< Levitiko 8 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
Et l'Éternel parla à Moïse en ces termes:
2 “Tenga Aaroni ndi ana ake, zovala zawo, mafuta wodzozera, ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo, nkhosa ziwiri zazimuna ndi dengu la buledi wopanda yisiti,
Prends Aaron et ses fils avec lui et les costumes et l'huile d'onction et le taureau d'expiation et les deux béliers et la corbeille des azymes
3 ndipo usonkhanitse gulu la anthu pa khomo la tenti ya msonkhano.”
et convoque toute l'Assemblée à l'entrée de la Tente du Rendez-vous.
4 Mose anachita zomwe Yehova anamulamula ndipo gulu la anthu linasonkhana pa khomo la tenti ya msonkhano.
Et Moïse exécuta l'ordre de l'Éternel, et l'Assemblée se réunit à l'entrée de la Tente du Rendez-vous.
5 Mose anawuza gulu la anthuwo kuti, “Izi ndi zimene Yehova walamulira kuti zichitike.”
Alors Moïse dit à l'Assemblée: Voici ce que l'Éternel a commandé de faire.
6 Pamenepo Mose anabwera ndi Aaroni ndi ana ake nawasambitsa ndi madzi.
Et Moïse amena Aaron et ses fils et fit leurs ablutions avec l'eau,
7 Anamuveka Aaroni mwinjiro, ndi kumumanga lamba mʼchiwuno. Anamuvekanso mkanjo wa efodi ndi efodiyo. Anamangira lamba efodiyo amene analukidwa mwaluso uja, motero efodiyo analimba mʼchiwunomo.
et il lui mit la Tunique et le ceignit de la Ceinture et le revêtit de la Robe et lui mit l'Ephod et il le ceignit de la ceinture de l'Ephod dont il le revêtit.
8 Anamuvekanso chovala chapachifuwa ndipo mʼchovalacho anayikamo Urimu ndi Tumimu.
Et il lui mit le Pectoral, et plaça sur le Pectoral l'Urim et le Thummim.
9 Kenaka anamuveka Aaroniyo nduwira kumutu ndipo patsogolo pa nduwirayo anayikapo duwa lagolide, chizindikiro chopatulika monga momwe Yehova analamulira Mose.
Et il lui couvrit la tête du Turban sur le devant duquel il fixa la Plaque d'or, diadème sacré, comme l'Éternel l'avait ordonné à Moïse.
10 Pamenepo Mose anatenga mafuta wodzozera nadzoza tenti ya msonkhano pamodzi ndi zonse zimene zinali mʼmenemo, ndipo potero anazipatula.
Et Moïse prit l'huile d'onction et oignit la Résidence et toutes les choses qui y sont, et ainsi, les consacra;
11 Anawaza mafuta ena pa guwa kasanu ndi kawiri, nalidzoza guwalo pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso beseni ndi tsinde lake, nazipatula.
et il en fit sept aspersions contre l'Autel, et il oignit l'Autel et tous ses ustensiles, et le Bassin et son support, afin de les consacrer.
12 Anathira mafuta wodzozera ena pamutu pa Aaroni ndipo anamudzoza ndi kumupatula.
Et il répandit de l'huile d'onction sur la tête d'Aaron et l'oignit afin de le consacrer.
13 Kenaka anabwera ndi ana a Aaroni. Anawaveka minjiro, ndi kuwamanga malamba mʼchiwuno ndi kuwaveka nduwira kumutu monga momwe Yehova analamulira Mose.
Et Moïse fit avancer les fils d'Aaron et les revêtit de tuniques et les ceignit de la ceinture, et leur attacha leurs bonnets, comme l'Éternel l'avait ordonné à Moïse.
14 Kenaka Mose anabwera ndi ngʼombe yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, ndipo Aaroni ndi ana ake anasanjika manja awo pamutu pa ngʼombeyo.
Et il fit amener le taureau expiatoire, et Aaron et ses fils posèrent leurs mains sur la tête du taureau expiatoire.
15 Mose anapha ngʼombeyo, ndi kutenga magazi ena angʼombeyo ndi kupaka ndi chala chake pa nyanga zaguwa lansembe, naliyeretsa. Magazi otsalawo anawakhuthulira pa tsinde laguwalo. Motero anachita mwambo wopepesera machimo.
