< Levitiko 1 >

1 Yehova anayitana Mose mu tenti ya msonkhano. Iye anati,
Povolal pak Hospodin Mojžíše, a mluvil k němu z stánku úmluvy, řka:
2 “Aliyense wa inu ngati abwera ndi nsembe kwa Yehova kuchokera pa ziweto zake, choperekacho chikhale ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi.
Mluv k synům Izraelským a rci jim: Když by kdo z vás obětoval obět Hospodinu, z hovad, totiž z volů aneb z drobného dobytka obětovati budete obět svou.
3 “‘Ngati munthu apereka nsembe yopsereza ya ngʼombe, ikhale yayimuna yopanda chilema. Aziyipereka pa khomo la tenti ya msonkhano, kuti Yehova alandire.
Jestliže zápalná obět jeho byla by z skotů, samce bez vady obětovati bude. U dveří stánku úmluvy obětovati jej bude dobrovolně, před oblíčejem Hospodinovým.
4 Munthuyo asanjike dzanja lake pa mutu pa nsembe yopserezayo, ndipo idzalandiridwa kuti ikhale yopepesera machimo ake.
A vloží ruku svou na hlavu oběti zápalné, i bude příjemná jemu k očištění jeho.
5 Pambuyo pake aphe ngʼombeyo pamaso pa Yehova, ndipo ansembe, ana a Aaroni, atenge magazi ake ndi kuwawaza mbali zonse za guwa lansembe limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
Tedy zabije volka toho před tváří Hospodinovou, a obětovati budou kněží, synové Aronovi, krev, a pokropí tou krví oltáře svrchu vůkol, kterýž jest u dveří stánku úmluvy.
6 Munthuyo asende nsembe yopserezayo ndi kuyidula nthulinthuli.
I stáhne kůži s oběti zápalné, a rozseká ji na díly své.
7 Ndipo ana a Aaroni, wansembe uja asonkhe moto pa guwa ndi kuyalapo nkhuni pa motopo.
A dají synové Arona kněze oheň na oltář, a narovnají dříví na tom ohni.
8 Kenaka ana a Aaroni, wansembe uja, ayike nthuli za nyamayo, mutu wake pamodzi ndi mafuta omwe pa nkhuni zimene zili paguwapo.
Potom zpořádají kněží, synové Aronovi, díly ty, hlavu i tuk, na dříví vložené na oheň, kterýž jest na oltáři.
9 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe awotche nyama yonse paguwapo. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chowotcha pa moto, cha fungo lokomera Yehova.
A droby jeho i nohy jeho vymyjete vodou. I páliti bude kněz všecko to na oltáři; zápal jest v obět ohnivou, vůně spokojující Hospodina.
10 “‘Koma ngati chopereka cha nsembe yopserezayo ndi nkhosa kapena mbuzi kuchokera pa ziweto zake, munthuyo apereke yayimuna yopanda chilema.
Jestliže pak z drobného dobytka bude obět jeho, z ovcí aneb z koz k oběti zápalné, samce bez poškvrny obětovati bude.
11 Ayiphere kumpoto kwa guwa, pamaso pa Yehova, ndipo ana a Aaroni amene ndi ansembe, awaze magazi ake mbali zonse za guwalo.
A zabije ho při straně oltáře půlnoční před tváří Hospodinovou, a pokropí kněží, synové Aronovi, krví oltáře vůkol.
12 Kenaka ayidule nyamayo nthulinthuli, ndipo wansembe ayike nthulizo pa guwa, atengenso mutu ndi mafuta omwe, ndipo ayike zonsezi pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa.
I rozseká ho na díly jeho s hlavou jeho i tukem jeho, a zpořádá je kněz na dříví vložené na oheň, kterýž jest na oltáři.
13 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe abwere nazo zonse ndi kuzitentha pa guwa. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chotentha pa moto, fungo lokomera Yehova.
A střeva jeho i nohy jeho vymyje vodou. Tedy obětovati bude kněz všecko to, a páliti bude to na oltáři; zápal jest v obět ohnivou, vůně spokojující Hospodina.
14 “‘Koma ngati chopereka kwa Yehova ndi nsembe yopsereza ya mbalame, ndiye ikhale njiwa kapena mawunda.
Jestliže pak z ptactva obět zápalnou obětovati bude Hospodinu, tedy ať obětuje z hrdliček aneb z holoubat obět svou.
15 Wansembe abwere nayo ku guwa, ayidule mutu moyipotola ndi kutentha mutuwo pa guwa. Magazi ake awathire pansi kuti ayenderere pambali pa guwa.
I vloží je kněz na oltář a nehtem natrhne hlavy jeho, a zapálí na oltáři, vytlače krev jeho na stranu oltáře.
16 Iye achotse chithokomiro pamodzi ndi nthenga zake zomwe ndi kuzitaya ku malo wotayirako phulusa, kummawa kwa guwalo.
Odejme také vole jeho s nečistotami jeho, a povrže je blízko oltáře k straně východní na místo, kdež jest popel.
17 Kenaka ayingʼambe pakati, koma asachotse mapiko. Ndipo wansembe ayiwotche pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa. Imeneyi ndi nsembe yopsereza, yowotcha pa moto ndiponso ya fungo lokomera Yehova.
A natrhne ho za křídla jeho, kterýchž však neodtrhne. I páliti bude je kněz na oltáři na dříví, kteréž jest na ohni; zápalť jest v obět ohnivou, vůně spokojující Hospodina.

< Levitiko 1 >