< Levitiko 8 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahvé parla à Moïse, et dit:
2 “Tenga Aaroni ndi ana ake, zovala zawo, mafuta wodzozera, ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo, nkhosa ziwiri zazimuna ndi dengu la buledi wopanda yisiti,
« Prends avec lui Aaron et ses fils, les vêtements, l'huile d'onction, le taureau expiatoire, les deux béliers et la corbeille de pains sans levain,
3 ndipo usonkhanitse gulu la anthu pa khomo la tenti ya msonkhano.”
et rassemble toute l'assemblée à l'entrée de la tente de la Rencontre. »
4 Mose anachita zomwe Yehova anamulamula ndipo gulu la anthu linasonkhana pa khomo la tenti ya msonkhano.
Moïse fit ce que Yahvé lui avait ordonné; et l'assemblée se rassembla à l'entrée de la tente de la Rencontre.
5 Mose anawuza gulu la anthuwo kuti, “Izi ndi zimene Yehova walamulira kuti zichitike.”
Moïse dit à l'assemblée: « Voici ce que l'Éternel a ordonné de faire. »
6 Pamenepo Mose anabwera ndi Aaroni ndi ana ake nawasambitsa ndi madzi.
Moïse fit venir Aaron et ses fils, et les lava avec de l'eau.
7 Anamuveka Aaroni mwinjiro, ndi kumumanga lamba mʼchiwuno. Anamuvekanso mkanjo wa efodi ndi efodiyo. Anamangira lamba efodiyo amene analukidwa mwaluso uja, motero efodiyo analimba mʼchiwunomo.
Il lui mit la tunique, lui attacha la ceinture, le revêtit de la robe, lui mit l'éphod, et il attacha sur lui la bande de l'éphod, habilement tissée, et la lui fixa avec elle.
8 Anamuvekanso chovala chapachifuwa ndipo mʼchovalacho anayikamo Urimu ndi Tumimu.
Il plaça sur lui le pectoral. Il mit l'urim et le thummim dans le pectoral.
9 Kenaka anamuveka Aaroniyo nduwira kumutu ndipo patsogolo pa nduwirayo anayikapo duwa lagolide, chizindikiro chopatulika monga momwe Yehova analamulira Mose.
Il mit le turban sur sa tête. Il plaça la plaque d'or, la couronne sacrée, sur le devant du turban, comme l'avait ordonné l'Éternel à Moïse.
10 Pamenepo Mose anatenga mafuta wodzozera nadzoza tenti ya msonkhano pamodzi ndi zonse zimene zinali mʼmenemo, ndipo potero anazipatula.
Moïse prit l'huile d'onction, oignit le tabernacle et tout ce qui s'y trouvait, et les sanctifia.
11 Anawaza mafuta ena pa guwa kasanu ndi kawiri, nalidzoza guwalo pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso beseni ndi tsinde lake, nazipatula.
Il en fit sept fois l'aspersion sur l'autel, et il oignit l'autel et tous ses ustensiles, ainsi que le bassin et sa base, pour les sanctifier.
12 Anathira mafuta wodzozera ena pamutu pa Aaroni ndipo anamudzoza ndi kumupatula.
Il versa de l'huile d'onction sur la tête d'Aaron et l'oignit, afin de le sanctifier.
13 Kenaka anabwera ndi ana a Aaroni. Anawaveka minjiro, ndi kuwamanga malamba mʼchiwuno ndi kuwaveka nduwira kumutu monga momwe Yehova analamulira Mose.
Moïse fit venir les fils d'Aaron, les revêtit de tuniques, leur attacha des ceintures et leur mit des bandeaux, comme Yahvé l'avait ordonné à Moïse.
14 Kenaka Mose anabwera ndi ngʼombe yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, ndipo Aaroni ndi ana ake anasanjika manja awo pamutu pa ngʼombeyo.
Il amena le taureau du sacrifice pour le péché, et Aaron et ses fils posèrent leurs mains sur la tête du taureau du sacrifice pour le péché.
