< Levitiko 7 >

1 “‘Malamulo a nsembe yopepesera kupalamula imene ndi nsembe yopatulika kwambiri ndi awa:
“‘Le yimithetho ephathelene lomnikelo wecala, oyiwo ongcwele kakhulu.
2 Nsembe yopepesera machimo iziphedwa pamalo pomwe amaphera nsembe yopsereza ndipo awaze magazi ake mbali zonse za guwa.
Umnikelo wecala kufanele uhlatshelwe endaweni lapho umnikelo wokutshiswa ohlatshelwa khona, njalo igazi lawo kufanele lichelwe emaceleni wonke e-alithare.
3 Tsono apereke mafuta ake onse: mchira wamafuta ndi mafuta amene amakuta matumbo.
Wonke amahwahwa awo azanikelwa: umsila ononileyo kanye ledanga elembesa ezangaphakathi,
4 Aperekenso impsyo ziwiri, mafuta ake pamodzi ndi mafuta onse amene ali chamʼchiwuno, ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi.
izinso zombili lamahwahwa azo aseduzane lesinqe, lamahwahwa aphezu kwesibindi, okufanele kukhutshwe lezinso.
5 Wansembe azitenthe pa guwa kuti zikhale nsembe yotentha pa moto, yoperekedwa kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo lopalamula.
Umphristi uzakukutshisela e-alithareni njengomhlatshelo wokudla onikelwa kuThixo. Kungumnikelo wecala.
6 Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kudyako nsembeyo koma adyere ku malo opatulika. Imeneyi ndi nsembe yopatulika kwambiri.
Wonke owesilisa emulini yomphristi angakudla, kodwa kufanele kudlelwe endaweni engcwele; ngoba kungcwele kakhulu.
7 “‘Nsembe yopepesera tchimo lopalamula ndi yofanana ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo. Ndipo nsembe ziwiri zonsezi zili ndi lamulo limodzi lokha. Wansembe amene wachita mwambo wa nsembe yopepesera machimo a kupalamula atenge nyamayo ngati yake.
Umthetho munye uyasetshenziswa emnikelweni wesono kanye lemnikelweni wecala. Ungowomphristi owenza kube lendlela yokubuyisana labo.
8 Wansembe wopereka nsembe yopsereza ya munthu wina aliyense, atenge chikopa cha nsembe yopserezayo kuti chikhale chake.
Umphristi onikela umnikelo wokutshiswa kabani lobani angazigcinela isigogo.
9 Chopereka chilichonse cha chakudya chophika mu uvuni kapena chokazinga mu mʼphika kapena mu chiwaya ndi cha wansembe amene wapereka nsembezo.
Wonke umnikelo wamabele ophekelwa eziko, loba ophekelwa embizeni, loba embizeni yensimbi ungowomphristi owunikelayo,
10 Ndipo chopereka china chilichonse cha chakudya chosakaniza ndi mafuta kapena chowuma, chikhale cha ana onse a Aaroni ndipo anawo achigawane mofanana.
njalo wonke umnikelo wamabele oyabe uhlanganiswe lamafutha loba womile, wonke ungowamadodana ka-Aroni ngokulinganayo.’”
11 “‘Malamulo a nsembe ya chiyanjano imene munthu angathe kupereka kwa Yehova ndi awa:
“‘Le yimithetho ephathelene lomnikelo wobudlelwano umuntu angawunikela kuThixo:
12 “‘Ngati munthuyo apereka chifukwa cha kuthokoza, apereke nsembeyo pamodzi ndi makeke wopanda yisiti, osakaniza ndi mafuta; timitanda ta buledi wopanda yisiti, topyapyala, topaka mafuta, ndiponso makeke a ufa wosalala wophikidwa bwino, wosakaniza ndi mafuta.
Nxa unganikelwa njengendlela yokubonga, kumele lumnikelo wokubonga unikelwe ndawonye lesinkwa esenziwe singelamvubelo sahlanganise lamafutha, amakhekhe ayizicecedu enziwe engelamvubelo njalo egcotshwe ngamafutha, kanye lamakhekhe efulawa ecolekileyo avutshwe kuhle ahlanganiswa lamafutha.
13 Pamodzi ndi nsembe yachiyanjano yothokozerayo abwerenso ndi makeke opangidwa ndi yisiti ngati chopereka chake.
Umnikelo wakhe wobudlelwano ongowokubonga kumele unikelwe ndawonye lomnikelo wezinkwa ezenziwe ngemvubelo.
