< Levitiko 7 >

1 “‘Malamulo a nsembe yopepesera kupalamula imene ndi nsembe yopatulika kwambiri ndi awa:
«و این است قانون قربانی جرم؛ این اقدس اقداس است.۱
2 Nsembe yopepesera machimo iziphedwa pamalo pomwe amaphera nsembe yopsereza ndipo awaze magazi ake mbali zonse za guwa.
در جایی که قربانی سوختنی را ذبح کنند، قربانی جرم را نیز ذبح بکنند، و خونش را به اطراف مذبح بپاشند.۲
3 Tsono apereke mafuta ake onse: mchira wamafuta ndi mafuta amene amakuta matumbo.
و ازآن همه پیه‌اش را بگذراند، دنبه و پیه که احشا رامی پوشاند.۳
4 Aperekenso impsyo ziwiri, mafuta ake pamodzi ndi mafuta onse amene ali chamʼchiwuno, ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi.
و دو گرده و پیهی که بر آنهاست که بر دو تهیگاه است، و سفیدی را که بر جگر است، با گرده‌ها جدا کند.۴
5 Wansembe azitenthe pa guwa kuti zikhale nsembe yotentha pa moto, yoperekedwa kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo lopalamula.
و کاهن آنها را برای هدیه آتشین بجهت خداوند بسوزاند. این قربانی جرم است.۵
6 Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kudyako nsembeyo koma adyere ku malo opatulika. Imeneyi ndi nsembe yopatulika kwambiri.
و هر ذکوری از کاهنان آن را بخورد، درمکان مقدس خورده شود. این قدس اقداس است.۶
7 “‘Nsembe yopepesera tchimo lopalamula ndi yofanana ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo. Ndipo nsembe ziwiri zonsezi zili ndi lamulo limodzi lokha. Wansembe amene wachita mwambo wa nsembe yopepesera machimo a kupalamula atenge nyamayo ngati yake.
«قربانی جرم مانند قربانی گناه است. آنها رایک قانون است. کاهنی که به آن کفاره کند از آن اوخواهد بود.۷
8 Wansembe wopereka nsembe yopsereza ya munthu wina aliyense, atenge chikopa cha nsembe yopserezayo kuti chikhale chake.
و کاهنی که قربانی سوختنی کسی را گذراند، آن کاهن پوست قربانی سوختنی را که گذرانید برای خود نگه دارد.۸
9 Chopereka chilichonse cha chakudya chophika mu uvuni kapena chokazinga mu mʼphika kapena mu chiwaya ndi cha wansembe amene wapereka nsembezo.
و هر هدیه آردی که در تنور پخته شود و هر‌چه بر تابه یا ساج ساخته شود از آن کاهن که آن راگذرانید خواهد بود.۹
10 Ndipo chopereka china chilichonse cha chakudya chosakaniza ndi mafuta kapena chowuma, chikhale cha ana onse a Aaroni ndipo anawo achigawane mofanana.
و هر هدیه آردی، خواه به روغن سرشته شده، خواه خشک، از آن همه پسران هارون بی‌تفاوت یکدیگر خواهدبود.۱۰
11 “‘Malamulo a nsembe ya chiyanjano imene munthu angathe kupereka kwa Yehova ndi awa:
«و این است قانون ذبیحه سلامتی که کسی نزد خداوند بگذراند.۱۱
12 “‘Ngati munthuyo apereka chifukwa cha kuthokoza, apereke nsembeyo pamodzi ndi makeke wopanda yisiti, osakaniza ndi mafuta; timitanda ta buledi wopanda yisiti, topyapyala, topaka mafuta, ndiponso makeke a ufa wosalala wophikidwa bwino, wosakaniza ndi mafuta.
اگر آن را برای تشکربگذراند پس با ذبیحه تشکر، قرصهای فطیرسرشته شده به روغن، و نازکهای فطیر مالیده شده به روغن، و از آرد نرم آمیخته شده، قرصهای سرشته شده به روغن را بگذراند.۱۲
13 Pamodzi ndi nsembe yachiyanjano yothokozerayo abwerenso ndi makeke opangidwa ndi yisiti ngati chopereka chake.
با قرصهای نان خمیر مایه دار قربانی خود را همراه ذبیحه تشکر سلامتی خود بگذراند.۱۳
14 Munthuyo atenge mtanda umodzi pa mtanda wa buledi wa mtundu uliwonse kuti ukhale nsembe yopereka kwa Yehova. Tsono mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe yachiyanjano.
