< Levitiko 8 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
Gospod je spregovoril Mojzesu, rekoč:
2 “Tenga Aaroni ndi ana ake, zovala zawo, mafuta wodzozera, ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo, nkhosa ziwiri zazimuna ndi dengu la buledi wopanda yisiti,
»Vzemi Arona in z njim njegove sinove, obleke, mazilno olje, bikca za daritev za greh, dva ovna in košaro nekvašenega kruha,
3 ndipo usonkhanitse gulu la anthu pa khomo la tenti ya msonkhano.”
in zberi skupaj ves zbor k vratom šotorskega svetišča skupnosti.«
4 Mose anachita zomwe Yehova anamulamula ndipo gulu la anthu linasonkhana pa khomo la tenti ya msonkhano.
Mojzes je storil, kakor mu je Gospod zapovedal in zbor je bil zbran skupaj k vratom šotorskega svetišča skupnosti.
5 Mose anawuza gulu la anthuwo kuti, “Izi ndi zimene Yehova walamulira kuti zichitike.”
Mojzes je rekel skupnosti: »To je stvar, ki jo je Gospod zapovedal, da se stori.«
6 Pamenepo Mose anabwera ndi Aaroni ndi ana ake nawasambitsa ndi madzi.
Mojzes je privedel Arona in njegove sinove ter jih umil z vodo.
7 Anamuveka Aaroni mwinjiro, ndi kumumanga lamba mʼchiwuno. Anamuvekanso mkanjo wa efodi ndi efodiyo. Anamangira lamba efodiyo amene analukidwa mwaluso uja, motero efodiyo analimba mʼchiwunomo.
Nadel mu je plašč, ga opasal s pasom, ga ogrnil s svečanim oblačilom, nanj položil efód in ga opasal s skrbno narejenim pasom efóda in ga s tem prevezal.
8 Anamuvekanso chovala chapachifuwa ndipo mʼchovalacho anayikamo Urimu ndi Tumimu.
Nanj je dal naprsnik. V naprsnik je položil tudi Urím in Tumím.
9 Kenaka anamuveka Aaroniyo nduwira kumutu ndipo patsogolo pa nduwirayo anayikapo duwa lagolide, chizindikiro chopatulika monga momwe Yehova analamulira Mose.
Turban je položil na njegovo glavo; tudi na turban, torej na njegov sprednji del, je položil zlato ploščico, sveto krono; kakor je Gospod zapovedal Mojzesu.
10 Pamenepo Mose anatenga mafuta wodzozera nadzoza tenti ya msonkhano pamodzi ndi zonse zimene zinali mʼmenemo, ndipo potero anazipatula.
Mojzes je vzel mazilno olje in mazilil šotorsko svetišče in vse, kar je bilo v njem in to posvetil.
11 Anawaza mafuta ena pa guwa kasanu ndi kawiri, nalidzoza guwalo pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso beseni ndi tsinde lake, nazipatula.
Od tega je sedemkrat poškropil po oltarju in mazilil oltar ter vse njegove posode, tako [okrogel] umivalnik kot njegovo vznožje, da jih posvéti.
12 Anathira mafuta wodzozera ena pamutu pa Aaroni ndipo anamudzoza ndi kumupatula.
Na Aronovo glavo je izlil mazilno olje in ga mazilil, da ga posvéti.
13 Kenaka anabwera ndi ana a Aaroni. Anawaveka minjiro, ndi kuwamanga malamba mʼchiwuno ndi kuwaveka nduwira kumutu monga momwe Yehova analamulira Mose.
Mojzes je privedel Aronove sinove, nanje položil plašče, jih opasal s pasovi in nanje položil klobučke; kakor je Gospod zapovedal Mojzesu.
14 Kenaka Mose anabwera ndi ngʼombe yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, ndipo Aaroni ndi ana ake anasanjika manja awo pamutu pa ngʼombeyo.
Privedel je bikca za daritev za greh. Aron in njegovi sinovi so svoje roke položili na glavo bikca daritve za greh.
