypocrisy.
2 Palibe chinthu chophimbika chimene sichidzawululika, kapena chobisika chimene sichidzadziwika.
There is nothing concealed that will not be revealed, or hidden that will not be known.
3 Chimene mwanena mu mdima chidzamveka dzuwa likuwala, ndipo zimene mwanongʼona mʼkhutu mʼchipinda chamʼkati, zidzayankhulidwa pa denga la nyumba.
Therefore whatever you have spoken in the dark will be heard in the light, and what you have whispered in the ear behind closed doors will be proclaimed from the housetops.
4 “Ine ndikuwuzani, abwenzi anga, musachite mantha ndi amene amapha thupi chifukwa akatero sangachitenso kanthu.
“Further, I say to you, my friends: do not be afraid of those who kill the body and after that have nothing more that they can do.
5 Koma Ine ndidzakuonetsani amene muyenera kumuopa: Wopani Iye, amene pambuyo pakupha thupi, ali ndi mphamvu yakukuponyani ku gehena. Inde, Ine ndikuwuzani, muopeni Iye. (Geenna g1067)
Rather, I will advise you whom you should fear—fear Him who after He kills has authority to cast into Gehenna; yes indeed, fear Him! (Geenna g1067)
6 Kodi atimba asanu samagulidwa ndi ndalama ziwiri? Ngakhale zili chomwecho palibe imodzi ya izo imene imayiwalika ndi Mulungu.
Are not five sparrows sold for two copper coins? Yet not one of them is forgotten before God.
7 Ndithudi, tsitsi lonse la mʼmutu mwanu ndi lowerengedwa. Musachite mantha; inu ndi oposa kwambiri mpheta zambiri.
Even the hairs of your head are all numbered! So do not be afraid; you are far more valuable than sparrows!
8 “Ine ndikukuwuza kuti, aliyense amene avomereza Ine pamaso pa anthu, Mwana wa Munthu adzamuvomerezanso pamaso pa angelo a Mulungu.
“Also I say to you, whoever claims me before men, the Son of the Man will also claim him before the angels of God.
9 Koma iye amene andikana Ine pamaso pa anthu adzakanidwanso pamaso pa angelo a Mulungu.
But whoever disclaims me before men will be disclaimed before the angels of God.
10 Ndipo aliyense amene ayankhulira Mwana wa Munthu mawu oyipa adzakhululukidwa, koma iye wochitira mwano Mzimu Woyera sadzakhululukidwa.
Anyone who speaks a word against the Son of the Man, it can be forgiven him; but to him who blasphemes against the Holy Spirit it will not be forgiven.
11 “Akadzakutengerani ku masunagoge pamaso pa oweruza ndi a maulamuliro, musadere nkhawa mmene mudzadzitchinjirizire nokha kapena chimene mudzayankhule,
Now whenever they bring you before synagogues, rulers and authorities, do not worry about how or what you will answer, or what you should say.
12 pakuti Mzimu Woyera nthawi imeneyo adzakuphunzitsani zoyenera kunena.”
Because the Holy Spirit will teach you in that very hour what you need to say.”
13 Munthu wina mʼgulu la anthu anati kwa Iye, “Aphunzitsi, muwuzeni mʼbale wanga andigawireko chuma chamasiye.”
Then someone from the crowd said to Him, “Teacher, tell my brother to divide the inheritance with me.”
14 Yesu anayankha kuti, “Munthu iwe, ndani anandiyika Ine kukhala woweruza kapena wogawa chuma pakati panu?”
But He said to him, “Man, who appointed me a judge or an arbiter over you?”
15 Kenaka Iye anawawuza kuti, “Chenjerani! Khalani tcheru ndi makhalidwe onse adyera; moyo wa munthu sukhala chifukwa cha kuchuluka kwa zimene ali nazo.”
Then He said to them, “Keep alert and guard against covetousness, because one's life does not consist in the abundance of his possessions.”
16 Ndipo Iye anawawuza fanizo ili, “Munda wa munthu wina wachuma unabereka kwambiri.
Then He told them a parable, saying: “The ground of a certain rich man produced well.
