< Levitiko 9 >

1 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Mose anayitana Aaroni, ana ake ndi akuluakulu a Aisraeli.
Le huitième jour, Moïse appela Aaron et ses fils, et les anciens d'Israël;
2 Ndipo anawuza Aaroni kuti, “Tenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yako yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza. Zonsezi zikhale zopanda chilema ndipo uzipereke pamaso pa Yehova.
Et il dit à Aaron: Prends un jeune veau pour le sacrifice pour le péché, et un bélier pour l'holocauste, l'un et l'autre sans défaut, et offre-les devant l'Éternel.
3 Kenaka uwawuze Aisraeli kuti, ‘Tengani mbuzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo. Mutengenso mwana wangʼombe ndi mwana wankhosa. Zonsezi zikhale za chaka chimodzi ndi zopanda chilema kuti zikhale nsembe yopsereza.
Et tu parleras aux enfants d'Israël, en disant: Prenez un bouc pour le sacrifice pour le péché; un veau et un agneau sans défaut, âgés d'un an, pour l'holocauste;
4 Mutengenso ngʼombe yayimuna ndi nkhosa yayimuna kuti zikhale nsembe yachiyanjano zoti ziperekedwe pamaso pa Yehova. Pamodzi ndi izi mubwerenso ndi nsembe yachakudya yosakaniza ndi mafuta pakuti lero Yehova akuonekerani.’”
Un taureau et un bélier pour le sacrifice de prospérités, pour sacrifier devant l'Éternel, et une offrande arrosée d'huile; car aujourd'hui l'Éternel vous apparaîtra.
5 Anthu anatenga zonse zimene Mose analamula nabwera nazo pa khomo la tenti ya msonkhano. Gululo linasendera pafupi ndi kuyima pamaso pa Yehova.
Ils amenèrent donc devant le tabernacle d'assignation ce que Moïse avait commandé; et toute l'assemblée s'approcha, et se tint devant l'Éternel.
6 Tsono Mose anati, “Izi ndi zimene Yehova walamula kuti muchite kuti ulemerero wa Yehova ukuonekereni.”
Et Moïse dit: Voici ce que l'Éternel a commandé, faites-le, et la gloire de l'Éternel vous apparaîtra.
7 Pambuyo pake Mose anawuza Aaroni kuti, “Sendera pafupi ndi guwa ndipo upereka nsembe yako yopepesera machimo ndi nsembe yako yopsereza ndikuchita mwambo wopepesera machimo ako ndi machimo a anthu. Anthuwa apereke nsembe zawo zopepesera machimo monga momwe Yehova walamulira.”
Puis Moïse dit à Aaron: Approche-toi de l'autel; fais ton sacrifice pour le péché et ton holocauste, et fais l'expiation pour toi et pour le peuple; présente aussi l'offrande du peuple, et fais l'expiation pour lui, comme l'Éternel l'a commandé.
8 Choncho Aaroni anasendera pafupi ndi guwa, napha mwana wangʼombe uja kukhala nsembe yake yopepesera machimo.
Alors Aaron s'approcha de l'autel, et égorgea le veau de son sacrifice pour le péché.
9 Ana a Aaroni anabwera ndi magazi kwa Aaroni ndipo iye anaviyika chala chake mʼmagaziwo, nawapaka pa nyanga za guwa. Magazi wotsalawo anawathira pa tsinde la guwalo.
Et les fils d'Aaron lui présentèrent le sang; il trempa son doigt dans le sang, en mit sur les cornes de l'autel, et répandit le sang au pied de l'autel.
10 Kenaka anatentha paguwapo, mafuta, impsyo pamodzi ndi mafuta amene amakuta chiwindi ngati nsembe yopepesera machimoyo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
Et il fit fumer sur l'autel la graisse, les rognons, et la membrane qui recouvre le foie de la victime pour le péché, comme l'Éternel l'avait commandé à Moïse.
11 Koma nyama ndi chikopa anazitenthera kunja kwa msasa.
Mais il brûla au feu, hors du camp, la chair et la peau.
