< Luka 12 >

1 Nthawi yomweyo, anthu miyandamiyanda atasonkhana, ndi kumapondanapondana, Yesu anayamba kuyankhula poyamba kwa ophunzira ake, nati, “Chenjereni ndi yisiti wa Afarisi, amene ndi chinyengo.
Mezitím se shromáždily tisíce lidí. Bylo jich tolik, že se málem ušlapali. Ježíš však nejprve promluvil ke svým učedníkům: „Varujte se pokrytectví farizejů. Je jako kvas, který snadno pronikne těsto.
2 Palibe chinthu chophimbika chimene sichidzawululika, kapena chobisika chimene sichidzadziwika.
Nic se nedá navždy zatajit.
3 Chimene mwanena mu mdima chidzamveka dzuwa likuwala, ndipo zimene mwanongʼona mʼkhutu mʼchipinda chamʼkati, zidzayankhulidwa pa denga la nyumba.
Všechno, co jste si řekli za tmy, bude jednou řečeno na denním světle. A co jste si šeptali za zavřenými dveřmi, bude voláno ze střech.
4 “Ine ndikuwuzani, abwenzi anga, musachite mantha ndi amene amapha thupi chifukwa akatero sangachitenso kanthu.
Jako přátelům vám radím: nebojte se těch, kteří mohou zabít jen tělo, ale víc vám udělat nemohou.
5 Koma Ine ndidzakuonetsani amene muyenera kumuopa: Wopani Iye, amene pambuyo pakupha thupi, ali ndi mphamvu yakukuponyani ku gehena. Inde, Ine ndikuwuzani, muopeni Iye. (Geenna g1067)
Jen toho se bojte, kdo má moc ukončit nejen časný život, ale rozhodnout i o vaší věčnosti: Boha mějte v úctě! (Geenna g1067)
6 Kodi atimba asanu samagulidwa ndi ndalama ziwiri? Ngakhale zili chomwecho palibe imodzi ya izo imene imayiwalika ndi Mulungu.
Jakou cenu má vrabec na vašem trhu? Pár haléřů. Vidíte, a ani na jednoho z nich Bůh nezapomene. Jak by tedy mohl zapomenout na vás?
7 Ndithudi, tsitsi lonse la mʼmutu mwanu ndi lowerengedwa. Musachite mantha; inu ndi oposa kwambiri mpheta zambiri.
On ví i to, kolik máte vlasů na hlavě. Proto se nebojte, vás si Bůh váží daleko víc než mnoha vrabců dohromady.
8 “Ine ndikukuwuza kuti, aliyense amene avomereza Ine pamaso pa anthu, Mwana wa Munthu adzamuvomerezanso pamaso pa angelo a Mulungu.
Říkám vám, kdo se ke mně hlásí před lidmi, toho jako Syn člověka zastoupím na posledním soudu.
9 Koma iye amene andikana Ine pamaso pa anthu adzakanidwanso pamaso pa angelo a Mulungu.
Kdo mě však před lidmi zapře, k tomu se hlásit nebudu.
10 Ndipo aliyense amene ayankhulira Mwana wa Munthu mawu oyipa adzakhululukidwa, koma iye wochitira mwano Mzimu Woyera sadzakhululukidwa.
Kdo urazí Syna člověka, tomu může být odpuštěno. Ale kdo uráží Ducha svatého, který působí skrze mne, tomu odpuštěno nebude.
11 “Akadzakutengerani ku masunagoge pamaso pa oweruza ndi a maulamuliro, musadere nkhawa mmene mudzadzitchinjirizire nokha kapena chimene mudzayankhule,
Až vás budou vyslýchat před úřady a soudy, nestarejte se, co a jak byste měli mluvit,
12 pakuti Mzimu Woyera nthawi imeneyo adzakuphunzitsani zoyenera kunena.”
protože Duch svatý vám to v té chvíli vnukne.“
13 Munthu wina mʼgulu la anthu anati kwa Iye, “Aphunzitsi, muwuzeni mʼbale wanga andigawireko chuma chamasiye.”
Jeden ze zástupu ho požádal: „Pane, řekni mému bratrovi, ať se se mnou spravedlivě rozdělí o dědictví.“
14 Yesu anayankha kuti, “Munthu iwe, ndani anandiyika Ine kukhala woweruza kapena wogawa chuma pakati panu?”
Ježíš mu odpověděl: „Nejsem tu na to, abych rozsuzoval vaše spory.“
15 Kenaka Iye anawawuza kuti, “Chenjerani! Khalani tcheru ndi makhalidwe onse adyera; moyo wa munthu sukhala chifukwa cha kuchuluka kwa zimene ali nazo.”
