< Luka 11 >

1 Tsiku lina Yesu amapemphera pamalo ena. Atamaliza, mmodzi wa ophunzira ake anati kwa Iye, “Ambuye tiphunzitseni kupemphera, monga momwe Yohane anaphunzitsira ophunzira ake.”
و هنگامی که او در موضعی دعا می‌کردچون فارغ شد، یکی از شاگردانش به وی گفت: «خداوندا دعا کردن را به ما تعلیم نما، چنانکه یحیی شاگردان خود را بیاموخت.»۱
2 Yesu anawawuza kuti, “Pamene mukupemphera muzinena kuti: “‘Atate, dzina lanu lilemekezedwe, ufumu wanu ubwere.
بدیشان گفت: «هرگاه دعا کنید گویید‌ای پدرما که در آسمانی، نام تو مقدس باد. ملکوت توبیاید. اراده تو چنانکه در آسمان است در زمین نیزکرده شود.۲
3 Mutipatse chakudya chathu chalero,
نان کفاف ما را روز به روز به ما بده.۳
4 mutikhululukire machimo athu, monga ifenso timakhululukira aliyense amene watilakwira. Ndipo musalole kuti tigwe mʼmayesero.’”
و گناهان ما را ببخش زیرا که ما نیز هر قرضدار خود را می‌بخشیم. و ما را در آزمایش میاور، بلکه ما را از شریر رهایی ده.»۴
5 Kenaka anawawuza kuti, “Tiyerekeze: Mmodzi mwa inu atakhala ndi bwenzi lake, ndipo iye nʼkupita ku nyumba yake pakati pa usiku, nakanena kuti, ‘Mnzanga, bwereke malofu atatu abuledi,
و بدیشان گفت: «کیست از شما که دوستی داشته باشد و نصف شب نزد وی آمده بگوید‌ای دوست سه قرص نان به من قرض ده،۵
6 chifukwa ndalandira bwenzi langa amene ali pa ulendo ndipo ine ndilibe choti ndimupatse.’
چونکه یکی از دوستان من از سفر بر من وارد شده وچیزی ندارم که پیش او گذارم.۶
7 “Ndipo yerekezani kuti amene ali mʼnyumbamo ndi kuyankha kuti, ‘Usandivutitse ine, ndatseka kale chitseko, ndipo ine ndi ana anga tagona. Ine sindingadzukenso kuti ndidzakupatse.’
پس او از اندرون در جواب گوید مرا زحمت مده، زیرا که الان دربسته است و بچه های من در رختخواب با من خفته‌اند نمی توانم برخاست تا به تو دهم.۷
8 Ine ndikukuwuzani kuti adzadzuka ndi kumupatsa bulediyo, osati chifukwa ndi bwenzi lake, koma chifukwa cha liwuma la munthu wopemphayo, ndipo kudzamupatsa zonse zimene akuzifuna.
به شمامی گویم هر‌چند به علت دوستی برنخیزد تا بدودهد، لیکن بجهت لجاجت خواهد برخاست و هرآنچه حاجت دارد، بدو خواهد داد.۸
9 “Choncho Ine ndikunena kwa inu kuti: Pemphani ndipo adzakupatsani. Funafunani ndipo mudzapeza. Gogodani ndipo adzakutsekulirani.
«و من به شما می‌گویم سوال کنید که به شماداده خواهد شد. بطلبید که خواهید یافت. بکوبیدکه برای شما بازکرده خواهد شد.۹
10 Pakuti aliyense amene amapempha amalandira. Munthu amene amafunafuna amapeza. Iye amene amagogoda amamutsekulira.
زیرا هر‌که سوال کند، یابد و هر‌که بطلبد، خواهد یافت وهرکه کوبد، برای او باز کرده خواهد شد.۱۰
11 “Ndani mwa inu abambo, kodi mwana wanu atapempha nsomba, mʼmalo mwake mungamupatse njoka?
