< Luka 10 >
1 Zitatha izi Ambuye anasankha enanso 72 ndi kuwatumiza awiriawiri patsogolo pake ku mzinda uliwonse ndi kumalo kumene Iye anatsala pangʼono kupitako.
tataḥ paraṁ prabhuraparān saptatiśiṣyān niyujya svayaṁ yāni nagarāṇi yāni sthānāni ca gamiṣyati tāni nagarāṇi tāni sthānāni ca prati dvau dvau janau prahitavān|
2 Iye anawawuza kuti, “Zokolola ndi zambiri, koma ogwira ntchito ndi ochepa. Pemphani Ambuye wa zokolola, kuti atumize antchito ku munda wake wa zokolola.
tebhyaḥ kathayāmāsa ca śasyāni bahūnīti satyaṁ kintu chedakā alpe; tasmāddhetoḥ śasyakṣetre chedakān aparānapi preṣayituṁ kṣetrasvāminaṁ prārthayadhvaṁ|
3 Pitani! Ine ndikukutumizani ngati nkhosa pakati pa mimbulu.
yūyaṁ yāta, paśyata, vṛkāṇāṁ madhye meṣaśāvakāniva yuṣmān prahiṇomi|
4 Musatenge chikwama kapena thumba kapena nsapato; ndipo musalonjere wina aliyense pa njira.
yūyaṁ kṣudraṁ mahad vā vasanasampuṭakaṁ pādukāśca mā gṛhlīta, mārgamadhye kamapi mā namata ca|
5 “Mukamalowa mʼnyumba, poyamba nenani kuti, ‘Mtendere pa nyumba ino.’
aparañca yūyaṁ yad yat niveśanaṁ praviśatha tatra niveśanasyāsya maṅgalaṁ bhūyāditi vākyaṁ prathamaṁ vadata|
6 Ngati mʼnyumbamo muli munthu wofuna mtendere, mtendere wanuwo udzakhala pa iyeyo; ngati mulibemo, mtendere wanuwo udzabwerera kwa inu.
tasmāt tasmin niveśane yadi maṅgalapātraṁ sthāsyati tarhi tanmaṅgalaṁ tasya bhaviṣyati, nocet yuṣmān prati parāvarttiṣyate|
7 Khalani mʼnyumba yomweyo, idyani ndi kumwa chilichonse chimene akupatsani, pakuti wantchito ayenera kulandira malipiro ake. Musachoke kumene mwafikirako ndi kupita ku nyumba zina.
aparañca te yatkiñcid dāsyanti tadeva bhuktvā pītvā tasminniveśane sthāsyatha; yataḥ karmmakārī jano bhṛtim arhati; gṛhād gṛhaṁ mā yāsyatha|
8 “Mukamalowa mʼmudzi, ndi kulandiridwa, idyani chilichonse akukonzerani.
anyacca yuṣmāsu kimapi nagaraṁ praviṣṭeṣu lokā yadi yuṣmākam ātithyaṁ kariṣyanti, tarhi yat khādyam upasthāsyanti tadeva khādiṣyatha|
9 Chiritsani odwala amene ali kumeneko ndipo muwawuze kuti, ‘Ufumu wa Mulungu wayandikira.’
tannagarasthān rogiṇaḥ svasthān kariṣyatha, īśvarīyaṁ rājyaṁ yuṣmākam antikam āgamat kathāmetāñca pracārayiṣyatha|
10 Koma mukalowa mʼmudzi ndipo osalandiridwa bwino, kapiteni ku misewu mʼmudzimo nʼkukanena kuti,
kintu kimapi puraṁ yuṣmāsu praviṣṭeṣu lokā yadi yuṣmākam ātithyaṁ na kariṣyanti, tarhi tasya nagarasya panthānaṁ gatvā kathāmetāṁ vadiṣyatha,
11 ‘Tikukusansirani ngakhale fumbi la mʼmudzi wanuwu limene lamamatira ku mapazi athuwa. Komabe dziwani izi: Ufumu wa Mulungu wayandikira.’
