< Levitiko 7 >

1 “‘Malamulo a nsembe yopepesera kupalamula imene ndi nsembe yopatulika kwambiri ndi awa:
Och detta är skuldoffrens lag, och det är det aldrahelgasta.
2 Nsembe yopepesera machimo iziphedwa pamalo pomwe amaphera nsembe yopsereza ndipo awaze magazi ake mbali zonse za guwa.
På det rummet, der man slagtar bränneoffret, skall man ock slagta skuldoffret, och stänka dess blod på altaret allt omkring.
3 Tsono apereke mafuta ake onse: mchira wamafuta ndi mafuta amene amakuta matumbo.
Och allt dess feta skall man offra, stjerten och det feta, som är på inelfverna;
4 Aperekenso impsyo ziwiri, mafuta ake pamodzi ndi mafuta onse amene ali chamʼchiwuno, ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi.
Båda njurarna med det feta, som derpå är vid länderna, och nätet öfver lefrena med njurarna.
5 Wansembe azitenthe pa guwa kuti zikhale nsembe yotentha pa moto, yoperekedwa kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo lopalamula.
Och Presten skall uppbränna det på altaret Herranom till ett offer; det är ett skuldoffer.
6 Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kudyako nsembeyo koma adyere ku malo opatulika. Imeneyi ndi nsembe yopatulika kwambiri.
Det mankön är ibland Presterna, skola det äta på heligt rum; ty det är det aldrahelgasta.
7 “‘Nsembe yopepesera tchimo lopalamula ndi yofanana ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo. Ndipo nsembe ziwiri zonsezi zili ndi lamulo limodzi lokha. Wansembe amene wachita mwambo wa nsembe yopepesera machimo a kupalamula atenge nyamayo ngati yake.
Såsom syndoffret, så skall ock skuldoffret vara; begges deras skall en lag vara; och skall höra Prestenom till, som derigenom försonar.
8 Wansembe wopereka nsembe yopsereza ya munthu wina aliyense, atenge chikopa cha nsembe yopserezayo kuti chikhale chake.
Den Prest något bränneoffer offrar, honom skall tillhöra huden af bränneoffret, som han offrat hafver.
9 Chopereka chilichonse cha chakudya chophika mu uvuni kapena chokazinga mu mʼphika kapena mu chiwaya ndi cha wansembe amene wapereka nsembezo.
Och allt spisoffer, som i ugn, eller på halster, eller uti panno bakadt varder, skall höra Prestenom till, som det offrar.
10 Ndipo chopereka china chilichonse cha chakudya chosakaniza ndi mafuta kapena chowuma, chikhale cha ana onse a Aaroni ndipo anawo achigawane mofanana.
Och allt spisoffer, som med oljo blandadt eller torrt är, det skall allom Aarons barnom tillhöra, så thy eno som thy andro.
11 “‘Malamulo a nsembe ya chiyanjano imene munthu angathe kupereka kwa Yehova ndi awa:
Och detta är tackoffers lag, det man Herranom offrar.
12 “‘Ngati munthuyo apereka chifukwa cha kuthokoza, apereke nsembeyo pamodzi ndi makeke wopanda yisiti, osakaniza ndi mafuta; timitanda ta buledi wopanda yisiti, topyapyala, topaka mafuta, ndiponso makeke a ufa wosalala wophikidwa bwino, wosakaniza ndi mafuta.
Vilja de göra ett lofoffer, så skola de offra osyrade kakor, blandade med oljo, och osyrade tunnkakor, bestrukna med oljo, och i panno bakade semlokakor, blandade med oljo.
13 Pamodzi ndi nsembe yachiyanjano yothokozerayo abwerenso ndi makeke opangidwa ndi yisiti ngati chopereka chake.
Och sådana offer skola de göra på en kako af syradt bröd till sitt tackoffers lofoffer.
