< Levitiko 7 >

1 “‘Malamulo a nsembe yopepesera kupalamula imene ndi nsembe yopatulika kwambiri ndi awa:
“'Esta é a lei da oferta de transgressão: É santíssima.
2 Nsembe yopepesera machimo iziphedwa pamalo pomwe amaphera nsembe yopsereza ndipo awaze magazi ake mbali zonse za guwa.
No lugar em que matarem a oferta queimada, ele matará a oferta de transgressão; e seu sangue ele aspergirá em torno do altar.
3 Tsono apereke mafuta ake onse: mchira wamafuta ndi mafuta amene amakuta matumbo.
Ele oferecerá toda sua gordura: a cauda gorda, e a gordura que cobre as entranhas,
4 Aperekenso impsyo ziwiri, mafuta ake pamodzi ndi mafuta onse amene ali chamʼchiwuno, ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi.
e tirará os dois rins, e a gordura que está sobre eles, que está junto aos lombos, e a cobertura do fígado, com os rins;
5 Wansembe azitenthe pa guwa kuti zikhale nsembe yotentha pa moto, yoperekedwa kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo lopalamula.
e o sacerdote os queimará no altar para uma oferta feita por fogo a Javé: é uma oferta de transgressão.
6 Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kudyako nsembeyo koma adyere ku malo opatulika. Imeneyi ndi nsembe yopatulika kwambiri.
Todo homem entre os sacerdotes pode comer dela. Será comido em lugar santo. É santíssimo.
7 “‘Nsembe yopepesera tchimo lopalamula ndi yofanana ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo. Ndipo nsembe ziwiri zonsezi zili ndi lamulo limodzi lokha. Wansembe amene wachita mwambo wa nsembe yopepesera machimo a kupalamula atenge nyamayo ngati yake.
“'Como é a oferta pelo pecado, assim é a oferta pela transgressão; há uma lei para eles. O sacerdote que fizer expiação com eles a terá.
8 Wansembe wopereka nsembe yopsereza ya munthu wina aliyense, atenge chikopa cha nsembe yopserezayo kuti chikhale chake.
O sacerdote que oferecer a oferta queimada de qualquer homem terá para si a pele do holocausto que ele ofereceu.
9 Chopereka chilichonse cha chakudya chophika mu uvuni kapena chokazinga mu mʼphika kapena mu chiwaya ndi cha wansembe amene wapereka nsembezo.
Toda oferta de refeição que for assada no forno, e tudo o que for preparado na panela e na chapa, será do padre que a oferecer.
10 Ndipo chopereka china chilichonse cha chakudya chosakaniza ndi mafuta kapena chowuma, chikhale cha ana onse a Aaroni ndipo anawo achigawane mofanana.
Toda oferta de refeição, misturada com óleo ou seca, pertence a todos os filhos de Aarão, tanto um como outro.
11 “‘Malamulo a nsembe ya chiyanjano imene munthu angathe kupereka kwa Yehova ndi awa:
“'Esta é a lei do sacrifício das ofertas de paz, que se deve oferecer a Iavé:
12 “‘Ngati munthuyo apereka chifukwa cha kuthokoza, apereke nsembeyo pamodzi ndi makeke wopanda yisiti, osakaniza ndi mafuta; timitanda ta buledi wopanda yisiti, topyapyala, topaka mafuta, ndiponso makeke a ufa wosalala wophikidwa bwino, wosakaniza ndi mafuta.
Se ele oferecer por uma ação de graças, então oferecerá com o sacrifício de bolos ázimos misturados com óleo, e bolachas ázimos untadas com óleo, e bolos misturados com óleo.
13 Pamodzi ndi nsembe yachiyanjano yothokozerayo abwerenso ndi makeke opangidwa ndi yisiti ngati chopereka chake.
Ele oferecerá sua oferta com o sacrifício de suas ofertas pacíficas para uma ação de graças com bolos de pão levedado.
14 Munthuyo atenge mtanda umodzi pa mtanda wa buledi wa mtundu uliwonse kuti ukhale nsembe yopereka kwa Yehova. Tsono mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe yachiyanjano.