14 Munthuyo atenge mtanda umodzi pa mtanda wa buledi wa mtundu uliwonse kuti ukhale nsembe yopereka kwa Yehova. Tsono mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe yachiyanjano.
Kufanele alethe okukodwa komhlobo munye ngamunye njengomnikelo onikelwa kuThixo. Ungowomphristi ochela igazi lomnikelo wobudlelwano.
15 Nyama ya nsembe yachiyanjano yothokozera idyedwe pa tsiku lomwe nsembeyo yaperekedwa ndipo isatsaleko mpaka mmawa.
Inyama yomnikelo wakhe wobudlelwano ingeyokubonga, kumele idliwe ngalelolanga inikelwa. Akumelanga eyinye isalele elakusasa.
16 “‘Koma ngati nsembe yakeyo apereka chifukwa cha lumbiro kapena mwaufulu, nsembeyo adye tsiku lomwe yaperekedwalo. Koma yotsala angathe kuyidya mmawa mwake.
Kodwa nxa umnikelo wakhe ungenxa yokugcwalisa isifungo loba ungumnikelo wesihle, umhlatshelo lowo uzadliwa ngalelolanga lokuwunikela, kodwa okuyabe kusele kungadliwa ngelanga elilandelayo.
17 Ngati nyama ina ya nsembe yatsalabe mpaka tsiku lachitatu, imeneyo itenthedwe pa moto.
Yonke inyama yomhlatshelo esalayo kuze kwedlule insuku ezintathu kufanele itshiswe.
18 Ngati munthu adya nyama yachiyanjano pa tsiku lachitatu, nsembeyo sidzalandiridwa. Amene wayipereka nsembeyo Mulungu sadzamulandira ndipo nsembeyo idzakhala yonyansa pamaso pa Mulungu, yosamupindulira kanthu woperekayo.
Nxa kulenyama yomnikelo wobudlelwano engadliwa ngelanga lesithathu, lowo oyinikeleyo kasoze amukeleke. Ayisoze ibalelwe kulowo oyinikeleyo, ngoba ingahlambulukanga. Umuntu odla enye yayo uzakuba lomlandu ngayo.
19 “‘Nyama imene yakhudza chilichonse chodetsedwa, munthu asayidye, koma itenthedwe pa moto. Aliyense amene ali woyeretsedwa angathe kudya nyama inayo.
Inyama ethinta loba yini engcolileyo ngokomkhuba akumelanga idliwe; kumele itshiswe. Kodwa eyinye inyama ingadliwa yiloba ngubani ohlambulukileyo ngokomkhuba.
20 Koma ngati munthu wina amene ndi wosayeretsedwa adya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.
Kodwa nxa kulomuntu ongcolileyo angadla inyama yomnikelo wobudlelwano engekaThixo, lowomuntu kumele axotshwe ebantwini bakibo.
21 Ndipo ngati munthu wina akhudza chinthu chodetsedwa, kaya chonyansa cha munthu kapena cha nyama, kapenanso chonyansa china chilichonse, ndipo kenaka nʼkudya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati anthu a mtundu wake.’”
Nxa kulomuntu othinta okuthile okungcolileyo, akukhathalekile kumbe kuyikungcola komuntu loba okwenyamazana loba okunye nje okungcolileyo, okwenyanyekayo, abesesidla inyama yomnikelo wobudlelwano engekaThixo, lowomuntu kumele axotshwe ebantwini bakibo.’”
22 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
UThixo wathi kuMosi,
23 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Musadye mafuta a ngʼombe, nkhosa kapenanso mbuzi.
“Tshela abako-Israyeli uthi: ‘Lingaze ladla amahwahwa enkomo, awezimvu loba awembuzi.
24 Mafuta a nyama yofa yokha, kapena mafuta a nyama yophedwa ndi zirombo akhoza kuwagwiritsa ntchito iliyonse, koma inu musadye mafuta amenewo.
Amahwahwa enyamazana ezifeleyo loba edatshulwe yizilo zeganga angasetshenziswa kokunye, kodwa akumelanga liwadle.
25 Pakuti munthu wakudya mafuta a nyama yoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe yotentha pa moto, ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
Umuntu odla amahwahwa enyamazana okungenziwa ngayo umnikelo wokutshiswa kuThixo kumele axotshwe ebantwini bakibo.
26 Ndipo kulikonse kumene mukakhale musakadye magazi a mbalame iliyonse kapena magazi a nyama iliyonse.
Njalo lingadli igazi lenyoni loba inyamazana yiphi kuzozonke izindawo elihlala kuzo.
