< Levitiko 9 >
1 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Mose anayitana Aaroni, ana ake ndi akuluakulu a Aisraeli.
A ósmego dnia Mojżesz wezwał Aarona, jego synów i starszych Izraela.
2 Ndipo anawuza Aaroni kuti, “Tenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yako yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza. Zonsezi zikhale zopanda chilema ndipo uzipereke pamaso pa Yehova.
I powiedział do Aarona: Weź sobie młodego cielca na ofiarę za grzech i barana na całopalenie, [oba] bez skazy, i złóż je w ofierze przed PANEM.
3 Kenaka uwawuze Aisraeli kuti, ‘Tengani mbuzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo. Mutengenso mwana wangʼombe ndi mwana wankhosa. Zonsezi zikhale za chaka chimodzi ndi zopanda chilema kuti zikhale nsembe yopsereza.
A do synów Izraela powiesz: Weźcie kozła z kóz na ofiarę za grzech oraz cielca i barana, jednoroczne i bez skazy, na całopalenie;
4 Mutengenso ngʼombe yayimuna ndi nkhosa yayimuna kuti zikhale nsembe yachiyanjano zoti ziperekedwe pamaso pa Yehova. Pamodzi ndi izi mubwerenso ndi nsembe yachakudya yosakaniza ndi mafuta pakuti lero Yehova akuonekerani.’”
Także wołu i barana na ofiary pojednawcze, by złożyć je przed PANEM, i ofiarę pokarmową zmieszaną z oliwą; bo dziś PAN wam się ukaże.
5 Anthu anatenga zonse zimene Mose analamula nabwera nazo pa khomo la tenti ya msonkhano. Gululo linasendera pafupi ndi kuyima pamaso pa Yehova.
I przyprowadzili to, co Mojżesz rozkazał, przed Namiot Zgromadzenia. A cały lud zbliżył się i stanął przed PANEM.
6 Tsono Mose anati, “Izi ndi zimene Yehova walamula kuti muchite kuti ulemerero wa Yehova ukuonekereni.”
Wtedy Mojżesz powiedział: Oto co PAN nakazał wam uczynić; a ukaże się wam chwała PANA.
7 Pambuyo pake Mose anawuza Aaroni kuti, “Sendera pafupi ndi guwa ndipo upereka nsembe yako yopepesera machimo ndi nsembe yako yopsereza ndikuchita mwambo wopepesera machimo ako ndi machimo a anthu. Anthuwa apereke nsembe zawo zopepesera machimo monga momwe Yehova walamulira.”
Do Aarona zaś Mojżesz powiedział: Zbliż się do ołtarza i złóż swoją ofiarę za grzech i swoje całopalenie, i dokonaj przebłagania za siebie i lud. Złóż też ofiarę ludu i dokonaj za niego przebłagania, jak PAN rozkazał.
8 Choncho Aaroni anasendera pafupi ndi guwa, napha mwana wangʼombe uja kukhala nsembe yake yopepesera machimo.
Aaron zbliżył się więc do ołtarza i zabił cielca na ofiarę za grzech za siebie.
9 Ana a Aaroni anabwera ndi magazi kwa Aaroni ndipo iye anaviyika chala chake mʼmagaziwo, nawapaka pa nyanga za guwa. Magazi wotsalawo anawathira pa tsinde la guwalo.
I synowie Aarona podali mu krew, a on umoczył swój palec we krwi i pomazał [nią] rogi ołtarza, a [resztę] krwi wylał u podstawy ołtarza;
10 Kenaka anatentha paguwapo, mafuta, impsyo pamodzi ndi mafuta amene amakuta chiwindi ngati nsembe yopepesera machimoyo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
Ale tłuszcz, nerki i płat tłuszczu na wątrobie z ofiary za grzech spalił na ołtarzu, jak PAN rozkazał Mojżeszowi;
11 Koma nyama ndi chikopa anazitenthera kunja kwa msasa.
Mięso zaś i skórę spalił w ogniu poza obozem.