15 Mose anapha ngʼombeyo, ndi kutenga magazi ena angʼombeyo ndi kupaka ndi chala chake pa nyanga zaguwa lansembe, naliyeretsa. Magazi otsalawo anawakhuthulira pa tsinde laguwalo. Motero anachita mwambo wopepesera machimo.
Il l'égorgea; Moïse prit le sang et le mit avec son doigt autour des cornes de l'autel; il purifia l'autel, versa le sang au pied de l'autel et le sanctifia pour en faire l'expiation.
16 Mose anatenganso mafuta onse okuta matumbo, mafuta ophimba chiwindi, ndiponso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake, nazitentha pa guwapo.
Il prit toute la graisse qui était sur les entrailles, la couverture du foie, les deux rognons et leur graisse, et Moïse les brûla sur l'autel.
17 Koma nyama yangʼombeyo, chikopa chake ndi matumbo ake anaziwotcha kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
Mais le taureau, sa peau, sa viande et ses excréments, il les brûla au feu en dehors du camp, comme Yahvé l'avait ordonné à Moïse.
18 Kenaka anabwera ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopsereza, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
Il présenta le bélier de l'holocauste. Aaron et ses fils posèrent leurs mains sur la tête du bélier.
19 Ndipo Mose anapha nkhosayo ndi kuwaza magazi ake mbali zonse zaguwalo.
Il l'égorgea et Moïse fit aspersion du sang tout autour de l'autel.
20 Anayidula nkhosayo nthulinthuli ndipo anatentha mutu wake, nthulizo ndi mafuta.
Il coupa le bélier en morceaux, et Moïse brûla la tête, les morceaux et la graisse.
21 Anatsuka matumbo ake ndi miyendo yake, ndi kutentha nkhosa yonseyo pa guwa lansembe kuti ikhale nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yachakudya yoperekedwa kwa Yehova monga Yehovayo analamulira Mose.
Il lava à l'eau les entrailles et les jambes, et Moïse brûla le bélier tout entier sur l'autel. C'était un holocauste pour un parfum agréable. C'était un sacrifice consumé par le feu à Yahvé, comme Yahvé l'avait ordonné à Moïse.
22 Kenaka Mose anapereka nkhosa yayimuna ina pamwambo wodzoza ansembe, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
Il présenta l'autre bélier, le bélier de consécration. Aaron et ses fils posèrent leurs mains sur la tête du bélier.
23 Mose anayipha nkhosayo ndipo anatenga magazi ake ena ndi kupaka ndewere za khutu la kudzanja lamanja la Aaroni, pa chala chake chachikulu cha kudzanja lamanja, ndi pa chala chake chachikulu cha phazi lakumanja.
Il l'égorgea; Moïse prit un peu de son sang et en mit sur le bout de l'oreille droite d'Aaron, sur le pouce de sa main droite et sur le gros orteil de son pied droit.
24 Pambuyo pake Mose anabwera ndi ana aamuna a Aaroni ndi kupaka magazi pa ndewere za makutu awo akumanja, pa zala zawo zazikulu za dzanja lamanja, ndiponso pa zala zawo zazikulu za kuphazi lakumanja. Kenaka iye anawaza magazi otsalawo mbali zonse za guwalo.
Il fit venir les fils d'Aaron; Moïse mit un peu de sang sur le bout de leur oreille droite, sur le pouce de leur main droite et sur le gros orteil de leur pied droit; Moïse fit asperger le sang tout autour de l'autel.
25 Anatenganso mafuta ake, mafuta a ku mchira wake, mafuta okuta matumbo, mafuta okuta chiwindi, impsyo zonse ziwiri ndi mafuta ake ndiponso ntchafu yakumanja.
Il prit la graisse, la queue, toute la graisse qui était sur les entrailles, la couverture du foie, les deux rognons et leur graisse, et la cuisse droite;
26 Ndipo mʼdengu la buledi wopanda yisiti limene linali pamaso pa Yehova, anatengamo buledi mmodzi, buledi mmodzi wokhala ndi mafuta a olivi, ndi buledi wopyapyala mmodzi. Zonsezi anaziyika pa mafuta aja ndi pa ntchafu ya ku dzanja lamanja ija.
et dans la corbeille de pains sans levain qui était devant l'Éternel, il prit un gâteau sans levain, un gâteau de pain huilé et une galette, et les plaça sur la graisse et sur la cuisse droite.