Všem potom řekl: „Varujte se chamtivosti. Vždyť smysl života není v tom, aby člověk hromadil.“
16 Ndipo Iye anawawuza fanizo ili, “Munda wa munthu wina wachuma unabereka kwambiri.
A pověděl jim k tomu příběh: „Když jeden člověk sklidil z polí velkou úrodu,
17 Iye anaganiza kuti, ‘Ndichite chiyani? Ndilibe malo osungiramo mbewu zanga.’
přemýšlel, kam ji uložit.
18 “Ndipo Iye anati, ichi ndi chimene ndidzachite: Ndidzaphwasula nkhokwe zanga zonse ndi kumanga zokulirapo, ndipo ndidzasungira mʼmenemo mbewu ndi katundu.
Rozhodl se, že dá zbořit staré stodoly a postaví prostornější, kam si všechno uskladní.
19 Ndipo ndidzawuza moyo wanga kuti, ‘Uli nazo zinthu zabwino zambiri zimene zikhalepo zaka zambiri, usapupulume; idya, imwa ndi kukondwera.’”
Těšil se, že bude mít na léta po starosti a v klidu a pohodě si bude všeho užívat.
20 “Koma Mulungu anati kwa iye, ‘Iwe wopusa! Usiku womwe uno moyo wako udzachotsedwa kwa iwe, ndipo ndi ndani amene adzatenge zimene iwe wadzikonzera?’
Ale promluvil k němu Bůh: ‚Blázne, dnes v noci zemřeš, a komu připadne, co sis nahromadil?‘“
21 “Umu ndi mmene zidzakhalire ndi aliyense amene amadziwunjikira chuma, koma si wachuma pamaso pa Mulungu.”
Ježíš uzavřel: „Tak se stane každému, kdo hromadí majetek a nestará se o to, co má věčnou hodnotu v Božích očích.“
22 Kenaka Yesu anati kwa ophunzira ake, “Choncho Ine ndikuwuzani kuti musadere nkhawa za moyo wanu, zimene mudzadya; kapena za thupi lanu, zimene mudzavala.
Pak ještě řekl svým učedníkům: „Týká se to i Vás: Nedělejte si starosti, co budete jíst, pít a jaké šaty si pořídíte.
23 Moyo uposa chakudya, ndi thupi liposa chovala.
Život je víc než pokrm a nápoj a tělo je důležitější než šaty.
24 Taonani makwangwala: iwo safesa kapena kukolola, alibe nyumba zosungamo zinthu kapena nkhokwe; komabe, Mulungu amawadyetsa. Koposa kotani inu amene ndi ofunikira kuposa mbalame.
Podívejte se na havrany! Nesejí, nežnou, nemají spíže ani stodoly a Bůh je živí. Pro něho máte větší cenu než ptáci!
25 Ndi ndani wa inu akhoza kuwonjeza ora pa moyo wake chifukwa cha kudandaula?
Kdyby se někdo z vás sebevíc snažil, může povyrůst třeba jen o jediný centimetr?
26 Popeza simungathe kuchita kanthu kakangʼono aka, nʼchifukwa chiyani mumadandaula ndi zinazi?
Když ani taková maličkost není ve vaší moci, proč se trápíte starostmi o to ostatní?
27 “Taonani mmene maluwa amakulira. Iwo sagwira ntchito kapena kusoka zovala. Koma Ine ndikuwuzani kuti, ngakhale Solomoni muulemelero wake wonse sanavalepo ngati limodzi la awa.
Podívejte se, jak rostou květiny na louce. Nepředou, netkají, a přece ani Šalomoun v celé své nádheře nebyl tak skvostně oblečen jako kterákoliv z nich.
28 Ngati umu ndi mmene Mulungu amavekera udzu wakuthengo, umene lero ulipo ndipo mawa uponyedwa pa moto, nanga Iye adzakuvekani inu motani. Haa! Inu achikhulupiriro chochepa!
Když tedy Bůh tak pěkně odívá rostlinu, která jeden den kvete a druhý den uvadá, jak by se tím spíše nepostaral o vás, vy malověrní.
29 Ndipo musayike mtima wanu pa zimene mudzadye kapena kumwa; musade nazo nkhawa.
A tak se tolik nepachtěte po tom, co byste jedli nebo pili, a netrapte se tím.
30 Pakuti anthu akunja amathamanga kufunafuna zinthu zotere, ndipo Atate amadziwa kuti mumazifuna zimenezi.
To bývá hlavní zájem lidí, kteří Boha neznají. Váš Otec ví, že i ty věci potřebujete.