yuṣmākaṁ nagarīyā yā dhūlyo'smāsu samalagan tā api yuṣmākaṁ prātikūlyena sākṣyārthaṁ sampātayāmaḥ; tathāpīśvararājyaṁ yuṣmākaṁ samīpam āgatam iti niścitaṁ jānīta|
12 Ine ndikuwuzani kuti adzachita chifundo polanga Sodomu pa tsikulo kusiyana ndi mudziwo.
ahaṁ yuṣmabhyaṁ yathārthaṁ kathayāmi, vicāradine tasya nagarasya daśātaḥ sidomo daśā sahyā bhaviṣyati|
13 “Ndiwe watsoka, iwe Korazini! Ndiwe watsoka, iwe Betisaida! Kukanakhala kuti zodabwitsa zimene zinachitika mwa inu zinachitika ku Turo ndi Sidoni, iwo akanatembenuka mtima kale lomwe, atavala ziguduli ndi kudzola phulusa.
hā hā korāsīn nagara, hā hā baitsaidānagara yuvayormadhye yādṛśāni āścaryyāṇi karmmāṇyakriyanta, tāni karmmāṇi yadi sorasīdono rnagarayorakāriṣyanta, tadā ito bahudinapūrvvaṁ tannivāsinaḥ śaṇavastrāṇi paridhāya gātreṣu bhasma vilipya samupaviśya samakhetsyanta|
14 Koma adzachita chifundo polanga Turo ndi Sidoni kusiyana ndi inu.
ato vicāradivase yuṣmākaṁ daśātaḥ sorasīdonnivāsināṁ daśā sahyā bhaviṣyati|
15 Kodi iwe Kaperenawo, adzakukweza mpaka kumwamba? Ayi, adzakutsitsa mpaka ku Malo a anthu akufa. (Hadēs )
he kapharnāhūm, tvaṁ svargaṁ yāvad unnatā kintu narakaṁ yāvat nyagbhaviṣyasi| (Hadēs )
16 “Womvera inu, akumvera Ine; wokana inu, akukana Ine. Ndipo wokana Ine; akukana Iye amene anandituma Ine.”
yo jano yuṣmākaṁ vākyaṁ gṛhlāti sa mamaiva vākyaṁ gṛhlāti; kiñca yo jano yuṣmākam avajñāṁ karoti sa mamaivāvajñāṁ karoti; yo jano mamāvajñāṁ karoti ca sa matprerakasyaivāvajñāṁ karoti|
17 Anthu 72 aja anabwerera ndi chimwemwe ndipo anati, “Ambuye, ngakhale ziwanda zinatigonjera ife mʼdzina lanu.”
atha te saptatiśiṣyā ānandena pratyāgatya kathayāmāsuḥ, he prabho bhavato nāmnā bhūtā apyasmākaṁ vaśībhavanti|
18 Iye anayankha kuti, “Ndinaona Satana akugwa kuchokera kumwamba ngati mphenzi.
tadānīṁ sa tān jagāda, vidyutamiva svargāt patantaṁ śaitānam adarśam|
19 Ine ndakupatsani ulamuliro woponda njoka ndi zinkhanira, ndi kugonjetsa mphamvu zonse za mdani; palibe chimene chidzakupwetekani.
paśyata sarpān vṛścikān ripoḥ sarvvaparākramāṁśca padatalai rdalayituṁ yuṣmabhyaṁ śaktiṁ dadāmi tasmād yuṣmākaṁ kāpi hāni rna bhaviṣyati|
20 Komabe musakondwere chifukwa mizimu yoyipa inakugonjerani, koma kondwerani chifukwa mayina anu analembedwa kumwamba.”
bhūtā yuṣmākaṁ vaśībhavanti, etannimittat mā samullasata, svarge yuṣmākaṁ nāmāni likhitāni santīti nimittaṁ samullasata|
21 Nthawi imeneyo Mzimu Woyera anadzaza Yesu ndi chimwemwe ndipo anati, “Ine ndikulemekeza Inu, Atate Ambuye a kumwamba ndi dziko lapansi, chifukwa mwawabisira anthu anzeru ndi ophunzira zinthu izi ndipo mwaziwulula kwa ana aangʼono. Inde, Atate, pakuti munachita zimenezi mwachifuniro chanu.