17 Iye anaganiza kuti, ‘Ndichite chiyani? Ndilibe malo osungiramo mbewu zanga.’
And he reasoned within himself saying, ‘What shall I do, because I have no place to store my crops?’
18 “Ndipo Iye anati, ichi ndi chimene ndidzachite: Ndidzaphwasula nkhokwe zanga zonse ndi kumanga zokulirapo, ndipo ndidzasungira mʼmenemo mbewu ndi katundu.
Then he said: ‘This is what I will do. I will tear down my barns and build bigger ones, and there I will store all my produce and my goods.
19 Ndipo ndidzawuza moyo wanga kuti, ‘Uli nazo zinthu zabwino zambiri zimene zikhalepo zaka zambiri, usapupulume; idya, imwa ndi kukondwera.’”
And I will say to my soul: Soul, you have many goods laid up for many years. Take life easy; eat, drink and enjoy yourself!’
20 “Koma Mulungu anati kwa iye, ‘Iwe wopusa! Usiku womwe uno moyo wako udzachotsedwa kwa iwe, ndipo ndi ndani amene adzatenge zimene iwe wadzikonzera?’
But God said to him: ‘Stupid! This very night your life is being taken back from you; then who will get the things you have prepared?’
21 “Umu ndi mmene zidzakhalire ndi aliyense amene amadziwunjikira chuma, koma si wachuma pamaso pa Mulungu.”
Just like that is he who accumulates treasure for himself and is not rich toward God.”
22 Kenaka Yesu anati kwa ophunzira ake, “Choncho Ine ndikuwuzani kuti musadere nkhawa za moyo wanu, zimene mudzadya; kapena za thupi lanu, zimene mudzavala.
Then He said to His disciples: “Therefore I say to you, do not worry about your life, what you will eat; nor about the body, what you will wear.
23 Moyo uposa chakudya, ndi thupi liposa chovala.
Life is more than food, and the body more than clothes.
24 Taonani makwangwala: iwo safesa kapena kukolola, alibe nyumba zosungamo zinthu kapena nkhokwe; komabe, Mulungu amawadyetsa. Koposa kotani inu amene ndi ofunikira kuposa mbalame.
Consider the ravens: they neither sow nor reap, they have neither storeroom nor barn, and God feeds them. You are far more valuable than the birds!
25 Ndi ndani wa inu akhoza kuwonjeza ora pa moyo wake chifukwa cha kudandaula?
And who among you can add one cubit to his height by worrying?
26 Popeza simungathe kuchita kanthu kakangʼono aka, nʼchifukwa chiyani mumadandaula ndi zinazi?
So if you cannot do even such a little thing, why worry about the rest?
27 “Taonani mmene maluwa amakulira. Iwo sagwira ntchito kapena kusoka zovala. Koma Ine ndikuwuzani kuti, ngakhale Solomoni muulemelero wake wonse sanavalepo ngati limodzi la awa.
“Consider the lilies, how they grow: they neither toil nor spin; I say to you, not even Solomon in all his splendor was clothed like one of these.
28 Ngati umu ndi mmene Mulungu amavekera udzu wakuthengo, umene lero ulipo ndipo mawa uponyedwa pa moto, nanga Iye adzakuvekani inu motani. Haa! Inu achikhulupiriro chochepa!
So if God so clothes the grass that today is in the field and tomorrow is thrown into an oven, how much more you, O little-faiths!
29 Ndipo musayike mtima wanu pa zimene mudzadye kapena kumwa; musade nazo nkhawa.
Do not concentrate on what you may eat or what you may drink; do not be anxious.
30 Pakuti anthu akunja amathamanga kufunafuna zinthu zotere, ndipo Atate amadziwa kuti mumazifuna zimenezi.
All these things really occupy the nations of the world, and your Father knows that you need them.
31 Koma funafunani ufumu wake, ndipo mudzapatsidwa zonsezi.
Rather, concentrate on the Kingdom of God, and all these things will be provided for you.
