< Levitiko 1 >

1 Yehova anayitana Mose mu tenti ya msonkhano. Iye anati,
Yahvé llamó a Moisés y le habló desde la Tienda del Encuentro, diciendo:
2 “Aliyense wa inu ngati abwera ndi nsembe kwa Yehova kuchokera pa ziweto zake, choperekacho chikhale ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi.
“Habla a los hijos de Israel y diles: ‘Cuando alguno de vosotros ofrezca una ofrenda a Yahvé, ofreceréis vuestra ofrenda del ganado, de la manada y del rebaño.
3 “‘Ngati munthu apereka nsembe yopsereza ya ngʼombe, ikhale yayimuna yopanda chilema. Aziyipereka pa khomo la tenti ya msonkhano, kuti Yehova alandire.
“‘Si su ofrenda es un holocausto del rebaño, ofrecerá un macho sin defecto. Lo ofrecerá a la puerta de la Tienda del Encuentro, para que sea aceptado ante el Señor.
4 Munthuyo asanjike dzanja lake pa mutu pa nsembe yopserezayo, ndipo idzalandiridwa kuti ikhale yopepesera machimo ake.
Pondrá su mano sobre la cabeza del holocausto, y le será aceptado para hacer expiación por él.
5 Pambuyo pake aphe ngʼombeyo pamaso pa Yehova, ndipo ansembe, ana a Aaroni, atenge magazi ake ndi kuwawaza mbali zonse za guwa lansembe limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
Matará el toro delante de Yahvé. Los hijos de Aarón, los sacerdotes, presentarán la sangre y la rociarán alrededor del altar que está a la puerta de la Tienda de reunión.
6 Munthuyo asende nsembe yopserezayo ndi kuyidula nthulinthuli.
Desollará el holocausto y lo cortará en pedazos.
7 Ndipo ana a Aaroni, wansembe uja asonkhe moto pa guwa ndi kuyalapo nkhuni pa motopo.
Los hijos del sacerdote Aarón pondrán fuego en el altar y pondrán la leña en orden sobre el fuego;
8 Kenaka ana a Aaroni, wansembe uja, ayike nthuli za nyamayo, mutu wake pamodzi ndi mafuta omwe pa nkhuni zimene zili paguwapo.
y los hijos de Aarón, los sacerdotes, pondrán los trozos, la cabeza y la grasa en orden sobre la leña que está sobre el fuego que está en el altar;
9 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe awotche nyama yonse paguwapo. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chowotcha pa moto, cha fungo lokomera Yehova.
pero lavará sus entrañas y sus patas con agua. El sacerdote lo quemará todo sobre el altar, como holocausto, ofrenda encendida, de aroma agradable para Yahvé.
10 “‘Koma ngati chopereka cha nsembe yopserezayo ndi nkhosa kapena mbuzi kuchokera pa ziweto zake, munthuyo apereke yayimuna yopanda chilema.
“‘Si su ofrenda es del rebaño, de las ovejas o de las cabras, para un holocausto, ofrecerá un macho sin defecto.
11 Ayiphere kumpoto kwa guwa, pamaso pa Yehova, ndipo ana a Aaroni amene ndi ansembe, awaze magazi ake mbali zonse za guwalo.
Lo matará en el lado norte del altar, delante de Yahvé. Los hijos de Aarón, los sacerdotes, rociarán su sangre alrededor del altar.
12 Kenaka ayidule nyamayo nthulinthuli, ndipo wansembe ayike nthulizo pa guwa, atengenso mutu ndi mafuta omwe, ndipo ayike zonsezi pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa.
Lo cortará en pedazos, con su cabeza y su grasa. El sacerdote los pondrá en orden sobre la leña que está sobre el fuego que está sobre el altar,
13 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe abwere nazo zonse ndi kuzitentha pa guwa. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chotentha pa moto, fungo lokomera Yehova.
pero las entrañas y las patas las lavará con agua. El sacerdote ofrecerá el conjunto y lo quemará sobre el altar. Es un holocausto, una ofrenda hecha por el fuego, de aroma agradable para Yahvé.
14 “‘Koma ngati chopereka kwa Yehova ndi nsembe yopsereza ya mbalame, ndiye ikhale njiwa kapena mawunda.
“‘Si su ofrenda a Yahvé es un holocausto de aves, ofrecerá su ofrenda de tórtolas o de pichones.
15 Wansembe abwere nayo ku guwa, ayidule mutu moyipotola ndi kutentha mutuwo pa guwa. Magazi ake awathire pansi kuti ayenderere pambali pa guwa.
El sacerdote la traerá al altar, le arrancará la cabeza y la quemará sobre el altar, y su sangre se derramará a un lado del altar;
16 Iye achotse chithokomiro pamodzi ndi nthenga zake zomwe ndi kuzitaya ku malo wotayirako phulusa, kummawa kwa guwalo.
y le quitará el buche y las plumas, y la echará junto al altar, en la parte oriental, en el lugar de las cenizas.
17 Kenaka ayingʼambe pakati, koma asachotse mapiko. Ndipo wansembe ayiwotche pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa. Imeneyi ndi nsembe yopsereza, yowotcha pa moto ndiponso ya fungo lokomera Yehova.
La arrancará por las alas, pero no la separará. El sacerdote lo quemará sobre el altar, sobre la leña que está sobre el fuego. Es un holocausto, una ofrenda hecha por el fuego, de aroma agradable para Yahvé.

< Levitiko 1 >