وکیست از شما که پدر باشد و پسرش از او نان خواهد، سنگی بدو دهد یا اگر ماهی خواهد، به عوض ماهی ماری بدو بخشد،۱۱
12 Kapena atapempha dzira, kodi mungamupatse chinkhanira?
یا اگرتخم‌مرغی بخواهد، عقربی بدو عطا کند.۱۲
13 Tsono ngati inu, anthu oyipa, mumadziwa kupereka mphatso zabwino kwa ana anu, koposa kotani Atate anu akumwamba, angalephere bwanji kupereka Mzimu Woyera kwa amene awapempha!”
پس اگر شما با آنکه شریر هستید می‌دانید چیزهای نیکو را به اولاد خود باید داد، چند مرتبه زیادترپدر آسمانی شما روح‌القدس را خواهد داد به هرکه از او سوال کند.»۱۳
14 Yesu amatulutsa chiwanda chimene chinali chosayankhula. Chiwandacho chitatuluka, munthu wosayankhulayo anayankhula, ndipo gulu la anthu linadabwa.
و دیوی را که گنگ بود بیرون می‌کرد وچون دیو بیرون شد، گنگ گویا گردید و مردم تعجب نمودند.۱۴
15 Koma ena mwa iwo anati, “Iye akutulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu mfumu ya ziwanda.”
لیکن بعضی از ایشان گفتند که «دیوها را به یاری بعلزبول رئیس دیوها بیرون می‌کند.»۱۵
16 Ena anamuyesa pomufunsa chizindikiro chochokera kumwamba.
و دیگران از روی امتحان آیتی آسمانی از او طلب نمودند.۱۶
17 Yesu anadziwa maganizo awo ndipo anawawuza kuti, “Ufumu uliwonse wogawikana udzawonongeka, ndipo nyumba yogawikana idzapasuka.
پس او خیالات ایشان را درک کرده بدیشان گفت: «هر مملکتی که برخلاف خود منقسم شود، تباه گردد و خانه‌ای که بر خانه منقسم شود، منهدم گردد.۱۷
18 Ngati Satana adziwukira yekha, ufumu wake ungalimbe bwanji? Ine ndikunena izi chifukwa inu mukuti Ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu.
پس شیطان نیز اگر به ضد خود منقسم شود سلطنت اوچگونه پایدار بماند. زیرا می‌گویید که من به اعانت بعلزبول دیوها را بیرون می‌کنم.۱۸
19 Tsopano ngati Ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu, nanga ophunzira anu amazitulutsa ndi mphamvu ya ndani? Choncho, iwowo ndiye adzakhala oweruza anu.
پس اگرمن دیوها را به وساطت بعلزبول بیرون می‌کنم، پسران شما به وساطت که آنها را بیرون می‌کنند؟ از اینجهت ایشان داوران بر شما خواهند بود.۱۹
20 Koma ngati ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Mulungu, ndiye kuti ufumu wa Mulungu wafika pakati panu.
لیکن هرگاه به انگشت خدا دیوها را بیرون می‌کنم، هرآینه ملکوت خدا ناگهان بر شما آمده است.۲۰
21 “Munthu wamphamvu, amene ali ndi zida, akamalondera nyumba yake, katundu wake amatetezedwa.
وقتی که مرد زورآور سلاح پوشیده خانه خود را نگاه دارد، اموال او محفوظ می‌باشد.۲۱
22 Koma pakabwera wina wamphamvu zoposa namugonjetsa, amalanda zida zimene munthuyo amazidalirazo ndi kugawa katundu wake.
اما چون شخصی زورآورتر از او آید بر او غلبه یافته همه اسلحه او را که بدان اعتماد می‌داشت، از او می‌گیرد و اموال او را تقسیم می‌کند.۲۲
23 “Munthu amene sali mbali yanga ndi wotsutsana nane. Ndipo wosandithandiza kusonkhanitsa, ameneyo ndi womwaza.