32 “Musachite mantha, inu kagulu kankhosa, pakuti zinakondweretsa Atate anu kuti akupatseni ufumu.
“Do not fear, little flock, because it pleased the Father to give you the Kingdom.
33 Gulitsani zonse zimene muli nazo, ndipo ndalama zake mupereke kwa osauka. Dzipezereni zikwama zandalama zimene sizidzatha, ndi kudzikundikira chuma chomwe sichidzatha kumwamba, kumene mbala sizingafikeko, ndipo dzimbiri silingawononge.
Sell your possessions and give to charity. Make for yourselves ‘purses’ that will not wear out, an unfailing treasure in the heavens, where a thief cannot approach, nor a moth destroy.
34 Popeza kumene kuli chuma chanu, mtima wanunso udzakhala komweko.”
Because where your treasure is, there your heart will be also.
35 “Khalani okonzekeratu ndipo nyale zanu ziziyaka,
“Let your waists be belted and your lamps burning,
36 ngati anthu oyembekezera kubwera kwa mbuye wawo kuchokera kuphwando la ukwati, kuti pamene afika ndi kugogoda akhoza nthawi yomweyo kumutsekulira chitseko.
and you yourselves like men waiting for their master when he returns from the wedding celebration, so that when he comes and knocks they may open to him immediately.
37 Zidzakhala bwino kwa antchitowo amene mbuye wawo pobwera adzawapeze akudikira. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti adzakonzekera kuwatumikira, adzakhala nawo pa tebulo ndipo adzabwera ndi kuwatumikira.
Blessed are those slaves whom the master will find watching when he comes. Assuredly I say to you that he will gird himself and have them recline, and will come and serve them.
38 Zidzakhala bwino kwa antchitowo amene mbuye wawo adzawapeze ali okonzeka, ngakhale iye atabwera pa ora lachiwiri kapena lachitatu usiku.
And if he should come in the second watch, or come in the third watch, and find them so, blessed are those slaves.
39 Koma zindikirani izi: Ngati mwini nyumba akanadziwa ora limene mbala ibwera, sakanalola kuti nyumba yake ithyoledwe.
But know this, that if the master of the house had known in what hour the thief was coming, he would have kept watch and not allowed his house to be broken into.
40 Inunso muyenera kukhala okonzeka, chifukwa Mwana wa Munthu adzabwera pa ora limene simukumuyembekezera Iye.”
Therefore you also be ready, because the Son of the Man is coming at an hour you do not expect.”
41 Petro anafunsa kuti, “Kodi mukunena fanizoli kwa ife, kapena kwa aliyense?”
Then Peter said to Him, “Lord, are you directing this parable to us, or to everyone?”
42 Ambuye anayankha kuti, “Kodi tsono woyangʼanira wokhulupirika ndi wanzeru ndani? Kodi ndi amene mbuye wake wamuyika kukhala oyangʼanira antchito ake kuti aziwapatsa ndalama yachakudya pa nthawi yake yoyenera?
So the Lord said: “Who then is the faithful and prudent steward whom his master will place over his household to give them the food allowance at the right time?
43 Zidzamukhalira bwino wantchito amene mbuye wake adzamupeza akuchita zimene pamene iye abwera.
Blessed is that slave whom his master will find so doing when he comes.
44 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti adzamuyika kukhala woyangʼanira katundu wake yense.
I tell you truly that he will put him in charge of all his possessions.
45 Koma tiyerekeze kuti wantchitoyo aziganiza mu mtima mwake kuti, ‘Bwana wanga akuchedwa kwambiri kubwera,’ ndipo kenaka ndi kuyamba kumenya antchito aamuna ndi aakazi ndi kudya, kumwa ndi kuledzera.
But if that servant should say in his heart, ‘My master won't come for a while,’ and should begin to hit the male and female servants, and to eat and drink and get drunk,
46 Mbuye wake adzabwera tsiku limene iye sakumuyembekezera ndi ora limene iye sakudziwa. Iye adzamulanga ndi kumusiya kumalo kumene kuli osakhulupirira.
the master of that slave will come on a day when he does not expect him, and at an hour that he does not know, and will cut him in two and appoint his portion with the unbelievers.
