< Levitiko 7 >

1 “‘Malamulo a nsembe yopepesera kupalamula imene ndi nsembe yopatulika kwambiri ndi awa:
And this is the lawe of sacrifice for trespas; it is hooli `of the noumbre of hooli thingis.
2 Nsembe yopepesera machimo iziphedwa pamalo pomwe amaphera nsembe yopsereza ndipo awaze magazi ake mbali zonse za guwa.
Therfor where brent sacrifice is offrid, also the sacrifice for trespas schal be slayn; the blood therof schal be sched bi the cumpas of the auter.
3 Tsono apereke mafuta ake onse: mchira wamafuta ndi mafuta amene amakuta matumbo.
Thei schulen offre the tail therof, and the fatnesse that hilith the entrailis,
4 Aperekenso impsyo ziwiri, mafuta ake pamodzi ndi mafuta onse amene ali chamʼchiwuno, ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi.
the twei litle reynes, and the fatnesse which is bisidis ilioun, and the calle of the mawe, with the litle reynes.
5 Wansembe azitenthe pa guwa kuti zikhale nsembe yotentha pa moto, yoperekedwa kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo lopalamula.
And the preest schal brenne tho on the auter; it is encense of the Lord, for trespas.
6 Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kudyako nsembeyo koma adyere ku malo opatulika. Imeneyi ndi nsembe yopatulika kwambiri.
Ech male of the preestis kyn schal ete these fleischis in the hooli place, for it is hooli `of the noumbre of hooli thingis.
7 “‘Nsembe yopepesera tchimo lopalamula ndi yofanana ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo. Ndipo nsembe ziwiri zonsezi zili ndi lamulo limodzi lokha. Wansembe amene wachita mwambo wa nsembe yopepesera machimo a kupalamula atenge nyamayo ngati yake.
As a sacrifice is offrid for synne, so and for trespas, o lawe schal be of euer eithir sacrifice; it schal perteyne to the preest, that offrith it.
8 Wansembe wopereka nsembe yopsereza ya munthu wina aliyense, atenge chikopa cha nsembe yopserezayo kuti chikhale chake.
The preest that offrith the beeste of brent sacrifice, schal haue the skyn therof.
9 Chopereka chilichonse cha chakudya chophika mu uvuni kapena chokazinga mu mʼphika kapena mu chiwaya ndi cha wansembe amene wapereka nsembezo.
And ech sacrifice of wheete flour, which is bakun in an ouene, and what euer is maad redi in a gridile, ethir in a friyng panne, it schal be that preestis, of whom it is offrid,
10 Ndipo chopereka china chilichonse cha chakudya chosakaniza ndi mafuta kapena chowuma, chikhale cha ana onse a Aaroni ndipo anawo achigawane mofanana.
whether it is spreynt with oile, ethir is drye. To alle the sones of Aaron euene mesure schal be departyd, `to ech `bi hem silf.
11 “‘Malamulo a nsembe ya chiyanjano imene munthu angathe kupereka kwa Yehova ndi awa:
This is the lawe of `the sacrifice of pesible thingis, which is offrid to the Lord.
12 “‘Ngati munthuyo apereka chifukwa cha kuthokoza, apereke nsembeyo pamodzi ndi makeke wopanda yisiti, osakaniza ndi mafuta; timitanda ta buledi wopanda yisiti, topyapyala, topaka mafuta, ndiponso makeke a ufa wosalala wophikidwa bwino, wosakaniza ndi mafuta.
If the offryng is for doyng of thankyngis, thei schulen offre looues without sour dow spreynt with oile, and `therf looues sodun in watir, that ben anoyntid with oile; and thei schulen offre wheete flour bakun, and thinne looues spreynt to gidere with the medlyng of oile.