31 Koma funafunani ufumu wake, ndipo mudzapatsidwa zonsezi.
Hledejte především Boží království a on vás opatří vším, co k životu potřebujete.
32 “Musachite mantha, inu kagulu kankhosa, pakuti zinakondweretsa Atate anu kuti akupatseni ufumu.
Nebojte se, ač je vás jen malá hrstka; jste občany Božího království.
33 Gulitsani zonse zimene muli nazo, ndipo ndalama zake mupereke kwa osauka. Dzipezereni zikwama zandalama zimene sizidzatha, ndi kudzikundikira chuma chomwe sichidzatha kumwamba, kumene mbala sizingafikeko, ndipo dzimbiri silingawononge.
Nelpěte na tom, co máte, ale dávejte to do služby a rozdávejte potřebným. To je to nejlepší, co můžete s pomíjivým majetkem udělat. Promění se v nevyčerpatelný poklad u Boha, kde ho žádný zloděj nemůže ukrást a mol rozežrat.
34 Popeza kumene kuli chuma chanu, mtima wanunso udzakhala komweko.”
Člověk totiž přilne k tomu, na čem mu opravdu záleží.
35 “Khalani okonzekeratu ndipo nyale zanu ziziyaka,
Buďte připraveni a udržujte své lampy rozsvícené.
36 ngati anthu oyembekezera kubwera kwa mbuye wawo kuchokera kuphwando la ukwati, kuti pamene afika ndi kugogoda akhoza nthawi yomweyo kumutsekulira chitseko.
Buďte jako sluhové, kteří čekají na svého pána, až se vrátí ze svatby, aby mu otevřeli na první zaklepání.
37 Zidzakhala bwino kwa antchitowo amene mbuye wawo pobwera adzawapeze akudikira. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti adzakonzekera kuwatumikira, adzakhala nawo pa tebulo ndipo adzabwera ndi kuwatumikira.
Pochválí ty, kteří budou při jeho příchodu vzhůru. Dokonce je posadí za stůl, sám si vezme zástěru a bude je obsluhovat.
38 Zidzakhala bwino kwa antchitowo amene mbuye wawo adzawapeze ali okonzeka, ngakhale iye atabwera pa ora lachiwiri kapena lachitatu usiku.
Dobře bude těm, které jejich pán najde bdělé, i kdyby přišel o půlnoci nebo až k ránu.
39 Koma zindikirani izi: Ngati mwini nyumba akanadziwa ora limene mbala ibwera, sakanalola kuti nyumba yake ithyoledwe.
Je přece jasné: Kdyby hospodář věděl, v kterou dobu přijde zloděj, jistě by se na něj přichystal.
40 Inunso muyenera kukhala okonzeka, chifukwa Mwana wa Munthu adzabwera pa ora limene simukumuyembekezera Iye.”
Proto buďte připravení vždycky, protože Syn člověka přijde ve chvíli, kdy se toho nenadějete.“
41 Petro anafunsa kuti, “Kodi mukunena fanizoli kwa ife, kapena kwa aliyense?”
Petr se zeptal: „Pane, to, co říkáš, platí jenom nám, anebo všem lidem?“
42 Ambuye anayankha kuti, “Kodi tsono woyangʼanira wokhulupirika ndi wanzeru ndani? Kodi ndi amene mbuye wake wamuyika kukhala oyangʼanira antchito ake kuti aziwapatsa ndalama yachakudya pa nthawi yake yoyenera?
Ježíš odpověděl: „Vy máte být jako dobrý správce, kterému pán dal na starost ostatní pracovníky, aby jim pravidelně rozděloval pokrm.
43 Zidzamukhalira bwino wantchito amene mbuye wake adzamupeza akuchita zimene pamene iye abwera.
Pán bude spokojen s takovým správcem, kterého zastihne, že to tak poctivě dělá.
44 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti adzamuyika kukhala woyangʼanira katundu wake yense.
Takovému pak svěří do správy celý svůj majetek.
45 Koma tiyerekeze kuti wantchitoyo aziganiza mu mtima mwake kuti, ‘Bwana wanga akuchedwa kwambiri kubwera,’ ndipo kenaka ndi kuyamba kumenya antchito aamuna ndi aakazi ndi kudya, kumwa ndi kuledzera.
Ale běda tomu správci, který by si říkal: ‚Můj pán se hned tak nevrátí‘a začal by špatně nakládat s těmi, kdo by mu byli svěřeni, a sám by hodoval a opíjel se.