14 Munthuyo atenge mtanda umodzi pa mtanda wa buledi wa mtundu uliwonse kuti ukhale nsembe yopereka kwa Yehova. Tsono mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe yachiyanjano.
Och ett af thy allo skall offras Herranom till häfoffer, och skall höra Prestenom till, som stänker tackoffrens blod.
15 Nyama ya nsembe yachiyanjano yothokozera idyedwe pa tsiku lomwe nsembeyo yaperekedwa ndipo isatsaleko mpaka mmawa.
Och lofoffrens kött, i sitt tackoffer, skall ätas på samma dagen, som det offradt varder, och intet låtas qvart intill morgonen.
16 “‘Koma ngati nsembe yakeyo apereka chifukwa cha lumbiro kapena mwaufulu, nsembeyo adye tsiku lomwe yaperekedwalo. Koma yotsala angathe kuyidya mmawa mwake.
Och ehvad det är ett löfte eller friviljogt offer, så skall det på samma dagen ätet varda, som det offradt är; om något qvart blifver till den andra dagen, skall man ändå ätat.
17 Ngati nyama ina ya nsembe yatsalabe mpaka tsiku lachitatu, imeneyo itenthedwe pa moto.
Men hvad qvart blifver af offradt kött intill tredje dagen, det skall uppbrännas i elde.
18 Ngati munthu adya nyama yachiyanjano pa tsiku lachitatu, nsembeyo sidzalandiridwa. Amene wayipereka nsembeyo Mulungu sadzamulandira ndipo nsembeyo idzakhala yonyansa pamaso pa Mulungu, yosamupindulira kanthu woperekayo.
Och om någor äter på tredje dagen af det offrade köttet af hans tackoffer, så blifver han icke tacknämlig, som det offrat hafver, det skall icke heller varda honom tillräknadt, utan det blifver en styggelse. Och hvad själ som deraf äter, hon är brottslig till en missgerning.
19 “‘Nyama imene yakhudza chilichonse chodetsedwa, munthu asayidye, koma itenthedwe pa moto. Aliyense amene ali woyeretsedwa angathe kudya nyama inayo.
Och det kött, som kommer vid något orent, det skall icke varda ätet, utan uppbrändt i elde. Den der ren är till lekamen, han skall äta det köttet.
20 Koma ngati munthu wina amene ndi wosayeretsedwa adya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.
Och den själ, som äter af tackoffrens kött, det Herranom tillhörer, hennes orenhet vare öfver henne, och hon skall varda utrotad utu sitt folk.
21 Ndipo ngati munthu wina akhudza chinthu chodetsedwa, kaya chonyansa cha munthu kapena cha nyama, kapenanso chonyansa china chilichonse, ndipo kenaka nʼkudya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati anthu a mtundu wake.’”
Och om en själ kommer vid något det orent är, vare sig oren menniska, boskap, eller hvad eljest styggeligit är, eller ock äter af tackoffrens kött, det Herranom tillhörer, den skall utrotad varda utu sitt folk.
22 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
Och Herren talade med Mose, och sade:
23 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Musadye mafuta a ngʼombe, nkhosa kapenanso mbuzi.
Tala med Israels barn, och säg: I skolen intet fett äta af fä, lambom och getom.
24 Mafuta a nyama yofa yokha, kapena mafuta a nyama yophedwa ndi zirombo akhoza kuwagwiritsa ntchito iliyonse, koma inu musadye mafuta amenewo.
Men det feta af ett as, och hvad af vilddjur rifvet är, bruker eder till allahanda nytto; men icke skolen I ätat.
25 Pakuti munthu wakudya mafuta a nyama yoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe yotentha pa moto, ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
Ty den som äter det feta af den boskap, som Herranom till offer gifven är, den samma själen skall utrotad varda utu sitt folk.
26 Ndipo kulikonse kumene mukakhale musakadye magazi a mbalame iliyonse kapena magazi a nyama iliyonse.
I skolen ock intet blod äta, antingen af boskap, eller af foglar, der I bon.
