< Luka 11 >

1 Tsiku lina Yesu amapemphera pamalo ena. Atamaliza, mmodzi wa ophunzira ake anati kwa Iye, “Ambuye tiphunzitseni kupemphera, monga momwe Yohane anaphunzitsira ophunzira ake.”
And it came to pass, as he was in a certain place praying, that, when he ceased, one of his disciples said to him: Lord, teach us to pray, as John also taught his disciples.
2 Yesu anawawuza kuti, “Pamene mukupemphera muzinena kuti: “‘Atate, dzina lanu lilemekezedwe, ufumu wanu ubwere.
And he said to them: When you pray, say, Our Father who art in heaven, hallowed be thy name; thy kingdom come; thy will be done, as in heaven, so on earth.
3 Mutipatse chakudya chathu chalero,
Give us, day by day, the bread sufficient for our support;
4 mutikhululukire machimo athu, monga ifenso timakhululukira aliyense amene watilakwira. Ndipo musalole kuti tigwe mʼmayesero.’”
and forgive us our sins, for we also forgive every one that is indebted to us; and lead us not into temptation, but deliver us from the evil one.
5 Kenaka anawawuza kuti, “Tiyerekeze: Mmodzi mwa inu atakhala ndi bwenzi lake, ndipo iye nʼkupita ku nyumba yake pakati pa usiku, nakanena kuti, ‘Mnzanga, bwereke malofu atatu abuledi,
And he said to them: Which of you shall have a friend, and shall go to him at midnight, and say to him, Friend, lend me three loaves;
6 chifukwa ndalandira bwenzi langa amene ali pa ulendo ndipo ine ndilibe choti ndimupatse.’
for a friend of mine, who is on a journey, has come to me, and I have nothing to set before him?
7 “Ndipo yerekezani kuti amene ali mʼnyumbamo ndi kuyankha kuti, ‘Usandivutitse ine, ndatseka kale chitseko, ndipo ine ndi ana anga tagona. Ine sindingadzukenso kuti ndidzakupatse.’
And he from within shall answer and say, Trouble me not; the door is already closed, and my children and myself are in bed; I can not rise and give you.
8 Ine ndikukuwuzani kuti adzadzuka ndi kumupatsa bulediyo, osati chifukwa ndi bwenzi lake, koma chifukwa cha liwuma la munthu wopemphayo, ndipo kudzamupatsa zonse zimene akuzifuna.
I say to you, Although he will not arise and give him, because he is his friend, yet, on account of his importunity, he will arise and give him as many as he needs.
9 “Choncho Ine ndikunena kwa inu kuti: Pemphani ndipo adzakupatsani. Funafunani ndipo mudzapeza. Gogodani ndipo adzakutsekulirani.
And I say to you, Ask, and it shall be given you; seek, and you shall find; knock, and it shall be opened to you.
10 Pakuti aliyense amene amapempha amalandira. Munthu amene amafunafuna amapeza. Iye amene amagogoda amamutsekulira.
For every one that asks, receives; and he that seeks, finds; and to him that knocks, it shall be opened.
11 “Ndani mwa inu abambo, kodi mwana wanu atapempha nsomba, mʼmalo mwake mungamupatse njoka?
If a son ask bread of any one of you that is a father, will he give him a stone? Or if he ask a fish, will he, instead of a fish, give him a serpent?
12 Kapena atapempha dzira, kodi mungamupatse chinkhanira?
Or if he ask an egg, will he give him a scorpion?
13 Tsono ngati inu, anthu oyipa, mumadziwa kupereka mphatso zabwino kwa ana anu, koposa kotani Atate anu akumwamba, angalephere bwanji kupereka Mzimu Woyera kwa amene awapempha!”
If, then, you, being evil, know how to give good gifts to your children, how much more will your heavenly Father give the Holy Spirit to them that ask him?
