< Levitiko 7 >

1 “‘Malamulo a nsembe yopepesera kupalamula imene ndi nsembe yopatulika kwambiri ndi awa:
“‘Çok kutsal olan suç sunusunun yasası şudur:
2 Nsembe yopepesera machimo iziphedwa pamalo pomwe amaphera nsembe yopsereza ndipo awaze magazi ake mbali zonse za guwa.
Suç sunusu yakmalık sununun kesildiği yerde kesilecek ve kanı sunağın her yanına dökülecek.
3 Tsono apereke mafuta ake onse: mchira wamafuta ndi mafuta amene amakuta matumbo.
Hayvanın bütün yağı alınacak, kuyruk yağı, bağırsak ve işkembe yağları, böbrekleri, böbrek üstü yağları, karaciğerden böbreklere uzanan perde ayrılacak.
4 Aperekenso impsyo ziwiri, mafuta ake pamodzi ndi mafuta onse amene ali chamʼchiwuno, ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi.
5 Wansembe azitenthe pa guwa kuti zikhale nsembe yotentha pa moto, yoperekedwa kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo lopalamula.
Kâhin bunların hepsini sunak üzerinde, RAB için yakılan sunu olarak yakacak. Bu suç sunusudur.
6 Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kudyako nsembeyo koma adyere ku malo opatulika. Imeneyi ndi nsembe yopatulika kwambiri.
Kâhinler soyundan gelen her erkek bu sunuyu yiyebilir. Sunu kutsal bir yerde yenecek, çünkü çok kutsaldır.
7 “‘Nsembe yopepesera tchimo lopalamula ndi yofanana ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo. Ndipo nsembe ziwiri zonsezi zili ndi lamulo limodzi lokha. Wansembe amene wachita mwambo wa nsembe yopepesera machimo a kupalamula atenge nyamayo ngati yake.
“‘Suç ve günah sunuları için aynı yasa geçerlidir. Et, sunuyu sunarak günahı bağışlatan kâhinindir.
8 Wansembe wopereka nsembe yopsereza ya munthu wina aliyense, atenge chikopa cha nsembe yopserezayo kuti chikhale chake.
Yakmalık sununun derisi de sunuyu sunan kâhinindir.
9 Chopereka chilichonse cha chakudya chophika mu uvuni kapena chokazinga mu mʼphika kapena mu chiwaya ndi cha wansembe amene wapereka nsembezo.
Fırında, tavada ya da sacda pişirilen her tahıl sunusu onu sunan kâhinin olacak.
10 Ndipo chopereka china chilichonse cha chakudya chosakaniza ndi mafuta kapena chowuma, chikhale cha ana onse a Aaroni ndipo anawo achigawane mofanana.
Zeytinyağıyla yoğrulmuş ya da kuru tahıl sunuları da Harunoğulları'na aittir. Aralarında eşit olarak bölüşülecektir.’”
11 “‘Malamulo a nsembe ya chiyanjano imene munthu angathe kupereka kwa Yehova ndi awa:
“‘RAB'be sunulacak esenlik kurbanının yasası şudur:
12 “‘Ngati munthuyo apereka chifukwa cha kuthokoza, apereke nsembeyo pamodzi ndi makeke wopanda yisiti, osakaniza ndi mafuta; timitanda ta buledi wopanda yisiti, topyapyala, topaka mafuta, ndiponso makeke a ufa wosalala wophikidwa bwino, wosakaniza ndi mafuta.
Eğer adam sunusunu RAB'be şükretmek için sunuyorsa, sunusunun yanısıra zeytinyağıyla yoğrulmuş mayasız pideler, üzerine zeytinyağı sürülmüş mayasız yufkalar ve iyice karıştırılmış ince undan yağla yoğrulmuş mayasız pideler de sunacak.
13 Pamodzi ndi nsembe yachiyanjano yothokozerayo abwerenso ndi makeke opangidwa ndi yisiti ngati chopereka chake.
RAB'be şükretmek için, esenlik sunusunu mayalı ekmek pideleriyle birlikte sunacak.