27 Ngati munthu aliyense adya magazi achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.’”
Hvilken själ, som äter något blod, hon skall utrotad varda utu sitt folk.
28 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
Och Herren talade med Mose, och sade:
29 “Awuze Aisraeli kuti, Aliyense amene apereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, abwere ndi gawo la nsembeyo kwa Yehova.
Tala med Israels barn, och säg: Den som Herranom sitt tackoffer göra vill, han skall ock bära med hvad som Herranom till ett tackoffer tillhörer.
30 Atenge ndi manja ake zigawo za chopereka zoyenera kuzitentha pa moto ngati chopereka kwa Yehova. Abweretse mafuta, pamodzi ndi chidale chomwe, ndipo chidalecho achiweyule kuti chikhale chopereka choweyula kwa Yehova.
Han skall med sine hand bärat fram till Herrans offer, nämliga det feta på bröstena skall han frambära, samt med bröstet, att de skola varda ett veftoffer för Herranom.
31 Wansembe atenthe mafutawo pa guwa koma chidalecho chikhale cha Aaroni ndi ana ake.
Och Presten skall uppbränna det feta på altaret. Och bröstet skall höra Aaron till, och hans söner.
32 Mumupatse wansembe ntchafu ya kumanja ya nsembe yanu yachiyanjano kuti ikhale chopereka chanu kwa iye.
Och den högra bogen skola de gifva Prestenom till häfoffer af deras tackoffer.
33 Mwana wa Aaroni amene amapereka magazi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano, adzitenga ntchafu ya kumanja kukhala gawo lake.
Och hvilken ibland Aarons söner offrar blodet af tackoffret, och det feta, han skall ock hafva den högra bogen på sin del.
34 Choncho pa zopereka zachiyanjano za Aisraeli, Ine ndatengapo chidale chomwe amaweyula ndi ntchafu zimene amapereka nsembe ndipo ndazipereka kwa wansembe Aaroni ndi ana ake. Izi ndizo gawo lawo nthawi zonse pa zopereka za Aisraeli.”
Ty veftebröstet och häfvebogen hafver jag tagit af Israels barn, af deras tackoffer, och hafver gifvit det Prestenom Aaron och hans söner, till en evig rätt.
35 Zimenezi ndi chigawo cha Aaroni ndi ana ake chotapidwa pa zopereka kwa Yehova zoti zitenthedwe pa moto zimene zinaperekedwa pa tsiku limene anapatulidwa kuti akhale ansembe otumikira Yehova.
Detta är Aarons och hans söners vigelse af Herrans offer, på den dagen då de öfverantvardade vordo till att vara Herranom Prester;
36 Yehova ndiye analamulira kuti pa zopereka za Aisraeli azitapapo zimenezi ndi kuwapatsa ansembe ngati gawo lawo. Yehovayo analamula zimenezi pa tsiku limene ansembewo anapatulidwa ndipo anachikhazikitsa ngati lamulo la nthawi zonse.
Då Herren böd, på den dagen, då han dem vigde, hvad dem af Israels barnom gifvas skulle, till en evig rätt, allom deras efterkommandom.
37 Awa ndi malamulo a nsembe izi: nsembe yopsereza, nsembe yachakudya, nsembe yopepesera machimo, nsembe yopepesera kupalamula, nsembe ya mwambo wodzoza ndi nsembe yachiyanjano.
Och detta är bränneoffrens lag, spisoffrens, syndoffrens, skuldoffrens, fyllooffrens och tackoffrens;
38 Malamulo amenewa Yehova anapereka kwa Mose pa Phiri la Sinai pa tsiku limene Yehova analamulira Aisraeli kuti abwere ndi zopereka za kwa Yehova, ku chipululu cha Sinai kuja.
Det Herren på Sinai berg Mose böd, den dagen då han böd honom till Israels barn, att de skulle offra deras offer Herranom uti den öknene Sinai.

< Levitiko 7 >