14 Yesu amatulutsa chiwanda chimene chinali chosayankhula. Chiwandacho chitatuluka, munthu wosayankhulayo anayankhula, ndipo gulu la anthu linadabwa.
And he was casting out a demon, and it was dumb; and it came to pass, when the demon had gone out, that the dumb man spoke: and the multitudes wondered.
15 Koma ena mwa iwo anati, “Iye akutulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu mfumu ya ziwanda.”
But some of them said: He casts out demons by Beelzebul, the prince of the demons.
16 Ena anamuyesa pomufunsa chizindikiro chochokera kumwamba.
And others, that they might tempt him, asked of him a sign from heaven.
17 Yesu anadziwa maganizo awo ndipo anawawuza kuti, “Ufumu uliwonse wogawikana udzawonongeka, ndipo nyumba yogawikana idzapasuka.
But, knowing their purpose, he said to them: Every kingdom divided against itself, is brought to desolation; and a house that is divided against a house, falls.
18 Ngati Satana adziwukira yekha, ufumu wake ungalimbe bwanji? Ine ndikunena izi chifukwa inu mukuti Ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu.
If Satan be divided against himself, how shall his kingdom stand? For you say, that I cast out demons by Beelzebul.
19 Tsopano ngati Ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu, nanga ophunzira anu amazitulutsa ndi mphamvu ya ndani? Choncho, iwowo ndiye adzakhala oweruza anu.
But if I cast out demons by Beelzebul, by whom do your sons cast them out? Therefore, they shall be your judges.
20 Koma ngati ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Mulungu, ndiye kuti ufumu wa Mulungu wafika pakati panu.
But if I cast out demons by the finger of God, then has the kingdom of God already come upon you.
21 “Munthu wamphamvu, amene ali ndi zida, akamalondera nyumba yake, katundu wake amatetezedwa.
When the strong man armed keeps guard over his palace, his goods are in peace;
22 Koma pakabwera wina wamphamvu zoposa namugonjetsa, amalanda zida zimene munthuyo amazidalirazo ndi kugawa katundu wake.
but when one stronger than he comes upon him and overcomes him, he takes away all his armor in which he trusted, and divides his spoils.
23 “Munthu amene sali mbali yanga ndi wotsutsana nane. Ndipo wosandithandiza kusonkhanitsa, ameneyo ndi womwaza.
He that is not with me, is against me; and he that gathers not with me, scatters.
24 “Mzimu woyipa ukatuluka mwa munthu, umakayendayenda ku malo owuma, kufunafuna malo opumulirako ndipo suwapeza. Kenaka umati, ‘Ndibwerera ku nyumba kwanga kumene ndachokera.’
When the unclean spirit has gone out of a man, he goes through dry places, seeking rest; and finding none, he says, I will return to my house out of which I came.
25 Ukafika umapeza mʼnyumba mosesedwa bwino ndi mokonza.
And he comes and finds it swept, and set in order.
26 Pamenepo umakatenga mizimu ina isanu ndi iwiri yoyipa kwambiri kuposa iwowo ndipo imakalowa ndi kukhala mʼmenemo. Ndipo makhalidwe otsiriza a munthuyo amakhala oyipa kuposa oyamba aja.”
Then he goes and takes with him seven other spirits, more wicked than himself, and they enter in, and dwell there: and the last state of that man is worse than the first.
27 Pamene Yesu ankanena zonsezi, mayi wina mʼgulu la anthuwo anafuwula nati, “Ndi wodala amayi amene anakubalani ndi kukulerani!”
And it came to pass, that, when he said these things, a certain woman from among the multitude lifted up her voice, and said to him: Blessed is the womb that bore thee, and the breasts that thou didst suck.
28 Koma Yesu anayankha kuti, “Odala ndi amene amamva mawu a Mulungu ndi kuwasunga.”
And he said: Yes, rather blessed are they that hear the word of God, and keep it.