12 Kenaka anapha nsembe yopsereza. Ana a Aaroni atabwera ndi magazi kwa iye, Aaroniyo anawawaza mbali zonse za guwa.
Zabił też ofiarę całopalną, a synowie Aarona podali mu krew, którą pokropił ołtarz dokoła.
13 Ana akewo anamupatsa nyama yoduladula ya nsembe yopsereza ija pamodzi ndi mutu ndipo anazitentha pa guwa.
Przynieśli mu też ofiarę całopalną [podzieloną] na części wraz z głową, a [on] spalił to na ołtarzu;
14 Aaroni anatsuka matumbo ndi miyendo nazitentha pa guwa pamodzi ndi nsembe yopsereza ija.
Obmył też wnętrzności oraz nogi i spalił je z ofiarą całopalną na ołtarzu.
15 Kenaka Aaroni anapereka zopereka za anthuwo. Anatenga mbuzi yopepesera machimo a anthuwo, yopereka chifukwa cha tchimo, nayipha ndi kuyipereka kuti ikhale yopepesera machimo monga anachitira ndi nsembe yoyamba ija.
Potem przyprowadził ofiarę ludu. Wziął kozła przeznaczonego na ofiarę za grzech za lud, zabił go i złożył na ofiarę za grzech, tak jak poprzednio.
16 Anabwera ndi nsembe yopsereza, nayipereka potsata mwambo wake.
Przyprowadził też ofiarę całopalną i uczynił z nią według przepisu.
17 Anabweranso ndi chopereka cha chakudya. Anatapa ufa dzanja limodzi ndi kutentha pa guwa, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa ija.
Przyprowadził też ofiarę pokarmową. Wziął z niej pełną garść i spalił na ołtarzu, oprócz ofiary całopalnej porannej.
18 Tsono Aaroni anapha ngʼombe ndi nkhosa yayimuna monga nsembe yachiyanjano ya anthu. Ana ake anamupatsira magazi ndipo anawawaza mbali zonse za guwa.
Zabił też wołu i barana jako ofiarę pojednawczą za lud. I synowie Aarona podali mu krew, którą pokropił ołtarz dokoła.
19 Anamupatsiranso mafuta a ngʼombeyo ndi nkhosa yayimunayo: mchira wamafuta, mafuta wokuta matumbo, impsyo ndi mafuta wokuta chiwindi.
[Podali] mu także tłuszcz z wołu i barana, ogon, tłuszcz pokrywający [wnętrzności] oraz nerki i płat tłuszczu na wątrobie.
20 Ana a Aaroni anayika mafutawo pa zidale. Pambuyo pake Aaroni anatentha mafutawo pa guwa lansembe.
Włożyli też tłuszcz na mostkach, a [on] spalił tłuszcz na ołtarzu;
21 Koma zidale ndi ntchafu ya kumanja Aaroni anaziweyula ngati chopereka choweyula pamaso pa Yehova.
Mostki zaś i prawą łopatkę Aaron kołysał na ofiarę kołysaną przed PANEM, jak Mojżesz nakazał.
22 Kenaka Aaroni anakweza manja ake pa anthuwo nawadalitsa. Ndipo atatha kupereka nsembe yopepesera machimo, nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano, anatsika pa guwapo.
Potem Aaron podniósł ręce w stronę ludu i pobłogosławił go, a po złożeniu ofiary za grzech, ofiary całopalnej i ofiary pojednawczej zszedł na dół.
23 Ndipo Mose pamodzi ndi Aaroni analowa mu tenti ya msonkhano. Atatulukamo anadalitsa anthuwo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa anthu onse.
Wtedy Mojżesz i Aaron weszli do Namiotu Zgromadzenia, potem wyszli i pobłogosławili lud. I chwała PANA ukazała się całemu ludowi.
24 Pomwepo moto unatuluka pamaso pa Yehova niwutentha nsembe zopsereza ndi mafuta zimene zinali pa guwa. Anthu onse ataona zimenezi anafuwula mwachimwemwe ndipo anaweramitsa nkhope zawo pansi.
I wyszedł ogień sprzed PANA, i strawił na ołtarzu ofiarę całopalną oraz tłuszcz. A gdy cały lud to ujrzał, krzyknął z radości i upadł na twarz.