13 Pamodzi ndi nsembe yachiyanjano yothokozerayo abwerenso ndi makeke opangidwa ndi yisiti ngati chopereka chake.
Also thei schulen offre `looues diyt with sour dow, with the sacrifice of thankyngis which is offrid for pesible thingis;
14 Munthuyo atenge mtanda umodzi pa mtanda wa buledi wa mtundu uliwonse kuti ukhale nsembe yopereka kwa Yehova. Tsono mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe yachiyanjano.
of whiche o loof schal be offrid to the Lord for the firste fruytis, and it schal be the preestis that schal schede the blood of the sacrifice,
15 Nyama ya nsembe yachiyanjano yothokozera idyedwe pa tsiku lomwe nsembeyo yaperekedwa ndipo isatsaleko mpaka mmawa.
whose fleischis schulen be etun in the same dai, nether ony thing of tho schal dwelle til the morewtid.
16 “‘Koma ngati nsembe yakeyo apereka chifukwa cha lumbiro kapena mwaufulu, nsembeyo adye tsiku lomwe yaperekedwalo. Koma yotsala angathe kuyidya mmawa mwake.
If a man offrith a sacrifice bi a vow, ethir bi fre wille, it schal be etun in lijk maner in the same dai; but also if ony thing dwellith `in to the morew, it is leueful to ete it;
17 Ngati nyama ina ya nsembe yatsalabe mpaka tsiku lachitatu, imeneyo itenthedwe pa moto.
sotheli fier schal waaste, whateuer thing the thridde day schal fynde.
18 Ngati munthu adya nyama yachiyanjano pa tsiku lachitatu, nsembeyo sidzalandiridwa. Amene wayipereka nsembeyo Mulungu sadzamulandira ndipo nsembeyo idzakhala yonyansa pamaso pa Mulungu, yosamupindulira kanthu woperekayo.
If ony man etith in the thridde dai of the fleischis of sacrifice of pesible thingis, his offryng schal be maad voide, nethir it schal profite to the offerere; but rather whateuer soule defoulith hym silf with suche mete, he schal be gilti of `brekyng of the lawe.
19 “‘Nyama imene yakhudza chilichonse chodetsedwa, munthu asayidye, koma itenthedwe pa moto. Aliyense amene ali woyeretsedwa angathe kudya nyama inayo.
Fleisch that touchith ony vnclene thing, schal not be etun, but it schal be brent bi fier; he that is clene, schal ete it.
20 Koma ngati munthu wina amene ndi wosayeretsedwa adya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.
A pollutid soule, that etith of the fleischis of the sacrifice of pesible thingis, which is offrid to the Lord, schal perische fro hise puplis.
21 Ndipo ngati munthu wina akhudza chinthu chodetsedwa, kaya chonyansa cha munthu kapena cha nyama, kapenanso chonyansa china chilichonse, ndipo kenaka nʼkudya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati anthu a mtundu wake.’”
And he that touchith vnclennesse of man, ether of beeste, ether of alle thing that may defoule, and etith of suche fleischis, schal perische fro hise puplis.
22 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
And the Lord spak to Moises,
23 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Musadye mafuta a ngʼombe, nkhosa kapenanso mbuzi.
and seide, Speke thou to the sones of Israel, Ye schulen not ete the ynnere fatnesse of a scheep, of an oxe, and of a geet;
24 Mafuta a nyama yofa yokha, kapena mafuta a nyama yophedwa ndi zirombo akhoza kuwagwiritsa ntchito iliyonse, koma inu musadye mafuta amenewo.
ye schulen haue in to dyuerse vsis the ynnere fatnesse of a carkeis deed by it silf, and of that beeste which is takun of a rauenus beeste.
25 Pakuti munthu wakudya mafuta a nyama yoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe yotentha pa moto, ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
If ony man etith the ynnere fatnesse, that owith to be offrid in to encense of the Lord, he schal perische fro his puple.
26 Ndipo kulikonse kumene mukakhale musakadye magazi a mbalame iliyonse kapena magazi a nyama iliyonse.
Also ye schulen not take in mete the blood of ony beeste, as wel of briddis as of beestis;
27 Ngati munthu aliyense adya magazi achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.’”
ech man that etith blood schal perische fro his puplis.