29 Pamene gulu la anthu limachuluka, Yesu anati, “Uno ndi mʼbado oyipa. Umafuna kuona chizindikiro chodabwitsa. Koma sadzachiona kupatula chizindikiro chija cha Yona.
And when the multitudes were crowded together, he began to say: This is an evil generation; it asks for a sign, and no sign shall be given to it but the sign of Jonah the prophet.
30 Monga Yona uja anali chizindikiro kwa anthu ku Ninive, momwemonso Mwana wa Munthu adzakhala chizindikiro kwa anthu a mʼbado uno.
For as Jonah was a sign to the Ninevites, so the Son of man shall also be to this generation.
31 Mfumu yayikazi yakummwera idzayimirira tsiku lachiweruzo pamodzi ndi anthu a mʼbado uno ndipo idzawatsutsa, chifukwa iyo inachokera kumapeto a dziko lapansi kudzamva nzeru za Solomoni. Ndipo tsopano pano pali wina woposa Solomoni.
The queen of the south shall rise in the judgment with the men of this generation, and shall condemn them; for she came from the most distant parts of the earth to hear the wisdom of Solomon; and lo, something greater than Solomon is here.
32 Anthu a ku Ninive adzayimirira tsiku lachiweruzo pamodzi ndi mʼbado uno ndipo adzawutsutsa, pakuti anatembenuka mtima ndi ulaliki wa Yona. Ndipo tsopano pano pali wina woposa Yona.
The men of Nineveh shall rise in the judgment with this generation, and condemn it; for they repented in accordance with the preaching of Jonah; and lo, something greater than Jonah is here.
33 “Palibe amene amayatsa nyale ndi kuyiika pa malo poti sionekera, kapena pansi pa mtsuko. Mʼmalo mwake amayika pa choyikapo chake, kuti iwo amene akulowamo aone kuwunika.
No one, when he has lighted a lamp, puts it in a secret place, nor under the measure, but upon the lamp-stand, that those who come in may see the light.
34 Diso lanu ndi nyale ya thupi lanu. Pamene maso anu ali bwino, thupi lanu lonse limadzaza ndi kuwunika. Koma ngati ali oyipa, thupi lanunso ndi lodzaza ndi mdima.
The lamp of the body is the eye; when, therefore, your eye is sound, your whole body also is light; but if it be diseased, your body also is dark.
35 Onetsetsani tsono, kuti kuwunika kuli mwa inu si mdima.
Take heed, therefore, lest the light that is in you be darkness.
36 Choncho, ngati thupi lanu lonse ndi lodzaza ndi kuwunika, ndiye kuti palibe dera lina lili mdima, lonselo lidzakhala kuwunika, monga momwe kuwunika kwa nyale kumakuwalirani.”
If, therefore, your whole body is light, having no part dark, the whole shall be light, as when a lamp, by its brightness, gives you light.
37 Yesu atamaliza kuyankhula, Mfarisi wina anamuyitana kuti akadye naye. Tsono Yesu analowa mʼnyumba ndi kukhala podyera.
And as he spoke, a certain Pharisee asked him to dine with him. And he went in and reclined at table.
38 Mfarisiyo anadabwa atazindikira kuti Yesu anayamba kudya wosatsata mwambo wawo wakasambidwe ka mʼmanja.
And when the Pharisee saw it, he wondered that he had not first immersed himself before dinner.
39 Kenaka Ambuye anamuwuza kuti, “Inu Afarisi mumatsuka kunja kwa chikho ndi mbale, koma mʼkati mwanu ndi modzaza ndi kudzikonda ndi zoyipa.
And the Lord said to him: Now you Pharisees cleanse the outside of the cup and the plate; but your inward part is full of extortion and wickedness.
40 Anthu opusa inu! Kodi amene anapanga zamʼkati sanapangenso zakunja?
Senseless men, did not he who made the outside, make the inside also?