کسی‌که با من نیست، برخلاف من است و آنکه با من جمع نمی کند، پراکنده می‌سازد.۲۳
24 “Mzimu woyipa ukatuluka mwa munthu, umakayendayenda ku malo owuma, kufunafuna malo opumulirako ndipo suwapeza. Kenaka umati, ‘Ndibwerera ku nyumba kwanga kumene ndachokera.’
چون روح پلید از انسان بیرون آید به مکانهای بی‌آب بطلب آرامی گردش می‌کند وچون نیافت می‌گوید به خانه خود که از آن بیرون آمدم برمی گردم.۲۴
25 Ukafika umapeza mʼnyumba mosesedwa bwino ndi mokonza.
پس چون آید، آن را جاروب کرده شده و آراسته می‌بیند.۲۵
26 Pamenepo umakatenga mizimu ina isanu ndi iwiri yoyipa kwambiri kuposa iwowo ndipo imakalowa ndi kukhala mʼmenemo. Ndipo makhalidwe otsiriza a munthuyo amakhala oyipa kuposa oyamba aja.”
آنگاه می‌رود وهفت روح دیگر، شریرتر از خود برداشته داخل شده در آنجا ساکن می‌گردد و اواخر آن شخص ازاوائلش بدتر می‌شود.»۲۶
27 Pamene Yesu ankanena zonsezi, mayi wina mʼgulu la anthuwo anafuwula nati, “Ndi wodala amayi amene anakubalani ndi kukulerani!”
چون او این سخنان را می‌گفت، زنی از آن میان به آواز بلند وی را گفت «خوشابحال آن رحمی که تو را حمل کرد و پستانهایی که مکیدی.»۲۷
28 Koma Yesu anayankha kuti, “Odala ndi amene amamva mawu a Mulungu ndi kuwasunga.”
لیکن او گفت: «بلکه خوشابحال آنانی که کلام خدا را می‌شنوند و آن را حفظمی کنند.»۲۸
29 Pamene gulu la anthu limachuluka, Yesu anati, “Uno ndi mʼbado oyipa. Umafuna kuona chizindikiro chodabwitsa. Koma sadzachiona kupatula chizindikiro chija cha Yona.
و هنگامی که مردم بر او ازدحام می‌نمودند، سخن‌گفتن آغاز کرد که «اینان فرقه‌ای شریرند که آیتی طلب می‌کنند و آیتی بدیشان عطا نخواهدشد، جز آیت یونس نبی.۲۹
30 Monga Yona uja anali chizindikiro kwa anthu ku Ninive, momwemonso Mwana wa Munthu adzakhala chizindikiro kwa anthu a mʼbado uno.
زیرا چنانکه یونس برای اهل نینوا آیت شد، همچنین پسر انسان نیزبرای این فرقه خواهد بود.۳۰
31 Mfumu yayikazi yakummwera idzayimirira tsiku lachiweruzo pamodzi ndi anthu a mʼbado uno ndipo idzawatsutsa, chifukwa iyo inachokera kumapeto a dziko lapansi kudzamva nzeru za Solomoni. Ndipo tsopano pano pali wina woposa Solomoni.
ملکه جنوب در روزداوری با مردم این فرقه برخاسته، بر ایشان حکم خواهد کرد زیرا که از اقصای زمین آمد تا حکمت سلیمان را بشنود و اینک در اینجا کسی بزرگتر ازسلیمان است.۳۱
32 Anthu a ku Ninive adzayimirira tsiku lachiweruzo pamodzi ndi mʼbado uno ndipo adzawutsutsa, pakuti anatembenuka mtima ndi ulaliki wa Yona. Ndipo tsopano pano pali wina woposa Yona.