و از آن از هرقربانی یکی را برای هدیه افراشتنی نزد خداوندبگذراند، و از آن آن کاهن که خون ذبیحه سلامتی را می‌پاشد خواهد بود.۱۴
15 Nyama ya nsembe yachiyanjano yothokozera idyedwe pa tsiku lomwe nsembeyo yaperekedwa ndipo isatsaleko mpaka mmawa.
و گوشت ذبیحه تشکرسلامتی او در روز قربانی وی خورده شود، چیزی از آن را تا صبح نگذارد.۱۵
16 “‘Koma ngati nsembe yakeyo apereka chifukwa cha lumbiro kapena mwaufulu, nsembeyo adye tsiku lomwe yaperekedwalo. Koma yotsala angathe kuyidya mmawa mwake.
و اگر ذبیحه قربانی او نذری یا تبرعی باشد، در روزی که ذبیحه خود را می‌گذراند خورده شود، و باقی آن در فردای آن روز خورده شود.۱۶
17 Ngati nyama ina ya nsembe yatsalabe mpaka tsiku lachitatu, imeneyo itenthedwe pa moto.
و باقی گوشت ذبیحه در روز سوم به آتش سوخته شود.۱۷
18 Ngati munthu adya nyama yachiyanjano pa tsiku lachitatu, nsembeyo sidzalandiridwa. Amene wayipereka nsembeyo Mulungu sadzamulandira ndipo nsembeyo idzakhala yonyansa pamaso pa Mulungu, yosamupindulira kanthu woperekayo.
و اگرچیزی از گوشت ذبیحه سلامتی او در روز سوم خورده شود مقبول نخواهد شد و برای کسی‌که آن را گذرانید محسوب نخواهد شد، نجس خواهد بود. و کسی‌که آن را بخورد گناه خود رامتحمل خواهد شد.۱۸
19 “‘Nyama imene yakhudza chilichonse chodetsedwa, munthu asayidye, koma itenthedwe pa moto. Aliyense amene ali woyeretsedwa angathe kudya nyama inayo.
و گوشتی که به هر چیزنجس برخورد، خورده نشود، به آتش سوخته شود، و هر‌که طاهر باشد از آن گوشت بخورد.۱۹
20 Koma ngati munthu wina amene ndi wosayeretsedwa adya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.
لیکن کسی‌که از گوشت ذبیحه سلامتی که برای خداوند است بخورد و نجاست او بر اوباشد، آن کس از قوم خود منقطع خواهد شد.۲۰
21 Ndipo ngati munthu wina akhudza chinthu chodetsedwa, kaya chonyansa cha munthu kapena cha nyama, kapenanso chonyansa china chilichonse, ndipo kenaka nʼkudya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati anthu a mtundu wake.’”
وکسی‌که هر چیز نجس را خواه نجاست آدمی، خواه بهیمه نجس، خواه هر چیز مکروه نجس رالمس کند، و از گوشت ذبیحه سلامتی که برای خداوند است بخورد، آن کس از قوم خود منقطع خواهد شد.»۲۱
22 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
و خداوند موسی را خطاب کرده، گفت:۲۲
23 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Musadye mafuta a ngʼombe, nkhosa kapenanso mbuzi.
«بنی‌اسرائیل را خطاب کرده، بگو: هیچ پیه گاوو گوسفند و بز را مخورید.۲۳
24 Mafuta a nyama yofa yokha, kapena mafuta a nyama yophedwa ndi zirombo akhoza kuwagwiritsa ntchito iliyonse, koma inu musadye mafuta amenewo.
اما پیه مردار و پیه حیوان دریده شده برای هر کار استعمال می‌شود، لیکن هرگز خورده نشود.۲۴
25 Pakuti munthu wakudya mafuta a nyama yoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe yotentha pa moto, ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
زیرا هر‌که پیه جانوری که از آن هدیه آتشین برای خداوندمی گذرانند بخورد، آن کس که خورد، از قوم خودمنقطع شود.۲۵
26 Ndipo kulikonse kumene mukakhale musakadye magazi a mbalame iliyonse kapena magazi a nyama iliyonse.
و هیچ خون را خواه از مرغ خواه از بهایم در همه مسکنهای خود مخورید.۲۶
27 Ngati munthu aliyense adya magazi achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.’”
هرکسی‌که از هر قسم خون بخورد، آن کس از قوم خود منقطع خواهد شد.»۲۷
28 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
و خداوند موسی را خطاب کرده، گفت:۲۸
29 “Awuze Aisraeli kuti, Aliyense amene apereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, abwere ndi gawo la nsembeyo kwa Yehova.