14 Munthuyo atenge mtanda umodzi pa mtanda wa buledi wa mtundu uliwonse kuti ukhale nsembe yopereka kwa Yehova. Tsono mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe yachiyanjano.
Her sunudan birini RAB'be bağış sunusu olarak sunacak ve o sunu esenlik sunusunun kanını sunağa döken kâhinin olacak.
15 Nyama ya nsembe yachiyanjano yothokozera idyedwe pa tsiku lomwe nsembeyo yaperekedwa ndipo isatsaleko mpaka mmawa.
RAB'be şükretmek için sunulan esenlik kurbanının eti, sununun sunulduğu gün yenecek, sabaha bırakılmayacak.
16 “‘Koma ngati nsembe yakeyo apereka chifukwa cha lumbiro kapena mwaufulu, nsembeyo adye tsiku lomwe yaperekedwalo. Koma yotsala angathe kuyidya mmawa mwake.
“‘Biri gönülden verilen bir sunu ya da dilediği adağı sunmak istiyorsa, kurbanın eti sununun sunulduğu gün yenecek, artakalırsa ertesi güne bırakılabilecek.
17 Ngati nyama ina ya nsembe yatsalabe mpaka tsiku lachitatu, imeneyo itenthedwe pa moto.
Ancak üçüncü güne bırakılan kurban eti yakılacak.
18 Ngati munthu adya nyama yachiyanjano pa tsiku lachitatu, nsembeyo sidzalandiridwa. Amene wayipereka nsembeyo Mulungu sadzamulandira ndipo nsembeyo idzakhala yonyansa pamaso pa Mulungu, yosamupindulira kanthu woperekayo.
Esenlik kurbanının eti üçüncü gün yenirse sunu kabul edilmeyecek, geçerli sayılmayacak. Çünkü et kirlenmiş sayılır ve her yiyen suçunun cezasını çekecektir.
19 “‘Nyama imene yakhudza chilichonse chodetsedwa, munthu asayidye, koma itenthedwe pa moto. Aliyense amene ali woyeretsedwa angathe kudya nyama inayo.
“‘Kirli sayılan herhangi bir şeye dokunan et yenmemeli, yakılmalıdır. Öteki etlere gelince, temiz sayılan bir insan o etlerden yiyebilir.
20 Koma ngati munthu wina amene ndi wosayeretsedwa adya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.
Ama biri kirli sayıldığı sürece RAB'be sunulan esenlik kurbanının etini yerse, halkın arasından atılacak.
21 Ndipo ngati munthu wina akhudza chinthu chodetsedwa, kaya chonyansa cha munthu kapena cha nyama, kapenanso chonyansa china chilichonse, ndipo kenaka nʼkudya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati anthu a mtundu wake.’”
Ayrıca kirli sayılan herhangi bir şeye, insandan kaynaklanan bir kirliliğe, kirli bir hayvana ya da kirli ve iğrenç bir şeye dokunup da RAB'be sunulan esenlik kurbanının etinden yiyen biri halkın arasından atılacak.’”
22 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
RAB Musa'ya şöyle dedi:
23 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Musadye mafuta a ngʼombe, nkhosa kapenanso mbuzi.
“İsrail halkına de ki, ‘İster sığır, ister koyun ya da keçi yağı olsun, hayvan yağı yemeyeceksiniz.
24 Mafuta a nyama yofa yokha, kapena mafuta a nyama yophedwa ndi zirombo akhoza kuwagwiritsa ntchito iliyonse, koma inu musadye mafuta amenewo.
Kendiliğinden ölen ya da yabanıl hayvanların parçaladığı bir hayvanın yağı başka şeyler için kullanılabilir, ama hiçbir zaman yenmemeli.
25 Pakuti munthu wakudya mafuta a nyama yoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe yotentha pa moto, ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
Kim yakılan ve RAB'be sunulan hayvanlardan birinin yağını yerse, halkımın arasından atılacak.
26 Ndipo kulikonse kumene mukakhale musakadye magazi a mbalame iliyonse kapena magazi a nyama iliyonse.
Nerede yaşarsanız yaşayın, hiçbir kuşun ya da hayvanın kanını yemeyeceksiniz.