مردم نینوا در روز داوری با این طبقه برخاسته بر ایشان حکم خواهند کرد زیرا که به موعظه یونس توبه کردند و اینک در اینجا کسی بزرگتر از یونس است.۳۲
33 “Palibe amene amayatsa nyale ndi kuyiika pa malo poti sionekera, kapena pansi pa mtsuko. Mʼmalo mwake amayika pa choyikapo chake, kuti iwo amene akulowamo aone kuwunika.
و هیچ‌کس چراغی نمی افروزد تا آن را درپنهانی یا زیر پیمانه‌ای بگذارد، بلکه بر چراغدان، تا هر‌که داخل شود روشنی را بیند.۳۳
34 Diso lanu ndi nyale ya thupi lanu. Pamene maso anu ali bwino, thupi lanu lonse limadzaza ndi kuwunika. Koma ngati ali oyipa, thupi lanunso ndi lodzaza ndi mdima.
چراغ بدن چشم است، پس مادامی که چشم تو بسیط است تمامی جسدت نیز روشن است و لیکن اگر فاسدباشد، جسد تو نیز تاریک بود.۳۴
35 Onetsetsani tsono, kuti kuwunika kuli mwa inu si mdima.
پس باحذر باش مبادا نوری که در تو است، ظلمت باشد.۳۵
36 Choncho, ngati thupi lanu lonse ndi lodzaza ndi kuwunika, ndiye kuti palibe dera lina lili mdima, lonselo lidzakhala kuwunika, monga momwe kuwunika kwa nyale kumakuwalirani.”
بنابراین هرگاه تمامی جسم تو روشن باشد وذره‌ای ظلمت نداشته باشد همه‌اش روشن خواهد بود، مثل وقتی که چراغ به تابش خود، تورا روشنایی می‌دهد.»۳۶
37 Yesu atamaliza kuyankhula, Mfarisi wina anamuyitana kuti akadye naye. Tsono Yesu analowa mʼnyumba ndi kukhala podyera.
و هنگامی که سخن می‌گفت یکی ازفریسیان از او وعده خواست که در خانه اوچاشت بخورد. پس داخل شده بنشست.۳۷
38 Mfarisiyo anadabwa atazindikira kuti Yesu anayamba kudya wosatsata mwambo wawo wakasambidwe ka mʼmanja.
امافریسی چون دید که پیش از چاشت دست نشست، تعجب نمود.۳۸
39 Kenaka Ambuye anamuwuza kuti, “Inu Afarisi mumatsuka kunja kwa chikho ndi mbale, koma mʼkati mwanu ndi modzaza ndi kudzikonda ndi zoyipa.
خداوند وی را گفت: «همانا شما‌ای فریسیان بیرون پیاله و بشقاب راطاهر می‌سازید ولی درون شما پر از حرص وخباثت است.۳۹
40 Anthu opusa inu! Kodi amene anapanga zamʼkati sanapangenso zakunja?
‌ای احمقان آیا او که بیرون راآفرید، اندرون را نیز نیافرید؟۴۰
41 Koma popereka kwa osauka, perekani chimene chili mʼkati ndipo chilichonse chidzakhala choyera.
بلکه از آنچه دارید، صدقه دهید که اینک همه‌چیز برای شماطاهر خواهد گشت.۴۱
42 “Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa mumapereka kwa Mulungu chakhumi cha timbewu tonunkhira, ndi timbewu tokometsera chakudya ndi mbewu zina zonse za mʼmunda, koma mumakana chilungamo ndi chikondi cha Mulungu. Mumayenera kuchita zomalizirazi osalekanso kuchita zoyambazi.
وای بر شما‌ای فریسیان که ده‌یک از نعناع و سداب و هر قسم سبزی رامی دهید و از دادرسی و محبت خدا تجاوزمی نمایید، اینها را می‌باید به‌جا آورید و آنها رانیز ترک نکنید.۴۲
43 “Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa mumakonda mipando yofunika kwambiri mʼmasunagoge ndi malonje mʼmalo a pa msika.