Et Moïse l'égorgea, et prit le sang, et de son doigt il en mit aux cornes de l'Autel tout autour et fit la purification de l'Autel, et le [reste du] sang il le répandit au pied de l'Autel qu'il consacra pour qu'on pût y faire la propitiation.
16 Mose anatenganso mafuta onse okuta matumbo, mafuta ophimba chiwindi, ndiponso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake, nazitentha pa guwapo.
Et il prit toute la graisse qui enveloppe les intestins, et le grand lobe du foie et les deux reins et leur graisse, et Moïse les fit fumer sur l'Autel.
17 Koma nyama yangʼombeyo, chikopa chake ndi matumbo ake anaziwotcha kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
Puis il brûla au feu en dehors du camp le taureau et sa peau et sa chair et sa fiente, comme l'Éternel l'avait ordonné à Moïse.
18 Kenaka anabwera ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopsereza, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
Et il offrit le bélier de l'holocauste, et Aaron et ses fils posèrent leurs mains sur la tête du bélier.
19 Ndipo Mose anapha nkhosayo ndi kuwaza magazi ake mbali zonse zaguwalo.
Et Moïse l'égorgea et en répandit le sang autour de l'Autel.
20 Anayidula nkhosayo nthulinthuli ndipo anatentha mutu wake, nthulizo ndi mafuta.
Et il détailla le bélier en ses quartiers, et Moïse fit fumer sur l'Autel la tête, les quartiers et la graisse.
21 Anatsuka matumbo ake ndi miyendo yake, ndi kutentha nkhosa yonseyo pa guwa lansembe kuti ikhale nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yachakudya yoperekedwa kwa Yehova monga Yehovayo analamulira Mose.
Et il lava dans l'eau la fressure et les jambes, et Moïse, fit fumer le bélier entier sur l'Autel, en holocauste, en parfum agréable, en sacrifice igné à l'Éternel, comme l'Éternel l'avait ordonné à Moïse.
22 Kenaka Mose anapereka nkhosa yayimuna ina pamwambo wodzoza ansembe, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
Et il offrit le second bélier, le bélier de l'installation, et Aaron et ses fils posèrent leurs mains sur la tête du bélier.
23 Mose anayipha nkhosayo ndipo anatenga magazi ake ena ndi kupaka ndewere za khutu la kudzanja lamanja la Aaroni, pa chala chake chachikulu cha kudzanja lamanja, ndi pa chala chake chachikulu cha phazi lakumanja.
Et Moïse l'égorgea et prit de son sang et en mit au bout de l'oreille droite d'Aaron et au pouce droit et au grand orteil droit.
24 Pambuyo pake Mose anabwera ndi ana aamuna a Aaroni ndi kupaka magazi pa ndewere za makutu awo akumanja, pa zala zawo zazikulu za dzanja lamanja, ndiponso pa zala zawo zazikulu za kuphazi lakumanja. Kenaka iye anawaza magazi otsalawo mbali zonse za guwalo.
Et il fit approcher les fils d'Aaron, et Moïse leur mit de ce sang au bout de l'oreille droite, au pouce droit et au grand orteil droit; et Moïse répandit le [reste du] sang autour de l'Autel.
25 Anatenganso mafuta ake, mafuta a ku mchira wake, mafuta okuta matumbo, mafuta okuta chiwindi, impsyo zonse ziwiri ndi mafuta ake ndiponso ntchafu yakumanja.
Et il prit la graisse et la queue grasse et toute la graisse qui enveloppe les intestins et le grand lobe du foie et les deux reins et leur graisse et l'éclanche droite;
26 Ndipo mʼdengu la buledi wopanda yisiti limene linali pamaso pa Yehova, anatengamo buledi mmodzi, buledi mmodzi wokhala ndi mafuta a olivi, ndi buledi wopyapyala mmodzi. Zonsezi anaziyika pa mafuta aja ndi pa ntchafu ya ku dzanja lamanja ija.
et de la corbeille des azymes qui était devant l'Éternel il prit une galette azyme et une galette de pain avec de l'huile et une oublie qu'il posa sur les graisses et l'éclanche droite;
27 Mose anapereka zonsezi mʼmanja mwa Aaroni ndi ana ake amene anazipereka kwa Yehova kuti zikhale nsembe yoweyula.
et il mit le tout dans les mains d'Aaron et dans les mains de ses fils, et le brandit en oblation agitée devant l'Éternel.