27 Ngati munthu aliyense adya magazi achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.’”
Kan yiyen herkes halkımın arasından atılacak.’”
28 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
RAB Musa'ya şöyle dedi:
29 “Awuze Aisraeli kuti, Aliyense amene apereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, abwere ndi gawo la nsembeyo kwa Yehova.
“İsrail halkına de ki, ‘RAB'be esenlik kurbanı sunmak isteyen biri, esenlik kurbanının bir parçasını RAB'be sunmalı.
30 Atenge ndi manja ake zigawo za chopereka zoyenera kuzitentha pa moto ngati chopereka kwa Yehova. Abweretse mafuta, pamodzi ndi chidale chomwe, ndipo chidalecho achiweyule kuti chikhale chopereka choweyula kwa Yehova.
RAB için yakılan sunusunu kendi eliyle getirmeli. Hayvanın yağını döşüyle birlikte getirecek ve döş RAB'bin huzurunda sallamalık bir sunu olarak sallanacak.
31 Wansembe atenthe mafutawo pa guwa koma chidalecho chikhale cha Aaroni ndi ana ake.
Kâhin yağı sunağın üzerinde yakacak, ama döş Harun'la oğullarının olacak.
32 Mumupatse wansembe ntchafu ya kumanja ya nsembe yanu yachiyanjano kuti ikhale chopereka chanu kwa iye.
Esenlik kurbanlarınızın sağ budunu bağış olarak kâhine vereceksiniz.
33 Mwana wa Aaroni amene amapereka magazi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano, adzitenga ntchafu ya kumanja kukhala gawo lake.
Harunoğulları arasında esenlik sunusunun kanını ve yağını kim sunuyorsa, sağ but onun payı olacak.
34 Choncho pa zopereka zachiyanjano za Aisraeli, Ine ndatengapo chidale chomwe amaweyula ndi ntchafu zimene amapereka nsembe ndipo ndazipereka kwa wansembe Aaroni ndi ana ake. Izi ndizo gawo lawo nthawi zonse pa zopereka za Aisraeli.”
İsrail halkının sunduğu esenlik kurbanlarından sallamalık döşü ve bağış olarak sunulan budu aldım. İsrail halkının payı olarak bunları sonsuza dek Kâhin Harun'la oğullarına verdim.’”
35 Zimenezi ndi chigawo cha Aaroni ndi ana ake chotapidwa pa zopereka kwa Yehova zoti zitenthedwe pa moto zimene zinaperekedwa pa tsiku limene anapatulidwa kuti akhale ansembe otumikira Yehova.
Harun'la oğulları kâhin atandıkları gün RAB için yakılan sunulardan paylarına bu düştü.
36 Yehova ndiye analamulira kuti pa zopereka za Aisraeli azitapapo zimenezi ndi kuwapatsa ansembe ngati gawo lawo. Yehovayo analamula zimenezi pa tsiku limene ansembewo anapatulidwa ndipo anachikhazikitsa ngati lamulo la nthawi zonse.
RAB onları meshettiği gün İsrail halkına buyruk vermişti. Adağın bu parçaları gelecek kuşaklar boyunca onların payı olacaktı.
37 Awa ndi malamulo a nsembe izi: nsembe yopsereza, nsembe yachakudya, nsembe yopepesera machimo, nsembe yopepesera kupalamula, nsembe ya mwambo wodzoza ndi nsembe yachiyanjano.
Yakmalık, tahıl, suç, günah, atanma sunularının ve esenlik kurbanlarının yasası budur.
38 Malamulo amenewa Yehova anapereka kwa Mose pa Phiri la Sinai pa tsiku limene Yehova analamulira Aisraeli kuti abwere ndi zopereka za kwa Yehova, ku chipululu cha Sinai kuja.
RAB, bu buyruğu çölde, Sina Dağı'nda İsrail halkından kendisine sunu sunmalarını istediği gün Musa'ya vermişti.

< Levitiko 7 >