< Levitiko 8 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
RAB Musa'ya şöyle dedi:
2 “Tenga Aaroni ndi ana ake, zovala zawo, mafuta wodzozera, ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo, nkhosa ziwiri zazimuna ndi dengu la buledi wopanda yisiti,
“Harun'la oğullarını, kâhin giysilerini, mesh yağını, günah sunusu olarak sunulacak boğayı, iki koçu ve mayasız ekmek sepetini Buluşma Çadırı'nın giriş bölümüne getir. Bütün topluluğu da oraya çağır.”
3 ndipo usonkhanitse gulu la anthu pa khomo la tenti ya msonkhano.”
4 Mose anachita zomwe Yehova anamulamula ndipo gulu la anthu linasonkhana pa khomo la tenti ya msonkhano.
Musa RAB'bin buyruğunu yerine getirdi. Herkes Buluşma Çadırı'nın önünde toplandı.
5 Mose anawuza gulu la anthuwo kuti, “Izi ndi zimene Yehova walamulira kuti zichitike.”
Musa topluluğa, “Şimdi RAB'bin buyruğunu yerine getireceğim” dedi.
6 Pamenepo Mose anabwera ndi Aaroni ndi ana ake nawasambitsa ndi madzi.
Harun'la oğullarını öne çıkarıp yıkadı.
7 Anamuveka Aaroni mwinjiro, ndi kumumanga lamba mʼchiwuno. Anamuvekanso mkanjo wa efodi ndi efodiyo. Anamangira lamba efodiyo amene analukidwa mwaluso uja, motero efodiyo analimba mʼchiwunomo.
Harun'a mintanı giydirdi, beline kuşağı bağladı, üzerine kaftanı, onun üzerine de efodu giydirdi. Ustaca dokunmuş şeridiyle efodu bağladı.
8 Anamuvekanso chovala chapachifuwa ndipo mʼchovalacho anayikamo Urimu ndi Tumimu.
Üzerine göğüslüğü taktı, göğüslüğün içine Urim ile Tummim'i koydu.
9 Kenaka anamuveka Aaroniyo nduwira kumutu ndipo patsogolo pa nduwirayo anayikapo duwa lagolide, chizindikiro chopatulika monga momwe Yehova analamulira Mose.
Başına sarığı sardı, ön kısmına kutsal tacı, altın levhayı koydu. Musa her şeyi RAB'bin buyurduğu gibi yaptı.
10 Pamenepo Mose anatenga mafuta wodzozera nadzoza tenti ya msonkhano pamodzi ndi zonse zimene zinali mʼmenemo, ndipo potero anazipatula.
Sonra mesh yağını aldı, Tanrı'nın Konutu'nu ve içindeki her şeyi meshederek kutsal kıldı.
11 Anawaza mafuta ena pa guwa kasanu ndi kawiri, nalidzoza guwalo pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso beseni ndi tsinde lake, nazipatula.
Yağı yedi kez sunağın üzerine serpti; sunağı, sunağın bütün aletlerini, kazanı ve ayaklıklarını kutsal kılmak için meshetti.
12 Anathira mafuta wodzozera ena pamutu pa Aaroni ndipo anamudzoza ndi kumupatula.
Harun'u kutsal kılmak için başına yağ dökerek meshetti.
13 Kenaka anabwera ndi ana a Aaroni. Anawaveka minjiro, ndi kuwamanga malamba mʼchiwuno ndi kuwaveka nduwira kumutu monga momwe Yehova analamulira Mose.
Harun'un oğullarını öne çıkardı, onlara mintan giydirdi, bellerine kuşak bağladı, başlarına başlık koydu. Musa her şeyi RAB'bin buyurduğu gibi yaptı.
14 Kenaka Mose anabwera ndi ngʼombe yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, ndipo Aaroni ndi ana ake anasanjika manja awo pamutu pa ngʼombeyo.
Sonra günah sunusu olarak sunulacak boğayı getirdi. Harun'la oğulları ellerini boğanın başına koydular.
15 Mose anapha ngʼombeyo, ndi kutenga magazi ena angʼombeyo ndi kupaka ndi chala chake pa nyanga zaguwa lansembe, naliyeretsa. Magazi otsalawo anawakhuthulira pa tsinde laguwalo. Motero anachita mwambo wopepesera machimo.