15 Mose anapha ngʼombeyo, ndi kutenga magazi ena angʼombeyo ndi kupaka ndi chala chake pa nyanga zaguwa lansembe, naliyeretsa. Magazi otsalawo anawakhuthulira pa tsinde laguwalo. Motero anachita mwambo wopepesera machimo.
Zaklal ga je in Mojzes je vzel kri in jo s svojim prstom dal vsenaokrog na rogove oltarja in očistil oltar in kri izlil ob vznožju oltarja in ga posvetil, da bi na njem opravil pobotanje.
16 Mose anatenganso mafuta onse okuta matumbo, mafuta ophimba chiwindi, ndiponso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake, nazitentha pa guwapo.
Vzel je vso tolščo, ki je bila na drobovju, opno nad jetri, dve ledvici, njuno tolščo in Mojzes je to sežgal na oltarju.
17 Koma nyama yangʼombeyo, chikopa chake ndi matumbo ake anaziwotcha kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
Toda bikca, njegovo kožo, njegovo meso in njegov iztrebek je z ognjem sežgal zunaj tabora; kakor je Gospod zapovedal Mojzesu.
18 Kenaka anabwera ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopsereza, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
In privedel je ovna za žgalno daritev, Aron in njegovi sinovi pa so svoje roke položili ovnu na glavo.
19 Ndipo Mose anapha nkhosayo ndi kuwaza magazi ake mbali zonse zaguwalo.
Zaklal ga je in Mojzes je kri poškropil naokoli po oltarju.
20 Anayidula nkhosayo nthulinthuli ndipo anatentha mutu wake, nthulizo ndi mafuta.
Ovna je razrezal na koščke in Mojzes je sežgal glavo, koščke in tolščo.
21 Anatsuka matumbo ake ndi miyendo yake, ndi kutentha nkhosa yonseyo pa guwa lansembe kuti ikhale nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yachakudya yoperekedwa kwa Yehova monga Yehovayo analamulira Mose.
Drobovje in noge je opral v vodi in Mojzes je celotnega ovna sežgal na oltarju. To je bila žgalna daritev v prijeten vonj in ognjena daritev Gospodu; kakor je Gospod zapovedal Mojzesu.
22 Kenaka Mose anapereka nkhosa yayimuna ina pamwambo wodzoza ansembe, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
Privedel je drugega ovna, ovna uméstitve, Aron in njegovi sinovi pa so svoje roke položili ovnu na glavo.
23 Mose anayipha nkhosayo ndipo anatenga magazi ake ena ndi kupaka ndewere za khutu la kudzanja lamanja la Aaroni, pa chala chake chachikulu cha kudzanja lamanja, ndi pa chala chake chachikulu cha phazi lakumanja.
In on ga je zaklal. Mojzes je vzel od njegove krvi, jo pomazal na konico Aronovega desnega ušesa, na palec njegove desne roke in na palec njegovega desnega stopala.
24 Pambuyo pake Mose anabwera ndi ana aamuna a Aaroni ndi kupaka magazi pa ndewere za makutu awo akumanja, pa zala zawo zazikulu za dzanja lamanja, ndiponso pa zala zawo zazikulu za kuphazi lakumanja. Kenaka iye anawaza magazi otsalawo mbali zonse za guwalo.
Privedel je Aronove sinove in Mojzes je dal od krvi na konico njihovih desnih ušes in na palce njihovih desnih rok in na palce njihovih desnih stopal; in Mojzes je kri poškropil naokoli po oltarju.
25 Anatenganso mafuta ake, mafuta a ku mchira wake, mafuta okuta matumbo, mafuta okuta chiwindi, impsyo zonse ziwiri ndi mafuta ake ndiponso ntchafu yakumanja.
Vzel je tolščo, tolsti rep, vso tolščo, ki je bila na drobovju, opno nad jetri, dve ledvici in njuno tolščo ter desno pleče.
26 Ndipo mʼdengu la buledi wopanda yisiti limene linali pamaso pa Yehova, anatengamo buledi mmodzi, buledi mmodzi wokhala ndi mafuta a olivi, ndi buledi wopyapyala mmodzi. Zonsezi anaziyika pa mafuta aja ndi pa ntchafu ya ku dzanja lamanja ija.