Dela ele oferecerá uma de cada oferta por uma oferta alçada a Yahweh. Será o sacerdote quem asperge o sangue das ofertas pacíficas.
15 Nyama ya nsembe yachiyanjano yothokozera idyedwe pa tsiku lomwe nsembeyo yaperekedwa ndipo isatsaleko mpaka mmawa.
A carne do sacrifício de suas ofertas pacíficas para ação de graças será comida no dia de sua oferta. Ele não deixará nada disso até a manhã.
16 “‘Koma ngati nsembe yakeyo apereka chifukwa cha lumbiro kapena mwaufulu, nsembeyo adye tsiku lomwe yaperekedwalo. Koma yotsala angathe kuyidya mmawa mwake.
“'Mas se o sacrifício de sua oferta for um voto, ou uma oferta de livre vontade, ele será comido no dia em que ele oferecer seu sacrifício. No dia seguinte, o que restar dele será comido,
17 Ngati nyama ina ya nsembe yatsalabe mpaka tsiku lachitatu, imeneyo itenthedwe pa moto.
mas o que restar da carne do sacrifício no terceiro dia será queimado com fogo.
18 Ngati munthu adya nyama yachiyanjano pa tsiku lachitatu, nsembeyo sidzalandiridwa. Amene wayipereka nsembeyo Mulungu sadzamulandira ndipo nsembeyo idzakhala yonyansa pamaso pa Mulungu, yosamupindulira kanthu woperekayo.
Se alguma das carnes do sacrifício de sua oferta pacífica for comida no terceiro dia, ela não será aceita, e não será creditada a quem a oferecer. Será uma abominação, e a alma que comer qualquer uma delas suportará sua iniqüidade.
19 “‘Nyama imene yakhudza chilichonse chodetsedwa, munthu asayidye, koma itenthedwe pa moto. Aliyense amene ali woyeretsedwa angathe kudya nyama inayo.
“'A carne que toca qualquer coisa impura não deve ser consumida. Deve ser queimada com fogo. Quanto à carne, todos que estiverem limpos poderão comê-la;
20 Koma ngati munthu wina amene ndi wosayeretsedwa adya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.
mas a alma que comer da carne do sacrifício das ofertas de paz que pertence a Iavé, tendo sua imundícia sobre ele, essa alma será cortada de seu povo.
21 Ndipo ngati munthu wina akhudza chinthu chodetsedwa, kaya chonyansa cha munthu kapena cha nyama, kapenanso chonyansa china chilichonse, ndipo kenaka nʼkudya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati anthu a mtundu wake.’”
Quando alguém tocar qualquer coisa impura, a imundícia do homem, ou um animal impuro, ou qualquer abominação impura, e comer alguma da carne do sacrifício das ofertas pacíficas que pertence a Iavé, essa alma será extirpada de seu povo'”.
22 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
Yahweh falou a Moisés, dizendo:
23 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Musadye mafuta a ngʼombe, nkhosa kapenanso mbuzi.
“Fale aos filhos de Israel, dizendo: “Não comereis gordura, nem de touro, nem de ovelha, nem de cabra”.
24 Mafuta a nyama yofa yokha, kapena mafuta a nyama yophedwa ndi zirombo akhoza kuwagwiritsa ntchito iliyonse, koma inu musadye mafuta amenewo.
A gordura daquilo que morre de si mesmo, e a gordura daquilo que é rasgado dos animais, pode ser usada para qualquer outro serviço, mas não comereis de forma alguma dela.
25 Pakuti munthu wakudya mafuta a nyama yoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe yotentha pa moto, ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
Para quem comer a gordura do animal que os homens oferecem como oferta feita pelo fogo a Javé, até mesmo a alma que a come será cortada de seu povo.
26 Ndipo kulikonse kumene mukakhale musakadye magazi a mbalame iliyonse kapena magazi a nyama iliyonse.
Você não comerá nenhum sangue, seja de pássaro ou de animal, em nenhuma de suas habitações.
27 Ngati munthu aliyense adya magazi achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.’”
Quem quer que seja que come qualquer sangue, essa alma será cortada de seu povo'”.