Musa boğayı kesti. Sunağı pak kılmak için kanını parmağıyla sunağın boynuzlarına çepeçevre sürdü. Artan kanı sunağın dibine döktü. Böylece sunağı arındırıp kutsal kıldı.
16 Mose anatenganso mafuta onse okuta matumbo, mafuta ophimba chiwindi, ndiponso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake, nazitentha pa guwapo.
Musa hayvanın bağırsak ve işkembe yağlarını, karaciğer perdesini, böbreklerini ve böbrek yağlarını sunağın üzerinde yaktı.
17 Koma nyama yangʼombeyo, chikopa chake ndi matumbo ake anaziwotcha kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
Boğanın geri kalan kısmını da –derisini, etini, gübresini– ordugahın dışında yaktı. Musa her şeyi RAB'bin buyurduğu gibi yaptı.
18 Kenaka anabwera ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopsereza, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
Sonra yakmalık sunu olarak sunulacak koçu getirdi. Harun'la oğulları ellerini koçun başına koydular.
19 Ndipo Mose anapha nkhosayo ndi kuwaza magazi ake mbali zonse zaguwalo.
Musa koçu kesti, kanını sunağın her yanına döktü.
20 Anayidula nkhosayo nthulinthuli ndipo anatentha mutu wake, nthulizo ndi mafuta.
Koçu parçalara ayırıp parçaları, başını ve iç yağını yaktı.
21 Anatsuka matumbo ake ndi miyendo yake, ndi kutentha nkhosa yonseyo pa guwa lansembe kuti ikhale nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yachakudya yoperekedwa kwa Yehova monga Yehovayo analamulira Mose.
Bağırsaklarını, işkembesini, ayaklarını yıkadı ve koçun tümünü sunağın üzerinde yaktı. Bu bir yakmalık sunu, RAB'bi hoşnut eden koku, yakılan sunuydu. Musa her şeyi RAB'bin buyurduğu gibi yaptı.
22 Kenaka Mose anapereka nkhosa yayimuna ina pamwambo wodzoza ansembe, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
Sonra öteki koçu, atanma sunusu olarak sunulacak koçu getirdi. Harun'la oğulları ellerini koçun başına koydular.
23 Mose anayipha nkhosayo ndipo anatenga magazi ake ena ndi kupaka ndewere za khutu la kudzanja lamanja la Aaroni, pa chala chake chachikulu cha kudzanja lamanja, ndi pa chala chake chachikulu cha phazi lakumanja.
Musa koçu kesti. Kanını Harun'un sağ kulak memesine, sağ elinin ve sağ ayağının baş parmaklarına sürdü.
24 Pambuyo pake Mose anabwera ndi ana aamuna a Aaroni ndi kupaka magazi pa ndewere za makutu awo akumanja, pa zala zawo zazikulu za dzanja lamanja, ndiponso pa zala zawo zazikulu za kuphazi lakumanja. Kenaka iye anawaza magazi otsalawo mbali zonse za guwalo.
Sonra Harun'un oğullarını öne çıkardı. Onların da sağ kulak memelerine, sağ ellerinin ve ayaklarının baş parmaklarına kan sürdü. Artan kanı sunağın her yanına döktü.
25 Anatenganso mafuta ake, mafuta a ku mchira wake, mafuta okuta matumbo, mafuta okuta chiwindi, impsyo zonse ziwiri ndi mafuta ake ndiponso ntchafu yakumanja.
Hayvanın yağını, kuyruk yağını, bağırsak ve işkembe yağlarını, karaciğer perdesini, böbreklerini, böbrek yağlarını ve sağ budunu aldı.
26 Ndipo mʼdengu la buledi wopanda yisiti limene linali pamaso pa Yehova, anatengamo buledi mmodzi, buledi mmodzi wokhala ndi mafuta a olivi, ndi buledi wopyapyala mmodzi. Zonsezi anaziyika pa mafuta aja ndi pa ntchafu ya ku dzanja lamanja ija.