47 “Wantchito amene amadziwa chifuniro cha mbuye wake koma wosakonzeka kapena wosachita chimene mbuye wake akufuna adzakwapulidwa zikwapu zambiri.
“That servant who knew his master's will, but neither got ready nor did according to that will, will be beaten with many blows.
48 Koma wantchito amene sadziwa koma nʼkuchita zinthu zoyenera chilango, adzakwapulidwa zikwapu zochepa. Aliyense amene anapatsidwa zambiri, adzayenera kubwezanso zambiri; ndipo amene anamusungitsa zambiri, adzamulamula kuti abweze zambirinso.”
But he who did not know, yet did things worthy of blows, will be beaten with few. Everyone to whom much has been given, from him much will be required; and to whom much was entrusted, of him much more will be asked.
49 “Ine ndabwera kudzayatsa moto pa dziko lapansi, ndipo ndikanakonda ukanayaka kale.
“I came to bring fire to the earth, and how I wish it were already kindled!
50 Koma Ine ndiyenera kubatizidwa, ndipo ndikusautsika mu mtima mpaka utachitika!
But I have a baptism to undergo, and how distressed I am until it is completed!
51 Kodi mukuganiza kuti Ine ndinabwera kudzabweretsa mtendere pa dziko lapansi? Ayi, Ine ndikukuwuzani kuti, ndinabweretsa kugawikana.
Do you imagine that I came to provide peace on the earth? Not at all, I tell you, but rather division.
52 Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo mʼbanja limodzi mudzakhala anthu asanu ndipo adzawukirana wina ndi mnzake, atatu kuwukira awiri, ndipo awiri kuwukira atatu.
Because from now on there will be five in one house divided: three against two and two against three.
53 Anthu adzawukirana. Abambo kudzawukira mwana wawo wamwamuna, mwana wawoyo adzawukira abambo ake. Amayi adzawukira mwana wawo wamkazi, mwana wawoyo adzawukira amayi ake. Amayi adzawukira mpongozi wawo wamkazi, mpongoziyo adzawukira amayiwo.”
Father will be divided against son and son against father, mother against daughter and daughter against mother, mother-in-law against her daughter-in-law and daughter-in-law against her mother-in-law.”
54 Iye anati kwa gulu la anthu, “Pamene mukuona mtambo ukukwera kummawa, nthawi yomweyo inu mumati, ‘kugwa mvula,’ ndipo imagwadi.
Then He also said to the crowds: “Whenever you see a cloud rising from the west, immediately you say, ‘A rainstorm is coming,’ and so it does.
55 Ndipo pamene mphepo yakummwera ikuwomba, inu mumati ‘kutentha’ ndipo kumaterodi.
And whenever a south wind blows, you say, ‘It will be hot,’ and it happens.
56 Achiphamaso inu! Inu mumadziwa kutanthauzira maonekedwe a dziko lapansi ndi thambo. Zikutheka bwanji kuti simukudziwa kumasulira kwa nthawi ino?
Hypocrites! You know how to interpret the appearance of the sky and of the earth, so how can you not discern this time?
57 “Bwanji simukuzindikira nokha zoyenera kuchita?
Also why, even of yourselves, do you not judge what is right?
58 Pamene mukupita kwa woweruza ndi amene munalakwirana naye, yesetsani kwambiri kuti muyanjane naye mʼnjiramo, chifukwa mukapanda kutero akhoza kukutengerani ku bwalo la milandu ndipo woweruzayo adzakuperekani kwa woyangʼanira ndende, ndipo woyangʼanira ndendeyo adzakuponyani mʼndende.
“When you are going with your adversary to the magistrate, make every effort along the way to settle with him, lest he drag you to the judge, the judge deliver you to the bailiff, and the bailiff throw you into prison.
59 Ine ndikuwuzani kuti, simudzatulukamo mpaka mutalipira ndalama zonse.”
I tell you, you will by no means get out of there until you have paid the last penny.”

< Luka 12 >