< Levitiko 9 >
1 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Mose anayitana Aaroni, ana ake ndi akuluakulu a Aisraeli.
А у осми дан сазва Мојсије Арона и синове његове и старешине израиљске.
2 Ndipo anawuza Aaroni kuti, “Tenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yako yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza. Zonsezi zikhale zopanda chilema ndipo uzipereke pamaso pa Yehova.
И рече Арону: Узми теле за жртву ради греха и овна за жртву паљеницу, оба здрава; и принеси их пред Господом.
3 Kenaka uwawuze Aisraeli kuti, ‘Tengani mbuzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo. Mutengenso mwana wangʼombe ndi mwana wankhosa. Zonsezi zikhale za chaka chimodzi ndi zopanda chilema kuti zikhale nsembe yopsereza.
А синовима Израиљевим кажи и реци: Узмите јаре за жртву ради греха, и теле и јагње, обоје од године дана, и здраво, за жртву паљеницу.
4 Mutengenso ngʼombe yayimuna ndi nkhosa yayimuna kuti zikhale nsembe yachiyanjano zoti ziperekedwe pamaso pa Yehova. Pamodzi ndi izi mubwerenso ndi nsembe yachakudya yosakaniza ndi mafuta pakuti lero Yehova akuonekerani.’”
И вола и овна за жртву захвалну, да принесете пред Господом, и дар с уљем замешен, јер ће вам се данас јавити Господ.
5 Anthu anatenga zonse zimene Mose analamula nabwera nazo pa khomo la tenti ya msonkhano. Gululo linasendera pafupi ndi kuyima pamaso pa Yehova.
И узеше шта заповеди Мојсије, и донесоше пред шатор од састанка, и приступивши сав збор стадоше пред Господом.
6 Tsono Mose anati, “Izi ndi zimene Yehova walamula kuti muchite kuti ulemerero wa Yehova ukuonekereni.”
И рече Мојсије: Учините шта је заповедио Господ, и показаће вам се слава Господња.
7 Pambuyo pake Mose anawuza Aaroni kuti, “Sendera pafupi ndi guwa ndipo upereka nsembe yako yopepesera machimo ndi nsembe yako yopsereza ndikuchita mwambo wopepesera machimo ako ndi machimo a anthu. Anthuwa apereke nsembe zawo zopepesera machimo monga momwe Yehova walamulira.”
И рече Мојсије Арону: Приступи к олтару, и принеси жртву за грех свој и жртву своју паљеницу, и очисти од греха себе и народ; и принеси жртву народну и очисти их од греха, као што је заповедио Господ.
8 Choncho Aaroni anasendera pafupi ndi guwa, napha mwana wangʼombe uja kukhala nsembe yake yopepesera machimo.
Тада Арон приступи к олтару и закла теле за се.
9 Ana a Aaroni anabwera ndi magazi kwa Aaroni ndipo iye anaviyika chala chake mʼmagaziwo, nawapaka pa nyanga za guwa. Magazi wotsalawo anawathira pa tsinde la guwalo.
И синови Аронови додаше му крв, а он замочи прст свој у крв, и помаза рогове олтару; а осталу крв изли на подножје олтару.
10 Kenaka anatentha paguwapo, mafuta, impsyo pamodzi ndi mafuta amene amakuta chiwindi ngati nsembe yopepesera machimoyo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
А сало и бубреге и мрежицу од јетре од жртве за грех запали на олтару, као што беше заповедио Господ Мојсију.
11 Koma nyama ndi chikopa anazitenthera kunja kwa msasa.
А месо и кожу сажеже огњем иза логора.
12 Kenaka anapha nsembe yopsereza. Ana a Aaroni atabwera ndi magazi kwa iye, Aaroniyo anawawaza mbali zonse za guwa.
Потом закла жртву своју паљеницу, и синови Аронови додаше му крв од ње, и покропи њом олтар одозго унаоколо.
13 Ana akewo anamupatsa nyama yoduladula ya nsembe yopsereza ija pamodzi ndi mutu ndipo anazitentha pa guwa.
И додаше му жртву паљеницу исечену на делове заједно с главом, и запали је на олтару.
14 Aaroni anatsuka matumbo ndi miyendo nazitentha pa guwa pamodzi ndi nsembe yopsereza ija.
И оправши црева и ноге од ње, запали их на олтару сврх жртве паљенице.
15 Kenaka Aaroni anapereka zopereka za anthuwo. Anatenga mbuzi yopepesera machimo a anthuwo, yopereka chifukwa cha tchimo, nayipha ndi kuyipereka kuti ikhale yopepesera machimo monga anachitira ndi nsembe yoyamba ija.
Потом принесе жртву народну: узе јаре за грех које беше за народ, и закла га, и принесе за грех као и прво.
16 Anabwera ndi nsembe yopsereza, nayipereka potsata mwambo wake.
Иза тога принесе и жртву паљеницу, и сврши по закону.
17 Anabweranso ndi chopereka cha chakudya. Anatapa ufa dzanja limodzi ndi kutentha pa guwa, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa ija.
Принесе и дар, и узевши од њега пуну шаку запали на олтару сврх јутарње жртве паљенице.
18 Tsono Aaroni anapha ngʼombe ndi nkhosa yayimuna monga nsembe yachiyanjano ya anthu. Ana ake anamupatsira magazi ndipo anawawaza mbali zonse za guwa.
Потом закла вола и овна на жртву захвалну за народ; и дадоше му синови Аронови крв, и покропи њом олтар одозго унаоколо.
19 Anamupatsiranso mafuta a ngʼombeyo ndi nkhosa yayimunayo: mchira wamafuta, mafuta wokuta matumbo, impsyo ndi mafuta wokuta chiwindi.
Па му додаше и сало од вола, и од овна реп, и сало што покрива црева, и бубреге и мрежицу с јетре,
20 Ana a Aaroni anayika mafutawo pa zidale. Pambuyo pake Aaroni anatentha mafutawo pa guwa lansembe.
И метнувши све сало на груди, и запали сало на олтару.
21 Koma zidale ndi ntchafu ya kumanja Aaroni anaziweyula ngati chopereka choweyula pamaso pa Yehova.
А груди и десно плеће обрну Арон тамо и амо на жртву обртану пред Господом, као што беше Господ заповедио Мојсију.
22 Kenaka Aaroni anakweza manja ake pa anthuwo nawadalitsa. Ndipo atatha kupereka nsembe yopepesera machimo, nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano, anatsika pa guwapo.
Тада подиже Арон руке своје према народу, и благослови их; и сиђе свршивши жртву за грех и жртву паљеницу и жртву захвалну.
23 Ndipo Mose pamodzi ndi Aaroni analowa mu tenti ya msonkhano. Atatulukamo anadalitsa anthuwo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa anthu onse.
Потом уђе Мојсије с Ароном у шатор од састанка, а кад опет изађоше благословише народ; и слава се Господња показа свему народу.
24 Pomwepo moto unatuluka pamaso pa Yehova niwutentha nsembe zopsereza ndi mafuta zimene zinali pa guwa. Anthu onse ataona zimenezi anafuwula mwachimwemwe ndipo anaweramitsa nkhope zawo pansi.
Јер дође огањ од Господа, и спали на олтару жртву паљеницу и сало. И видевши то сав народ повика и паде ничице.