«بنی‌اسرائیل را خطاب کرده، بگو: هر‌که ذبیحه سلامتی خود را برای خداوند بگذراند، قربانی خود را از ذبیحه سلامتی خود نزد خداوندبیاورد.۲۹
30 Atenge ndi manja ake zigawo za chopereka zoyenera kuzitentha pa moto ngati chopereka kwa Yehova. Abweretse mafuta, pamodzi ndi chidale chomwe, ndipo chidalecho achiweyule kuti chikhale chopereka choweyula kwa Yehova.
به‌دستهای خود هدایای آتشین خداوند را بیاورد، پیه را با سینه بیاورد تا سینه بجهت هدیه جنبانیدنی به حضور خداوندجنبانیده شود.۳۰
31 Wansembe atenthe mafutawo pa guwa koma chidalecho chikhale cha Aaroni ndi ana ake.
و کاهن پیه را بر مذبح بسوزاند، و سینه از آن هارون و پسرانش خواهد بود.۳۱
32 Mumupatse wansembe ntchafu ya kumanja ya nsembe yanu yachiyanjano kuti ikhale chopereka chanu kwa iye.
وران راست را برای هدیه افراشتنی از ذبایح سلامتی خود به کاهن بدهید.۳۲
33 Mwana wa Aaroni amene amapereka magazi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano, adzitenga ntchafu ya kumanja kukhala gawo lake.
آن کس از پسران هارون که خون ذبیحه سلامتی وپیه را گذرانید، ران راست حصه وی خواهد بود.۳۳
34 Choncho pa zopereka zachiyanjano za Aisraeli, Ine ndatengapo chidale chomwe amaweyula ndi ntchafu zimene amapereka nsembe ndipo ndazipereka kwa wansembe Aaroni ndi ana ake. Izi ndizo gawo lawo nthawi zonse pa zopereka za Aisraeli.”
زیرا سینه جنبانیدنی و ران افراشتنی را از بنی‌اسرائیل از ذبایح سلامتی ایشان گرفتم، و آنها را به هارون کاهن و پسرانش به فریضه ابدی از جانب بنی‌اسرائیل دادم.»۳۴
35 Zimenezi ndi chigawo cha Aaroni ndi ana ake chotapidwa pa zopereka kwa Yehova zoti zitenthedwe pa moto zimene zinaperekedwa pa tsiku limene anapatulidwa kuti akhale ansembe otumikira Yehova.
این است حصه مسح هارون و حصه مسح پسرانش از هدایای آتشین خداوند، در روزی که ایشان را نزدیک آورد تابرای خداوند کهانت کنند.۳۵
36 Yehova ndiye analamulira kuti pa zopereka za Aisraeli azitapapo zimenezi ndi kuwapatsa ansembe ngati gawo lawo. Yehovayo analamula zimenezi pa tsiku limene ansembewo anapatulidwa ndipo anachikhazikitsa ngati lamulo la nthawi zonse.
که خداوند امرفرمود که به ایشان داده شود، در روزی که ایشان را از میان بنی‌اسرائیل مسح کرد، این فریضه ابدی در نسلهای ایشان است.۳۶
37 Awa ndi malamulo a nsembe izi: nsembe yopsereza, nsembe yachakudya, nsembe yopepesera machimo, nsembe yopepesera kupalamula, nsembe ya mwambo wodzoza ndi nsembe yachiyanjano.
این است قانون قربانی سوختنی و هدیه آردی و قربانی گناه و قربانی جرم و قربانی تقدیس و ذبیحه سلامتی،۳۷
38 Malamulo amenewa Yehova anapereka kwa Mose pa Phiri la Sinai pa tsiku limene Yehova analamulira Aisraeli kuti abwere ndi zopereka za kwa Yehova, ku chipululu cha Sinai kuja.
که خداوند به موسی در کوه سینا امر فرموده بود، درروزی که بنی‌اسرائیل را مامور فرمود تاقربانی های خود را نزد خداوند بگذرانند درصحرای سینا.۳۸

< Levitiko 7 >