وای بر شما‌ای فریسیان که صدر کنایس و سلام در بازارها را دوست می‌دارید.۴۳
44 “Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa muli ngati manda osawaka, amene anthu amangoyendapo, osawadziwa.”
وای بر شما‌ای کاتبان و فریسیان ریاکار زیرا که مانند قبرهای پنهان شده هستید که مردم بر آنها راه می‌روند و نمی دانند.»۴۴
45 Mmodzi mwa akatswiri a Malamulo anamuyankha Iye nati, “Aphunzitsi, pamene mukunena zinthu izi, mukutinyoza ifenso?”
آنگاه یکی از فقها جواب داده گفت: «ای معلم، بدین سخنان ما را نیز سرزنش می‌کنی؟»۴۵
46 Yesu anayankha kuti, “Tsoka kwa inunso akatswiri a Malamulo chifukwa mumawalemetsa anthu ndi mtolo umene iwo sangathe kunyamula, ndipo inu eni ake simutenga chala chanu kuti muwathandize.
گفت «وای بر شما نیز‌ای فقها زیرا که بارهای گران را بر مردم می‌نهید و خود بر آن بارها، یک انگشت خود را نمی گذارید.۴۶
47 “Tsoka kwa inu, chifukwa mumawaka manda a aneneri, komatu ndi makolo anu amene anawapha.
وای بر شما زیراکه مقابر انبیا را بنا می‌کنید و پدران شما ایشان راکشتند.۴۷
48 Tsono potero mumachitira umboni za zimene makolo anu anachita. Anapha aneneri, ndipo inu mumawaka manda awo.
پس به‌کارهای پدران خود شهادت می‌دهید و از آنها راضی هستید، زیرا آنها ایشان را کشتند و شما قبرهای ایشان را می‌سازید.۴۸
49 Chifukwa cha ichi, Mulungu mu nzeru zake anati, ‘Ine ndidzawatumizira aneneri ndi atumwi, ena mwa iwo adzawapha ndipo ena adzawazunza.’
ازاین‌رو حکمت خدا نیز فرموده است که به سوی ایشان انبیا و رسولان می‌فرستم و بعضی از ایشان را خواهند کشت و بر بعضی جفا کرد،۴۹
50 Choncho mʼbado uwu udzasenza magazi a aneneri onse amene anakhetsedwa kuyambira pachiyambi cha dziko,
تا انتقام خون جمیع انبیا که از بنای عالم ریخته شد از این طبقه گرفته شود.۵۰
51 kuyambira magazi a Abele kufikira magazi a Zakariya amene anaphedwa pakati pa guwa lansembe ndi malo opatulika. Inde, Ine ndikuwuzani inu, mʼbado uno udzasenza zonsezi.
از خون هابیل تا خون زکریاکه در میان مذبح و هیکل کشته شد. بلی به شمامی گویم که از این فرقه بازخواست خواهد شد.۵۱
52 “Tsoka kwa inu akatswiri a Malamulo, chifukwa mwachotsa kiyi wachidziwitso inu eni akenu musanalowemo, ndipo mwatsekerezanso iwo amene amalowa.”
وای بر شما‌ای فقها، زیرا کلید معرفت رابرداشته‌اید که خود داخل نمی شوید و داخل‌شوندگان را هم مانع می‌شوید.»۵۲
53 Pamene Yesu anachokamo, Afarisi ndi aphunzitsi a Malamulo anayamba kumamutsutsa koopsa ndi kumupanikiza ndi mafunso,
و چون او این سخنان را بدیشان می‌گفت، کاتبان و فریسیان با او بشدت درآویختند و درمطالب بسیار سوالها از او می‌کردند.۵۳
54 pofuna kumukola muchina chilichonse chimene Iye angayankhule.
و در کمین او می‌بودند تا نکته‌ای از زبان او گرفته مدعی اوبشوند.۵۴

< Luka 11 >