27 Ngati munthu aliyense adya magazi achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.’”
Nxa umuntu esidla igazi, lowomuntu kumele axotshwe ebantwini bakibo.’”
28 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
UThixo wathi kuMosi,
29 “Awuze Aisraeli kuti, Aliyense amene apereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, abwere ndi gawo la nsembeyo kwa Yehova.
“Tshela abako-Israyeli uthi: ‘Umuntu oletha umnikelo wobudlelwano kuThixo kumele alethe ingxenye yawo njengomhlatshelo wakhe kuThixo.
30 Atenge ndi manja ake zigawo za chopereka zoyenera kuzitentha pa moto ngati chopereka kwa Yehova. Abweretse mafuta, pamodzi ndi chidale chomwe, ndipo chidalecho achiweyule kuti chikhale chopereka choweyula kwa Yehova.
Kumele anikele ngezandla zakhe umhlatshelo wokudla kuThixo. Kumele alethe amahwahwa, ndawonye lesifuba, abesezunguza isifuba phambi kukaThixo njengomnikelo wokuzunguza.
31 Wansembe atenthe mafutawo pa guwa koma chidalecho chikhale cha Aaroni ndi ana ake.
Umphristi uzatshisa amahwahwa e-alithareni, kodwa isifuba ngesika-Aroni kanye lamadodana akhe.
32 Mumupatse wansembe ntchafu ya kumanja ya nsembe yanu yachiyanjano kuti ikhale chopereka chanu kwa iye.
Kumele uphe umphristi umlenze wesokunene eminikelweni yakho yobudlelwano ube ngumnikelo wakho.
33 Mwana wa Aaroni amene amapereka magazi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano, adzitenga ntchafu ya kumanja kukhala gawo lake.
Indodana ka-Aroni enikela igazi lamahwahwa omnikelo wobudlelwano izathola umlenze wesokunene njengesabelo sayo.
34 Choncho pa zopereka zachiyanjano za Aisraeli, Ine ndatengapo chidale chomwe amaweyula ndi ntchafu zimene amapereka nsembe ndipo ndazipereka kwa wansembe Aaroni ndi ana ake. Izi ndizo gawo lawo nthawi zonse pa zopereka za Aisraeli.”
Ngithethe isifuba esizunguzwayo kanye lomlenze onikelwayo emnikelweni wobudlelwano wabako-Israyeli ngapha u-Aroni umphristi kanye lamadodana akhe njengesabelo sabo sezikhathi zonke esivela kwabako-Israyeli.’”
35 Zimenezi ndi chigawo cha Aaroni ndi ana ake chotapidwa pa zopereka kwa Yehova zoti zitenthedwe pa moto zimene zinaperekedwa pa tsiku limene anapatulidwa kuti akhale ansembe otumikira Yehova.
Le yingxenye yemihlatshelo yokudla enikelwa kuThixo eyabelwa u-Aroni kanye lamadodana akhe ngelanga abethulwa ngalo ukuba basebenzele uThixo njengabaphristi.
36 Yehova ndiye analamulira kuti pa zopereka za Aisraeli azitapapo zimenezi ndi kuwapatsa ansembe ngati gawo lawo. Yehovayo analamula zimenezi pa tsiku limene ansembewo anapatulidwa ndipo anachikhazikitsa ngati lamulo la nthawi zonse.
Ngelanga abagcotshwa ngalo, uThixo walaya abako-Israyeli ukuthi banikele lokho njengasabelo sabo sezikhathi zonke kuzizukulwane ezizayo.
37 Awa ndi malamulo a nsembe izi: nsembe yopsereza, nsembe yachakudya, nsembe yopepesera machimo, nsembe yopepesera kupalamula, nsembe ya mwambo wodzoza ndi nsembe yachiyanjano.
Le-ke yiyo imithetho emayelana lomnikelo wokutshiswa, umnikelo wamabele, umnikelo wesono, umnikelo wecala, umnikelo wokugcotshwa lomnikelo wobudlelwano,
38 Malamulo amenewa Yehova anapereka kwa Mose pa Phiri la Sinai pa tsiku limene Yehova analamulira Aisraeli kuti abwere ndi zopereka za kwa Yehova, ku chipululu cha Sinai kuja.
uThixo awupha uMosi entabeni yeSinayi ngelanga alaya ngalo abako-Israyeli ukuthi balethe iminikelo yabo kuThixo, enkangala yaseSinayi.

< Levitiko 7 >