tadghaṭikāyāṁ yīśu rmanasi jātāhlādaḥ kathayāmāsa he svargapṛthivyorekādhipate pitastvaṁ jñānavatāṁ viduṣāñca lokānāṁ purastāt sarvvametad aprakāśya bālakānāṁ purastāt prākāśaya etasmāddhetostvāṁ dhanyaṁ vadāmi, he pitaritthaṁ bhavatu yad etadeva tava gocara uttamam|
22 “Atate anga anapereka zinthu zonse mʼmanja mwanga. Palibe amene amadziwa Mwana kupatula Atate yekha, ndipo palibe amene amadziwa Atate kupatula Mwana yekha, ndiponso amene Mwanayo akufuna kumuwululira.”
pitrā sarvvāṇi mayi samarpitāni pitaraṁ vinā kopi putraṁ na jānāti kiñca putraṁ vinā yasmai janāya putrastaṁ prakāśitavān tañca vinā kopi pitaraṁ na jānāti|
23 Kenaka anatembenukira kwa ophunzira ake nawawuza iwo okha kuti, “Ndi odala maso amene akuona zimene mukuonazi.
tapaḥ paraṁ sa śiṣyān prati parāvṛtya guptaṁ jagāda, yūyametāni sarvvāṇi paśyatha tato yuṣmākaṁ cakṣūṁṣi dhanyāni|
24 Pakuti kunena zoona aneneri ambiri ndi mafumu anafunitsitsa kuona zimene mukuonazi koma sanazione, ndi kumva zimene mukumvazi koma sanazimve.”
yuṣmānahaṁ vadāmi, yūyaṁ yāni sarvvāṇi paśyatha tāni bahavo bhaviṣyadvādino bhūpatayaśca draṣṭumicchantopi draṣṭuṁ na prāpnuvan, yuṣmābhi ryā yāḥ kathāśca śrūyante tāḥ śrotumicchantopi śrotuṁ nālabhanta|
25 Nthawi ina katswiri wa malamulo anayimirira kuti ayese Yesu. Iye anati, “Aphunzitsi, ndichite chiyani kuti ndikhale ndi moyo wosatha?” (aiōnios )
anantaram eko vyavasthāpaka utthāya taṁ parīkṣituṁ papraccha, he upadeśaka anantāyuṣaḥ prāptaye mayā kiṁ karaṇīyaṁ? (aiōnios )
26 Yesu anayankha kuti, “Mwalembedwa chiyani mʼMalamulo, ndipo iwe umawerenga zotani?”
yīśuḥ pratyuvāca, atrārthe vyavasthāyāṁ kiṁ likhitamasti? tvaṁ kīdṛk paṭhasi?
27 Iye anayankha kuti, “Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu zako zonse ndi nzeru zako zonse, ndi kukonda mnansi wako monga iwe mwini.”
tataḥ sovadat, tvaṁ sarvvāntaḥkaraṇaiḥ sarvvaprāṇaiḥ sarvvaśaktibhiḥ sarvvacittaiśca prabhau parameśvare prema kuru, samīpavāsini svavat prema kuru ca|
28 Yesu anayankha kuti, “Iwe wayankha bwino, chita zimenezi ndipo udzakhala ndi moyo.”
tadā sa kathayāmāsa, tvaṁ yathārthaṁ pratyavocaḥ, ittham ācara tenaiva jīviṣyasi|
29 Koma iye anafuna kudzilungamitsa yekha, ndipo anamufunsanso Yesu kuti, “Kodi mnansi wanga ndani?”
kintu sa janaḥ svaṁ nirddoṣaṁ jñāpayituṁ yīśuṁ papraccha, mama samīpavāsī kaḥ? tato yīśuḥ pratyuvāca,
30 Yesu pomuyankha anati, “Munthu wina ankatsikira ku Yeriko kuchokera ku Yerusalemu. Pa njira anavulazidwa ndi achifwamba. Anamuvula zovala zake, namumenya ndi kuthawa, namusiya ali pafupi kufa.