41 Koma popereka kwa osauka, perekani chimene chili mʼkati ndipo chilichonse chidzakhala choyera.
But give as charity the contents of the cup, and behold, all things are clean for you.
42 “Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa mumapereka kwa Mulungu chakhumi cha timbewu tonunkhira, ndi timbewu tokometsera chakudya ndi mbewu zina zonse za mʼmunda, koma mumakana chilungamo ndi chikondi cha Mulungu. Mumayenera kuchita zomalizirazi osalekanso kuchita zoyambazi.
But alas for you, Pharisees! for you tithe mint and rue and every herb, and pass by the justice and the love of God; these you ought to have done, and those you ought not to have left undone.
43 “Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa mumakonda mipando yofunika kwambiri mʼmasunagoge ndi malonje mʼmalo a pa msika.
Alas for you, Pharisees! for you love the chief seat in the synagogues, and greetings in the markets.
44 “Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa muli ngati manda osawaka, amene anthu amangoyendapo, osawadziwa.”
Alas for you, scribes and Pharisees, hypocrites! for you are like graves that are not seen; and men that walk over them know it not.
45 Mmodzi mwa akatswiri a Malamulo anamuyankha Iye nati, “Aphunzitsi, pamene mukunena zinthu izi, mukutinyoza ifenso?”
And one of the lawyers answered and said to him: Teacher, in saying these things, you reproach us also.
46 Yesu anayankha kuti, “Tsoka kwa inunso akatswiri a Malamulo chifukwa mumawalemetsa anthu ndi mtolo umene iwo sangathe kunyamula, ndipo inu eni ake simutenga chala chanu kuti muwathandize.
He replied: Alas for you, lawyers, also! for you bind upon men burdens hard to be borne, and you yourselves touch not the burdens with one of your fingers,
47 “Tsoka kwa inu, chifukwa mumawaka manda a aneneri, komatu ndi makolo anu amene anawapha.
Alas for you! for you build the sepulchers of the prophets, and your fathers killed them.
48 Tsono potero mumachitira umboni za zimene makolo anu anachita. Anapha aneneri, ndipo inu mumawaka manda awo.
Therefore you attest and approve the deeds of your fathers; for they indeed killed them, and you build their sepulchers.
49 Chifukwa cha ichi, Mulungu mu nzeru zake anati, ‘Ine ndidzawatumizira aneneri ndi atumwi, ena mwa iwo adzawapha ndipo ena adzawazunza.’
For this reason also the Wisdom of God said: I will send them prophets and apostles, and some of them they will kill, and persecute,
50 Choncho mʼbado uwu udzasenza magazi a aneneri onse amene anakhetsedwa kuyambira pachiyambi cha dziko,
that the blood of all the prophets, which has been shed from the foundation of the world, may be required of this generation;
51 kuyambira magazi a Abele kufikira magazi a Zakariya amene anaphedwa pakati pa guwa lansembe ndi malo opatulika. Inde, Ine ndikuwuzani inu, mʼbado uno udzasenza zonsezi.
from the blood of Abel to the blood of Zachariah, who perished between the altar and the temple; yes, I say to you, It shall be required of this generation.
52 “Tsoka kwa inu akatswiri a Malamulo, chifukwa mwachotsa kiyi wachidziwitso inu eni akenu musanalowemo, ndipo mwatsekerezanso iwo amene amalowa.”
Alas for you, lawyers! for you have taken away the key of knowledge; you did not go in yourselves, and those who were entering in, you prevented.
53 Pamene Yesu anachokamo, Afarisi ndi aphunzitsi a Malamulo anayamba kumamutsutsa koopsa ndi kumupanikiza ndi mafunso,
And when he said these things to them, the scribes and the Pharisees began to be very angry, and to put questions to him about many things,
54 pofuna kumukola muchina chilichonse chimene Iye angayankhule.
trying to entrap him, and seeking to lay hold on something from his mouth, that they might accuse him.

< Luka 11 >