28 Kenaka Mose anazitenga mʼmanja mwawo ndipo anazipsereza pa guwa lansembe pamwamba penipeni pamodzi ndi nsembe yopsereza ija kuti ikhale nsembe yopereka pamwambo wodzoza ansembe, kuti ipereke fungo lokoma, chopereka chachakudya kwa Yehova.
Et Moïse retira ces choses de leurs mains, et les fit fumer sur l'Autel, sur l'holocauste, comme sacrifice d'installation, en parfum agréable, en sacrifice igné à l'Éternel.
29 Mose anatenga chidale cha nkhosa yayimuna, chomwe ndi gawo lake pamwambo wodzoza ansembe, ndipo anachiweyula pamaso pa Yehova kuti chikhale nsembe yoweyula monga momwe Yehova analamulira Mose.
Et Moïse prit du bélier d'installation la poitrine et l'agita en oblation agitée devant l'Éternel, elle échut à Moïse pour sa part, comme l'Éternel l'avait ordonné à Moïse.
30 Kenaka Mose anatenga mafuta wodzozera ansembe ndi magazi amene anali pa guwa nawaza pa Aaroni ndi zovala zake ndiponso ana ake aja ndi zovala zawo. Motero Mose anapatula Aaroni ndi zovala zake, ndiponso ana ake ndi zovala zawo.
Et Moïse prit de l'huile d'onction et du sang qui était sur l'Autel et en fit jaillir sur Aaron et sur ses vêtements, sur ses fils et sur les vêtements de ses fils avec lui, et consacra ainsi Aaron et ses vêtements et ses fils, et les vêtements de ses fils avec lui.
31 Mose anawuza Aaroni ndi ana ake kuti, “Phikani nyamayo pa khomo la tenti ya msonkhano, ndipo mudyere pomwepo pamodzi ndi buledi amene ali mʼdengu la zopereka za pamwambo wodzoza ansembe monga Yehova analamulira kuti, ‘Aaroni ndi ana ake azidya zimenezi.’
Et Moïse dit à Aaron et à ses fils: Faites cuire la chair à l'entrée de la Tente du Rendez-vous et l'y mangez, ainsi que le pain contenu dans la corbeille d'installation, comme je l'ai prescrit en disant: Aaron et ses fils la mangeront;
32 Ndipo nyama ndi buledi zotsalazo, muziwotche.
et vous brûlerez au feu ce qui restera de la chair et du pain,
33 Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano kwa masiku asanu ndi awiri mpaka masiku amwambo wokudzozani unsembe atatha, pakuti mwambowu ndi wa masiku asanu ndi awiri.
et pendant sept jours vous ne sortirez pas de la porte de la Tente du Rendez-vous jusqu'à ce que les jours de votre installation soient accomplis; car votre installation doit durer sept jours.
34 Zimene zachitika lerozi analamula ndi Yehova kuti zichitike ngati nsembe yopepesera machimo anu.
Ce qu'on a fait aujourd'hui, l'Éternel a ordonné de le faire comme propitiation pour vous;
35 Muzikhala pa khomo la tenti ya msonkhano usana ndi usiku kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo muzichita zimene Yehova wakulamulani kuti musafe, pakuti zimenezi ndi zomwe Yehova wandilamulira.”
et vous resterez jour et nuit pendant sept jours à l'entrée de la Tente du Rendez-vous, et vous observerez ce que vous êtes tenus d'observer envers l'Éternel, afin que vous ne mouriez pas; car tel est l'ordre que j'ai reçu.
36 Choncho Aaroni ndi ana ake anachita zonse zimene Yehova analamula kudzera mwa Mose.
Et Aaron et ses fils se conformèrent en tout point à l'ordre que l'Éternel avait donné par Moïse.