Iz košare nekvašenega kruha, ki je bila pred Gospodom, je vzel en nekvašen kolač, kolač oljnatega kruha in en vafelj ter jih položil na tolščo in na desno pleče.
27 Mose anapereka zonsezi mʼmanja mwa Aaroni ndi ana ake amene anazipereka kwa Yehova kuti zikhale nsembe yoweyula.
Vse to je dal na Aronove roke in na roke Aronovih sinov in jih majal za majalno daritev pred Gospodom.
28 Kenaka Mose anazitenga mʼmanja mwawo ndipo anazipsereza pa guwa lansembe pamwamba penipeni pamodzi ndi nsembe yopsereza ija kuti ikhale nsembe yopereka pamwambo wodzoza ansembe, kuti ipereke fungo lokoma, chopereka chachakudya kwa Yehova.
Mojzes jih je vzel iz njihovih rok in jih sežgal na oltarju nad žgalno daritvijo. To so bile uméstitvene [daritve] za prijeten vonj. To je ognjena daritev Gospodu.
29 Mose anatenga chidale cha nkhosa yayimuna, chomwe ndi gawo lake pamwambo wodzoza ansembe, ndipo anachiweyula pamaso pa Yehova kuti chikhale nsembe yoweyula monga momwe Yehova analamulira Mose.
Mojzes je vzel prsi in jih majal za majalno daritev pred Gospodom, kajti od ovna uméstitve je bil to Mojzesov delež; kakor je Gospod zapovedal Mojzesu.
30 Kenaka Mose anatenga mafuta wodzozera ansembe ndi magazi amene anali pa guwa nawaza pa Aaroni ndi zovala zake ndiponso ana ake aja ndi zovala zawo. Motero Mose anapatula Aaroni ndi zovala zake, ndiponso ana ake ndi zovala zawo.
Mojzes je vzel od mazilnega olja in od krvi, ki je bila na oltarju in to poškropil na Arona, na njegove obleke, na njegove sinove in na obleke njegovih sinov z njim; in posvetil je Arona, njegove obleke, njegove sinove in obleke njegovih sinov z njim.
31 Mose anawuza Aaroni ndi ana ake kuti, “Phikani nyamayo pa khomo la tenti ya msonkhano, ndipo mudyere pomwepo pamodzi ndi buledi amene ali mʼdengu la zopereka za pamwambo wodzoza ansembe monga Yehova analamulira kuti, ‘Aaroni ndi ana ake azidya zimenezi.’
Mojzes je rekel Aronu in njegovim sinovim: »Meso skuhajte pri vratih šotorskega svetišča skupnosti. Tam ga pojejte s kruhom, ki je v košari uméstitvenih [daritev], kakor sem zapovedal, govoreč: ›Aron in njegovi sinovi bodo to jedli.‹
32 Ndipo nyama ndi buledi zotsalazo, muziwotche.
To, kar pa ostane od mesa in od kruha, boste sežgali z ognjem.
33 Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano kwa masiku asanu ndi awiri mpaka masiku amwambo wokudzozani unsembe atatha, pakuti mwambowu ndi wa masiku asanu ndi awiri.
Sedem dni ne boste šli od vrat šotorskega svetišča skupnosti, dokler dnevi vaše uméstitve ne bodo končani, kajti sedem dni vas bo uméščal.
34 Zimene zachitika lerozi analamula ndi Yehova kuti zichitike ngati nsembe yopepesera machimo anu.
Kakor je storil ta dan, tako je Gospod zapovedal storiti, da za vas opravi spravo.
35 Muzikhala pa khomo la tenti ya msonkhano usana ndi usiku kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo muzichita zimene Yehova wakulamulani kuti musafe, pakuti zimenezi ndi zomwe Yehova wandilamulira.”
Zato boste sedem dni, dan in noč, ostajali pri vratih šotorskega svetišča skupnosti in se boste držali Gospodovega naročila, da ne umrete, kajti tako mi je bilo zapovedano.«
36 Choncho Aaroni ndi ana ake anachita zonse zimene Yehova analamula kudzera mwa Mose.
Tako so Aron in njegovi sinovi storili vse stvari, ki jih je Gospod zapovedal po Mojzesovi roki.