< Levitiko 1 >

1 Yehova anayitana Mose mu tenti ya msonkhano. Iye anati,
and to call: call to to(wards) Moses and to speak: speak LORD to(wards) him from tent meeting to/for to say
2 “Aliyense wa inu ngati abwera ndi nsembe kwa Yehova kuchokera pa ziweto zake, choperekacho chikhale ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi.
to speak: speak to(wards) son: descendant/people Israel and to say to(wards) them man for to present: bring from you offering to/for LORD from [the] animal from [the] cattle and from [the] flock to present: bring [obj] offering your
3 “‘Ngati munthu apereka nsembe yopsereza ya ngʼombe, ikhale yayimuna yopanda chilema. Aziyipereka pa khomo la tenti ya msonkhano, kuti Yehova alandire.
if burnt offering offering his from [the] cattle male unblemished to present: bring him to(wards) entrance tent meeting to present: bring [obj] him to/for acceptance his to/for face: before LORD
4 Munthuyo asanjike dzanja lake pa mutu pa nsembe yopserezayo, ndipo idzalandiridwa kuti ikhale yopepesera machimo ake.
and to support hand his upon head [the] burnt offering and to accept to/for him to/for to atone upon him
5 Pambuyo pake aphe ngʼombeyo pamaso pa Yehova, ndipo ansembe, ana a Aaroni, atenge magazi ake ndi kuwawaza mbali zonse za guwa lansembe limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
and to slaughter [obj] son: young animal [the] cattle to/for face: before LORD and to present: bring son: child Aaron [the] priest [obj] [the] blood and to scatter [obj] [the] blood upon [the] altar around: side which entrance tent meeting
6 Munthuyo asende nsembe yopserezayo ndi kuyidula nthulinthuli.
and to strip [obj] [the] burnt offering and to cut [obj] her to/for piece her
7 Ndipo ana a Aaroni, wansembe uja asonkhe moto pa guwa ndi kuyalapo nkhuni pa motopo.
and to give: put son: child Aaron [the] priest fire upon [the] altar and to arrange tree: wood upon [the] fire
8 Kenaka ana a Aaroni, wansembe uja, ayike nthuli za nyamayo, mutu wake pamodzi ndi mafuta omwe pa nkhuni zimene zili paguwapo.
and to arrange son: child Aaron [the] priest [obj] [the] piece [obj] [the] head and [obj] [the] suet upon [the] tree: wood which upon [the] fire which upon [the] altar
9 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe awotche nyama yonse paguwapo. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chowotcha pa moto, cha fungo lokomera Yehova.
and entrails: inner parts his and leg his to wash: wash in/on/with water and to offer: burn [the] priest [obj] [the] all [the] altar [to] burnt offering food offering aroma soothing to/for LORD
10 “‘Koma ngati chopereka cha nsembe yopserezayo ndi nkhosa kapena mbuzi kuchokera pa ziweto zake, munthuyo apereke yayimuna yopanda chilema.
and if from [the] flock offering his from [the] sheep or from [the] goat to/for burnt offering male unblemished to present: bring him
11 Ayiphere kumpoto kwa guwa, pamaso pa Yehova, ndipo ana a Aaroni amene ndi ansembe, awaze magazi ake mbali zonse za guwalo.
and to slaughter [obj] him upon thigh [the] altar north [to] to/for face: before LORD and to scatter son: child Aaron [the] priest [obj] blood his upon [the] altar around: side
12 Kenaka ayidule nyamayo nthulinthuli, ndipo wansembe ayike nthulizo pa guwa, atengenso mutu ndi mafuta omwe, ndipo ayike zonsezi pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa.
and to cut [obj] him to/for piece his and [obj] head his and [obj] suet his and to arrange [the] priest [obj] them upon [the] tree: wood which upon [the] fire which upon [the] altar
13 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe abwere nazo zonse ndi kuzitentha pa guwa. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chotentha pa moto, fungo lokomera Yehova.
and [the] entrails: inner parts and [the] leg to wash: wash in/on/with water and to present: bring [the] priest [obj] [the] all and to offer: burn [the] altar [to] burnt offering he/she/it food offering aroma soothing to/for LORD
14 “‘Koma ngati chopereka kwa Yehova ndi nsembe yopsereza ya mbalame, ndiye ikhale njiwa kapena mawunda.
and if from [the] bird burnt offering offering his to/for LORD and to present: bring from [the] turtledove or from son: young animal [the] dove [obj] offering his
15 Wansembe abwere nayo ku guwa, ayidule mutu moyipotola ndi kutentha mutuwo pa guwa. Magazi ake awathire pansi kuti ayenderere pambali pa guwa.
and to present: bring him [the] priest to(wards) [the] altar and to nip [obj] head his and to offer: burn [the] altar [to] and to drain blood his upon wall [the] altar
16 Iye achotse chithokomiro pamodzi ndi nthenga zake zomwe ndi kuzitaya ku malo wotayirako phulusa, kummawa kwa guwalo.
and to turn aside: remove [obj] crop his in/on/with plumage her and to throw [obj] her beside [the] altar east [to] to(wards) place [the] ashes
17 Kenaka ayingʼambe pakati, koma asachotse mapiko. Ndipo wansembe ayiwotche pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa. Imeneyi ndi nsembe yopsereza, yowotcha pa moto ndiponso ya fungo lokomera Yehova.
and to cleave [obj] him in/on/with wing his not to separate and to offer: burn [obj] him [the] priest [the] altar [to] upon [the] tree: wood which upon [the] fire burnt offering he/she/it food offering aroma soothing to/for LORD

< Levitiko 1 >