Sonra RAB'bin huzurunda bulunan mayasız ekmek sepetinden bir ekmek, yağlı pide ve yufka alıp hayvanın yağlarının ve sağ budunun üzerine koydu.
27 Mose anapereka zonsezi mʼmanja mwa Aaroni ndi ana ake amene anazipereka kwa Yehova kuti zikhale nsembe yoweyula.
Hepsini Harun'la oğullarının eline verdi. Bunları RAB'bin huzurunda sallamalık sunu olarak salladı.
28 Kenaka Mose anazitenga mʼmanja mwawo ndipo anazipsereza pa guwa lansembe pamwamba penipeni pamodzi ndi nsembe yopsereza ija kuti ikhale nsembe yopereka pamwambo wodzoza ansembe, kuti ipereke fungo lokoma, chopereka chachakudya kwa Yehova.
Sonra ellerinden alıp sunakta yakmalık sununun üzerinde yaktı. Bunlar atanma sunusu, RAB'bi hoşnut eden koku ve RAB için yakılan sunuydu.
29 Mose anatenga chidale cha nkhosa yayimuna, chomwe ndi gawo lake pamwambo wodzoza ansembe, ndipo anachiweyula pamaso pa Yehova kuti chikhale nsembe yoweyula monga momwe Yehova analamulira Mose.
Bundan sonra Musa döşü aldı ve sallamalık sunu olarak RAB'bin huzurunda salladı. Atanma sunusu olarak sunulan koçtan Musa'nın payına düşen buydu. Musa her şeyi RAB'bin buyurduğu gibi yaptı.
30 Kenaka Mose anatenga mafuta wodzozera ansembe ndi magazi amene anali pa guwa nawaza pa Aaroni ndi zovala zake ndiponso ana ake aja ndi zovala zawo. Motero Mose anapatula Aaroni ndi zovala zake, ndiponso ana ake ndi zovala zawo.
Musa mesh yağını ve sunağın üzerindeki kanı alıp Harun'la oğullarının ve giysilerinin üzerine serpti. Böylece Harun'u, oğullarını ve giysilerini kutsal kılmış oldu.
31 Mose anawuza Aaroni ndi ana ake kuti, “Phikani nyamayo pa khomo la tenti ya msonkhano, ndipo mudyere pomwepo pamodzi ndi buledi amene ali mʼdengu la zopereka za pamwambo wodzoza ansembe monga Yehova analamulira kuti, ‘Aaroni ndi ana ake azidya zimenezi.’
Sonra Harun'la oğullarına, “Eti Buluşma Çadırı'nın giriş bölümünde haşlayın” dedi, “‘Eti Harun'la oğulları yiyecek’ diye buyurmuştum. Atanma sunularının bulunduğu sepetteki ekmekle birlikte onu orada yiyin.
32 Ndipo nyama ndi buledi zotsalazo, muziwotche.
Etten ve ekmekten artanı yakın.
33 Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano kwa masiku asanu ndi awiri mpaka masiku amwambo wokudzozani unsembe atatha, pakuti mwambowu ndi wa masiku asanu ndi awiri.
Atanma günleriniz doluncaya kadar, yedi gün boyunca Buluşma Çadırı'nın giriş bölümünden ayrılmayın. Çünkü atanmanız yedi gün sürecek.
34 Zimene zachitika lerozi analamula ndi Yehova kuti zichitike ngati nsembe yopepesera machimo anu.
Bugün yapılan her şeyi günahlarınızı bağışlatmak için RAB buyurdu.
35 Muzikhala pa khomo la tenti ya msonkhano usana ndi usiku kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo muzichita zimene Yehova wakulamulani kuti musafe, pakuti zimenezi ndi zomwe Yehova wandilamulira.”
Yedi gün boyunca gece gündüz Buluşma Çadırı'nın giriş bölümünde bekleyecek, RAB'bin buyruğunu yerine getireceksiniz. Öyle ki, ölmeyesiniz. Bana böyle buyruk verildi.”
36 Choncho Aaroni ndi ana ake anachita zonse zimene Yehova analamula kudzera mwa Mose.
Böylece Harun'la oğulları RAB'bin Musa aracılığıyla verdiği bütün buyrukları yerine getirdiler.

< Levitiko 8 >