28 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
Javé falou a Moisés, dizendo:
29 “Awuze Aisraeli kuti, Aliyense amene apereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, abwere ndi gawo la nsembeyo kwa Yehova.
“Fale aos filhos de Israel, dizendo: 'Aquele que oferecer o sacrifício de suas ofertas de paz a Javé trará sua oferta a Javé do sacrifício de suas ofertas de paz'.
30 Atenge ndi manja ake zigawo za chopereka zoyenera kuzitentha pa moto ngati chopereka kwa Yehova. Abweretse mafuta, pamodzi ndi chidale chomwe, ndipo chidalecho achiweyule kuti chikhale chopereka choweyula kwa Yehova.
Com suas próprias mãos ele trará as ofertas de Iavé feitas pelo fogo”. Ele trará a gordura com o peito, para que o peito possa ser acenado para uma oferta de ondas diante de Iavé.
31 Wansembe atenthe mafutawo pa guwa koma chidalecho chikhale cha Aaroni ndi ana ake.
O sacerdote queimará a gordura sobre o altar, mas o peito será de Aarão e de seus filhos.
32 Mumupatse wansembe ntchafu ya kumanja ya nsembe yanu yachiyanjano kuti ikhale chopereka chanu kwa iye.
A coxa direita que você dará ao sacerdote para uma oferta alçada dos sacrifícios de suas ofertas pacíficas.
33 Mwana wa Aaroni amene amapereka magazi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano, adzitenga ntchafu ya kumanja kukhala gawo lake.
Ele entre os filhos de Aarão que oferecer o sangue das ofertas pacíficas, e a gordura, terá a coxa direita por uma porção.
34 Choncho pa zopereka zachiyanjano za Aisraeli, Ine ndatengapo chidale chomwe amaweyula ndi ntchafu zimene amapereka nsembe ndipo ndazipereka kwa wansembe Aaroni ndi ana ake. Izi ndizo gawo lawo nthawi zonse pa zopereka za Aisraeli.”
Pelo peito ondulado e pela coxa pesada que tirei dos filhos de Israel dos sacrifícios de suas ofertas pacíficas, e os dei a Arão, o sacerdote, e a seus filhos como porção para sempre dos filhos de Israel”.
35 Zimenezi ndi chigawo cha Aaroni ndi ana ake chotapidwa pa zopereka kwa Yehova zoti zitenthedwe pa moto zimene zinaperekedwa pa tsiku limene anapatulidwa kuti akhale ansembe otumikira Yehova.
Esta é a porção consagrada de Aarão, e a porção consagrada de seus filhos, das ofertas de Iavé feitas pelo fogo, no dia em que ele os apresentou para ministrar a Iavé no gabinete do sacerdote;
36 Yehova ndiye analamulira kuti pa zopereka za Aisraeli azitapapo zimenezi ndi kuwapatsa ansembe ngati gawo lawo. Yehovayo analamula zimenezi pa tsiku limene ansembewo anapatulidwa ndipo anachikhazikitsa ngati lamulo la nthawi zonse.
que Iavé ordenou que lhes fosse dada dos filhos de Israel, no dia em que ele os ungiu. É a porção deles para sempre através de suas gerações.
37 Awa ndi malamulo a nsembe izi: nsembe yopsereza, nsembe yachakudya, nsembe yopepesera machimo, nsembe yopepesera kupalamula, nsembe ya mwambo wodzoza ndi nsembe yachiyanjano.
Esta é a lei do holocausto, a oferta de refeição, a oferta pelo pecado, a oferta pela culpa, a consagração e o sacrifício de ofertas de paz
38 Malamulo amenewa Yehova anapereka kwa Mose pa Phiri la Sinai pa tsiku limene Yehova analamulira Aisraeli kuti abwere ndi zopereka za kwa Yehova, ku chipululu cha Sinai kuja.
que Javé ordenou a Moisés no Monte Sinai no dia em que ordenou aos filhos de Israel que oferecessem suas ofertas a Javé, no deserto do Sinai.

< Levitiko 7 >