27 Mose anapereka zonsezi mʼmanja mwa Aaroni ndi ana ake amene anazipereka kwa Yehova kuti zikhale nsembe yoweyula.
Il mit tout cela dans les mains d'Aaron et dans les mains de ses fils, et il les agita comme une offrande par agitation devant l'Éternel.
28 Kenaka Mose anazitenga mʼmanja mwawo ndipo anazipsereza pa guwa lansembe pamwamba penipeni pamodzi ndi nsembe yopsereza ija kuti ikhale nsembe yopereka pamwambo wodzoza ansembe, kuti ipereke fungo lokoma, chopereka chachakudya kwa Yehova.
Moïse les prit de leurs mains et les brûla sur l'autel, sur l'holocauste. Elles constituaient une offrande de consécration pour un parfum agréable. C'était une offrande faite par le feu à Yahvé.
29 Mose anatenga chidale cha nkhosa yayimuna, chomwe ndi gawo lake pamwambo wodzoza ansembe, ndipo anachiweyula pamaso pa Yehova kuti chikhale nsembe yoweyula monga momwe Yehova analamulira Mose.
Moïse prit la poitrine et l'agita comme une offrande par agitation devant Yahvé. C'était la part de Moïse du bélier de consécration, comme Yahvé l'avait ordonné à Moïse.
30 Kenaka Mose anatenga mafuta wodzozera ansembe ndi magazi amene anali pa guwa nawaza pa Aaroni ndi zovala zake ndiponso ana ake aja ndi zovala zawo. Motero Mose anapatula Aaroni ndi zovala zake, ndiponso ana ake ndi zovala zawo.
Moïse prit de l'huile d'onction et du sang qui était sur l'autel; il en fit l'aspersion sur Aaron, sur ses vêtements, sur ses fils et sur les vêtements de ses fils avec lui, et il sanctifia Aaron, ses vêtements, ses fils et les vêtements de ses fils avec lui.
31 Mose anawuza Aaroni ndi ana ake kuti, “Phikani nyamayo pa khomo la tenti ya msonkhano, ndipo mudyere pomwepo pamodzi ndi buledi amene ali mʼdengu la zopereka za pamwambo wodzoza ansembe monga Yehova analamulira kuti, ‘Aaroni ndi ana ake azidya zimenezi.’
Moïse dit à Aaron et à ses fils: « Faites bouillir la viande à l'entrée de la tente de la Rencontre, et là, mangez-la, ainsi que le pain qui est dans la corbeille de consécration, comme je l'ai ordonné, en disant: « Aaron et ses fils la mangeront ».
32 Ndipo nyama ndi buledi zotsalazo, muziwotche.
Ce qui restera de la viande et du pain, vous le brûlerez au feu.
33 Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano kwa masiku asanu ndi awiri mpaka masiku amwambo wokudzozani unsembe atatha, pakuti mwambowu ndi wa masiku asanu ndi awiri.
Tu ne sortiras pas de l'entrée de la Tente d'assignation pendant sept jours, jusqu'à ce que les jours de ta consécration soient accomplis, car il te consacrera sept jours.
34 Zimene zachitika lerozi analamula ndi Yehova kuti zichitike ngati nsembe yopepesera machimo anu.
Ce qui a été fait aujourd'hui, Yahvé a ordonné de le faire, afin de faire l'expiation pour vous.
35 Muzikhala pa khomo la tenti ya msonkhano usana ndi usiku kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo muzichita zimene Yehova wakulamulani kuti musafe, pakuti zimenezi ndi zomwe Yehova wandilamulira.”
Tu resteras jour et nuit à l'entrée de la Tente de la Rencontre, pendant sept jours, et tu observeras l'ordre de l'Éternel, afin que tu ne meures pas; car c'est ainsi qu'on me l'ordonne. »
36 Choncho Aaroni ndi ana ake anachita zonse zimene Yehova analamula kudzera mwa Mose.
Aaron et ses fils firent tout ce que l'Éternel avait ordonné par Moïse.

< Levitiko 8 >