46 Mbuye wake adzabwera tsiku limene iye sakumuyembekezera ndi ora limene iye sakudziwa. Iye adzamulanga ndi kumusiya kumalo kumene kuli osakhulupirira.
Když jeho pán nenadále přijde, potrestá ho a vyhodí.
47 “Wantchito amene amadziwa chifuniro cha mbuye wake koma wosakonzeka kapena wosachita chimene mbuye wake akufuna adzakwapulidwa zikwapu zambiri.
Kdo zná vůli svého pána, ale neřídí se podle ní, bude tvrdě potrestán;
48 Koma wantchito amene sadziwa koma nʼkuchita zinthu zoyenera chilango, adzakwapulidwa zikwapu zochepa. Aliyense amene anapatsidwa zambiri, adzayenera kubwezanso zambiri; ndipo amene anamusungitsa zambiri, adzamulamula kuti abweze zambirinso.”
kdo ji nezná a udělá něco, co zasluhuje trestu, nedopadne tak zle. Od toho, komu bylo mnoho svěřeno, bude mnoho očekáváno, a kdo dostal jasné pokyny, od toho bude mnoho vyžadováno.
49 “Ine ndabwera kudzayatsa moto pa dziko lapansi, ndipo ndikanakonda ukanayaka kale.
Zvěst o spáse, kterou jsem přinesl na zem, se bude šířit jako oheň; a jak si přeji, aby už vzplál!
50 Koma Ine ndiyenera kubatizidwa, ndipo ndikusautsika mu mtima mpaka utachitika!
Předtím ovšem musím projít křtem utrpení. Jak je mi úzko, než se dokoná.
51 Kodi mukuganiza kuti Ine ndinabwera kudzabweretsa mtendere pa dziko lapansi? Ayi, Ine ndikukuwuzani kuti, ndinabweretsa kugawikana.
Myslíte si, že jsem přišel, aby zůstalo všechno při starém? S tím nepočítejte! Zvěst o mně každého zneklidní a dokonce postaví i lidi proti sobě navzájem.
52 Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo mʼbanja limodzi mudzakhala anthu asanu ndipo adzawukirana wina ndi mnzake, atatu kuwukira awiri, ndipo awiri kuwukira atatu.
I leckterá rodina se rozdělí do dvou táborů:
53 Anthu adzawukirana. Abambo kudzawukira mwana wawo wamwamuna, mwana wawoyo adzawukira abambo ake. Amayi adzawukira mwana wawo wamkazi, mwana wawoyo adzawukira amayi ake. Amayi adzawukira mpongozi wawo wamkazi, mpongoziyo adzawukira amayiwo.”
otec se postaví proti synovi a syn proti otci, matka proti dceři, dcera proti matce, tchyně proti snaše a snacha proti tchyni.“
54 Iye anati kwa gulu la anthu, “Pamene mukuona mtambo ukukwera kummawa, nthawi yomweyo inu mumati, ‘kugwa mvula,’ ndipo imagwadi.
Pak Ježíš řekl zástupům: „Když vidíte, že se od západu zatahuje, čekáte déšť a míváte pravdu.
55 Ndipo pamene mphepo yakummwera ikuwomba, inu mumati ‘kutentha’ ndipo kumaterodi.
Když vane jižní vítr, očekáváte horko a bývá horko.
56 Achiphamaso inu! Inu mumadziwa kutanthauzira maonekedwe a dziko lapansi ndi thambo. Zikutheka bwanji kuti simukudziwa kumasulira kwa nthawi ino?
Chytráci! Úkazy na nebi i na zemi posuzujete a umíte z nich vyvodit závěry. Jak to, že nedovedete posoudit znamení této doby?
57 “Bwanji simukuzindikira nokha zoyenera kuchita?
Jestliže je tu chvíle rozhodnutí, proč otálíte dát věci do pořádku?
58 Pamene mukupita kwa woweruza ndi amene munalakwirana naye, yesetsani kwambiri kuti muyanjane naye mʼnjiramo, chifukwa mukapanda kutero akhoza kukutengerani ku bwalo la milandu ndipo woweruzayo adzakuperekani kwa woyangʼanira ndende, ndipo woyangʼanira ndendeyo adzakuponyani mʼndende.
Je to tak, jako když tě věřitel už vede k soudu. Snažíš se s ním ještě cestou vyrovnat. Jinak tě předá soudu a skončíš ve vězení.
59 Ine ndikuwuzani kuti, simudzatulukamo mpaka mutalipira ndalama zonse.”
Odtamtud se nedostaneš dříve, dokud svůj dluh do posledního haléře nezaplatíš.“

< Luka 12 >