eko jano yirūśālampurād yirīhopuraṁ yāti, etarhi dasyūnāṁ kareṣu patite te tasya vastrādikaṁ hṛtavantaḥ tamāhatya mṛtaprāyaṁ kṛtvā tyaktvā yayuḥ|
31 Wansembe ankapita pa njira yomweyo, ndipo ataona munthuyo, analambalala.
akasmād eko yājakastena mārgeṇa gacchan taṁ dṛṣṭvā mārgānyapārśvena jagāma|
32 Chimodzimodzinso, Mlevi wina pamene anafika pa malopo ndi kumuona, analambalalanso.
ittham eko levīyastatsthānaṁ prāpya tasyāntikaṁ gatvā taṁ vilokyānyena pārśvena jagāma|
33 Koma Msamariya wina, ali pa ulendo wake, anafika pamene panali munthuyo; ndipo atamuona, anamva naye chisoni.
kintvekaḥ śomiroṇīyo gacchan tatsthānaṁ prāpya taṁ dṛṣṭvādayata|
34 Anapita panali munthu wovulalayo, nathira mafuta ndi vinyo pa zilonda zake, nʼkuzimanga. Kenaka anamukweza pa bulu wake, napita naye ku nyumba ya alendo, namusamalira.
tasyāntikaṁ gatvā tasya kṣateṣu tailaṁ drākṣārasañca prakṣipya kṣatāni baddhvā nijavāhanopari tamupaveśya pravāsīyagṛham ānīya taṁ siṣeve|
35 Mmawa mwake anatenga ndalama ziwiri zasiliva nazipereka kwa woyangʼanira nyumbayo, nati, ‘Musamalireni munthuyu, ndipo pobwera ndidzakubwezerani zonse zimene mugwiritse ntchito.’
parasmin divase nijagamanakāle dvau mudrāpādau tadgṛhasvāmine dattvāvadat janamenaṁ sevasva tatra yo'dhiko vyayo bhaviṣyati tamahaṁ punarāgamanakāle pariśotsyāmi|
36 “Kodi ukuganiza ndi ndani mwa atatuwa, amene anali mnansi wa munthu amene anavulazidwa ndi achifwambawo?”
eṣāṁ trayāṇāṁ madhye tasya dasyuhastapatitasya janasya samīpavāsī kaḥ? tvayā kiṁ budhyate?
37 Katswiri wa Malamulo uja anayankha kuti, “Amene anamuchitira chifundo.” Yesu anamuwuza kuti, “Pita, uzikachita chimodzimodzi.”
tataḥ sa vyavasthāpakaḥ kathayāmāsa yastasmin dayāṁ cakāra| tadā yīśuḥ kathayāmāsa tvamapi gatvā tathācara|
38 Yesu ndi ophunzira ake akuyenda, anafika pa mudzi kumene mayi wotchedwa Marita anamulandira Iye mʼnyumba mwake.
tataḥ paraṁ te gacchanta ekaṁ grāmaṁ praviviśuḥ; tadā marthānāmā strī svagṛhe tasyātithyaṁ cakāra|
39 Mayiyu anali ndi mchemwali wake wotchedwa Mariya, amene anakhala pa mapazi a Yesu kumverera zimene Iye ankanena.
tasmāt mariyam nāmadheyā tasyā bhaginī yīśoḥ padasamīpa uvaviśya tasyopadeśakathāṁ śrotumārebhe|
40 Koma Marita anatanganidwa ndi zokonzekera zonse zimene zimayenera kuchitika. Iye anabwera kwa Yesu namufunsa kuti, “Ambuye, kodi simusamala kuti mchemwali wanga wandisiya kuti ndichite ntchito yonse ndekha? Muwuzeni andithandize!”
kintu marthā nānāparicaryyāyāṁ vyagrā babhūva tasmāddhetostasya samīpamāgatya babhāṣe; he prabho mama bhaginī kevalaṁ mamopari sarvvakarmmaṇāṁ bhāram arpitavatī tatra bhavatā kiñcidapi na mano nidhīyate kim? mama sāhāyyaṁ karttuṁ bhavān tāmādiśatu|
41 Ambuye anati, “Marita, Marita, ukudandaula ndi kuvutika ndi zinthu zambiri,
tato yīśuḥ pratyuvāca he marthe he marthe, tvaṁ nānākāryyeṣu cintitavatī vyagrā cāsi,
42 koma chofunika nʼchimodzi chokha. Mariya wasankha chinthu chabwino, ndipo palibe angamulande chimenechi.”
kintu prayojanīyam ekamātram āste| aparañca yamuttamaṁ bhāgaṁ kopi harttuṁ na śaknoti saeva mariyamā vṛtaḥ|