12 Kenaka anapha nsembe yopsereza. Ana a Aaroni atabwera ndi magazi kwa iye, Aaroniyo anawawaza mbali zonse za guwa.
Ensuite il égorgea l'holocauste. Les fils d'Aaron lui présentèrent le sang, et il le répandit sur l'autel tout autour.
13 Ana akewo anamupatsa nyama yoduladula ya nsembe yopsereza ija pamodzi ndi mutu ndipo anazitentha pa guwa.
Ils lui présentèrent aussi l'holocauste, coupé par morceaux, et la tête, et il les fit fumer sur l'autel.
14 Aaroni anatsuka matumbo ndi miyendo nazitentha pa guwa pamodzi ndi nsembe yopsereza ija.
Puis il lava les entrailles et les jambes, et il les fit fumer sur l'holocauste à l'autel.
15 Kenaka Aaroni anapereka zopereka za anthuwo. Anatenga mbuzi yopepesera machimo a anthuwo, yopereka chifukwa cha tchimo, nayipha ndi kuyipereka kuti ikhale yopepesera machimo monga anachitira ndi nsembe yoyamba ija.
Il offrit aussi l'offrande du peuple. Il prit le bouc du sacrifice pour le péché qui était pour le peuple; il l'égorgea, et l'offrit pour le péché, comme le premier sacrifice;
16 Anabwera ndi nsembe yopsereza, nayipereka potsata mwambo wake.
Et il offrit l'holocauste, et le fit selon l'ordonnance.
17 Anabweranso ndi chopereka cha chakudya. Anatapa ufa dzanja limodzi ndi kutentha pa guwa, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa ija.
Ensuite il présenta l'offrande; il en remplit la paume de sa main, et la fit fumer sur l'autel, outre l'holocauste du matin.
18 Tsono Aaroni anapha ngʼombe ndi nkhosa yayimuna monga nsembe yachiyanjano ya anthu. Ana ake anamupatsira magazi ndipo anawawaza mbali zonse za guwa.
Il égorgea aussi le taureau et le bélier en sacrifice de prospérités pour le peuple. Les fils d'Aaron lui présentèrent le sang, et il le répandit sur l'autel tout autour.
19 Anamupatsiranso mafuta a ngʼombeyo ndi nkhosa yayimunayo: mchira wamafuta, mafuta wokuta matumbo, impsyo ndi mafuta wokuta chiwindi.
Ils lui présentèrent aussi la graisse du taureau et du bélier, la queue, ce qui couvre les entrailles, les rognons, et la membrane qui recouvre le foie;
20 Ana a Aaroni anayika mafutawo pa zidale. Pambuyo pake Aaroni anatentha mafutawo pa guwa lansembe.
Et ils mirent les graisses sur les poitrines, et il fit fumer les graisses sur l'autel;
21 Koma zidale ndi ntchafu ya kumanja Aaroni anaziweyula ngati chopereka choweyula pamaso pa Yehova.
Puis Aaron agita devant l'Éternel, en offrande, les poitrines et la jambe droite, comme Moïse l'avait commandé.
22 Kenaka Aaroni anakweza manja ake pa anthuwo nawadalitsa. Ndipo atatha kupereka nsembe yopepesera machimo, nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano, anatsika pa guwapo.
Et Aaron éleva ses mains vers le peuple, et le bénit; et il descendit, après avoir offert le sacrifice pour le péché, l'holocauste et le sacrifice de prospérités.
23 Ndipo Mose pamodzi ndi Aaroni analowa mu tenti ya msonkhano. Atatulukamo anadalitsa anthuwo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa anthu onse.
Alors Moïse et Aaron entrèrent dans le tabernacle d'assignation, puis ils sortirent et bénirent le peuple; et la gloire de l'Éternel apparut à tout le peuple:
24 Pomwepo moto unatuluka pamaso pa Yehova niwutentha nsembe zopsereza ndi mafuta zimene zinali pa guwa. Anthu onse ataona zimenezi anafuwula mwachimwemwe ndipo anaweramitsa nkhope zawo pansi.
Un feu sortit de devant l'Éternel, et consuma sur l'autel l'holocauste et les graisses; et tout le peuple le vit, et ils poussèrent des cris de joie, et se jetèrent sur leurs faces.

< Levitiko 9 >