28 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
And the Lord spak to Moises,
29 “Awuze Aisraeli kuti, Aliyense amene apereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, abwere ndi gawo la nsembeyo kwa Yehova.
and seide, Speke thou to the sones of Israel, He that offrith a sacrifice of pesible thingis to the Lord, offre togidere also a sacrifice, that is, fletynge offryngis therof.
30 Atenge ndi manja ake zigawo za chopereka zoyenera kuzitentha pa moto ngati chopereka kwa Yehova. Abweretse mafuta, pamodzi ndi chidale chomwe, ndipo chidalecho achiweyule kuti chikhale chopereka choweyula kwa Yehova.
He schal holde in the hondis the ynnere fatnesse of the sacrifice, and the brest; and whanne he hath halewid bothe offrid to the Lord, he schal yyue to the preest,
31 Wansembe atenthe mafutawo pa guwa koma chidalecho chikhale cha Aaroni ndi ana ake.
which schal brenne the ynnere fatnesse on the auter; sotheli the brest schal be Aarons and hise sones;
32 Mumupatse wansembe ntchafu ya kumanja ya nsembe yanu yachiyanjano kuti ikhale chopereka chanu kwa iye.
and the riyt schuldur of the sacrifices of pesible thingis schal turne in to the firste fruytis of the preest.
33 Mwana wa Aaroni amene amapereka magazi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano, adzitenga ntchafu ya kumanja kukhala gawo lake.
He that of Aarons sones offrith the blood, and the ynnere fatnesse, schal haue also the riyt schuldur in his porcioun.
34 Choncho pa zopereka zachiyanjano za Aisraeli, Ine ndatengapo chidale chomwe amaweyula ndi ntchafu zimene amapereka nsembe ndipo ndazipereka kwa wansembe Aaroni ndi ana ake. Izi ndizo gawo lawo nthawi zonse pa zopereka za Aisraeli.”
For Y haue take fro the sones of Israel the brest of reisyng, and the schuldur of departyng, of the pesible sacrifices `of hem, and Y haue youe to Aaron the preest and to hise sones, bi euerlastynge lawe, of al the puple of Israel.
35 Zimenezi ndi chigawo cha Aaroni ndi ana ake chotapidwa pa zopereka kwa Yehova zoti zitenthedwe pa moto zimene zinaperekedwa pa tsiku limene anapatulidwa kuti akhale ansembe otumikira Yehova.
This is the anoyntyng of Aaron, and of hise sones, in the cerymonyes of the Lord, in the dai where ynne Moises offride hem that thei schulden be set in preesthod,
36 Yehova ndiye analamulira kuti pa zopereka za Aisraeli azitapapo zimenezi ndi kuwapatsa ansembe ngati gawo lawo. Yehovayo analamula zimenezi pa tsiku limene ansembewo anapatulidwa ndipo anachikhazikitsa ngati lamulo la nthawi zonse.
and whiche thingis the Lord comaundide to be youun to hem of the sones of Israel, bi euerlastynge religioun in her generaciouns.
37 Awa ndi malamulo a nsembe izi: nsembe yopsereza, nsembe yachakudya, nsembe yopepesera machimo, nsembe yopepesera kupalamula, nsembe ya mwambo wodzoza ndi nsembe yachiyanjano.
This is the lawe of brent sacrifice, and of sacrifice for synne, and for trespas, and for halewyng, and for the sacrifices of pesible thingis;
38 Malamulo amenewa Yehova anapereka kwa Mose pa Phiri la Sinai pa tsiku limene Yehova analamulira Aisraeli kuti abwere ndi zopereka za kwa Yehova, ku chipululu cha Sinai kuja.
which lawe the Lord ordeynede to Moises in the hil of Synay, whanne he comaundide to the sones of Israel that thei schulden offre her offryngis to the Lord, in the deseert of Synay.

< Levitiko 7 >